13/08/2026
Komiti yomwe ikufufuza za ngozi yandege yomwe inachitika ku Chikangawa yayamba kuzukuta maumboni omwe inalandira mundime yoyamba yakafukufukuyu dzulo.
Malingana ndi uthenga omwe nyumba yamalamulo yatulutsa aphunguwa apitiliza kukumana mukachipinda komata lero pantchito younika maumboniyi pamene akukonzekera kuyamba ndime yachiwiri pa 24 August chaka chino.
Wapampando wakomitiyi Walter Nyamilandu wati ndime yoyamba inayala maziko abwino omwe athandize komiti patsogolo la ntchitoyi.
Ndime yachiwiri ya kafukufuku ikhudzanso kuwunika matupi ndi a katswiri owunika matupi ochokera mdziko la South Africa, Robert Gabriel Ngunde ndi Wilson Sibusiso Ntsele.
Wolemba: Joseph Mazizi