10/06/2026
Timu ya Creck Sporting yalengeza kuti yachotsa ntchito mphunzitsi wamkulu Eliya Kananji, wachiwiri wake Harrison Saidi komanso wochititsa mafizo Blessings Tembo.
Atatuwa anaimitsidwa pa ntchito masiku apitawa potsatira kusachita bwino kwa timuyi.
Komabe, mu kalata yomwe yatulutsa, timuyi yayamikira aphunzitsiwa chifukwa cha kulimbikira kwawo pantchito ndipo yawafunira zabwino.
Timu ya Creck sinapambanepo masewero aliwonse mu FDH Premiership ndipo iri pansi penipeni pa mndandanda wa matimu mu mpikisanowu ndi ma point awiri okha basi.
Wolemba: Rhodes Msonkho Jr.