MBC Digital

MBC Digital Malawi's TV broadcaster featuring various programs both local and international.

09/09/2025



Mtsutso wachiwiri wa ena mwa atsogoleri a zipani omwe apikisane pa 16 September tsopano wayamba ku Bingu International Convention Centre ku Lilongwe.

Mwazina, atsogoleriwa akhala akuyankha mafunso ndi kufotokoza mfundo zawo, maka pa zomwe adzachite m'magawo osiyanasiyana akawasankha pa chisankhochi.

Mtsogoleri wa UTM, a Dalitso Kabambe komanso mtsogoleri wa UDF, a Atupele Muluzi, ndi omwe ali pa mtsutsowu.

Olemba: Beatrice Mwape

09/09/2025

Presidential Debate (9 September 2025)

09/09/2025
09/09/2025

Ndi Ifeyo Mangochi Young Politicians Union (9 September 2025)

  Taekwondo Association of Malawi has secured a K2 million sponsorship from Anchor Industries, through its medicated ski...
09/09/2025



Taekwondo Association of Malawi has secured a K2 million sponsorship from Anchor Industries, through its medicated skin care soap, Detrex.

The sponsorship is meant for the Malawi National Taekwondo Team to travel for the Africa Open Series Zone 6, taking place in Maputo, Mozambique from 20 to 21 September.

Unveiling the sponsorship in Blantyre, the company's Head of Marketing, Faraz Dalv,i said this is not just sponsorship but a commitment to nurturing future champions and inspiring a new generation.

Taekwondo Association of Malawi General Secretary, Medson Mtila, commended Anchor Industries for bailing them out, while coach for the team, Stanislaus Phiri, assured the sponsors that they will bring home gold medals.

Team Malawi is made up of Lucy Mphande and Joseph Phiri, and will compete against athletes from nine other countries.

By Norbert Jameson

  Malawi Communications Regulatory Authority (MACRA), says there is need to bridge the gap on internet access and knowle...
09/09/2025



Malawi Communications Regulatory Authority (MACRA), says there is need to bridge the gap on internet access and knowledge usage between the urban areas and rural or marginalised areas.

MACRA Deputy Legal Director responsible for consumer protection, Kelious Mlenga, made the remarks during the ground breaking ceremony for the construction of Gomani Chikuse CDSS ICT laboratory with 60 computers in Kasale Village, T/A Kwataine in Ntcheu District. The project is worth K400 million.

Headmaster of the school, Joseph Mphezi, stressed the need to beef for more security of the school computers when the laboratory is finished.

Group Village Head Kasale thanked MACRA for bringing development in her area through the laboratory at Gomani Chikuse CDSS.

By Hudson Nkumbira, Ntcheu

  Mmodzi mwa achinyamata omwe akupikisana nawo pa chisankho ngati khansala oyima payekha kudera la Chitawira-Nkolokosa-M...
09/09/2025



Mmodzi mwa achinyamata omwe akupikisana nawo pa chisankho ngati khansala oyima payekha kudera la Chitawira-Nkolokosa-Manja, a Ramadan Chikondi Binali, alonjeza anthu mderali kudzabweretsa chipatala choyendayenda akawasankha pa udindowu.

Iwo afotokozera MBC kuti derali, kwa nthawi yaitali, lakhala likutsalira pa chitukuko, zomwe zawalimbikitsa kuima pa chisankho ngati mbali imodzi yofuna kutukula miyoyo ya anthu.

Kumbali ya zomangamanga, a Binali ati adzayesetsa kukonza misewu yomwe imalumikiza madera atatuwa.

Wolemba: Ruth Chinangwa, Blantyre.

09/09/2025

Nkhani za Chisankho (9 September 2025)

  Yemwe akuima payekha pampikisano wa uphungu wanyumba ya malamulamulo, Lita Langa, wauza anthu kwa Nyama Yaphwisa ku Mc...
09/09/2025



Yemwe akuima payekha pampikisano wa uphungu wanyumba ya malamulamulo, Lita Langa, wauza anthu kwa Nyama Yaphwisa ku Mchinji kuti amuvotere kuti adzasinthe miyoyo yawo mderali.

Langa wati adzakonza mavuto monga kumanga sukulu ndi zipatala kutengera ndizomwe zikufunika kuderako ndipo anapitiriza kunena kuti azidzakhala ndi mafumu, kufunsa zomwe zikufunika.

Gulupu Nyama Yaphwisa apempha a Langa kuti akasankhidwa adzawakonzereko mavuto amadzi chifukwa madzi akuvuta kwambiri kudera kwawo ndipo amayi akuyenda ulendo wautali kukasaka madzi.

Wolemba Chancy Chirwa Mchinji

09/09/2025



Nduna ya zaulimi, a Sam Kawale, ati kupatula ndondomeko ya AIP, boma laikanso ndondomeko ina yomwe ithandizire alimi kugula feteleza otsika mtengo, yomwe akuitcha Affordable Fertiliser Programme.

A Kawale ati cholinga cha ndondomekoyi ndikuthandizira alimi omwe ali mmagulu ndipo adziloredwa kugula matumba anayi a feteleza. Iwo anaonjezera kuti alimi omwe akhale pansi pa ndondomekoyi akuyenera kulembetsa malo awo.

Ndunayi yatsimikiziranso alimi m’dziko muno kuti alimi ayamba kugula feteleza yemwe ali pansi pa ndondomeko ya AIP pa 1 October (mwezi wa mawa) ndipo feteleza yemwe ali pansi pa ndondomeko ya feteleza otsika mtengo, alimi ayamba kugula mwezi uno.

Iwo atinso feteleza yemwe ali pansi pa ndondomeko ya feteleza otsika mtengo adzigulitsidwa pa mtengo wa K90, 000 ndipo feteleza yemwe ali pansi pa ndondomeko ya AIP adzigulitsidwa pa mtengo wa K15,000.

A Kawale ati boma layamba ntchito yogula feteleza ku kampani ya United Fertiliser Capital mdziko la Zambia, ndipo mu gawo loyamba, boma ligula matani 300,000 a fetelezayi.

Olemba: Madalitso Mhango

  Mfumu yaikulu Mizinga ya m'boma la Machinga, yalangiza mafumu onse m’dziko muno kuti alimbikitse kupereka uthenga wa b...
09/09/2025



Mfumu yaikulu Mizinga ya m'boma la Machinga, yalangiza mafumu onse m’dziko muno kuti alimbikitse kupereka uthenga wa bata ndi mtendere pakati pa andale ndi mmadera mwawo mumasiku asanu ndi awiri omwe atsala kuti dziko lino lichite chisankho.

A Mizinga ati ndikofunika kulimbikitsa bata ndicholinga chodzakhala ndi chisankho chopanda ziwawa.

Iwo amayankhula izi lero pa sukulu ya Nanyumbu pomwe amakumana ndi akuluakulu andale m’bomali pofuna kuwalimbikitsa kusunga bata ndi mtendere.

M'mawu ake, Andrew Sachidu amene ndi gavanala wa chipani chotsutsa boma cha DPP, wati awonetsetsa kuti nthawi yatsalayi akuchita kampeni wa bata.

Bungwe loyendetsa chisankho m’dziko muno la MEC litseka ntchito yokopa anthu lamulungu lino.

Wolemba: Serah Chikwapula Machinga

09/09/2025



Karonga First Grade Magistrate’s Court has fined 22-year-old Samuel Mphwanthe K900,000 for causing death by reckless driving and driving without a licence.

The case follows a February 2024 incident in which Mphwanthe, driving a Toyota Sienta without a licence, crashed into a tree, killing passenger Wandumi Mwangululukula.

According to Karonga Police spokesperson Constable Margret Msiska, Senior Resident Magistrate Ephraim Chikwakwa ordered Mphwanthe to pay K700,000 for causing death and K200,000 for driving without a licence, or serve six months in prison.

Msiska added that K500,000 of the fine will go to the deceased’s family as compensation.

By Blessings Mtika, Karonga

Address

P.O. Box 30133
Chichiri
312225

Telephone

+2651872498

Alerts

Be the first to know and let us send you an email when MBC Digital posts news and promotions. Your email address will not be used for any other purpose, and you can unsubscribe at any time.

Contact The Business

Send a message to MBC Digital:

Share