Nation Publications Limited

Nation Publications Limited Established in 1993, Nation Publications Ltd is an award-winning media house providing credible news

Nation Publications Limited, Publishers of The Nation, Weekend Nation, Nation On Sunday, Nation Online and Fuko

 A polisi m'boma la Rumphi apempha anthu kuti akhale osamala pamene akusangalalira tsiku la anakubala pa 15 mwezi uno lo...
13/10/2025



A polisi m'boma la Rumphi apempha anthu kuti akhale osamala pamene akusangalalira tsiku la anakubala pa 15 mwezi uno lomwe liri lachitatu likubwerali.

Poyankhula ndi Nation Online, mneneri wa apolisi m'bomali a Noel Kamchenga ati apolisi akhala akuyendera usiku ndi usana kupereka chitetezo pa nthawiyi.

"Tikupempha anthu amene adzisangalala pa tsikuli kuti agwilitse ntchito magalimoto ovomerezeka komanso asiye anthu m'makomo mwawo akamachoka pamene ife apolisi tikhala tikupereka chitetezo chokhwima pa nthawiyi kuyambira pa 14 mpaka 16 mwezi uno" Kamchenga watero.

A Kamchenga ati apempha anthu kuti akadzawona zachilendo chilichons azawauze apolisi chifukwa anthu ena amapezerapo mwayi ochita upandu anzawo pa nthawiyi.

"Anthu akawona chilichonse chawupandu chikuchitika azatiziwitse chifukwa ifeyo tikufuna tchuthi chimenechi chikhale chopambana" iwo atero.

(Wolemba: Taonga Chizinga Nyirenda-Correspondent)

 Alimi okwana 3000 kuchokera m'boma la Machinga akuyembekezeka kupindula ndi thandizo la zipangizo za ulimi, pansi pa nt...
13/10/2025



Alimi okwana 3000 kuchokera m'boma la Machinga akuyembekezeka kupindula ndi thandizo la zipangizo za ulimi, pansi pa ntchito yotchedwa Hope Fields initiative, yomwe mpingo wa Salvation for All Ministries wakhadzikitsa lero m'bomali.

Poyankhula lero pambuyo pokhazikitsa magulu alimi m'madera Mfumu Nyambi ndi Mlomba, mtsogoleri wa Mpingowu, Clifford Kawinga, wati ntchitoyi yakhazikitsidwa be cholinga chofuna kuthana ndi vuto la njala komanso kuonetsetsa kuti mabanja akutha kudziimira pa okha.

A Kawinga anatsindika za kufunika kogwirana manja pakati pa anthu omwe ali ndi kuthekera pantchito yothana ndi vuto la njala lomwe lakuta mabanja ochuluka mdziko muno.

Mwazina mpingowu wapereka zipangizo monga matumba 50 a feteleza, mbewu ya chimanga yolemera makilogalamu 50, makina opopela madzi kudzera ku mphavu ya dzuwa, makasu olimira, komanso matumba a chimanga.

Poyankhula atalandira thandizoli, a Mfumu Nyambi ati ndiokondwa kuti anthu awo azitha kuchita ulimi osiyanasiyana kwa chaka chonse zomwe ati zithandizira dera lake kukhala ndi chakudya chokwanira.

(Wolemba: Haneeph Maulana-Correspondent)

 Wild game hunter Ian Bartlett has released a new book, “Memoirs of a Real Crocodile Hunter,” sharing his experiences de...
13/10/2025



Wild game hunter Ian Bartlett has released a new book, “Memoirs of a Real Crocodile Hunter,” sharing his experiences dealing with dangerous animals that threaten people’s livelihoods.

Bartlett, who worked with the Department of National Parks and Wildlife for over 10 years, said the book aims to help rural communities manage problem animals such as crocodiles, hyenas, and buffaloes.

Now based in the UK, Bartlett describes his work as a blend of adventure, humour, and survival.

The book is available at www.therealcrocodilehunter.com

(Report by Wisdom Chirombo – Correspondent)

 Moto watentha nyumba ya mayi  wina yemwe amachita malonda m’boma la Nkhata Bay, a Fatima Kilembe momwe katundu wa ndala...
13/10/2025



Moto watentha nyumba ya mayi wina yemwe amachita malonda m’boma la Nkhata Bay, a Fatima Kilembe momwe katundu wa ndalama zokwana K25 Miliyoni wapsera momwemo.

Mneneri wa polisi m’bomali a Enala Kalua ati izi zachitikira m’mudzi mwa Singo pomwe mayiwa anasiya ana awo awiri ndikupita kochita malonda.

“Kenaka anawa akusewera ndi anzawo, anawona moto ukuyaka zomwe zinachititsa kuti adziwitse anthu ena koma anthu akufuna kwabwino analephera kuzimitsa motuwu,” iwo atero.

Iwo ati wina mwa katundu yemwe wawonongeka ndi monga mafiliji, wayilesi ya kanema ya mtundu wa Plasma, sofa, matilesi, zipangizo zoyimbira, ziwiya za ku kitchini, zipangizo zophikira za magetsi mwa katundu wina.

(Wolemba: Zondani Mbale -Correspondent)

 University of Malawi (Unima) and UNDP have launched the Nzeru Hub in Zomba to boost digital literacy and skills.Unima V...
13/10/2025



University of Malawi (Unima) and UNDP have launched the Nzeru Hub in Zomba to boost digital literacy and skills.

Unima Vice Chancellor Samson Sajidu said the hub will drive Malawi’s digital transformation through training, innovation, and accessibility.

UNDP’s Phyllis Chibisa said the hub, powered by Microsoft, will equip students, women, and communities with vital digital skills and certifications.

(Report by Holyce Kholowa – Correspondent)

  I repaid mega farm loan in full-Chilomba Documentation we have seen shows that acting Director General of the Anti-Cor...
13/10/2025



I repaid mega farm loan in full-Chilomba

Documentation we have seen shows that acting Director General of the Anti-Corruption Bureau (ACB) Hilary Chilomba paid in full the K113.7 million loan that he got through the Mega Farm project under the Ministry of Agriculture.


The Mega Farm project is a government initiative which is run by the Ministry of Agriculture through the Mega Farm Support Unit Department in partnership with the Malawi Agriculture and Industrial Corporation (MAIIC).


The social media has since yesterday been awash with documents showing the list of people who got loans from the project.

In the loan, Chilomba got 800 bags of fertiliser (Urea and NPK), totalling K83.2 million, maize seed valued at K16 million, pesticides and chemicals at K6.6 million. This translated to a principal loan of K105.8 million, while interest charged, by June 2025, amounted to K7.9 million.


Documents show that on seven separate occasions in August 2025, Chilomba supplied 117 820 kilograms of maize as loan repayment through the National Food Reserve Agency (NFRA).

A separate letter from MAIIC acting chief executive officer Lloyd Banda on August 20, confirms that Chilomba made the said supply, and his balance had been cleared.

It reads: “We refer to your financing facility under the Malawi Agriculture and Industrial Corporation Plc (MAIIC), administered through the Mega Farms Department, and the subsequent maize deliveries made to the National Food Reserve Agency (NFRA) in line with your off-take agreement.

“We are pleased to confirm that MAIIC has received the full value of the maize delivered (totalling 117, 820kgs) and that the corresponding proceeds have been applied towards the full settlement of your outstanding loan balance. Accordingly, your loan account is now fully cleared and closed, with no further obligations on your part under this facility.”

In an interview, Chilomba decried continued misinformation on social media regarding the loan repayment, saying, “Some people are just trying to dent my image and score political mileage.”


Report by Joseph Mwale

 People's Development Party (PDP) president and sole member of Parliament-elect Kondwani Nankhumwa is eyeing the positio...
13/10/2025



People's Development Party (PDP) president and sole member of Parliament-elect Kondwani Nankhumwa is eyeing the position of Speaker of Parliament.

Nankhumwa's spokesperson, Rhodes Msonkho, has confirmed that the Mulanje Central legislator-elect is interested in the position.

A poster promoting Nankhumwa's bid states that the former Leader of Opposition has a vision to provide impartial stewardship and a commitment to maintaining order, decorum and efficiency in Parliament.

The election of Speaker, First Deputy Speaker and Second Deputy Speaker will take place on October 29 following the swearing in of newly elected legislators on October 27 and 28.

Last week, governing Democratic Progressive Party and UTM Party confirmed that their legislators had shown interest in the Speakership while the Malawi Congress Party said it was still strategising.

 Mkulu wa zaulimi m'boma la Mulanje, a Osmund Chapotoka, wapempha alimi kuchita ulimi ngati bizinezi kuti azipindula ndi...
13/10/2025



Mkulu wa zaulimi m'boma la Mulanje, a Osmund Chapotoka, wapempha alimi kuchita ulimi ngati bizinezi kuti azipindula ndi thukuta lawo.

Polankhula Lolemba pa chiwonetsero cha zaulimi m'dera la Mbande, Chapotoka adati ndi mavuto akusintha kwa nyengo omwe akusokoneza ulimi, alimi atsate njira za makono zopindulitsa monga kusanduliza zokolola komanso kuteteza mbewu kuti zichite bwino.

Mfumu Juma idati kusintha kwa nyengo kwapangitsa njira zamakolo kukoledzera njala ndi umphawi.

"Nthawi yakwana yochita zinthu zopindulitsa monga kuika madonga m'munda ndi kuthira manyowa kuti mbewu zizichita bwino zomwe zithandize kuthetsa njala ndi kuchita malonda bwino," iwo adatero.

Chiwonetsero cha masiku awirichi chikuchitika pa mutu wolimbikitsa malonda ndi kutukuka kudzera mu njira za ulimi zokhazikika.

(Wolemba: Temwa Mhone, Correspondent)

13/10/2025

Online

Apolisi m'boma la Zomba amanga abambo awiri a Peter Champion a zaka 22 ndi a Lojasi Mukholi a zaka 50 powaganizira kuti adapha mayi Dorothy Maluwa a zaka 41 mdera la Mpyupyu m'bomalo.

Mneneri wa apolisi m'bomalo a Patricia Sipiliano ati pa October 3 chaka chino mayiyo adapeza abambowo kusaka ganyu yomanyamula katundu wawo kumakasiya ku doko la Thongwe ku nyanja ya Chilwa.

Mneneriyo wati ganyuyo idapezekadi ndipo anamuwuza mayiyo kuti adzayambe tsiku lotsatira pa October 4.

"Malemuwo atafika kukayamba ganyuyo, abambowo adagwilira mayiyo kenako kumupha ndikumukwilira ku bafa kwa nyumba yawoyo," atero a Sipiliano.

Mneneriyo wati achibale a malemuwo atalengezetsa zakusowa kwa m'bale wawoyo, kafukufuku adayambika kufikira thupilo litapezeka patadutsa masiku.

"Zotsatira za chipatala zaonetsa kuti mayiyo adachita kupotokoledwa khosi ndipo oganizilidwawo adavomera kuti adaphadi mayiyo," adatero Sipiliano.

Abambowo amene onse amachokera m'mudzi wa Chipiyoni kwa Senior Chief Mwambo m'bomalo akawonekera ku bwalo la milandu posachedwapa kukayankha mulanduwo.

(Wolemba Holyce Kholowa-Corresspondent)

 Likoma Secondary School will host a cultural festival on October 25 to promote Malawi’s diverse traditions. Patron of E...
13/10/2025



Likoma Secondary School will host a cultural festival on October 25 to promote Malawi’s diverse traditions.

Patron of Entertainment Mozes Mwankhwawa said the event, involving both primary and secondary schools, aims to expose students to various careers and strengthen learning in social studies and life skills.

Chima Primary School teacher Sandra Ngwale hailed the initiative, saying it will help students appreciate and embrace their cultural heritage amid growing Western influence. Thirteen schools are expected to participate.

(Report by Florence Nyasulu – Correspondent)

 Bungwe la Orphans of Africa Foundation lapereka mipira isanu yogwiritsa ntchito ana omwe ali ndi vuto losawona ku sukul...
13/10/2025



Bungwe la Orphans of Africa Foundation lapereka mipira isanu yogwiritsa ntchito ana omwe ali ndi vuto losawona ku sukulu ya ana aulumaliri maka osawona ya St Maria Gorrette m’boma la Nkhata Bay.

Mkulu woyang’anira bungweli a Timothy Mwale ati ndi cholinga cha bungwe lawo kuwonetsetsa kuti mwana aliyense kuphatikiza aulumali wosiyanasiyana akutenga nawo gawo pa masewero a mpira.

Mkulu woyanga’anira kaphunzitsidwe ka masewero m’bomali a Shadreck Chiundiza ayamikira bungweli pothandiza kuti ana a maulumali osiyanasiyana akutenga nawo gawo pa masewero a mpira osiyanasiyana.

Glory Banda yemwe amaphunzira sitandade 6 pa sukuluyi anayamikira bungweli powapatsa thandizoli zomwe anati ziwathandiza kutukula magawo awo osiyanasiyana.

(Wolemba: Zondani Mbale -Correspondent)

  Pomwe dziko lonse likukumbukira tsiku lochepetsa chiopsezo cha ngozi zogwa mwadzidzi lero  pa 13 October, nthambi ya b...
13/10/2025



Pomwe dziko lonse likukumbukira tsiku lochepetsa chiopsezo cha ngozi zogwa mwadzidzi lero pa 13 October, nthambi ya boma yoona za ngozi zogwa mwadzidzidzi ya DoDMA yati tsikuli ndilofunikira kwambiri kuno kwathu ku Malawi.

Muuthenga wawo mkulu wanthambiyi mbusa Moses Chimphepo wati bungwe la mgwirizano wamayiko wonse la United Nations ndi limene linakhazikitsa tsikuli pa msonkhano wake waukulu mchaka cha 1989 kuti apeze njira zochepetsera chiopsezo cha ngozi zogwa mwadzidzidzi.

M'mawu ake mneneri wa nthambi ya DoDMA a Chipiliro Khamula ati nkofunika kuti Maunduna ndi Nthambi zaboma zizigajizira zoikiratu ndalama zothandizira kuchepetsa chiopsezo cha ngozi zogwa mwadzidzidzi mu ndondomeko zachitukuko.

Chaka chino tsikuli akulikumbukira pamutu woti "Kuthandiza ndi ndalama pantchito yochepetsa chiopsezo ndi kuchilimika ku ngozi zadzidzidzi osati pa nthawi yomwe ngozi zadzidzidzi zachitika.

Wolemba: Martin Gela Jnr - Correspondent)

Address

Salmin Amour Road
Chichiri

Alerts

Be the first to know and let us send you an email when Nation Publications Limited posts news and promotions. Your email address will not be used for any other purpose, and you can unsubscribe at any time.

Contact The Business

Send a message to Nation Publications Limited:

Share