15/06/2026
FM Nkhani
Bungwe lomenyera Ufulu wa odwala mdziko muno la Patient and Community Welfare Foundation of Malawi (PAWEM) layambitsa kampeni ya dziko lonse yolimbana ndi mchitidwe okuba mankhwala ndi chinyengo mzipatala zonse za m'dziko muno.
Izi zili chomwechi kutsatira zokambirana zomwe zachitika pakati pa bungweli ndi Komiti ya Zaumoyo ku Nyumba ya Malamulo, komwe mwazina aphungu avomela kuti anthu akudera atengepo mbali pothandiza kuteteza chuma cha umoyo, mzipatala.
Kudzera mu pulogalamu ya Community Health Rights Watch Initiative, PAWEM igwira ntchito m’maboma onse 28 mdziko muno Ndipo akuyembekezela kugwila Ntchito ndimagulu onse okhudzidwa kuphatikiza Atolankhani.
Ndi ntchitoyi Anthu azikwanitsa kunena za mchitidwe wa kuba mankhwala, kuwuza odwala kuti apekeke ndalama kuti apeze thandizo, tsankho kapena nkhanza zina.
Malingana ndi PAWEM yati anthu ammudzi ndiwo amakhala oyamba kuona mchitidwe uliinse wa Chinyengo omwe ukuchitika kudera.
Choncho ati atsogoleri akudera, achinyamata, amayi, achipembedzo ndi mabungwe a anthu olumala alinawo mu Campeniyi.
Walemba: Fatsani Kamwendo