Nyungwe Community Radio

Nyungwe Community Radio Nyungwe Community Radio serves as a powerful advocacy platform promoting social and economic change among over 300,000 people of Chikwawa District.

This includes addressing gender based violence and mitigating against environmental degradation.

  FM Nkhani Chiwelengero cha Anthu omwe afika mdziko muno kuchoka mdziko la South Africa chafika pa 753 kutsatira ena ok...
18/06/2026

FM Nkhani

Chiwelengero cha Anthu omwe afika mdziko muno kuchoka mdziko la South Africa chafika pa 753 kutsatira ena okwana 92 omwe afika tsopano pa bwalo la Kamuzu munzinda wa Blantyre.

Mwa omwe afikawa Amayi oyembekezela asanu ndiomwe afika mdziko muno pomwe awiri abelekera munjira.

Boma kudzera kunthambi yowona za ngozi zogwa mwadzidzidzi yati iwonetsetsa kuti anthuwa akusamalidwa bwino.

Wolemba Prosper Phiri

  FM Zamasewero Timu ya Creck Sporting Club yalengeza kuti Gerald Phiri Senior ndi Fischer Kondowe kuti ndiwo achiwiri k...
18/06/2026

FM Zamasewero

Timu ya Creck Sporting Club yalengeza kuti Gerald Phiri Senior ndi Fischer Kondowe kuti ndiwo achiwiri kwa mphunzitsi wamkulu wa timuyi Ernest Mtawali tsopano ndipo onse asayina contract ya chaka chimodzi.

Mlembi wamkulu watimuyi Aaron Kandiwo Mtaya wati awiriwa abwera kutsatila chilimbikitso cha mphunzitsi wamkulu ndipo alindi chiyembekezo kuti kubwera kwawo kuthandiza kusintha zinthu ku timuyi.

Creck Sporting Club pakadali pano ili mmunsi mwa logtable ya FDH Bank Premiership ndipo ikusakasaka chipambano chake choyamba pambuyo pamasewera asanu ndi amodzi omwe asewera.

Wolemba Prosper Phiri

  FM Nkhani Bungwe lomenyera Ufulu wa odwala mdziko muno la Patient and Community Welfare Foundation of Malawi (PAWEM) l...
15/06/2026

FM Nkhani

Bungwe lomenyera Ufulu wa odwala mdziko muno la Patient and Community Welfare Foundation of Malawi (PAWEM) layambitsa kampeni ya dziko lonse yolimbana ndi mchitidwe okuba mankhwala ndi chinyengo mzipatala zonse za m'dziko muno.

Izi zili chomwechi kutsatira zokambirana zomwe zachitika pakati pa bungweli ndi Komiti ya Zaumoyo ku Nyumba ya Malamulo, komwe mwazina aphungu avomela kuti anthu akudera atengepo mbali pothandiza kuteteza chuma cha umoyo, mzipatala.

Kudzera mu pulogalamu ya Community Health Rights Watch Initiative, PAWEM igwira ntchito m’maboma onse 28 mdziko muno Ndipo akuyembekezela kugwila Ntchito ndimagulu onse okhudzidwa kuphatikiza Atolankhani.

Ndi ntchitoyi Anthu azikwanitsa kunena za mchitidwe wa kuba mankhwala, kuwuza odwala kuti apekeke ndalama kuti apeze thandizo, tsankho kapena nkhanza zina.

Malingana ndi PAWEM yati anthu ammudzi ndiwo amakhala oyamba kuona mchitidwe uliinse wa Chinyengo omwe ukuchitika kudera.

Choncho ati atsogoleri akudera, achinyamata, amayi, achipembedzo ndi mabungwe a anthu olumala alinawo mu Campeniyi.

Walemba: Fatsani Kamwendo

  FM Zamasewero Mpikisano wa 2026 Airtel Top 8 ukuyembekezeka kuyamba lero Loweruka pa 13 June 2026, pomwe matimu okwana...
13/06/2026

FM Zamasewero

Mpikisano wa 2026 Airtel Top 8 ukuyembekezeka kuyamba lero Loweruka pa 13 June 2026, pomwe matimu okwana anayi akuyembekezeka kukumana pa bwalo la zamasewero la Bingu munzinda wa Lilongwe.

Blue Eagles Fc ikumana ndi Civo Service United pomwe matimu a FCB Nyasa Big Bullets ndi Ekhaya akumana 5 Koloko madzuro.

Nyasa Big Bullets Fc ndiyomwe ikusunga ndi kuteteza ukatswiriwu pomwe inatenga itagonjetsa Silver Strikers Fc munzinda wa Lilongwe.

  FM Nkhani Alimi omwe amapanga ulimi wa Nsomba mboma la Chikwawa adandsaula kuti kusowa kwa Ana a Nsomba kukukhudza uli...
13/06/2026

FM Nkhani

Alimi omwe amapanga ulimi wa Nsomba mboma la Chikwawa adandsaula kuti kusowa kwa Ana a Nsomba kukukhudza ulimi wawo.

Izi zadziwika lachisanu pomwe wachiwiri kwa nduna ya zachilengedwe Chipiliro Mpinganjira, anayendera alimiwa ku Kasinthula m’boma lino.

Polankhula ndi Wailesi ino yemwe amaona nkhani ya za chuma ku Peka Fisheries, Ramzan Kalimu wati mavuto akusowa kwa ana a Nsomba akudza chifukwa magulu onse omwe akuchita ulimiwu m’boma lino amadalira malo amodzi ogula, komabe watsindika kuti mu ulimi wa nsomba muli phindu.

Kumbali yake wachiwiri kwa nduna, Chipiliro Mpinganjira wati unduna wawo ukuzindikira bwino za ubwino wa ulimiwu kotero alonjeza kuti aika chidwi potukula ulimiwu.

Wolemba Prosper Phiri

  FM NewsCommunity Focus says its education support program across primary schools in Chikwawa District is making steady...
12/06/2026

FM News

Community Focus says its education support program across primary schools in Chikwawa District is making steady progress.

Speaking to Nyungwe FM, COFO Monitoring and Evaluation Officer Andrew Tembo said the organization is planning to increase electricity capacity in schools around the district, including Mantchombe and Chilongoma.

“This will help learners prepare better for exams and have more time to study during night hours,” Tembo explained.

Despite the infrastructure push, Tembo urged parents to do their part, He called on them to encourage children by emphasizing the value of education, instead of assigning household tasks that cut into study time.

“Parental involvement in promoting education can help learners quickly realize the benefits of schooling,” he added.

Reported by Prosper Phiri

M’MENE NYENGO IKHALIRE  PA 12 JUNE 2026 Tiyembekezere nyengo yozizira m’madera ambiri ndi chifunga m’madera ena. Masana,...
12/06/2026

M’MENE NYENGO IKHALIRE PA 12 JUNE 2026

Tiyembekezere nyengo yozizira m’madera ambiri ndi chifunga m’madera ena.

Masana, tiyembekezere nyengo ya mitambo yapatalipatali ndi yofunda m’madera ambiri

Langizo, tiyembekezele mphepho ya mphamvu nthawi zina pa nyanja zathu zonse

Mphepo Ikuomba kuchokera kumwera chakumvuma

Loweruka tiyembekezere Nyengo ya dzuwa ndi yofunda

*M’MENE NYENGO IKHALIRE  PA 12 JUNE 2026* Tiyembekezere nyengo yozizira m’madera ambiri ndi chifunga m’madera ena. Masan...
12/06/2026

*M’MENE NYENGO IKHALIRE PA 12 JUNE 2026*

Tiyembekezere nyengo yozizira m’madera ambiri ndi chifunga m’madera ena.

Masana, tiyembekezere nyengo ya mitambo yapatalipatali ndi yofunda m’madera ambiri

Langizo, tiyembekezele mphepho ya mphamvu nthawi zina pa nyanja zathu zonse

Mphepo Ikuomba kuchokera kumwera chakumvuma

Loweruka tiyembekezere Nyengo ya dzuwa ndi yofunda

  Timu ya FCB Nyasa Big Bullets tsopano ili ndi mphunzitsi watsopano. Akuluakulu oyendetsa timuyi alengeza kuti Wedson N...
10/06/2026



Timu ya FCB Nyasa Big Bullets tsopano ili ndi mphunzitsi watsopano.

Akuluakulu oyendetsa timuyi alengeza kuti Wedson Nyilenda wamdziko la Zambia ndiye mphunzitsi yemwe wasinthana ndi Gilbert Chirwa.

Izi zalengezedwa lero pa msonkhano wa atolankhani omwe timuyi inakomza munzinda wa Blantyre.

10/06/2026

FM Nkhani

Ku Chikwawa bwalo la milandu la First Grade Magistrate lagamula a Francis Kagome a zaka 30 zakubadwa kupeleka chindapusa Cha ndalama zokwana 700,000 popezeka wolakwa pa mulandu ochita malonda a chipatala komanso kugulitsa mankhwala achipatala popanda mapepala achilolezo

Wofalitsa Nkhani za polisi ku Chikwawa Sergeant Dickson Matemba wati bwaloli lagamula a Kagome lachiwiri pa 9 June 2026 pamene lidamva kuchokera kwa woyimira boma pa milandu Assistant Superintendent Ernest Mangwena kuti pa 29 May chaka chino anthu akufuna kwabwino adawatsina khutu apolisi kuti Kagome akuchita malonda achipatala pa nsika wa mapelera komwenso amagulitsa mankhwala popanda chilolezo ndipo apolisi atathamangira pa malowa adapeza Kagome ndipo atamufusa za mapepala achilolezo adakanika kuwonetsa zomwe zidachititsa apolisi kumutsekera mchitokosi chawo

Pokawonekera ku bwalo la milandu Kagome adapempha chigamulo chofewa ponena kuti adavomera mulanduwo mwachangu mosatayitsa nthawi bwaloli komanso uwu unali ulendo oyamba kupalamula

Popeleka chigamulo chake First Grade Magistrate Annie Chikhadzula adagwilizana ndi woyimira boma pa milandu Assistant Superintendent Ernest Mangwena kuti Kagome akuyenera kulandira chigamulo chokhwima pofuna kuthetsa m'chitidwe wochita malonda achipatala ndi kugulitsa mankhwala achipatala popanda mapepala achilolezo omwe uli ndi kuthekera koyika miyoyo ya anthu pa chiopsezo kotero bwaloli lalamula Kagome kupeleka chindapusa Cha ndalama zokwana 700,000 kapena kukagwira ndende ya kalavula gaga kwa zaka ziwiri ndipo mankhwala omwe adalandidwawo akuyenera kupititsidwa Malo osungira mankhwala kuti akawaunike

Francis Kagome amachokera m'mudzi mwa Mafumbi kwa mfumu yaikulu Makhuwira m'bomali

Wolemba Martha M'biza

Address

Chikwawa

Alerts

Be the first to know and let us send you an email when Nyungwe Community Radio posts news and promotions. Your email address will not be used for any other purpose, and you can unsubscribe at any time.

Share