Chibvomelezi FM

Chibvomelezi FM Chibvomelezi Fm 107.6 MHZ is a vibrant and Commercial modern community radio station based in Ngabu.

The Radio is currently the Winner of the Best Community Media House of the year 2025/2026 MISA Malawi Award .

Anthu okhala mozungulira nkhalango yosungiramo nyama za ntchire ya Lengwe National Park awadandaulira kuti asiye mchitid...
17/06/2025

Anthu okhala mozungulira nkhalango yosungiramo nyama za ntchire ya Lengwe National Park awadandaulira kuti asiye mchitidwe wakuba ndi kuwononga waya wa mpanda ozungulira nkhalangoyi.

Dandauloli likudza potsatira kutuluka kwa nyama za mu nkhalango ya Lengwe zomwe kamba ka kubedwa kwa waya wa mpanda wake otchinjiriza kutuluka kwa nyamazi, zayika pa chiopsezo umoyo wa anthu a mbomali.

Izi zikutsatiranso kuphedwa kwa anthu awiri ndi kuvulazidwanso kwa anthu awiri kwa Jombo mu dera la mfumu yayikulu Ngabu m’boma la Chikwawa, ndi njati yolusa yomwe inathawa mu nkhalango yosungiramo nyama za ntchire ya Lengwe.

Choncho potsatira kupezeka ndi kuphedwa kwa njatiyi dzulo ndi alenje aboma, Kennedy Nzeru, yemwe ndi mkulu oyang’anira nkhalango ya Lengwe, wati kuthawa kwa nyamazi mu nkhalangoyi ndi chifukwa cha mchitidwe wa anthu wena ozungulira nkhalangoyi omwe anaba waya wa mpanda yemwe amathandiza kuti nyama zisamathawe mu nkhalangoyo.

Malingana ndi Nzeru, waya wa mpanda wa nkhalango ya Lengwe anabedwa patangopita nthawi yochepa chimuyikire pa mpanda wa nkhalangoyi.

Ndipo ngakhale sanakambe za nthawi yomwe mpanda wina udzayikidwenso ku nkhalangoyi, Nzeru wauza wailesi ya Chibvomelezi kuti asanayambe ntchito yokonzanso mpandawu, akhala akukambirana ndi anthu ozungulira nkhalangoyi kuti apeze njira zothandiza kuti anthuwa adzikhala ndi umwini komanso udindo osamalira mpanda wa nkhalangoyi.

Bungwe lotolera misonkho mdziko muno la Malawi Revenue Authority (MRA) alipempha kuti liwonjezere nthawi yolemba nkaundu...
16/06/2025

Bungwe lotolera misonkho mdziko muno la Malawi Revenue Authority (MRA) alipempha kuti liwonjezere nthawi yolemba nkaundula njinga za kabaza zomwe zilipo mdziko muno.

Pempholi likuchokera kwa Moses Michael Mwalabu yemwe ndi wa pampando wa eni njinga za kabaza mdziko muno.

Pempholi likudza pomwe pangotsala sabata ziwiri kuti nthawi ithe yomwe inayikidwa kuti njinga za kabaza zikhale zitalembedwa mu kaundula wake mdziko muno.

Boma kudzera kwa bungwe la MRA linakhazikitsa 30 June 2025 ngati mathero a ntchito yolemba mu kaundula wa njinga za kabaza mdziko muno.

Koma Mwalabu akuti mkofunika kuti nthawiyi ayiwonjezere kuti eni njingazi apeze ndalama zokwanira zolembetsera njinga zao mu kaundulayu.

Malingana ndi Mwalabu, eni njinga za kabaza ambiri akukumana ndi vuto la za chuma, mwa zina kamba ka kusowa kwa mafuta a galimoto, omwe abwenzeretsa pa mbuyo ntchito zawo mdziko muno.

Chomcho Mwalabu wati kuonjezera nthawiyi ndi miyezi ina itatu kuthandiza kuti eni njingazi apeze ndalama yokwanira yolipilira kalemberayu komanso kuzindikira za ubwino otenga nawo mbali pa kalemberayu.

Fodya olemera ma kilogalamu 98.4 million ndi yemwe wagulitsidwa chitsekulire msika wa chaka chino wa fodya sabata zokwan...
16/06/2025

Fodya olemera ma kilogalamu 98.4 million ndi yemwe wagulitsidwa chitsekulire msika wa chaka chino wa fodya sabata zokwana khumi zapitazo.

Malingana ndi bungwe loyang’anira malonda a fodya mdziko muno la la To***co Commission (TC), fodya ameneyu wapezetsa dziko lino ndalama zokwana $245.6 million, zomwe ndi zokwana K420 million.

Koma malingana ndi bungweli, ndalamazi ndi zochepa poyerekezera ndi ndalama zokwana $299 million zomwe zinapezeka pa nthawi ngati yomweyi, kuchokera ku malonda a fodya.

Pa nthawiyi, mkuti dziko lino litagulitsa fodya okwana ma kilogalamu 100 million pa mtengo wa pakati kati pa $2.89 pa kilogalamu imodzi ya fodya.

Mpingo wa CCAP wayika 10 July 2025 ngati tsiku lomwe lidzakhale ndi mapemphero a padera opemphelera chisankho cha patatu...
16/06/2025

Mpingo wa CCAP wayika 10 July 2025 ngati tsiku lomwe lidzakhale ndi mapemphero a padera opemphelera chisankho cha patatu chomwe chichitike mdziko muno kumapeto a chaka chino.

Izi ndi malingana ndi kalata yomwe watulutsa ndi Baxton Maulidi yemwe ndi wachiwiri kwa Moderator wa Synod ya Blantyre ya mpingo wa CCAP.

Kalatayi yati pa tsiku la mapempherowo omwe adzachitikire ku holo ya HHI Multipurpose mu mzinda wa Blantyre, kudzakhala kupemphelera zisankhozi kuti zidzakhale za bata ndi mtendere.

Kuonjezera apo Maulidi wati mapempherowa akonzedwanso kuti pa zisankhozi Mulungu adzadalitse, kupereka chisomo komanso kutsogolera anthu kusankha atsogoleri aku mtima kwao.

Pakali pano mpingowu wapempha akhristu ake kuti ayike nthawi ya padera yopemphelera zisankhozi.

Ma komishonala omwe asankhidwanso kuti apitilire kugwira ntchito yao ku bungwe la Malawi Electoral Commission (MEC) awap...
16/06/2025

Ma komishonala omwe asankhidwanso kuti apitilire kugwira ntchito yao ku bungwe la Malawi Electoral Commission (MEC) awapempha kuti adzigwira ntchitoyi motsatira malamulo.

Pempholi laperekedwa pa mwambo olumbitritsa ma komishonalawa, omwe ndi atatu, omwe wachitika dzulo ku bwalo la likulu la milandu la mu mzinda wa Lilongwe.

Ma komishonalawa ndi Caroline Mfune, Dr Emmanuel Fabiano, komanso Richard Chapweteka.

Polankhula pa mwambowu, mkulu wa ma bwalo a milandu mdziko muno Rezine Mzikamanda, yemwe anayendetsa mwambowu, anati kusankhidwanso kachiwiri kwa makomishonalawa kukutanthauza kuthekera kwao kogwira bwino ntchitoyi mokomera anthu mdziko muno.

Chomcho Mzikamanda wati ndi kofunika kwambiri kuti ma komishonalawa agwire ntchito yawo motsata malamulo oyendetsera zisankho mdziko muno.

Naye Anabel Mtalimanja, yemwe ndi wapampando wa bungwe la MEC, wapempha makomishonalawa kuti asamakondere mbali pa kagwiridwe ka ntchito yao.

Ofesi ya kalembera wa zipani za ndale mdziko muno yati kufikira pano, dziko la Malawi lili ndi zipani ziwiri zokha zomwe...
16/06/2025

Ofesi ya kalembera wa zipani za ndale mdziko muno yati kufikira pano, dziko la Malawi lili ndi zipani ziwiri zokha zomwe zili ndi zoziyenereza kulandira thandizo la ndalama kuchokera ku boma.

Mkulu wa ofesiyi Kizito Tenthani ndi yemwe wanena izi pa msonkhano wa olemba nkhani omwe anachititsa mu mzinda wa Lilongwe.

Zipanizi ndi cholamula cha Malawi Congress Party (MCP) komanso chotsutsa boma cha Democratic Progressive Party (DPP).

Malingana ndi Tenthani, chipani chimayenera kulandira thandizo la ndalama kuchokera ku boma ngati chili ndi aphungu okwana mmodzi pa 10 ali onse omwe ali ku nyumba ya malamulo.

Ndipo Tenthani wati kuyambira mu chaka cha 2023 kufika cha 2024, chipani cha MCP chinalandira ndalama zokwana K78, 205, 128. 20, pomwe chipani cha DPP chinalandira zokwana K71, 794, 871. 80.

Koma kufikira pano, Tenthani wati ndi chipani cha MCP chokha chomwe chabweretsa ku ofesi yake ndandanda wa momwe chinagwiritsira ntchito ndalamazi.

Pakali pano, Tenthani watinso palibe chipani chili chonse mdziko muno chomwe chalandira thandizo la ndalama kuchokera kwa anthu komanso mabungwe wena akufuna kwabwino.

Iye wati izi zili chomwechi chifukwa palibe chipani chomwe chabweretsa ku ofesi yake ndandanda wa ndalama zomwe chalandira kuchokera kwa anthu komanso mabungwe akufuna kwabwinowa.

Mtsogoleri wa chipani cha Democratic Progressive Party (DPP) Peter Mutharika tsopano wakatenga kalata zosonyeza chidwi c...
16/06/2025

Mtsogoleri wa chipani cha Democratic Progressive Party (DPP) Peter Mutharika tsopano wakatenga kalata zosonyeza chidwi chake chodzayimira pa mpando wa mtsogoleri wa dziko lino pa chisankho cha patatu chomwe chichitike mdziko muno mu mwezi wa September.

Ganizo la Mutharika lokatenga kalatazi likudza pomwe pakhala pali manong’o nong’o kuti sadzayima pa udindowu potsatira kuchedwa kwake kokatenga kalata ku likulu la bungwe la Malawi Electoral Commission (MEC) mu mzinda wa Lilongwe.

Manong’o-nong’owa anadza potsatira malipoti wena omwe akhala akumveka kuti iwowa ali mchipatala china cha mdziko la South Africa kulandira thandizo la mankhwala, manong’onong’o omwe chipani chake cha DPP chawatsutsa.

Koma malingana ndi Sangwani Mwafulirwa yemwe ndi mneneri wa bungwe la MEC, Mutharika wakatenga kalatazi dzulo limodzi ndi Frank Mwenefumbo yemwe akuyembekezeka kudzayimira chipani cha National Development Party (NDP).

Izi zachititsa chiwerengero cha atsogoleri omwe atenga kalata zosonyeza chidwi chofuna kudzayimira pa mpando wa mtsogoleri wa dziko lino pa chisankhochi, kufika pa khumi (10).

Izi zikutsatira ganizo la wena asanu ndi atatu (8) omwe atenga kale kalatazi.

Iwowa ndi monga Reverend Hardwick Kaliya, Atupele Muluzi, Joyce Banda, Akwame Bandawe, Lazarus Chakwera, Kondwani Nankhumwa, Adil James Chilungo, komanso Milward Tobias.

Alenje a ku nkhalango yosungiramo nyama zakutchire ya Lengwe National Park lero lino akwanitsa kupeza ndi kupha njati yo...
16/06/2025

Alenje a ku nkhalango yosungiramo nyama zakutchire ya Lengwe National Park lero lino akwanitsa kupeza ndi kupha njati yolusa yomwe dzulo yapha anthu awiri ndi kuvulazanso wena awiri kwa Jombo dera la mfumu yayikulu Ngabu m’boma la Chikwawa.

Malingana ndi Kennedy Nzeru, yemwe ndi mkulu wa nthambi yoona za nkhalango ya Lengwe, njatiyi ayipeza ndi zipolopolo za mfuti zomwe akuganizira kuti ndi zochita kukonza okha anthu a mmidzi omwe amasaka nyama zakutchire popanda chilolezo.

Nzeru akuganiza kuti zipolopolozi ndi zomwe zinachititsa njatiyi kuti iluse kufika poyamba kupha komanso kuvulaza anthu mdera la Jombo.

Pakali pano Nzeru watinso akwaniritsa kukusira mu nkhalango ya Lengwe njati zina zisanu zomwe zinathawa mdziko la Mozambique kulowa mdziko muno.

Aphungu aku nyumba ya malamulo komaso ma khansala a mboma la Chikwawa awadandaulira kuti amalizitse ntchito zonse za chi...
16/06/2025

Aphungu aku nyumba ya malamulo komaso ma khansala a mboma la Chikwawa awadandaulira kuti amalizitse ntchito zonse za chitukuko zomwe anaziyamba kale, chisanafike chisankho cha patatu chomwe chichitike mdziko muno kumapeto a chaka chino.

Martin Gonche, yemwe ndi wa pampando wa khonsolo ya mboma la Chikwawa ndi yemwe wapereka pempholi polankhula ndi wailesi ya Chivomelezi.

Pempho la Gonche likudza pomwe pangotsala miyezi itatu kuti chisankhochi chichitike mdziko muno, pomwe makhansala komaso a phungu a ku nyumba ya malamulo, pakanali pano, akuoneka kuti ayika chidwi chao chonse pa ntchito yokopa anthu kuti adzawavoterenso pa ma udindowa pa chisankho chikudza, mmalo mopitiriza zitukuko zomwe anaziyamba.

Popereka pempholi, Gonche wadzudzula aphungu ndi makhansala omwe akuchita izi ponena kuti nthawi yosiya kugwira zitukukozi sinakwane.

Malingana ndi Gonche, adindowa akuyenera kudzasiya ntchitoyi pa tsiku la chisankho.

Pakali pano, Gonche wapemphanso mafumu ndi makomiti osiyana siyana aku madera a kumidzi kuti awonetsetse kuti akulondoloza ntchito za chitukuko zomwe zikuchitika mmadera awo, mmalo mochita nawo ndale.

By Henry Mponya (Chibvomelezi FM Reporter)

Tsogolo la msika wa chaka chino wa thonje ku chigwa cha mtsinje wa Shire silikuoneka bwino, potsatira kusamvana komwe ku...
16/06/2025

Tsogolo la msika wa chaka chino wa thonje ku chigwa cha mtsinje wa Shire silikuoneka bwino, potsatira kusamvana komwe kukupitilira pakati pa alimi komanso akulu akulu oyendetsa msikawu komanso kampani zogula mbewuyi.

Izi zikutsatira mikumano iwiri yomwe yaitanitsidwa sabata yatha komanso lero lolemba kwa Ngabu mboma la Chikwawa, yomwe ikuoneka kuti yalephera kupeza yankho ku kusamvanaku.

Chatsitsa dzaye kuti njovu itchoke mnyanga ndi kutsekedwa kwa misika ya thonje mbomali, itangotsekulidwa kumene, kamba ka mkwiyo wa alimi a Thonje, omwe unadza, mwa zina, kamba ka kutsika kwa mitengo yomwe kampani zimagulira mbewuyi.

Malingana ndi Malita Nyaika yemwe ndi mmodzi mwa alimi a thonje ku dera la Saopa mbomali, msikawu utatsekulidwa sabata yatha, kampani zimagula thonjeli pa mtengo wa K1, 200, omwe ndi otsika kuchoka pa mtengo wa K1, 400 omwe boma linalengeza kuti ndi ovomerezeka kugulira thonjeli.

Nyaika anati ndi zodabwitsa kuti bungwe la Cotton Council of Malawi linalora kuti kampani zidzigula thonje pa mtengo otsika chonsecho, msikawu usanayambe, linanenetsa kuti silipereka chitupa chogulira thonje ku kampani zomwe zidzigula thonjeli pa mtengo osafikira K1, 400 pa kilogalamu imodzi ya mbewuyi.

Kamba ichi, alimiwa ali ndi mantha kuti mwina kampanizi komanso bungwe la Cotton Council of Malawi agwirizana mwa nseli kuti mtengo wa thonje ukhale K1, 200 ndi cholinga choti K200 yotsala pa mtengo ovomerezeka wa K1, 400 ichotsedwe kupita ku mbewu yomwe kampanizi zinapatsa alimi pangongole kuti adzale poyamba; mbeu yomwe inalephera kubereka thonje.

Naye Montfort Lazo, yemwe ndi mlimi wina wa thonje wati iwo sakukondwa ndi ndondomeko za makono zomwe zinakhazikitsidwa zogulira thonjeli kudzera ku banki, chifukwa ambiri mwa iwo sanatsekule ma akaunti a ku banki.

Kuonjezera apo, Lazo wati alimiwa sakukondwa kuti wena mwa iwo sanalandirebe ndalama zomwe anagulitsira thonje zaka zingapo zapitazo.

Kamba ka ichi, Daniel Tambala, yemwe ndi wa pampando wà za ulimi mboma la Chikwawa, anati mkumano anawukonza ndi cholinga choti mbali zokhudzidwa pa nkhaniyi zikambirane njira zothetsa kusamvanaku.

Malingana ndi Tambala, mwa omwe amayenera kukhala nawo ku mkumanowu ndi akulu akulu a bungwe la Cotton Council of Malawi, Cotton Farmers Association of Malawi, kampani zogula thonje komanso akulu akulu ochokera ku unduna owona za ulimi.

Koma mmalo mwake, akulu akulu a ku Cotton Council of Malawi ndi kampani zogula thonje sizinabwere nawo ku mkumanowu, zomwe zayika pa chikaiko tsogolo la msika wa thonje wa chaka chino, poti mbali ziwirizi ndi zomwe zimayenera kukayankha mafunso ochokera kwa alimi ku mkumanowo komanso kupereka tsogolo la msika wa chaka chino.

Pakali pano alimi apempha boma kuti lilowelere pa nkhaniyi kuti alimi akwaniritse kugulitsa thonje lawo pa mtengo ovomerezeka.

Ntchito ya a polisi komanso alenje a boma yalowa mu tsiku la chiwiri yosaka njati yolusa yomwe ikuganiziridwa kuti yapha...
16/06/2025

Ntchito ya a polisi komanso alenje a boma yalowa mu tsiku la chiwiri yosaka njati yolusa yomwe ikuganiziridwa kuti yapha anthu awiri kwa Jombo mu dera la mfumu yayikulu Ngabu m’boma la Chikwawa.

Mwa ophedwawa, malingana ndi Dickson Matemba, yemwe ndi mneneri wa a polisi mbomalo ndi mayi wa zaka 64 komanso mwana wa khanda.

Njati yolusayi, yomwe ikuganiziridwa kuti yathawa mu nkhalango yosungilako nyama zakutchire ya Lengwe, yavulazanso anthu ena awiri omwe pakali pano akulandira thandizo la mankhwala ku chipatala cha chikulu cha pa boma la Chikwawa.

Izi zachititsa anthu okhala kwa Jombo ndi madera wena ozungulira kumeneko kuti azikhala mwa mantha.

Ndipo malingana ndi mfumu Jeffrey, ntchito zosiyana siyana kumeneko, kuphatikizapo za kumunda komanso za chitukuko zaima kamba ka mantha omwe anthu ali nawo ku nyamazi.

Koma Kennedy Nzeru, yemwe ndi mkulu wa nthambi yoona za nkhalango ya Lengwe, wati nthambiyi yafika kale kumalo angoziyi kufunafuna komwe kwathawira njati yolusayi.

Malingana ndi Nzeru, vutoli ndi kaamba ka kuwonongeka kwa mpanda oteteza nyamazi kuti zisamatuluke omwe waya wake anabedwa ndi anthu akuba chaposachedwapa.

Iye wati pogwira ntchitoyi, akufufuzanso njati zina zisanu zomwe zinathawa mdziko la Mozambique kulowa mdziko muno, ndipo wapempha kuti aliyense angawone nyamazi atsine khutu mwa changu nthambi yao yoona za nkhalango.

Boma lati likuchita chili chonse chothekera pothana ndi vuto la kusowa kwa mafuta lomwe lamanga nthenje mdziko muno.Mafu...
16/06/2025

Boma lati likuchita chili chonse chothekera pothana ndi vuto la kusowa kwa mafuta lomwe lamanga nthenje mdziko muno.

Mafuta maka maka a Petrol akhala akusowa mdziko muno kwa sabata zingapo tsopano, zomwe zasokoneza ntchito zosiyana siyana za malonda mdziko muno.

Poyankhulapo pa nkhaniyi, Clement Kanyama yemwe ndi mkulu wa bungwe la National Oil Company of Malawi (NOCMA) wati vutoli lakula chotere chifukwa cha nyengo yoyipa yomwe ili mu mchigawo cha kumpoto .

Malingana ndi Kanyama, nyengoyi ikupangitsa kukhala kovuta ntchito yobweretsa mafutawa kuchoka mchigawo cha ku mpoto kufika mzigawo za pakati ndi kummwera.

Komabe Kanyama watsindika kuti galimoto zambiri zonyamula mafutawa zili mu njira pomwe zina zafika kale mdziko muno lero ndi mafuta, zomwe zichititse kuti vutoli lichepe mu sabata yomwe yayambikayi.

Address

Ngabu
Chikwawa
315110

Alerts

Be the first to know and let us send you an email when Chibvomelezi FM posts news and promotions. Your email address will not be used for any other purpose, and you can unsubscribe at any time.

Contact The Business

Send a message to Chibvomelezi FM:

Share