Chibvomelezi FM

Chibvomelezi FM Chibvomelezi Fm 107.6 MHZ is a vibrant and Commercial modern community radio station based in Ngabu.

The Radio is currently the Winner of the Best Community Media House of the year 2025/2026 MISA Malawi Award .

Yemwe akuyembekezeka kudzayimira pa mpando wa phungu wa dera la kummwera kwa boma la Chikwawa Iliyas Abdul Karim wati ak...
31/07/2025

Yemwe akuyembekezeka kudzayimira pa mpando wa phungu wa dera la kummwera kwa boma la Chikwawa Iliyas Abdul Karim wati akufunitsitsa kuti akasankhidwanso pa chisankho chomwe chichitike mu mwezi wa September, adzapitilize zitukuko zomwe anayamba mderali.

Karim walankhula izi dzulo pakutha pa kupereka ku bungwe la Malawi Electoral Commission (MEC) kalata zosonyeza chidwi chake chodzayima pa chisankhocho.

Karim wati akasankhidwanso adzatukula derali kuti likhale lotukuka ndi zitukuko zosiyana siyana.

Ndipo iye wati ali ndi chikhulupiliro kuti adzapambana pa chisankhochi ndi mavoti ochuluka.

Pa chisankhochi, Karim akuyembekezeka kudzayimira pa udindowu ngati oyima payekha; mafumu, akulu akulu a mipingo, achinyamata, amayi ndi wena atamupempha kuti asinthe ganizo lake losiya kaye ndale.

Kampani yopanga Sugar ya Illovo yatsindika kuti ikuchita chili chonse chotheka kuti Sugar ochuluka adzipezeka mmadera os...
31/07/2025

Kampani yopanga Sugar ya Illovo yatsindika kuti ikuchita chili chonse chotheka kuti Sugar ochuluka adzipezeka mmadera osiyanasiyana a mdziko muno.

Kondwani Msimuko, yemwe ndi mkulu wa kampani ya Illovo wanena izi pakutha pa mkumano wa masiku awiri wa olemba nkhani omwe kampaniyi yake inakonza kumayambiliro a sabata ino.

Mu mkumanowu, kampaniyi imaonetsa olemba nkhaniwa mmene kampani yawo imagwilira ntchito zake zosiyana siyana monga za ku minda yake ya mzimbe komanso ku fakitale yake yopanga Sugar.

Polankhula ndi wailesi ya Chibvomelezi, Msimuko wati anayitanitsa olemba nkhaniwa pofuna kuti adziwitse a Malawi, momwe kampani yawo imagwilira ntchito zake.

Msimuko wati Sugar pakali pano akupezeka mmadera osiyana siyana a mdziko muno potsatira ntchito yomwe kampaniyi yalimbikitsa yopanga Sugar ochuluka.

Ndipo iye anati cholinga cha ntchitoyi ndi kuonetsetsa kuti Sugar akwanire mdziko muno, kampaniyi isanayambe kumugulitsa kunja kwa dziko lino.

Pakali pano, Msimuko wati kampaniyi ili ndi lingaliro lopanga mphamvu za magetsi pofuna kuonjezera mphamvu za magetsi zomwe imagwiritsa ntchito pa ntchito zake, kuchokela ku kampani ya ESCOM.

Iye wati malingaliro amenewa akatheka, magetsi amenewa, kupatula kugwilitsa ntchito yopanga Sugar, adzawaperekanso ku dziko lonse la Malawi kudzela ku kampani ya ESCOM.

⚽  MKANGO SPORTS UPDATETimu ya FCB Nyasa Big Bullets yagonjetsa timu ya Mzuzu City Hammers mu mpikisano wa TNM Super Lea...
31/07/2025

⚽ MKANGO SPORTS UPDATE

Timu ya FCB Nyasa Big Bullets yagonjetsa timu ya Mzuzu City Hammers mu mpikisano wa TNM Super League.

Mmasewero omwe anaseweredwa pa bwalo la Rumphi Stadium mboma la Rumphi, Bullets yagonjetsa timu ya Hammers ndi zigoli ziwiri kwa duuu!!!!

Timu ya Hammers inayamba bwino masewerowo pomwe imapanikiza timu ya Bullets mu chigawo chake chomwe.

Ndipo zinali zosadabwitsa pomwe timuyi inapeza penote, yomwe mwa tsoka lake, goloboyi wa timu ya Bullets Innocent Nyasulu anayichotsa kuti isalowe pa golo pake.

Kuchoka apo, timu ya Bullets inadzambatuka kutulo, pomwe inayamba kupanikiza timu ya Hammers.

Ndipo mu mphindi 77 za masewerowo, Bullets inagoletsa chigoli chake choyamba kudzera mwa Chikumbutso Salima, otseka kumbuyo kwa timu ya Hammers atalephera kuchotsa mpira omwe anasewera Andrew Juvinala.

Ndipo Hassan Kajoke anabwera ndi chigoili cha chiwiri chomwe anachita kusumbira ndi mutu potsatira free-kick yomwe anasewera Peter Banda.

Ndipo pakutha pa masewerowo, Nyasulu ndi yemwe anasankhidwa kuti wasewera bwino kuposa wena onse mbwalomo.

Bungwe la Pensioners Association of Malawi lapereka mgwazo wa mwezi umodzi ku boma kuti likhale litalipira anthu omwe an...
31/07/2025

Bungwe la Pensioners Association of Malawi lapereka mgwazo wa mwezi umodzi ku boma kuti likhale litalipira anthu omwe anapuma pa ntchito, ndalama zawo zopumira pa ntchito, Pension mchingerezi.

Bungweli lapereka mgwazowu pa mkumano wa olemba nkhani omwe linayitanitsa lero mu mzinda wa Blantyre.

Polankhula pa mkumanowu, Nellie Mkhumba yemwe ndi mtsogoleri wa bungweli, wati anthu ambiri omwe anapuma pa ntchito zao, atathandiza kwambiri pa chitukuko cha dziko lino, sakulandira ndalama zawo.

Izi, malingana ndi Mkhumba ndi zosemphana ndi malamulo oyendetsera thumba la ndalama za anthu opuma pa ntchito, zomwe zimanenetsa kuti anthuwa akuyendera kulandira ndalamazi pasanathe miyezi itatu, chipumire pa ntchito yao.

Iwo awopseza kuti ndalamazi ngati sizilipiridwa pofika pa 30 mu mwezi wa August, sachitira mwina koma kutengera boma ku bwalo la milandu.

Chipani cha Democratic Progressive Party (DPP) chalimbikitsa zokonzekera zake za msonkhano wa ndale omwe chichititse ku ...
31/07/2025

Chipani cha Democratic Progressive Party (DPP) chalimbikitsa zokonzekera zake za msonkhano wa ndale omwe chichititse ku mapeto kwa sabata ino mu mzinda wa Blantyre.

Cholinga cha msonkhanowu, omwe uchitikire pa Njamba Freedom Park la mulungu likudzali, ndi chokhazikitsa ntchito yake yokopa anthu kudzera mu manifesito ake.

Ndipo usanachitike mkumanowu, mtsogoleri wa chipanichi Peter Mutharika, komanso Jane Ansah yemwe wasankhidwa ngati odzayima naye pa mpando wa mtsogoleri wa dziko pa chisankho cha mu mwezi wa September, adzakhazikitsa Manifesito a chipanicho.

Mwambo okhazikitsa manifesitowa udzachitika mmawa wa la mulungu lomwelo ku hotelo ya Mount Soche.

Mtsogoleri wa chipani cha People's Party (PETRA) Kamuzu Chibambo walengeza kuti Chris Bulakwacha ndi yemwe adzayime ngat...
31/07/2025

Mtsogoleri wa chipani cha People's Party (PETRA) Kamuzu Chibambo walengeza kuti Chris Bulakwacha ndi yemwe adzayime ngati wachiwiri wake pa mpando wa mtsogoleri pa chisankho chomwe chichitike mdziko muno mu mwezi wa September.

Chibambo walengeza izi pa mkumano wa olemba nkhani omwe anayitanitsa lero mu mzinda wa Lilongwe.

Kulengezaku kukudza patapita masiku atatu bungwe la Malawi Electoral Commission (MEC) litabwenza zikalata za Chibambo zotsimikiza chidwi chake chodzayimira pa mpando wa mtsogoleri wa dziko, ati poti sizinafikire zina zofunikira.

Mwa zina zofunikirazo zinali zoti wachiwiri wakeyu anali asanamalizitse kulemba mu zikalata zosonyeza chidwi chake chodzayima pa chisankhocho, komanso sanapezeke pomwe Chibambo amakapereka kalatazo.

Ndipo Chibambo anauzidwa kuti akonze zofookazi lisanafike dzulo lomwe bungwe la MEC lamalizitsa ntchito yolandira kalatazi.

Ndipo polankhula lero pa mwambo wa olemba nkhani, Chibambo wati anakwaniritsa kuchita zomwe bungwe la MEC linamuuza kuti achite, ndipo tsopano zatsimikizia kuti Bulakwacha adzakhala wachiwiri wake pa chisankhocho.

Malingana ndi Chibambo, kalatazi anakazipereka ku bungwe la MEC isanafike 4 koloko yomwe anauzidwa ndi bungwelo.

Pakali pano, Chibambo wati akadzasankhidwa mboma, adzathetsa ndale zothana, zomwe wati zikubwenzeresa mbuyo chitukuko cha dziko lino.

Mneneri wa chipani cha Democratic Progressive Party-DPP Shadric Namalomba komanso Noel Masangwi yemwe ndi mmodzi mwa aku...
31/07/2025

Mneneri wa chipani cha Democratic Progressive Party-DPP Shadric Namalomba komanso Noel Masangwi yemwe ndi mmodzi mwa akulu akulu a chipani cha UTM lero lino atuluka pa belo.

Namalomba anamangidwa dzulo pomwe Masangwi wamangidwa lero ati powaganizira pa mulandu otulutsa katundu wa mu nkhalango oletsedwa.

Ndipo pomwe anakaonekera ku bwalo la milandu la mu mzinda wa Blantyre, awiriwa awatsekulira milandu yolephera kugwiritsa bwino ma udindo awo.

Ku bwaloli, Michael Kalonga yemwe akuyimira pa mulanduwo bungwe la Anti-Corruption Bureau (ACB) anapempha bwaloli kuti liwapatse sabata ziwiri kuti afufuze zambiri, mulanduwu usanayambike.

Izi zinapangitsa Asanta Maxwell yemwe akuzenga mulanduwu kuti atulutse awiriwa pa belo.

Ngati chikole cha beloyo, Maxwell walamula Namalomba komanso Masangwi kuti aliyense wa iwo apereke ndalama zokwana K1 million.

Komanso awiriwa awalamula kuti apereke ku bungwe la ACB zitupa zawo zoyendera komanso kuti adzikaonekera ku bungweli la chisanu la sabata ziwiri zili zonse.

Anthu mdziko muno awalimbikitsa kuti akasiye ku polisi mifuti yomwe akugwiritsa ntchito mosatsata malamulo.Wapereka pemp...
31/07/2025

Anthu mdziko muno awalimbikitsa kuti akasiye ku polisi mifuti yomwe akugwiritsa ntchito mosatsata malamulo.

Wapereka pempholi lero ndi Ackis Muwanga yemwe ndi wachiwiri kwa mkulu wa apolisi mdziko muno.

Muwanga wapereka pempholi lero mu mzinda wa Lilongwe pa mwambo owotcha mifuti yomwe inalandidwa kwa anthu mdziko muno, ngati njira imodzi yokumbukira tsiku lowononga zida zowopsa pa dziko lonse, Fi****ms Destruction Day mchingerezi.

Pa mwambowu paotchedwa mifuti yokwana 733, yomwe ndi kuphatikizapo mifuti 33 ya AK47, mfuti zing’onozing’ono 39 za mtundu wa pistol, komanso zina zokwana 640 zochita kupangidwa pa manja ndi anthu.

Mfuti zimenezi ndi zomwe a polisi analanda kuchokera kwa anthu omwe amazigwiritsa ntchito pobera anzawo, kupha nyama za kutchire mopanda chilolezo, ndi milandu ina yoopsa.

Ndipo polankhula pa mwambowo, Muwanga anati a polisi ndi odzipereka kwathunthu pa ntchito yothana ndi mchitidwe okhala ndi mifuti opanda chilolezo mdziko muno.

Chomcho Muwanga wapempha anthu mdziko muno kuti adzikasiya okha ku polisi mifuti yomwe akugwiritsa ntchito mopanda chilolezo.

Iye anati apolisi adzateteza onse omwe achite izi paokha, osadikira kuti achite kugwidwa, omwe zikatero adzalandire chilango.

⚽  MKANGO SPORTS UPDATEMpikisano wa chaka chino wa mu chikho cha FDH Bank Cup ukuyembekezeka kuyambika sabata ziwiri zik...
31/07/2025

⚽ MKANGO SPORTS UPDATE

Mpikisano wa chaka chino wa mu chikho cha FDH Bank Cup ukuyembekezeka kuyambika sabata ziwiri zikudzazi pa 16 August 2025.

Izi zalengezedwa ku mwambo omwe banki ya FDH inakonza lero mu mzinda wa Blantyre, mogwirizana ndi bungwe loyendetsa mpira mdziko muno la Football Association of Malawi (FAM).

Cholinga cha mwambowu chinali kuchita mayere a momwe ma timu okwana 32 akumanirane koyambilira kwa mpikisanowu.

16 mwa matimumuwa ndi omwe amasewera mu mpikisano wa TNM Super League, pomwe 16 wenawo ndi omwe amasewera mu ma ligi ang’onoang’ono a mzigawo za mdziko muno.

Ndipo potsatira mayelewo, timu ya Nyasa Big Bullets yomwe ikuteteza chikhochi ikuyembekezeka kukumana ndi timu ya Changalume Barracks, Mighty Wanderers ikumana ndi timu ya MAFCO, pomwe Silver Strikers ikumana ndi timu ya Mighty Tigers.

Mabwalo komanso masiku omwe masewerowa adzaseweredwe alengezedwabe.

Opambana mu ndime ya ma timu 32, ya chikhochi, adzafika mu ndime ya matimu 16.

⚽  MKANGO SPORTS UPDATEOsewera kutsogolo kwa timu ya FCB Nyasa Big Bullets Maxwell Gastin Phodo wati ndi okondwa kuti ma...
29/07/2025

⚽ MKANGO SPORTS UPDATE

Osewera kutsogolo kwa timu ya FCB Nyasa Big Bullets Maxwell Gastin Phodo wati ndi okondwa kuti masewero ake a mpira akupita patsogolo chibwelere ku timuyi.

Phodo wanena izi la chiwiri pomwe wasaina mgwirizano owonjezera kuti akhalebe ku timuyi kwa zaka zina ziwiri zomwe zikubwerazi.

Polankhula atasaina mgwirizanowo, Phodo wati akuona kuti kaseweredwe kake kapita patsogolo, kusiyana ndi poyamba.

Phodo wati izi zili chomwechi chifukwa timu ya Bullets imamupatsa mtima ofuna kuti idzichita bwino nthawi zonse.

Chomcho Phodo wati akufuna kukhalabe ku timuyi kuti apitirize kuyithandiza kuti idzichita bwino mu mipikisano yosiyana siyana.

Ndipo Peter Mponda yemwe ndi mphunzitsi wa timuyi wati ndi okondwa kuti Phodo wasaina kontarakiti yokhalabe ku timuyi.

Iye wati izi zithandiza kwambiri podziwa kuti Phodo ndi mmodzi mwa osewera omwe utsogoleri wake komanso luntha lake pa mpira lithandiza osewera wena a chisodzera a timuyi mu zinthu zosiyana siyana zokhudza masewero a mpira.

⚽  MKANGO SPORTS UPDATEOsewera wakale wa timu ya Premier Bet Dedza Dynamos Khumbo Banda watayira kamtengo mphunzitsi wa ...
29/07/2025

⚽ MKANGO SPORTS UPDATE

Osewera wakale wa timu ya Premier Bet Dedza Dynamos Khumbo Banda watayira kamtengo mphunzitsi wa timu ya FCB Nyasa Big Bullets pokhala mmodzi mwa omwe akhala akumulimbikitsa pa masewero ake a mpira.

Banda wanena izi pomwe tsopano wakwaniritsa khumbo lake losewera mu timu yaikulu pomwe wasainira mgwirizano wake wa zaka ziwiri ndi timu ya Bullets.

Banda akuyembekezeka kukhala mlowammalo wa Blessings Mpokera yemwe akuyembekezeka kupita kukasewera mdziko la South Africa ku timu ya Durban City FC.

Malingana ndi Banda, iye wapita patali ndi masewero ake a mpira chifukwa cha Mponda, yemwe wakhala akumamulimbikitsa kuti apitilire mmaseweredwe ake.

“Mponda wakhala akumandilimbikitsa kuti ndipitilire ndi chidwi changa pa masewero a mpira. Chomcho pomwe anandiuza kuti akufuna kuti ndibwere ku timu ya Bullets, sindinali odabwa,” watero Banda.

Chomcho iye walonjeza kuti achilimika kuti athandize timu ya Bullets kutenga zikho zochuluka.

Pakali pano, Mponda wati kubwera kwa Banda kuthandiza kulimbitsa kumbuyo kwa timuyi.

⚽  MKANGO SPORTS UPDATEFrancisco Madinga yemwe wakhala akusewelera Mighty Wanderers tsopano wachoka ku timuyi.Kuchoka kw...
29/07/2025

⚽ MKANGO SPORTS UPDATE

Francisco Madinga yemwe wakhala akusewelera Mighty Wanderers tsopano wachoka ku timuyi.

Kuchoka kwa Madinga kukutsatira kulephera kwa mbali ziwirizi kugwirizana za kontarakiti yatsopano potsatira kutha mu mwezi wa June kwa mgwirizano omwe unalipo poyamba.

Mbali ziwirizi zakhala zikukambirana za mgwirizanowu kuyambira mu mwezi wa June pomwe mgwirizanowu unatha.

Malingana ndi malipoti wena, mwa zifukwa zomwe mbali ziwirizi sizinamvane ndi ndalama zokwana K900, 000 zomwe Madinga anapempha kuti akufuna adzilandira pa mwezi.

Koma timu ya Wanderers, malingana ndi malipoti wena, siyinali yokonzeka kupereka ndalama zochuluka motere.

Chinanso chomwe chapangitsa kuti mbali ziwirizi zisamvane ndi ganizo la timu ya Wanderers loti idzipereka ndalama zomusainira osewerayu pang’ono pang’ono, zomwe sizinakondweretse osewerayu.

Pakali pano malipoti wena akusonyeza kuti Madinga atha kulowera mdziko la Mozambique komwe akasewere ku timu ya Costa Do Sol.

Malipoti wena akhalanso akumveka kuti matimu wena mdziko muno amamufunanso osewerayu, kuphatikizapo ya Bullets.

Address

Ngabu
Chikwawa
315110

Alerts

Be the first to know and let us send you an email when Chibvomelezi FM posts news and promotions. Your email address will not be used for any other purpose, and you can unsubscribe at any time.

Contact The Business

Send a message to Chibvomelezi FM:

Share