
31/07/2025
Yemwe akuyembekezeka kudzayimira pa mpando wa phungu wa dera la kummwera kwa boma la Chikwawa Iliyas Abdul Karim wati akufunitsitsa kuti akasankhidwanso pa chisankho chomwe chichitike mu mwezi wa September, adzapitilize zitukuko zomwe anayamba mderali.
Karim walankhula izi dzulo pakutha pa kupereka ku bungwe la Malawi Electoral Commission (MEC) kalata zosonyeza chidwi chake chodzayima pa chisankhocho.
Karim wati akasankhidwanso adzatukula derali kuti likhale lotukuka ndi zitukuko zosiyana siyana.
Ndipo iye wati ali ndi chikhulupiliro kuti adzapambana pa chisankhochi ndi mavoti ochuluka.
Pa chisankhochi, Karim akuyembekezeka kudzayimira pa udindowu ngati oyima payekha; mafumu, akulu akulu a mipingo, achinyamata, amayi ndi wena atamupempha kuti asinthe ganizo lake losiya kaye ndale.