Chibvomelezi FM

Chibvomelezi FM Chibvomelezi Fm 107.6 MHZ is a vibrant and Commercial modern community radio station based in Ngabu.

The Radio is currently the Winner of the Best Community Media House of the year 2025/2026 MISA Malawi Award .

03/09/2025

News update on Chibvomelezi radio

Akatswiri omwe amalankhula pa nkhani zosiyana siyana ati ndi zokhumudwitsa kuti ufulu wa olembankhani ukupitilira kuphwa...
03/09/2025

Akatswiri omwe amalankhula pa nkhani zosiyana siyana ati ndi zokhumudwitsa kuti ufulu wa olembankhani ukupitilira kuphwanyidwa dziko muno.

Iwo alankhula izi pomwe mmodzi mwa olembankhani a wailesi ya Chibvomelezi David Nota analetsedwa kugwira ntchito yake pa malo pomwe mmodzi mwa omwe akupikisana nawo pa mpando wa phungu wa ku nyumba ya Malamulo mdera la kummwera kwa boma la Chikwawa, Luckson Ngalu amachitsa msonkhano wawo okopa anthu kudzawasankha pa chisankho chomwe chichitike pa 16 mwezi uno.

Izi zachitika pa malo ochitira malonda a Nsangwe mboma la Chikwawa.

Koma pomwe olemba nkhani wathuyu amagwira ntchito yake pa malo a msonkhanowu, anthu otsatira Ngalu anayamba kumugwiragwira, kenako kumulanda zida zake zogwilira ntchito.

Pochita izi, otsatirawa amamunena olembankhaniyu kuti watumidwa pa malowa ndi anthu ena omwe akupikisana ndi a Ngalu kudelali.

Ndipo pomwe zimachitika izi, ma kanema komanso zinthuzi zomwe iye anali atajambula pa malowa ati zosonyeza a Ngalu akugawa ndalama kwa anthu ndi zina, zinafufutidwa ndi anthuwa.

Koma a Ngalu omwe pa nthawiyo anali pamalo a ziwawawo uku akuwonelera izi zikuchitika, sakuyakha lamya zanthu za manja kwa nthawi zingapo zomwe takhala tikuwayimbira pa nkhaniyi.

Ndipo polankhulapo pa nkhaniyi, bungwe lophunzitsa zinthu zosiyanasiyana la NICE, lati zomwe zachitikazi ndi zodandaulitsa komanso zosemphana ndi malamulo a utolankhani mdziko muno.

Malingana ndi mkulu wa bungweli m’boma la Chikwawa, Chiyembekezo Gwazayani, kuletsa atolankhani kapena munthu wina kucheza ndi anthu omwe ali pa misonkhano yokopa anthu kapena kuwaletsa kujambula zithunzi, ndi mlandu kutengera ndi ndime 33 ya lamulo la Political Parties la chaka cha 2018.

Gwazayani wati munthu akapezeka akuchita izi monga momwe a luckson Ngalu achitira ndi anthu awo owatsatira, amapeleka chindapusa chandalama.

Naye Katswiri olakhulilapo pa nkhani zosiyanasiyana mdziko muno Humphreys Mvula wati ndi zokhumudwitsa kuti ufulu wa atolankhani ukupitilira kuphwanyidwa dziko muno.

Mvula wati izi ndi zosephana ndi malamulo a utolankhani maka mu nyengo ino yokopa anthu kudzatenga mbali pa chisankho chikudza.

Chomcho Mvula walangiza atsogoleri a ndale kuti asiye kuchita izi ponena kuti atha kuchotsedwa pa ndandanda wa anthu omwe akupikisana nawo pa zisankho zomwe zilipo mwezi uno akadzapezeka olakwa ngati mabungwe ena omenyera ufulu wa atolankhani mdziko muno angapitilire kuyikoka nkhaniyi.

Ma banja khumi omwe anakhudzidwa kwambiri ndi namondwe wa Freddy mmudzi wa Chikuse mfumu yaikulu Makhwira mboma la Chikw...
12/08/2025

Ma banja khumi omwe anakhudzidwa kwambiri ndi namondwe wa Freddy mmudzi wa Chikuse mfumu yaikulu Makhwira mboma la Chikwawa akusimba lokoma potsatira nyumba za makono zomwe alandira kuchokera ku kampani yopanga Sugar ya Illovo Malawi.

Malingana ndi kampani ya Illovo, nyumba zimenezi zamangidwa ndi ndalama zokwana K180 million kwacha.

Albert Mkumbwa, yemwe ndi mmodzi mwa akulu akulu a kampaniyi ati iwo anaganiza zochita izi potsatira pempho la boma kuti anthu komanso mabungwe akufuna kwabwino alithandize pomangira nyumba anthu amene anakhudzidwa ndi namondweyu mu mwezi wa March mchaka cha 2023.

Mkumbwa watinso kampani yao inamanga nyumbazi pofunanso kuwonetsetsa kuti ubale wake ndi wabwino ndi anthu ozungulira kampaniyi.

Ndipo kupatula kumanga nyumbazi, Mkumbwa wati kampaniyi ikumagwiranso ntchito zina monga zokhudza umoyo, ulimi, maphunziro, chitetezo pofuna kuonetsetsa kuti miyoyo ya anthu ozungulira kampaniyi komanso ogwira ntchito ku kampaniyi ikhale yabwino.

Ndipo Nardin Kamba, yemwe ndi bwanamkubwa wa boma la Chikwawa wayamikira kampani ya Illovo kamba kokhulupilira khonsolo yake ndi ndalama komanso ntchito yomanga nyumbazi.

Pakali pano, nduna yowoona za malo Deus Mgumbwa, yemwenso anali mulendo olemekezeka pa mwambo opereka nyumbazi wati boma likhala likuonjezelanso nyumba zina kwa anthu ena amene anakhudzika ndi namondwe wa Freddy.

Boma lalimbikitsa ntchito yothana ndi vuto la kunyentchera, kupinimbira komanso kutupikana pakati pa ana a mboma la Chik...
12/08/2025

Boma lalimbikitsa ntchito yothana ndi vuto la kunyentchera, kupinimbira komanso kutupikana pakati pa ana a mboma la Chikwawa.

Mwa zina, mu ntchitoyi, ofesi yoona za kadyedwe koyenera ndi ntchito yolimbana ndi kufala kwa kachirombo ka HIV komanso matenda a AIDS m'boma la Chikwawa ikuphunzitsa olemba nkhani pa momwe angalembere nkhani zokhudza kadyedwe koyenera.

Maphunzirowa omwe akuchitikira ku Nchalo m'bomali ayamba lolemba pa 11 August, ndipo akuyembekezeka kufika kumapeto la chisanu pa 15 August 2025.

Ndipo polankhula ndi wailesi ya Chibvomelezi, Chifundo Michael Manong'a, yemwe ndi mkulu oyang’anira nkhani zokhudza kadyedwe koyenera komanso ntchito yolimbana ndi kufala kwa kachirombo ka HIV mu ofesi ya za umoyo ya mboma la Chikwawa wati maphunzirowa akudza pomwe chiwerengero chikuonetsa kuti mu mbomali muli ana ambiri omwe ali ndi vuto lonyentchera.

Malingana ndi Manong’a, ana pafupifupi 39 mwa 100 ali onse ndi omwe anapezeka kuti ali ndi vuto lopinimbira mbomali.

“Kuopsa kwa kupinimbira ndi koti patsogolo pake kumapereka chiopsezo kwa anawa kuti avutike ku nkhani ya maphunziro. Chomcho zikatero, zimapangitsa kuti asadzakhale mzika zodalirika pa chitukuko cha dziko,” watero Manong’a.

Chomcho Manong’a wapempha makolo kuti asamachedwe kulozana dzala kuti ana otere asemphedwa, koma kuti mmalo mwake adziwapatsa anawa chakudya choyenera komanso kupeza uphungu wabwino kuchokera ku chipatala.

Pakali pano, Jossen Tembo, yemwe ndi mkulu woona za chitukuko pa khonsolo ya m'boma la Chikwawa wati maphunziro omwe akonza a olemba nkhani athandiza atolankhaniwa kumvetsetsa nkhani zokhudza kadyedwe kabwino ndi koyenera komanso kulemba nkhani zochuluka zozindikiritsa anthu ubwino otsatira ndondomeko za kadyedwe koyenera.

Yemwe akuyembekezeka kudzayimira pa mpando wa phungu wa dera la kummwera kwa boma la Chikwawa Iliyas Abdul Karim wati ak...
31/07/2025

Yemwe akuyembekezeka kudzayimira pa mpando wa phungu wa dera la kummwera kwa boma la Chikwawa Iliyas Abdul Karim wati akufunitsitsa kuti akasankhidwanso pa chisankho chomwe chichitike mu mwezi wa September, adzapitilize zitukuko zomwe anayamba mderali.

Karim walankhula izi dzulo pakutha pa kupereka ku bungwe la Malawi Electoral Commission (MEC) kalata zosonyeza chidwi chake chodzayima pa chisankhocho.

Karim wati akasankhidwanso adzatukula derali kuti likhale lotukuka ndi zitukuko zosiyana siyana.

Ndipo iye wati ali ndi chikhulupiliro kuti adzapambana pa chisankhochi ndi mavoti ochuluka.

Pa chisankhochi, Karim akuyembekezeka kudzayimira pa udindowu ngati oyima payekha; mafumu, akulu akulu a mipingo, achinyamata, amayi ndi wena atamupempha kuti asinthe ganizo lake losiya kaye ndale.

Kampani yopanga Sugar ya Illovo yatsindika kuti ikuchita chili chonse chotheka kuti Sugar ochuluka adzipezeka mmadera os...
31/07/2025

Kampani yopanga Sugar ya Illovo yatsindika kuti ikuchita chili chonse chotheka kuti Sugar ochuluka adzipezeka mmadera osiyanasiyana a mdziko muno.

Kondwani Msimuko, yemwe ndi mkulu wa kampani ya Illovo wanena izi pakutha pa mkumano wa masiku awiri wa olemba nkhani omwe kampaniyi yake inakonza kumayambiliro a sabata ino.

Mu mkumanowu, kampaniyi imaonetsa olemba nkhaniwa mmene kampani yawo imagwilira ntchito zake zosiyana siyana monga za ku minda yake ya mzimbe komanso ku fakitale yake yopanga Sugar.

Polankhula ndi wailesi ya Chibvomelezi, Msimuko wati anayitanitsa olemba nkhaniwa pofuna kuti adziwitse a Malawi, momwe kampani yawo imagwilira ntchito zake.

Msimuko wati Sugar pakali pano akupezeka mmadera osiyana siyana a mdziko muno potsatira ntchito yomwe kampaniyi yalimbikitsa yopanga Sugar ochuluka.

Ndipo iye anati cholinga cha ntchitoyi ndi kuonetsetsa kuti Sugar akwanire mdziko muno, kampaniyi isanayambe kumugulitsa kunja kwa dziko lino.

Pakali pano, Msimuko wati kampaniyi ili ndi lingaliro lopanga mphamvu za magetsi pofuna kuonjezera mphamvu za magetsi zomwe imagwiritsa ntchito pa ntchito zake, kuchokela ku kampani ya ESCOM.

Iye wati malingaliro amenewa akatheka, magetsi amenewa, kupatula kugwilitsa ntchito yopanga Sugar, adzawaperekanso ku dziko lonse la Malawi kudzela ku kampani ya ESCOM.

⚽  MKANGO SPORTS UPDATETimu ya FCB Nyasa Big Bullets yagonjetsa timu ya Mzuzu City Hammers mu mpikisano wa TNM Super Lea...
31/07/2025

⚽ MKANGO SPORTS UPDATE

Timu ya FCB Nyasa Big Bullets yagonjetsa timu ya Mzuzu City Hammers mu mpikisano wa TNM Super League.

Mmasewero omwe anaseweredwa pa bwalo la Rumphi Stadium mboma la Rumphi, Bullets yagonjetsa timu ya Hammers ndi zigoli ziwiri kwa duuu!!!!

Timu ya Hammers inayamba bwino masewerowo pomwe imapanikiza timu ya Bullets mu chigawo chake chomwe.

Ndipo zinali zosadabwitsa pomwe timuyi inapeza penote, yomwe mwa tsoka lake, goloboyi wa timu ya Bullets Innocent Nyasulu anayichotsa kuti isalowe pa golo pake.

Kuchoka apo, timu ya Bullets inadzambatuka kutulo, pomwe inayamba kupanikiza timu ya Hammers.

Ndipo mu mphindi 77 za masewerowo, Bullets inagoletsa chigoli chake choyamba kudzera mwa Chikumbutso Salima, otseka kumbuyo kwa timu ya Hammers atalephera kuchotsa mpira omwe anasewera Andrew Juvinala.

Ndipo Hassan Kajoke anabwera ndi chigoili cha chiwiri chomwe anachita kusumbira ndi mutu potsatira free-kick yomwe anasewera Peter Banda.

Ndipo pakutha pa masewerowo, Nyasulu ndi yemwe anasankhidwa kuti wasewera bwino kuposa wena onse mbwalomo.

Bungwe la Pensioners Association of Malawi lapereka mgwazo wa mwezi umodzi ku boma kuti likhale litalipira anthu omwe an...
31/07/2025

Bungwe la Pensioners Association of Malawi lapereka mgwazo wa mwezi umodzi ku boma kuti likhale litalipira anthu omwe anapuma pa ntchito, ndalama zawo zopumira pa ntchito, Pension mchingerezi.

Bungweli lapereka mgwazowu pa mkumano wa olemba nkhani omwe linayitanitsa lero mu mzinda wa Blantyre.

Polankhula pa mkumanowu, Nellie Mkhumba yemwe ndi mtsogoleri wa bungweli, wati anthu ambiri omwe anapuma pa ntchito zao, atathandiza kwambiri pa chitukuko cha dziko lino, sakulandira ndalama zawo.

Izi, malingana ndi Mkhumba ndi zosemphana ndi malamulo oyendetsera thumba la ndalama za anthu opuma pa ntchito, zomwe zimanenetsa kuti anthuwa akuyendera kulandira ndalamazi pasanathe miyezi itatu, chipumire pa ntchito yao.

Iwo awopseza kuti ndalamazi ngati sizilipiridwa pofika pa 30 mu mwezi wa August, sachitira mwina koma kutengera boma ku bwalo la milandu.

Chipani cha Democratic Progressive Party (DPP) chalimbikitsa zokonzekera zake za msonkhano wa ndale omwe chichititse ku ...
31/07/2025

Chipani cha Democratic Progressive Party (DPP) chalimbikitsa zokonzekera zake za msonkhano wa ndale omwe chichititse ku mapeto kwa sabata ino mu mzinda wa Blantyre.

Cholinga cha msonkhanowu, omwe uchitikire pa Njamba Freedom Park la mulungu likudzali, ndi chokhazikitsa ntchito yake yokopa anthu kudzera mu manifesito ake.

Ndipo usanachitike mkumanowu, mtsogoleri wa chipanichi Peter Mutharika, komanso Jane Ansah yemwe wasankhidwa ngati odzayima naye pa mpando wa mtsogoleri wa dziko pa chisankho cha mu mwezi wa September, adzakhazikitsa Manifesito a chipanicho.

Mwambo okhazikitsa manifesitowa udzachitika mmawa wa la mulungu lomwelo ku hotelo ya Mount Soche.

Mtsogoleri wa chipani cha People's Party (PETRA) Kamuzu Chibambo walengeza kuti Chris Bulakwacha ndi yemwe adzayime ngat...
31/07/2025

Mtsogoleri wa chipani cha People's Party (PETRA) Kamuzu Chibambo walengeza kuti Chris Bulakwacha ndi yemwe adzayime ngati wachiwiri wake pa mpando wa mtsogoleri pa chisankho chomwe chichitike mdziko muno mu mwezi wa September.

Chibambo walengeza izi pa mkumano wa olemba nkhani omwe anayitanitsa lero mu mzinda wa Lilongwe.

Kulengezaku kukudza patapita masiku atatu bungwe la Malawi Electoral Commission (MEC) litabwenza zikalata za Chibambo zotsimikiza chidwi chake chodzayimira pa mpando wa mtsogoleri wa dziko, ati poti sizinafikire zina zofunikira.

Mwa zina zofunikirazo zinali zoti wachiwiri wakeyu anali asanamalizitse kulemba mu zikalata zosonyeza chidwi chake chodzayima pa chisankhocho, komanso sanapezeke pomwe Chibambo amakapereka kalatazo.

Ndipo Chibambo anauzidwa kuti akonze zofookazi lisanafike dzulo lomwe bungwe la MEC lamalizitsa ntchito yolandira kalatazi.

Ndipo polankhula lero pa mwambo wa olemba nkhani, Chibambo wati anakwaniritsa kuchita zomwe bungwe la MEC linamuuza kuti achite, ndipo tsopano zatsimikizia kuti Bulakwacha adzakhala wachiwiri wake pa chisankhocho.

Malingana ndi Chibambo, kalatazi anakazipereka ku bungwe la MEC isanafike 4 koloko yomwe anauzidwa ndi bungwelo.

Pakali pano, Chibambo wati akadzasankhidwa mboma, adzathetsa ndale zothana, zomwe wati zikubwenzeresa mbuyo chitukuko cha dziko lino.

Mneneri wa chipani cha Democratic Progressive Party-DPP Shadric Namalomba komanso Noel Masangwi yemwe ndi mmodzi mwa aku...
31/07/2025

Mneneri wa chipani cha Democratic Progressive Party-DPP Shadric Namalomba komanso Noel Masangwi yemwe ndi mmodzi mwa akulu akulu a chipani cha UTM lero lino atuluka pa belo.

Namalomba anamangidwa dzulo pomwe Masangwi wamangidwa lero ati powaganizira pa mulandu otulutsa katundu wa mu nkhalango oletsedwa.

Ndipo pomwe anakaonekera ku bwalo la milandu la mu mzinda wa Blantyre, awiriwa awatsekulira milandu yolephera kugwiritsa bwino ma udindo awo.

Ku bwaloli, Michael Kalonga yemwe akuyimira pa mulanduwo bungwe la Anti-Corruption Bureau (ACB) anapempha bwaloli kuti liwapatse sabata ziwiri kuti afufuze zambiri, mulanduwu usanayambike.

Izi zinapangitsa Asanta Maxwell yemwe akuzenga mulanduwu kuti atulutse awiriwa pa belo.

Ngati chikole cha beloyo, Maxwell walamula Namalomba komanso Masangwi kuti aliyense wa iwo apereke ndalama zokwana K1 million.

Komanso awiriwa awalamula kuti apereke ku bungwe la ACB zitupa zawo zoyendera komanso kuti adzikaonekera ku bungweli la chisanu la sabata ziwiri zili zonse.

Anthu mdziko muno awalimbikitsa kuti akasiye ku polisi mifuti yomwe akugwiritsa ntchito mosatsata malamulo.Wapereka pemp...
31/07/2025

Anthu mdziko muno awalimbikitsa kuti akasiye ku polisi mifuti yomwe akugwiritsa ntchito mosatsata malamulo.

Wapereka pempholi lero ndi Ackis Muwanga yemwe ndi wachiwiri kwa mkulu wa apolisi mdziko muno.

Muwanga wapereka pempholi lero mu mzinda wa Lilongwe pa mwambo owotcha mifuti yomwe inalandidwa kwa anthu mdziko muno, ngati njira imodzi yokumbukira tsiku lowononga zida zowopsa pa dziko lonse, Fi****ms Destruction Day mchingerezi.

Pa mwambowu paotchedwa mifuti yokwana 733, yomwe ndi kuphatikizapo mifuti 33 ya AK47, mfuti zing’onozing’ono 39 za mtundu wa pistol, komanso zina zokwana 640 zochita kupangidwa pa manja ndi anthu.

Mfuti zimenezi ndi zomwe a polisi analanda kuchokera kwa anthu omwe amazigwiritsa ntchito pobera anzawo, kupha nyama za kutchire mopanda chilolezo, ndi milandu ina yoopsa.

Ndipo polankhula pa mwambowo, Muwanga anati a polisi ndi odzipereka kwathunthu pa ntchito yothana ndi mchitidwe okhala ndi mifuti opanda chilolezo mdziko muno.

Chomcho Muwanga wapempha anthu mdziko muno kuti adzikasiya okha ku polisi mifuti yomwe akugwiritsa ntchito mopanda chilolezo.

Iye anati apolisi adzateteza onse omwe achite izi paokha, osadikira kuti achite kugwidwa, omwe zikatero adzalandire chilango.

Address

Ngabu
Chikwawa
315110

Alerts

Be the first to know and let us send you an email when Chibvomelezi FM posts news and promotions. Your email address will not be used for any other purpose, and you can unsubscribe at any time.

Contact The Business

Send a message to Chibvomelezi FM:

Share