
17/06/2025
Anthu okhala mozungulira nkhalango yosungiramo nyama za ntchire ya Lengwe National Park awadandaulira kuti asiye mchitidwe wakuba ndi kuwononga waya wa mpanda ozungulira nkhalangoyi.
Dandauloli likudza potsatira kutuluka kwa nyama za mu nkhalango ya Lengwe zomwe kamba ka kubedwa kwa waya wa mpanda wake otchinjiriza kutuluka kwa nyamazi, zayika pa chiopsezo umoyo wa anthu a mbomali.
Izi zikutsatiranso kuphedwa kwa anthu awiri ndi kuvulazidwanso kwa anthu awiri kwa Jombo mu dera la mfumu yayikulu Ngabu m’boma la Chikwawa, ndi njati yolusa yomwe inathawa mu nkhalango yosungiramo nyama za ntchire ya Lengwe.
Choncho potsatira kupezeka ndi kuphedwa kwa njatiyi dzulo ndi alenje aboma, Kennedy Nzeru, yemwe ndi mkulu oyang’anira nkhalango ya Lengwe, wati kuthawa kwa nyamazi mu nkhalangoyi ndi chifukwa cha mchitidwe wa anthu wena ozungulira nkhalangoyi omwe anaba waya wa mpanda yemwe amathandiza kuti nyama zisamathawe mu nkhalangoyo.
Malingana ndi Nzeru, waya wa mpanda wa nkhalango ya Lengwe anabedwa patangopita nthawi yochepa chimuyikire pa mpanda wa nkhalangoyi.
Ndipo ngakhale sanakambe za nthawi yomwe mpanda wina udzayikidwenso ku nkhalangoyi, Nzeru wauza wailesi ya Chibvomelezi kuti asanayambe ntchito yokonzanso mpandawu, akhala akukambirana ndi anthu ozungulira nkhalangoyi kuti apeze njira zothandiza kuti anthuwa adzikhala ndi umwini komanso udindo osamalira mpanda wa nkhalangoyi.