29/06/2020
ANZERU A KUM'MAWA
Kodi anzeru a kummawa anali Ndani? Nanga analipo angati? Kodi anabwera liti kudzamuona Yesu? Nanga baibulo limati chani za iwo?
Kodi anzeru a kummawa analipo angati?
Baibulo silinakambepo za maina a anthu omwe anali kutchedwa anzeruwa. Inde silinenanso kuti analipo angati. Ndipo chomwe ilo limanena ndicho chakuti anthuwa anabweretsa Mphatso za mitundu itatu pa tsiku lomwe anabwera kudzaona Yesu. Mphatsozi zinali golide, libano komanso mure. Inde palibe paliponse mu baibulo pamene amanena kuti anzeru a kum'mawa analipo atatu. Zikhoza kuthekha kuti anali opitilira atatu. Anthuwa kwao kunali kutali kummawa. Ndipo malo omwe anali kutchedwa kummawa anali madera monga babulo.
Anthuwa pachingerezi anali kutchedwa 'magi' kutanthauza anzeru, aula kapena openduza. Ndipo ndi anthu angati omwewa amene mafumu otchuka monga Farao, Nebukadineza komanso Amedi ndi Aperesi anali kuwagwiritsa ntchito pamene pachitika chododometsa. Iwo anali akatswiri pa nkhani yodziwa za mlengalenga, kutanthauza maloto komanso kuchita zamatsenga.
Nebukadineza anapanga Daniel ndi anzake kukhala mu gulu la anzeru ake (Daniel 2:11,18,24,27). Ndipo Daniel anasankhidwa kukhala mkulu wa anzeruwa Ku Babulo.
Kudza kwa anzeru a kummawa sikunali kudzalambira Yesu monga Mwana wa Mulungu ayi. Pajatu anthuwa anali okhulupilira zakuthambo osati mlengi. Chotero nkosatheka watsenga kulambira Mulungu.
Kodi anzeruwa anabwera usiku omwe Yesu anabadwa?
Nthawi Zambiri maka mu desembala timaona zithunzi zojambula khanda litagonekedwa mu chodyera ng'ombe ndipo anzeru a kummawa atatu atagwada kumpembedza.
Mateyu 2 :1-2
1Ndipo pa kubadwa kwace kwa Yesu m'Betelehemu wa Yudeya m'masiku a Herode mfumu, onani, Anzeru a kum'mawa anafika ku Yerusalemu,2nati, Ali kuti amene anabadwa Mfumu ya Ayuda? cifukwa tinaona nyenyezi yace kum'mawa, ndipo tinadzera kudzamlambira Iye.
Mukawerenga mwachidwi mauwa, muona kuti iwo anadza Yesu atabadwa kale. Ndipo atafika Ku Yerusalemu anayamba kumufufuza komwe anabadwira.