Mtunthama Broadcasting Station

Mtunthama Broadcasting Station Mtunthama Broadcasting Station is a media house broadcasting from Kasungu in Malawi.

The station believes in objectivity, accuracy and creativity throughout it's programming.

Mkulu wabungwe la Chifukwato cha Achewa Kalonga Sosola wapempha alimi m'boma la Kasungu kuti azionetsetsa kuti akutenga ...
15/07/2025

Mkulu wabungwe la Chifukwato cha Achewa Kalonga Sosola wapempha alimi m'boma la Kasungu kuti azionetsetsa kuti akutenga ulimi ngati malonda ndi cholinga choti azipeza phindu lochuluka pa ulimi.
Kalonga Sosola wayankhula izi pomwe bungwe lawo limodzi ndi kampani ya Afri-oils amasayinirana mgwilizano oti alimi a kopaletivi ya Mtukula mdera la Sub TA Kasera mfumu yandodo Kaomba kuti azilima mbewu ya mtedza komanso nyemba.

Pansi pa mgwirizanowu kopaletiviyi yalandira makina opopela madzi pa ulimi wa mthirira ngati njira imodzi yowalimbikitsa kuti ulimi wawo upitililire kupita patsogolo.

Dalitso Odala yemwe ndi mkulu wa kampani ya Afri-oils wamema alimiwa kuti achilimike kulima mbewu zochuluka ponena kuti msika ulipo kale.

Wapampando wa kopaletivi ya Mtuluka Mofatt Nthembwe wati awonetsetsa kuti akulima mbewu zambiri zomwe zithandizira kutukula miyoyo yawo.

Kumbali yosamalira makina omwe alandila ati awonetsetsa kuti akuyika chitetezo chokwanira kuti anthu asabe kapena kuononga.

Mgwilizano omwe asayinirana ndi wazaka khumi ndipo alimi azipanga ulimi wa mtedza komanso nyemba pochita ulimi wamthilira komanso wamvula ndi kumagulitsa ku kampani ya Afri-oils ndipo maanja okwana 10,000 akudera la Kaomba, Kaluluma mwa ena ndiomwe apindule nawo.

Wolemba: Linly Kamanga

Joel Misias wazaka 49 wamwalira galimoto yomwe anakwera itawomba ntengo omwe unali m’mbali mwa nsewu pa malo ochitira ma...
15/07/2025

Joel Misias wazaka 49 wamwalira galimoto yomwe anakwera itawomba ntengo omwe unali m’mbali mwa nsewu pa malo ochitira malonda a Chikwawa m’boma la Salima.

Malinga ndi Faith Gosten kuchokera kupolisi ya Salima wati a Yoweri Laiton amayendetsa galimoto ya ntundu wa Toyota Dyna nambala yake CA 9810 yomwe imachokera ku Nkhotakota ndipo itafika pa msikawu Dalayivala analephera kuwongolera bwino zomwe zinapangitsa kuti agunde ntengo.

Kutsatira ngoziyi Misias anavulala kwambiri m’mutu ndipo wamwalira atangofika naye kuchipatala cha Khombedza ndipo Laiton wavulala kwambiri m’mutu, pakamwa komanso mwendo wakumanzere ndipo akulandilanso thandizo pa chipatala chomwechi.

Misias amachokera m’mudzi wa Seketani mfumu yayikulu Khombedza m’boma lomweri la Salima.

Wolemba: Mathews Benard

A Joseph Manguluti omwe akupikisana paokha ngati phungu ku dera la kumwera kwa boma la Kasungu wati pali andale ena omwe...
15/07/2025

A Joseph Manguluti omwe akupikisana paokha ngati phungu ku dera la kumwera kwa boma la Kasungu wati pali andale ena omwe akuphwanya mwadala malamulo chinsankho monga kugawa ndalama kumema mafumu kuti azikaniza anthu ena kudzachita misonkhano m’madera awo komanso kuwopsyeza anthu.

Malinga ndi Manguluti aphungu ambiri omwe alephera kutukula madera awo tsopano njira ya bwino yomwe akuwona kuti akhoza akugwiritsa ntchito pokopa anthu ndi ndalama komanso kuwopsyeza anthu ena.

Poyankhula, mkulu ya nthambi yolemba zipani pachingelezi Registrar of Political Parties a Kizito Tenthani ati iwo a awonetsetsa kuti lamulo likugwira ntchito pa aliyense yemwe ataphwanye malamulo a mundondomeko ya kayendetsedwe ka zipani.

Malinga ndi Tenthani ndi zoletsedwa kugawa ndalama pa nthawi yokopa anthu, kukopa anthu kumaliro komanso m’matchalitchi.

Iwo atinso mipingo isamalandire ndalama, kupempha ndalama anthu andale monga m’mene ziliri masiku ano pomwe mipingo ikumaitana anthu andale.

Wolemba: Mathews Benard
Mtunthama_Nkhani

M’modzi mwa anthu omwe akupikisana nawo pa mpando wa phungu wa nyumba ya malamulo kudera la kumpoto chakumadzulo kwa bom...
15/07/2025

M’modzi mwa anthu omwe akupikisana nawo pa mpando wa phungu wa nyumba ya malamulo kudera la kumpoto chakumadzulo kwa boma la Kasungu (North West) Sam Kazombo wati anthu kuderali akupitilira kukumana ndi mavuto ngakhale kuti akhala ndi phungu kwa zaka zisanu ndi chimodzi.

Malinga ndi Kazombo anthu kudelari akumwabe madzi oyipa, akuvutika kupeza misika ya mbeu, sukulu zili patalipatali komanso misewu silibwino kotero izi zikubwezeretsa m’buyo chitukuko cha delari.

Komabe iwo ati ngakhale izi zili choncho chiyembekezo chilipo kuti anthu akawasankha kukhala phungu wa delari pa 16 September adzakonza mavutowa.

Wolemba: Mathews Benard
Mtunthama_Nkhani

Akuluakulu achipani cha Democratic Progressive (DPP) lero ayitana mashado MP komanso khansala achigawo chapakati ku nkum...
15/07/2025

Akuluakulu achipani cha Democratic Progressive (DPP) lero ayitana mashado MP komanso khansala achigawo chapakati ku nkumano omwe cholinga chake ati ndikuwaunikila momwe angakopere anthu molingana ndi mfundo zimene chipani cha DPP chakonza kuti chitukulire dziko lino kuyambira pa 16 September akalowanso m’boma.

Mkumanowu omwe ukuchitikira ku Edge Water mu m’zinda wa Lilongwe ndi gawo limodzi lomwe chipani cha DPP chimagwiritsa ntchito pokopa (campaign directorate)

Pamkumanowu, mlendo olemekezeka ndi wachiwiri kwa mtsogoleri wa chipani cha DPP m’chigawo cha pakati Alfred Gangata, mkulu oyendesa ntchito za chisankho mchipani a Jean Mathanga, a Francis Mphepo, Dr Justin Saidi, a Sameer Suleman, olemekezeka Dr Ben Phiri, komanso mkulu oyan'ganira ntchito yokopa anthu mchipani cha DPP Chifundo Makande.

Wolemba: Mathews Benard

M’modzi mwa atsogoleri a gulu la Citizens for Credible Elections Steve Chimwaza wati amayembekezera kuti mtsogoleri wa d...
15/07/2025

M’modzi mwa atsogoleri a gulu la Citizens for Credible Elections Steve Chimwaza wati amayembekezera kuti mtsogoleri wa dziko lino a Lazarus Chakwera ayankhulapo pa zomwe zinachitika pa 26 June pa ziwonetsero mu m’zinda wa Lilongwe.

Malinga ndi a Chimwaza pomwe a Chakwera amayankhula ku mtundu wa a Malawi amayenera kudzudzula mchitidwe wa anthu ena omwe anamenya a Sylevester Namiwa mwankhaza apolisi komanso asilikali agulu la nkhondo akuwona pa bwalo la Lilongwe community.

Chimwaza wati pomwe a Malawi amavetsera uthenga wawo anali ndi chidwi kuti amva a Chakwera akulamula mkulu wa apolisi m’dziko muno kuwonetsetsa kuti onse omwe anachitira za ntopola a Namiwa amangidwe koma anali odabwa kuti sanapangepo kanthu.

A Chakwera pa 14 July anayankhula ku mtundu wa a Malawi zoyenera kuchita maka mu nyengo ino yokopa anthu ndi cholinga choti m’dziko muno mukhale bata.

Wolemba: Mathews Benard

Mtsogoleri wa chipani cha Alliance for Democracy (AFORD) Enock Chihana ati kuchuluka kwa anthu omwe atenga zikalata zofu...
15/07/2025

Mtsogoleri wa chipani cha Alliance for Democracy (AFORD) Enock Chihana ati kuchuluka kwa anthu omwe atenga zikalata zofuna kupikisana nawo pa udindo wa mtsogoleri wa dziko zikungobweletsa poyera kuti anthu ambili andale ndi adyera.

Malinga ndi a Chihana ndizodabwitsa kuti dziko laling’ono ngati la Malawi anthu 18 ndi omwe akufuna udindo wa mtsogoleri wa dziko.

A Chihana ati ambiri mwa anthuwa alibe ukadaulo komanso luntha pa kayendetsedwe ka dziko choncho anthu akuyenera kuvotera chipani chawo komanso kuwasankha kuti akhale mtsogoleri wa dziko lino ponena kuti ndi omwe ali ndi mayankho kumavuto omwe dziko lino likukumana nawo.

Iwo atsindikanso kuti kuyambira pa 16 akalowa m’boma anthu sakumana ndi mavuto omwe alipo pano ponena kuti utsogoleri wawo ukhala wakumva madandaulo a anthu.

Wolemba: Mathews Benard

14/07/2025

A Maulana Nkhoma azaka 68 amwalira pa ngozi ya pansewu yomwe yachitika pa malo ochitira malonda a Chinkhoma msewu wa Santhe- Chinkhoma M18 m’boma la Kasungu.

Othandizira mneneri wa polisi ya Kasungu Sergeant Chifundo Nedi galimoto yomwe imayendetsedwa ndi a Chifundo Chumba Nissan UD Lorry yomwe nambala yake ndi Kel 7772 imachokera kwa Santhe kupita town ya Kasungu.

Galimotoyi itafika pa malo ochitira malonda a Chinkhoma inagunda a Nkhoma omwe pa nthawiyo amawoloka msewu kuchokera mbali ya kumanja kupita ku manzere.

Zotsatira za chipatala Zatsimikiza kuti Nkhoma wamwalira kaamba kovulala kwambiri m’mutu.

Maulana Nkhoma amachokera m’mudzi wa Fambo mfumu yayikulu Lukwa m’boma la Kasungu

Wolemba: Mathews Benard

Abusa awiri amangidwa kwa Kaning'a kamba kodya nkhuyu za ana m'boma la Kasungu.Apolisi m'boma la Kasungu amanga abambo a...
11/07/2025

Abusa awiri amangidwa kwa Kaning'a kamba kodya nkhuyu za ana m'boma la Kasungu.

Apolisi m'boma la Kasungu amanga abambo awiri powaganizira kuti amagona ndi ana azaka za pakati pa 13 ndi 15.

Oganiziridwawa ndi a Mangitsani Banda azaka 46 komanso Joshua Phiri azaka 23.

Mneneri wa apolisi m'boma la Kasungu Joseph Kachikho wati awiriwa ndi amazitchula kuti azibusa a mpingo wa Vision of God.

Oganiziridwawa amakhala limodzi ndi asungwana m'nyumba ina kwa Kaning'a (Four ways) yomwe nthawi zina amayigwiritsanso ntchito ngati tchalitchi.

Malinga ndi Kachikho ana anayi anapita kwa abusawa ponena kuti anali ndi mavuto osiyanasiyina omwe amafunika kupempheleledwa (Deliverance).

Abusa akhala akugonana ndi anawa kuyambira mwezi wa June mpaka July.

Izi zadwika pomwe m'modzi mwa makolo a anawa anakapeleka dandaulo ku polisi ya Nkhamenya.

Apolisi atapita ku malowo anakapezadi mwanayo limodzi ndi anzake ena atatu.

Malinga ndi zotsatira za chipatala zatsimikiza kuti anawa akhala akugonedwa.

Mangitsani Banda amachokera m'mudzi wa Mtanga mfumu yayikulu Khongoni m'boma la Lilongwe ndipo Joshua Phiri amachokera m'mudzi mwa Mbwizi mfumu yayikulu Kafuzira m'boma la Nkhotakota.

Wolemba: Mathews Benard

10/07/2025


Ophunzira pa sukulu ya sekondale ya Mtunthama All Saints m’boma la Kasungu usiku wapitawu aswa magalasi azipinda zophunz...
10/07/2025

Ophunzira pa sukulu ya sekondale ya Mtunthama All Saints m’boma la Kasungu usiku wapitawu aswa magalasi azipinda zophunzilira komanso amafuna kuyatsa moto chipinda chowelengera mabuku.

Mneneri mu unduna wa zamaphunziro aku pulayimale ndi sekondale Christopher Kapachika Banda watsimikiza za nkhaniyi ndipo wati chifukwa chenicheni chomwe apangira izi sichinadziwike kotero akhazikitsa kafukufuku kuti apeze zenizeni za nkhaniyi.

Ena mwa ophunzira pa sukuluyi ati izi zachitika kaamba kosakondwa ndi chakudya chomwe ophunzira ogonera akulandira ponena kuti sichikugwirizana ndi ndalama za fizi zomwe akulipira.

Undunawu wati ndi okhumudwa ndi kukula kwa mchitidwe owononga katundu komanso zipangizo za sukulu pakakhala kusamvana pakati pa ophunzira ndi aphunzitsi.

Wolemba: Mathews Benard

Pokondwelera kuti dziko lino lakwanitsa zaka 61 lili pa ufulu wozilamulira gulu la Son's and Daughters of Kasungu linaka...
07/07/2025

Pokondwelera kuti dziko lino lakwanitsa zaka 61 lili pa ufulu wozilamulira gulu la Son's and Daughters of Kasungu linakacheza ku ndende ya m’bomali komwe mwazina amawalimbikitsa moyo wa uzimu komanso kuwapatsa katundu osiyanasiyana.

Olipa Banda Mlembi wa gululi wati akudziwa bwino mavuto omwe ali ku ndende kotero ndi chifukwa chake anaganiza zosonkhanitsa kangachepe komwe apeleka lero.

Malinga ndi Banda nthawi zambiri anthu omwe akusungidwa ku ndende amakhala opanda chiyembekezo choncho ndi kofunikira kuti magulu osiyanasiyana adzilimbikitsanso akayidi umoyo wa uzimu.

Wina mwa katundu yemwe apeleka ndi sopo ochapira mafuta odzola, nyemba komanso soya pieces mwa zina.

Chancy likwanga owona za uzimu pa ndendeyi wayamikira thandizo lomwe alandira kuti labwera mu nthawi yake ponena kuti pa ndendeyi pali mavuto ochuluka omwe akufunika thandizo mwansanga.

Mphatso whisky M***a yemwe anayimira akayidi anati ndi okondwa kwambiri kuti tsopano azidya ndiwo zabwino kusambira sopo kenako ndi kudzola mafuta kotero wapempha abweziwa kuti ulendo wina awayenderenso nthawi ina.

Wolemba: Beauty Chinseu

Address

Kasungu

Opening Hours

09:00 - 17:00

Telephone

+265999017357

Website

Alerts

Be the first to know and let us send you an email when Mtunthama Broadcasting Station posts news and promotions. Your email address will not be used for any other purpose, and you can unsubscribe at any time.

Contact The Business

Send a message to Mtunthama Broadcasting Station:

Share