08/06/2026
phungu wadera la pakati m’boma la Kasungu Chikondi Kampachike Chisale wapeleka ndalama zokwana K350,000 kwa ophunzira 32 kuti agwiritse ntchito pa ndondomeko yopelekera kalata ku bungwe la Higher Education Students Loans and Grants Boards (HESLGB) kuti apeze mwayi wa ngongole yolipilira maphunziro.
Kampachike Chisale wati zimakhala zodandaulitsa kuti munthu azilephera kupeza maphunziro kaamba kosowa ndalama pomwe boma linayika kale ndondomeko zothandiza ophunzira osowa.
Iye wayankhula izi pomwe amapeleka upangiri kwa ophunzirawa momwe angapangire kuti apeze mwayi wa ngongole yolipilira maphunziro kuchokera ku bungweri.
Malinga ndi Kampachike Chisale ophunzira ambiri amalephera kupeza mwayi kaamba kolephera kutsatira ndondomeko zomwe zimafunikira.
M’modzi mwa ophunzirawa Wanga Chinsima yemwe anasankhidwira ku Mzuzu University wati upangiri omwe apeza kuchokera kwa a Chisale uwathandizira kwambiri ponena kuti amavutika kwambiri kuti apeze zofunikira pa maphunziro.
Wolemba: Mathews Benard