Mtunthama Broadcasting Station

Mtunthama Broadcasting Station Mtunthama Broadcasting Station is a media house broadcasting from Kasungu in Malawi.

The station believes in objectivity, accuracy and creativity throughout it's programming.

Anthu okwiya komanso a chibale a malemu  Olipa Aluveta Nanthambwe akumba manda pa nkhonde la nyumba ya Daniel Zimpita ye...
09/08/2026

Anthu okwiya komanso a chibale a malemu Olipa Aluveta Nanthambwe akumba manda pa nkhonde la nyumba ya Daniel Zimpita yemwe akumuganizira kuti wapha mayiyo.

Malinga ndi Sitima apolisi ndi a chipatala apempha mafumu ndi adzukulu kuti akakumbe mandawo malo ena.

Pomwe izi zikuchitika Zimpita akusungidwa ndi Polisi ndipo akawonekela ku bwalo la milandu.

Wolemba:Mathews Benard

Apolisi m'boma la Dowa amanga  Daniel Zimpita wazaka 37 pomuganizira kuti wapha mkazi wake Olipa Aluveta Nanthambwe wa z...
09/08/2026

Apolisi m'boma la Dowa amanga Daniel Zimpita wazaka 37 pomuganizira kuti wapha mkazi wake Olipa Aluveta Nanthambwe wa zaka 37 pa Msasa wa Dzaleka m'boma la Dowa.

Ofalitsa nkhani za apolisi m'bomali Alice Sitima wati awiriwa banja lawo linali litatha komabe malemuyo amabwerabe kudzawona woganizilidwayu mobisa ngakhale anali atakwatira mkazi wina.

Malinga ndi Sitima pa 8 August 2026 malemuyo anapita kumwambo owona chiliza ku midzi ya kufupi ndi Dzaleka koma ati atachoka kumeneko anapita kokakumana ndi a Zimpita koma sanabwelerenso.

Patapita masiku angapo thupi Nanthambwe linapezeka mminda ya pafupi ndi Msasa wa Dzaleka lili maliseche komanso lili ndi magazi.

Litapezeka thupilo anathamangira nalo ku chipatala cha m'bomali komwe achipatala atayeza anapeza kuti malemuyo wafa kaamba kobanika chifukwa chakuvulazidwa.

Wolemba Mathews Benard

08/08/2026

Mneneri wa Mulungu m’boma la Kasungu ali mchitokosi cha apolisi pomuganizira kuti
wakhala akugwilira mwana obeleka yekha wazaka 18.

Wachiwiri kwa mneneri wapolisi ku Kasungu Miracle Hauli wati mneneriyu ndi Collins Banda.

Malinga ndi Hauli, Banda anasiyana banja ndi amayi ake a msungwanayo kotero anakwatira mkazi wina yemwe amakhala naye limodzi ndi mwana wakeyo.

Mchaka cha 2024 Banda anawuza mwana wake kuti agone naye ndi cholinga choti apeze chuma ndipo msungwanayo navomera atamuopsyeza kuti akakana apenga misala ndipo kuchokera nthawi imeneyo Banda wakhala akugonana ndi mwana wakeyo.

Kwa mkazi watsopano Banda anamuuza kuti mphavu zake zimachokera kwa mwana wakeyo kotero nkaziyo akuyeneranso kutenga mphavu kuchokera kwa mwanayo kotero njira yopangira izi ndi kuti Banda agonane ndi onse awiri nthawi imodzi.

Apolisi atalandira nkhaniyi anapita ku chipatala ndi msungwanayo komwe atsimikiza kuti wakhala akugonedwa mwankhaza ndipo bambo akewo akusungidwa mchitokosi cha apolisi.

Wolemba Mathews Benard

The Director General of the Malawi Broadcasting Corporation, MBC, Brian Banda, has died.Banda died at Mwaiwathu Private ...
08/08/2026

The Director General of the Malawi Broadcasting Corporation, MBC, Brian Banda, has died.

Banda died at Mwaiwathu Private Hospital in Blantyre following a short illness.

Confirming the death, MBC Public Relations and Customer Affairs Manager, Chisomo Mwamadi, said the corporation will provide further details in due course.

Banda’s death is a loss to Malawi’s media industry.

Reported by Mathews Benard

Mkulu owona za umoyo ndi chilengedwe m’boma la Kasungu a Rudolf Zinkanda Banda ati anthu ambiri omwe akumapita ku chipat...
07/08/2026

Mkulu owona za umoyo ndi chilengedwe m’boma la Kasungu a Rudolf Zinkanda Banda ati anthu ambiri omwe akumapita ku chipatala kulandira thandizo la matenda otsegula m’mimba ndi kaamba kogwiritsa ntchito madzi oyipa.

Malinga ndi a Banda madzi abwino komanso aukhondo ndi njira yokhayo yothana ndi matendawa kotero ngati boma akuyika chidwi powonetsetsa kuti anthu ochuluka m’bomali akukhala ndi mwayi opeza madzi abwino.

Iwo ayankhula izi kwa Nduwa m’dera la mfumu yayikulu Wimbe pomwe bungwe la Beyond Water limapeleka pampu ya madzi oyendera mphavu ya dzuwa yomwe yamangidwa ndi thandizo la ndalama kuchokera ku Rotary Club of Lilongwe.

M’mawu ake mkulu wa bungwe la Beyond Water Philip Chidawati wati anaganiza zoyika madziwa kwa Nduwa potengera ndi mavuto omwe anthu amakumana nawo pa nkhani yokhudza madzi aukhondo.

Naye wapampando yemwe wangosankhidwa kumene ku Rotary Club of Lilongwe Mphanda Mkandawire wati amazindikira bwino kufunikira kwa madzi aukhondo pa umoyo wa munthu kotero ndi chifukwa chake akudzipeleka pothandiza ndi ndalama kuti anthu akhale ndi mwayi opeza madzi abwino.

M’madzi a mipopi omwe apelekedwa lero afikira anthu pafupifupi 10,000 a m’mudziwu komanso madera ena ozungulira.

Wolemba: Mathews Benard

Apolisi m’boma la Kasungu amanga Laston Damiano wazaka 21 kaamba koyendetsa njinga ya moto mosasamala yomwe yapha a Haji...
06/08/2026

Apolisi m’boma la Kasungu amanga Laston Damiano wazaka 21 kaamba koyendetsa njinga ya moto mosasamala yomwe yapha a Hajira Ibrahim azaka 35 komanso kuvulaza amayi ena awiri pa mphambano ya Chayamba m’manisipalite ya bomali.

Wachiwiri kwa mneneri wapolisi ya Kasungu Miracle Hauli wati pa 2 mwezi uno Damiano amayendetsa njinga ya moto kuchokera ku Chiphaso kulowera mtauni ya Kasungu ndipo atafika pa malowa anawomba amayi atatu omwe amagulitsa malonda.

Kutsatira ngoziyi Ibrahim anavulala kwambiri m’mutu ndipo anamwalira atangofika nawo ku chipatala cha Kasungu pomwe a Benadeta Mumba komanso a Liness Asibu onse azaka 29 akulandira thandizo la mankhwala.

Malinga ndi Hauli Daminao akumuganizira milandu inayi yomwe ndi kudzetsa imfa poyendetsa njinga mosasamala, kugwirista ntchito njinga ya moto yosalembetsedwa, kuyendetsa njinga opanda chiphaso komanso kugwiritsa ntchito njinga yosakhomera.

Damiano amachokera m’mudzi wa Yamwala mfumu yayikulu Kaomba ndipo akawonekera kubwalo la milandu posachedwa.

Wolemba: Mathews Benard

Bwalo la Chief Resident Magistrate  lagamula Peter Tholo wazaka 28 kuti akakhale kundende zaka 4 atapezeka olakwa pa mla...
05/08/2026

Bwalo la Chief Resident Magistrate lagamula Peter Tholo wazaka 28 kuti akakhale kundende zaka 4 atapezeka olakwa pa mlandu owononga komanso kuba ma meter amadzi m'manisipalite ya Kasungu.

Powonekera ku bwalo la milandu Tholo anapempha bwalo lamilandu kuti limuganizire pomupatsa chilngo chofewa koma oyimira boma pa mlanduwu a Gladys Jentala anati uyu akufunika chilango chokhwima.

Malinga ndi Jentala madzi m'manisipalite ya Kasungu ndi ovuta kale kotero zomwe anapanga Tholo ndi zolakwika komanso kuwonjezera mavuto omwe alipo kale.

Popeleka chigamulo Chief Resident Magistrate Brian Sambo anagwirizana ndi a Jentala kotero wapeleka chilango cha zaka 4 kuti likhale phunziro kwa ena.

Tholo amachokera m'mudzi mwa Yamwala mfumu yayikulu Kaomba m'boma la Kasungu.

Wolemba:Mathews Benard

Apolisi m'boma la Kasungu amanga Peter Tholo wazaka 28 pomuganizira kuti amaba komanso kuwononga ma meter amadzi omwe am...
02/08/2026

Apolisi m'boma la Kasungu amanga Peter Tholo wazaka 28 pomuganizira kuti amaba komanso kuwononga ma meter amadzi omwe amayikidwa ndi kampani ya Water Board m'manisipalite ya bomali.

Wachiwiri kwa mneneri wa polisi ya Kasungu Miracle Hauli wati akhala akulandira madandaulo ochuluka kuchokera kwa anthu okhala m'manisipaliteyi za kubedwa kwa ma meter wa.

Kutsatira kafukufuku yemwe apolisi anakhazikitsa akwanitsa kupeza ma meter 12, mipopi komanso ma pipe amadzi omwe iye amawasunga.

Pakanali pano a Central Region Water Board avomereza kuti ma meter wo ndi awo ndipo oganiziridwayu akawonekera kubwalo la milandu posachedwa.

Tholo amachokera m'mudzi mwa Yamwala mfumu yayikulu Kaomba m'boma la Kasungu.

Wolemba:Mathews Benard

01/08/2026

News

At least 27 people have been killed and 44 others seriously injured after a passenger bus overturned in Boumerdès, in northern Algeria.

The accident happened on the evening of Friday, 31 July 2026

President Abdelmadjid Tebboune has declared three days of national mourning, with national flags to be flown at half-mast across the country.

Prime Minister Sifi Ghrieb has visited victims receiving treatment at Boumerdès University Hospital, where many of those injured remain admitted.

Ndalama zokwana K2.134 billion ndi zomwe Khonsolo ya boma la Kasungu yalandira pansi pa ntchito za Governance to Enable ...
01/08/2026

Ndalama zokwana K2.134 billion ndi zomwe Khonsolo ya boma la Kasungu yalandira pansi pa ntchito za Governance to Enable Service Delivery (GESD) kuti ichitire ntchito zachitukuko zosiyanasiyana m'chaka cha 2026-27 kaamba kogwiritsa bwino ntchito ndalama zomwe inalandira chaka chatha.

Malinga ndi zotsatira za kuwuniwuni wa Local Authority Performance Assessment (LAPA) khonsoloyi yakhala yachitatu pa makhonsolo onse m'dziko.

Kawuniwuniyi amaona momwe makhonsolo agwiritsira ntchito ndalama zomwe analandira chaka chatha moyenera kapena ayi.

Poyankhula pambuyo polandira ndalamazi komanso kuchita bwino bwanamkubwa wabomali Dr Lawford Palani ati izi zachitika kaamba ka kugwirana manja pakati pa khonsoloyi, mafumu, mabungwe komanso adindo andale.

Ntchito pansi pa Governance to Enable Service Delivery (GESD) imalandira thandizo la ndalama kuchokera ku World Bank kudzera ku bungwe la National Local Government Finance Committee (NLGFC).

Kupatula ndalamazi Khonsoloyi yalandiranso K493 million yomwe igwiritse ntchito pochita chitukuko cholimbana ndi kusintha kwa nyengo (Regional Climate Resilient Programme - RCRP - 2).

Mundondomeko yi makhonsolo omwe achita bwino amalandira ndalama yochuluka kuposa omwe alephera (Performance Based Grant).

Address

Box 125
Kasungu

Opening Hours

09:00 - 17:00

Telephone

+265999017357

Website

Alerts

Be the first to know and let us send you an email when Mtunthama Broadcasting Station posts news and promotions. Your email address will not be used for any other purpose, and you can unsubscribe at any time.

Contact The Business

Send a message to Mtunthama Broadcasting Station:

Shortcuts

Share