Mtandire Community Radio

Mtandire Community Radio Our vision is to be the most valued, trusted and vibrant radio station that inspires communities.

  Mukava Hiiii Hoooo Arsenal yafika, ichi chinali chiwoye Cha otsatira team ya Arsenal pomwe mphunzitsi watimuyi Mikel A...
27/05/2026



Mukava Hiiii Hoooo Arsenal yafika, ichi chinali chiwoye Cha otsatira team ya Arsenal pomwe mphunzitsi watimuyi Mikel Arteta wasankhidwa kukhala mphunzitsi oposa onse mu Premier League ya 2025-26 (PL manager of the season) k*tsatira kuyitsogolera kwake k*ti team yake ipambane League.

Ma Gunners anapambana chikho chawo choyamba cha Premier League m’zaka 22 zapitazo, atamaliza ndi mapointsi asanu ndi awiri patsogolo pa team ya Manchester City.

Arteta wasankhidwa, atapambana aphunzitsi ena monga Andoni Iraola wa AFC Bournemouth ndi Régis Le Bris wa Sunderland F.C, omwe onse athandiza matimu awo kufika ku mmipikisano ya Europe.

Arteta anatenga utsogoleri wa Arsenal pa nthawi yomwe timuyi inali isakuchita bwino, mu December 2019, ndipo m’zaka zisanu ndi theka zapitazi wabwezeretsa timuyi kukhala imodzi mwa matimu amphamvu kwambiri ku Mangalande.

Wolemba: Frezer Kamputa -Lilongwe

 Omenyera ufulu wa ana komanso akatswiri a za maphunziro apempha boma k*ti lifulumizitse kukonza ndondomeko yolola ophun...
26/05/2026


Omenyera ufulu wa ana komanso akatswiri a za maphunziro apempha boma k*ti lifulumizitse kukonza ndondomeko yolola ophunzira a m’masukulu a pulaimale a boma kuvala ma buluku ndi malaya a manja ataliatali makamaka munyengo yozizira.

M’modzi mwa omenyera ufulu wa ana, a Amos Chibwana, ati adapereka kale malingaliro awo ku unduna wa za maphunziro atafufuza mavuto omwe ophunzira amakumana nawo chifukwa cha kuzizira kusukulu.

Nawonso a Island Mtambo omwe amalankhulapo pa nkhani za maphunziro ati kusintha kwa uniform kumeneku kunayenera kuchitika kalekale, ndipo ati ma buluku akhoza kukhala mbali ya uniform yovomerezeka m’masukulu a boma.

Koma mneneri wa unduna wa za maphunziro, a Lilly Kampani, ati undunawu adzafotokoza zambiri pa nkhaniyi mtsogolo.
Pakadali pano, ophunzira ambiri a m’masukulu a pulaimale a boma amavala makabudula ndi malaya odula mikono, pamene ana a m’masukulu ena omwe si aboma amaloledwa kuvala ma buluku ndi malaya a manja ataliatali.

Wolemba: Frezer Kamputa -Lilongwe (26/05/26)

 TIMU YA LAUDON IDEAS FC YAGONJETSA TIMU YA MTSILIZA DORTMUND FCTimu ya Laudon Ideas Football Club la Mulungu yagonjetsa...
25/05/2026



TIMU YA LAUDON IDEAS FC YAGONJETSA TIMU YA MTSILIZA DORTMUND FC

Timu ya Laudon Ideas Football Club la Mulungu yagonjetsa timu ya Mtsiliza Dortmund FC zigoli ziwiri kwa chimodzi.

Pamasewerawa wosewera wa timu ya Laudon Ideas Football Club Chikondi Amosi ndiyemwe anasewera bwino kuposela onse (Man of the match) komanso ndiyemwe anagoletsa zigoli Zonse kumbali ya Laudon Ideas Fc.

Masewelowa anachitikira pabwalo lamasewero la Mwenela kwa Mtsiliza.

Wolemba: Thokozani Similton

YOUTH INNOVATION FUND OUTREACH IN LILONGWE EMPOWERS YOUNG INNOVATORS FOR MALAWI 2063National Youth Council of Malawi (NY...
25/05/2026

YOUTH INNOVATION FUND OUTREACH IN LILONGWE EMPOWERS YOUNG INNOVATORS FOR MALAWI 2063

National Youth Council of Malawi (NYCOM) has opened a call for young people (18-35 Years) with innovative, impactful, scalable, and sustainable ideas to apply for funding. The ideas should fall within the sectors of Agriculture, Tourism, Mining, Digitisation, And Manufacturing, with strong potential for job creation, value addition, and problem-solving.

The call was officially launched on 18 May, with closing date set for 8 June 2026. As a Trade Officer working with Lilongwe City Council, I was privileged to attend an Information Session on 15TH June 2026, organised to provide guidance on the initiative.

The main aim of the Fund is to accelerate the implementation of Malawi 2063 (MW2063) through promoting innovative youth-led initiatives. During the session, we were provided with detailed guidance on the Youth Innovation Fund (YIF) application process. Youth from across Lilongwe City attended the training. Among the key requirements highlighted were business concepts, budgets, implementation plans, timelines, and clearly stated problems together with practical solutions aligned to the priority sectors.

National Youth Council volunteered to support youth-led organisations in Lilongwe with the preparation of their applications.
On 23 May, Saturday 2026 I fulfilled this commitment when I visited Chimbalame Youth Club in Mtandire–Mtsiliza Ward, where we spent time engaging with young people and discussing the application process in detail.

What they have noticed is that the youth are ready to take the development of this nation to another level, but many lack access to information. Most of them know very little about Malawi Vision 2063 and the Malawi Implementation Plans, yet these are the people who will live in the Malawi of 2063. As a country, we need to invest more in youth awareness and engagement.

The training session was successful and truly eye-opening for the youth.

By Alinafe James - Correspondent Reporter

This is how teams have concluded the 2025/2026 English Premier League season. Yanuyo zayenda??
24/05/2026

This is how teams have concluded the 2025/2026 English Premier League season. Yanuyo zayenda??

 MWAI KWA OPHUNZIRA OMWE AKUFUNA NGONGOLE YA BOMAUyambira pa 25may bungwe la Higher Education students Loads and Grants(...
24/05/2026



MWAI KWA OPHUNZIRA OMWE AKUFUNA NGONGOLE YA BOMA

Uyambira pa 25may bungwe la Higher Education students Loads and Grants(HESLGB) lati latsekula mwai Kwa ophunzira asukulu za ukachenjede wofunsira ngongole ndi thandizo la ndalama kwa ophunzira omwe akufunikira thandizo Li.

Izi yalengeza mu kalata Yomwe bungweli atulutsa kudzera pa website yawo.

Iwo achenjeza so k*t ophunzira omwe afune nawo mwaiyu apereke zoyenera zonse monga makalata onse olondora komanso ofunikira k*ti mwaiwu usawaphonye.

Wolemba Yohane Lackson Nyirongo

 Pamalo Ena otchedwa Bawi m boma la Ntcheu pachitika ngozi ya bus ya sososo, Ngoziyi yachitika pomwe busiyi imachokera k...
24/05/2026



Pamalo Ena otchedwa Bawi m boma la Ntcheu pachitika ngozi ya bus ya sososo, Ngoziyi yachitika pomwe busiyi imachokera ku Lilongwe ndipo inaombana ndi lorry ya 3 tonne yomwe imalowera mbali ya chingeni.

Pakanali pano sizinadziwike k*ti avulirara alipo angati Pangoziyi.

Wolemba Yohane Lackson Nyirongo

24/05/2026



MWAZINA ZOMWE WALANKHULA DR ANSAH

Mtsogoleri wachiwiri wa dziko lino Dr Jane ansa wachenjeza yemwe Anatumiza drone kunyumba kwake.

Mukulankhula kwawo ku tchalitchi cha Soche CCAP ku Blantyre iwo ati Mulungu adzawalanga aliwonse omwe akukhudzidwa ndi mchitidwewu.

Wolemba Yohane Lackson Nyirongo

 Ochita Malonda amsika wa Wakawaka Ali kakasi pomwe khosolo ya Lilongwe yagwetsa msikawo. Kugwetsedwaku kukudza pomwe kh...
22/05/2026


Ochita Malonda amsika wa Wakawaka Ali kakasi pomwe khosolo ya Lilongwe yagwetsa msikawo.

Kugwetsedwaku kukudza pomwe khosololi lid anena k*ti pofika pa 1 April msikawu usamukukire ku kanyenje ku mseu WA bypass.

Pakali pano pamsikau Pali chipwilikiti moti mwaena mwaanthuwo akumafuna k*tseka mseu.

Wolemba Yohane Lackson Nyirongo

 Gulu loyimba  lochokera ku Mtandire mumzinda WA Lilongwe lotchedwa  Madalitso Band lanyamuka lero lachinayi kupita ku u...
21/05/2026



Gulu loyimba lochokera ku Mtandire mumzinda WA Lilongwe lotchedwa Madalitso Band lanyamuka lero lachinayi kupita ku ulaya komwe akakhale ndi maimbidwe wosachepera 50.

Ulendo uno gululi momwe muli Yobu Maligwa ndi Yosefe Kalekeni akafika mpaka maiko a Japan, South Korea komanso Canada.

Maligwa ndi Kalekeni ati akhala akukonzekera ulendowu kwa kanthawi kotero k*ti akonzeka kukweza mbendera ya dziko lino kumeneku.

Maimbidwe awo ayamba lachisanu mdziko la France kenako apita ku United Kingdom asanapite ku Holland komanso Poland paulendowu apitaso ndi manejala wawo Neil Nayar.

Kumeneko sakayimba kokha komanso akawonesanso kanema yawo ya The Banjo Boys komanso kuphunzitsa.

Wolemba: Julius Kasim

Zina ukanva kamba anga mwala.Amayi omwe amachita malonda ogulitsa thupi m'boma la Thyolo apempha akuluakulu a zaumoyo pa...
20/05/2026

Zina ukanva kamba anga mwala.

Amayi omwe amachita malonda ogulitsa thupi m'boma la Thyolo apempha akuluakulu a zaumoyo pa chipatala chachikulu cha m'bomali k*ti adziwalola kuchotsa mimba zosayembekezera akapita ku chipatala.

M'modzi mwa amayiwa, a Linda Banda ndiwo apereka pempholi pa nkumano omwe bungwe la Abwezi 360 linachititsa pofuna kubweretsa pamodzi azimayi oyendayenda ndi ogwira ntchito za umoyo m'bomali

Wolemba: Frezer Kamputa -Lilongwe

Address

Lilongwe

Telephone

+265999138043

Website

Alerts

Be the first to know and let us send you an email when Mtandire Community Radio posts news and promotions. Your email address will not be used for any other purpose, and you can unsubscribe at any time.

Share

Category