News Online in Brief- NOB

News Online in Brief- NOB Informing the mass

Mfuti ndi zipolopolo 207 zapezeka ndi Youngstone Kaunda ku Nanthenje mzinda wa Lilongwe.Izi zili malingana ndi Inspector...
22/03/2025

Mfuti ndi zipolopolo 207 zapezeka ndi Youngstone Kaunda ku Nanthenje mzinda wa Lilongwe.

Izi zili malingana ndi Inspector Hastings Chigalu yemwe ndi mneneri wa apolisi ya Lilongwe.

A Chigalu ati amanga Kaunda atalandira dandaulo pa zomwe iye amachita ndi mfutiyi usiku monga kuwombera m'mwamba ndi kuopsheza makolo ena omwe amati ana awo amakamubera mbatata m'munda mwake.

Momwe zimachitika izi, ndikuti Kaunda ali ndi mlandu wina okhapa munthu ndipo adali akuthawathawa. Iye amachokera m'mudzi Reuben, kwa Kalumbu m'bomali ndipo akhala akukaonekera ku bwalo posachedwapa.

Olemba : Sammey Saulos

Anthu oposera 35 afa pa ngozi.....Miyoyo ya anthu pafupipafupi makumi atatu ndi asanu( 35) yaluzika kutsatira ndi ngozi ...
23/08/2024

Anthu oposera 35 afa pa ngozi.....

Miyoyo ya anthu pafupipafupi makumi atatu ndi asanu( 35) yaluzika kutsatira ndi ngozi zikuluzikulu zomwe zachitika m'maboma a Thyolo, Neno, Kasungu ndi Zomba.

Loweruka sabata yathayi, m'boma la Thyolo, galimoto lidasempha msewu ndikulowa mbali yochitira malonda komwe idavulaza ndikupha anthu asanu ndi anayi ndipo ena adavulalala modetsa nkhawa ndipo Lachiwiri lake madzulo, minibasi ina yomwe inkachokera mtunda wa Blantyre kulowera ku Mwanza, idaphulika teyala ndikugudubuzika. Anthu atatu omwe adali ku mpando wa kutsogolo adafera pomwepo ndipo ena ochuluka adavulalala modetsa nkhawa.

Dzulo pa 21, m'boma la Kasungu anthu makumi awiri ndi asanu afa minibasi yomwe adakwera itayaka kutsatira kuombedwa ndi galimoto lina lonyamula mafuta. Pa ngoziyi, galimoto yaikuluyi idaombanso wakapalasa wina pomwe imayesera kumuzemba.

Ndipo ngozi ina yoophsanso yachitika dzulo lomweli m'boma la Zomba pomwe anthu anayi afa pa ngozi ya minibasi.

Kupatula ngozi izi, dziko lino lalembetsa ngozi zochuluka m'masabata apitawa m'maboma a Dedza, Ntcheu ndi Mzimba pomwe anthu asanu ndi atatu adafa pa ngozi ya ndege m'khalango ya Chikangawa.

Olemba: Robin Samuel Saulos

Hope Chisanu yemwe masiku ambuyowa amagwira ku wailesi ya MBC, wamwalira. Malingana ndi lipoti lomwe wailesi ya MBC yatu...
01/06/2024

Hope Chisanu yemwe masiku ambuyowa amagwira ku wailesi ya MBC, wamwalira. Malingana ndi lipoti lomwe wailesi ya MBC yatulutsa, Chisanu wamwalira ali mdziko la America ndipo nsuwani wake, Sharon Bakali Machinjiri ndiye wadzimikiza za izi.

Tikupatsirani zambiri mmaripoti ena.

Muchithunzi: Hope Chisanu

 Kuchitika zoophsa.....Aphunzitsi a IPTE 14-17 awophseza....Gulu la aphunzitsi a ndondomeko ya IPTE 14 mpaka 17 alembera...
21/03/2024



Kuchitika zoophsa.....

Aphunzitsi a IPTE 14-17 awophseza....

Gulu la aphunzitsi a ndondomeko ya IPTE 14 mpaka 17 alembera kalata yodzudzula ma unduna a Zamaphunziro, Zachuma ndi Maboma a ng'ono kamba kogwira ntchito mosalabadira aphunzitsiwa powalemba ntchito pomwe ena athano zaka zisanu chimalizireni maphunziro awo a ntchitoyi.

Malingana ndi chikalata chomwe chasaininidwa ndi mtsogoleri wagululi, Onesmus Banda, chopita ku ma undunawa kudzera ku Nyumba ya Malamulo, chaloza mkhalidwe wawo olowetsa ndale ku maphunziro pomwe akufuna kulemba ntchito aphunzitsiwa zomwe ati ndizosapindulira nsanamira yomwe imati 'maphunziro ndi gwero la zonse' [education is a key to success].

Chikalatachi chapitiririza kudzudzulanso unduna wa maphunziro pomwe chati undunawu ukupitiriza kusula aphunzitsi mmakoleji osiyanasiyana pomwe ulibe dongosolo lowalembera ntchito, ukulephera kulondoloza ndalama zomwe zikumaikidwa m'makhosolo pa ntchito yolemba aphunzitsi ngati zagwira ntchito yake yoyenera komanso kusowekera utsogoleri wa cholinga pa ndondomeko yolemba ntchito aphunzitsiwa mwa zina . Kalatayi yadzudzulanso mneneri waku undunawu a Mphatso Mkuonera omwe ati akumayankhula zipongwe aphunzitsiwa akafuna kudziwa zinthu zina malingana ndi dongosolo lawo lowalemba ntchito. Adati a Mkuonera amaiwala kuti ali pa udindo umenewo chifukwa cha anthu omwe amadulidwa misonkho ndipo mmalo mwake akumadzimva ngati ndi oyamba kukhala pa udindo ngati umenewo.

Pomaliza, kalatayi yaophseza kuti aphunzitsi pafupipafupi 10,000 omwe afuna kulembedwa ntchitowa, achita zionetsero zoophsa ngati ma undunawa apitirize kusalabadira zowalemba ntchito mu bajeti ya 2024-2025 yomwe ikhale ikuvomerezedwa ndi nyumba ya malamulo posachedwapa.

Boma kudzera mu thandizo lochokera ku World Bank, chaka chathachi lidalemba ntchito aphunzitsi a msukulu za pulaimale osapyola 2500 dziko lonse la Malawi kudzera m'makhosolo a maboma ena.

Olemba: Sammey Saulos

16/12/2023

Breaking: Haiya ndi mtsogoleri wa FAM, wagwetsa Nyamilandu ndi 23- 13

Zisankho za DPP zalephereka.....Mfundo za Glezelder sizikugwiranso ntchito......Olemba: Sammey SaulosFumbi likulephera k...
11/12/2023

Zisankho za DPP zalephereka.....

Mfundo za Glezelder sizikugwiranso ntchito......

Olemba: Sammey Saulos

Fumbi likulephera kuwusa ku chipani cha DPP pomwe mikangano ikunka iberekeraberekera.

Patangodutsa masiku ochepa, Mlembi wamkulu ku chipanichi a Glezelder Jeffrey atalengeza kuti chipani chawo chili ndi Konveshoni pa 16 December chaka Chino ndipo atsogoleri okapikisana atha kuyamba makapmpeni, lero mmodzi wa aphungu kuchipanichi wakatenga chiletso pa msonkhano waukuluwo omwe umayenera kuchitika kumathero asabatayi mzinda wa Lilongwe.

Malingana ndi chikalata chochokera ku Hayi Khothi chosainidwa ndi Jaji Simeon Mdeza, chiletsochi chakatengedwa ndi phungu wa DPP mdera la pakati ku Blantyre a Chipiriro Mpinganjira chomwe chikuletsanso a Jeffrey kuti mfundo zawo zomwe anauza atolankhani sabata yathayi zisagwire ntchito.

Kutsatira ndi izi, kulibe chisankho chosankha mtsogoleri wachipanichi ndi maudindo ena ngakhale akuluakulu ena anali mkati kukonzekera chisankhochi.

Izi zikudzanso pomwe zikuonetsa kuti mchipani cha DPP muli magulu awiri, mbali ya a Kondwani Nankhumwa komaso Prof Arthur Peter Muthalika ndipo ndikwanthawi tsopano mbali ziwirizi zikukanika kumvana kuchokera mchaka cha 2020 pomwe analuza zisankho za mtsogoleri wa dziko maka payemwe angatsogolere chipanichi.

11/12/2023

Nankhumwa: Ine sindikuthandizidwa ndi MCP ndipo iyi ndi propaganda ya kagulu ka anthu enake omwe akufuna kundigwetsa mphwayi

11/12/2023

Nankhumwa: Ine ndili pano ngati okapikisana pa chisankho cha Pulezidenti wa DPP ndipo aliyense udindo wanga akuwudziwa kuti ndine wachiwiri wa mtsogoleri wa chipani cha DPP kummwera ndipo ndi anthu omwe adandisankha angandichotse udindowu

11/12/2023

Nankhumwa wakana udindo omwe APM wamupatsa okhala mulangizi wake

11/12/2023

Nankhumwa: Anthu ena akhala akundipeza ine kuti ndipange zoti a Muthalika asaime pa zisankho koma ndidati ayi aime chifukwa ndi ufulu wawo ndipo abwere tidzapikisane. Ngati iwo angawine ndidzawapanga sapoti ndipo ngati ndingawine ndukhulupiranso adzandipanga sapoti ndipo pasapezeke kagulu komanyoza ndikutukwana APM chifukwa zimenezo ndiye mfundo za demokilase . Ine mukagulu konyoza a Muthalika mulibemo

11/12/2023

Nankhumwa: Chipani cha DPP chinachotsedwa m'boma pa zifukwa ndipo kuchokera pamenepo sichinakhalepo pansi kuti akambirane kufikira pano chipani chikutitimira.

11/12/2023

Nankhumwa: Ena amati ndine mwana osapola pamchombo koma mkati mwa ine ndi wamkulu. Nditha kuoneka osauka koma mwa ine ali olemera. Ndilibe digiri ya upulofesa koma ali mwa ine ndioposa zimenezo. Ndiye okamba adzikamba koma ine ndikupitirirabe. Tikupanga kampeni chifukwa a Secretary General adalengeza za chisankho posachedwapa ndipo aliyese yemwe akupikisana asalole kuophsezedwa

Address

Lilongwe
NOTHING

Telephone

+265992747685

Website

Alerts

Be the first to know and let us send you an email when News Online in Brief- NOB posts news and promotions. Your email address will not be used for any other purpose, and you can unsubscribe at any time.

Share