Mfumu Solomo - Pabwalo

Mfumu Solomo - Pabwalo Pabwalo ili pamaikidwa zinthu zosiyanasiyana monga malo achilendo, zachilengedwe komanso nkhani zosi

19/09/2025

Mwadzuka bwanji?

Amene tingakwanitse ulonda mmasukulu a secondary school mu ma Dera awa

Lilongwe
Mzuzu
Rumphi

Ndiyankhuleni ku Inbox. Mawa ma interview. Musakhala kutali ndi maderawa

18/09/2025

Lero lero, amene akuziwa kuti ali ndi ma qualifications a uphunzitsi ndipo atha kukwanitsa kuphunzitsa ku Mzuzu pa Carthage Private Secondary School

Ayimbireni a Head apa School Po pa

+265899019370

+265992460741

Mukhale ndi UCE , Registered, kapena TCM licenced

Amene mukufuna ku school imene yangoyamba kumene ku LILONGWE, ndi Rumphi

Ndiyankhuleni INBOX

06/09/2025

NGATI MWANA WANU KAPENA INUYO MWALEPHERA MAYESO.

Choyamba Umoyo umapitirirabe ngakhale munthu sanapambane mayeso ndipo palibe amene chipumi chake chimalembedwa kuti walephera mayeso a form 4.

Ena analephera mayeso , panopa ndi amene akuthandidzanso kwambiri mmamizi ndi mmataunimu. Ena ali ndi zinthu zambiri , ali ndi minda, zigayo, mabanja abwino, magalimoto ndi zambiri zofunika pamoyo, komano pa umoyo wawo sanachitepo bwino pa nkhani za maphunziro izi.

Ndiye muzizindikiranso kuti ena anapambana bwino zedi atalembanso mayeso awo.

Palibe amene tsogolo lake lingafere panjiira chifukwa chakulephera mayeso awawa. Pedzani njira Ina yopambanira.

Osawawawitsa ana mitima. Enatu amakhumudwa kwambiri nkufika potenga nazo chingwe. Ena amangoziimba mlandu.

Aliyense ali ndi kuthekera kopedzanso njira Ina yotukulira moyo wake... M***a kusaka school yaluso la manja , kuyamba business ndi zinthu zina.

KUNYOZA MWANA NKUNYONGA

27/08/2025

ngati simukuziwa AVIATOR muli pabwino.

Lero ndinali ku Inbox komano anyamata ambiri odutsa 7 amafunsa za mankhwala amene angamwe kuti angomwalira osamva ululu kwambiri pambuyo pobwetsa ndalama za nkhani nkhani pa njuga yapa Foni.

KODI INUYO MMATANI KUTI MUSABETSE NDALAMA ZANU CHIFUKWA CHA NJUGA.

Yankho lanu lithandidza ena

" dinari!!!"    dinariiii" _____________________________________________Lero tiyeni tilowe  nawo mu dziko ili la KUWAIT....
23/08/2025

" dinari!!!" dinariiii"

_____________________________________________

Lero tiyeni tilowe nawo mu dziko ili la KUWAIT. Dziko la Kuwait lili ku Middle East
ndipo limalumikizana ndi maiko ena aakulu monga IRAQ ku kumpoto ndi SAUDI ARABIA ku kumwera. Mbali ina, lilinso ndi nyanja yotchedwa PERSIAN GULF, yomwe amagwiritsa ntchito posenza mafuta kupita ku maiko ena.

Dziko la Kuwait ndi laling'ono, koma ndi limodzi mwa maiko olemera kwambiri padziko lapansi. Izi zili tere chifukwa dzikoli limapeza ndalama zambiri kuchokera ku mafuta achilengedwe. Mafutawa amagwiritsidwa ntchito kupanga petulo, dizilo, ndi zinthu zina zomwe maiko ambiri amafuna.

Ndalama ya ku Kuwait imatchedwa KUIWAITI DINAR, ndipo ndi yamphamvu zedi. Kuwaiti Dinar imodzi ili ofanana ndi pafupifupi 5,700 Malawi Kwacha. Ndipo chifukwa cha kusiyana kumeneku, anthu ambiri amafuna kukagwira ntchito ku Kuwait kuti apeze ndalama zambiri.

Anthu ambiri a ku Kuwait amapeza ndalama mwa kugwira ntchito m'makampani opanga mafuta. Ndalama zimene dzikoli limapeza, limagwiritsa ntchito kumanga misewu wabwino, zipatala, mashopu akulu, komanso nyumba zazitali za m’tauni.

Pena mabwana amatuma antchito awo kuti alengezetse mmizinda zoti kukufunika antchito, ndiyeetu kumakhala kufuula ndi ma sipika , kukuwa ndithu kuti '" DINARIIII, DINARII" apopo amene ndi lova amayenera kusunzira kufupi ndi kumene kukumveka uthengako, ntchito sisowa kwenikweni.

Anthu ambiri ochokera ku Malawi ndi mayiko ena amapita ku Kuwait kukagwira ntchito monga ya mnyumba, ogwira ntchito yoyeretsa, ogwira ntchito yomanga nyumba, ulonda komanso m'ma hotelo. Ngakhale ntchitozi sizapamwamba ku Kuwait, amalipidwa bwino poyerekezera ndi ntchito zina zaku Malawi, ndipo zimawathandiza.

Ndalama ya ku Kuwait imatchedwa KUIWAITI DINAR, ndipo ndi yamphamvu zedi. Kuwaiti Dinar imodzi ili ofanana ndi pafupifupi 5,700 Malawi Kwacha.
Anthu ambiri a ku Kuwait amapeza ndalama mwa kugwira ntchito m'makampani opanga mafuta. Ndalama zimene dzikoli limapeza, limagwiritsa ntchito kumanga misewu wabwino, zipatala, mashopu akulu, komanso nyumba zazitali za m’tauni.

Pena mabwana amatuma antchito awo kuti alengezetse mmizinda zoti kukufunika antchito, ndiyeetu kumakhala kufuula ndi ma sipika , kukuwa ndithu kuti '" DINARIIII, DINARII" apopo amene ndi lova amayenera kusunzira kufupi ndi kumene kukumveka uthengako, ntchito sisowa kwenikweni.

Anthu ambiri ochokera ku Malawi ndi mayiko ena amapita ku Kuwait kukagwira ntchito monga ya mnyumba, ogwira ntchito yoyeretsa, ogwira ntchito yomanga nyumba, ulonda komanso m'ma hotelo. Ngakhale ntchitozi sizapamwamba ku Kuwait, amalipidwa bwino poyerekezera ndi ntchito zina zaku Malawi, ndipo zimawathandiza.

Chiarabu ndi chilankhulo chawo chomwe ndichofala, koma chingelezi chimagwiritsidwa ntchito kwambiri m'maofesi, mashopu, ndi zipatala.
Likulu la dziko la Kuwait limatchedwa Kuwait City. Mu city iyi muli muli matawa, nyumba zazitali, komanso malo ambiri owonera zinthu, mashopu akuluakulu, ndi malo achikhalidwe.

BWANJI TIFIKE MU MADERA ENA A MDZIKO ILI KUTI TIONEKO ZINA NDI ZINA?

PANGANI LIKE PAGE ILI LA Mfumu Solomo - Pabwalo TIYENDERE LIMODZI PA ULENDOWU

22/08/2025

Ndili ndi zochitika mu Lilongwe komano Photographer amene tidapangana naye foni ikungoitana , komano ndalama ndinamupatsiratu.

Alipo Photographer amene ali ndi suit ya blue , ndikufuna andiperekeze ku mwambo womwe ndikupitawu. Tikayamba 2 koloko. Ganyu yake ndi ya matsiku awiri. Lero ndi mawa , Saturday. Atha kukhalapo awiri vuto palibe.

Ikani Number kapena ndiyankhuleni ku Inbox ndili active.

Mukhale kuti muli mu Lilongwe momuno, kapena m***a kufika mu Lilongwe mmaola osadutsa atatu

10/08/2025

MWADZUKA BWANJI KUMENEKO?

09/08/2025

Moni Sir, mwadzuka bwanji?

Timafuna tifunse nawo maganizo. Ndinagula njinga zakabaza 10 komano anjingawa amangoti awabera njinga mu town mpaka ndinasala ndi imodzi. Kupita ku police palibe chimene chimaphulapo kanthu. Ndiye zana ndinalanda njinga imene ndimaikaikira kuti ndiyanga. Titafika ku polisi anandisekera akuti ndinalanda njinga mwachipongwe , zimayenera kuzera ku polisi. Ndatuluka , ndapitaso ku polisi kukawauza kuti ndaona njinga yanga, akuti zilibe umboni.

Abwana Kodi ineyo mwina ndi umbuli komano anzanga amene amachita business ya njinga akapita ku polisi amathandizidwa bwino bwino ? Kapena ineyo ndine ndikukhomereredwa. Chifukwa ndikayankhula ndikumaopsezedwanao pakatundu wanga.

09/08/2025

MULI BWANJI ?

Kodi mmadziwa kumanga ndipo m***a kuimika zipupa bwinobwino?
Ngati muli ku Mzuzu , imbani manambala awa.

0999544511
0981056492
0888501594
0998793030

Akufuna anthu angapo ndithu. Ndipo mmodzi wawo ndinuyo.

Ngati mukufuna ntchito yamnyumba, muli ndi zaka za mma40, ndipo muli mu Lilongwe. Mmadziwa kuphika zamakono , lembani uthenga ku 0999746398 / 0991197635
Malipiro Anu mukachita kuwatchula nokha kuti mukufuna zingati, komano mukayetsedwa matsiku awiri, abwana akaone kuti ukadaulo wanu ngotani. Kaonetseni LUSO kumeneko, Zabwino zonse.

07/08/2025

Mwadzuka bwanji?

Tsiku lina ndinakwera minibus pamene ndimachoka mu Kasungu nkumalowera mu boma la Mzimba. Mu minibus mo, ndinakumanizanamo ndi mnyamata ndi mtsikana amene amaoneka otchena bwino ndithu moti ndinawafunsa komwe akupita komano onse anangoti duu osandiyankha. Anali bize pa foni, ndiye momo munali madala ena analinso ndi mwana wawo wa ku primary school , ndiye nawo anafunsa kuti Kodi mesa akuluwa akufunsani funso ana Inu?

Pomva funso ili, Mnyamata yo anangofikira kuyankha madala aja kuti
" Ndimadana ndi mafunso opusa".

Tonse tinangoti chete, popedza ineyo mmtima ndimaziwa kuti tili mu galimoto ya anthu akuba. Mtima umandiudza ndithu kuti minibus iyi sili bwino ndiye ndimafuna ndiwauze kuti tonse tisasiyane tikasikire pamene ineyo ndizikasika.

Nditafika Malo amene ndimayenera kusiya , ndinamuuza driver kuti ineyo ndi madala wo, ndi mwanayo tisikira pano. Ndinapereka sign Kwa madala aja kuti tisike. Sanachedwe anasikamo. Tonse titasika, madala aja adandiuzanso kuti ineyo mtima umandiudza kuti lero nditha kuphedwa , minibus ija sili bwino.

Tikukambirana izi , tinangoona, minibus ija ikusiya tala nkumalowa mmsewu wafumbi umene unali patsogolo kwambiri. Madalawo adati , Inu tiimbe kupolisi. Minibus ija sili bwino. Mwatsoka lanji sitinapeze number yoti tingaimbe. Ndiye tinangoimitsa wa tax , kuti tiisatire minibus ija. Titaimitsa , titayamba kuyenda tinamuuza kuti tilowe pa njira imene padalowera minibus ija, eh anakana akuti kumeneko ine ayi, ndinu achifwamba eti? Basi mmtima tinangoziwa kuti ana aja apangidwa chipongwe , tili mkati mwa makambirano tidangolimba mtima nkuyamba kulowako, titayenda Kwa 5 minutes, tinaona ana aja akuyenda wapansi komano mtsikana akulira amabwerera mu mmsewu watala. Titawafunsa adatifotokozera kuti aberedwa mafoni, laptop ndi ndalama nkumenyedwa. Mwayi adangowasiya kuti azipita.

Ndiye mnyamata yo andifunsa amvekere " So apapa titani?" Misozi ikuseseleka ndithu.

Kuchokera pompo ndinaziwa kuti tikakhala gulu tisamakule mtima kwenikweni, pena magalimoto timakwerawa amatha kutichitanso chipongwe. Komano anyamata athu amene muli pabwalo pano, sibwino kunyoza achikulire.

31/07/2025

Mwadzuka bwanji?

Lero tiyamba kuika nkhani komano bwanji tiyambe motere?

Kwa amene amakwanitsa kumeta mwina anagwirapo ntchito mu babashop, imbani 0991607909, kuli ganyu ku Mzuzu , barbershop yake ili ku sosbeline.

Kodi munakonde kumagulitsa zovala mu Blantyre? Lembani Email Kwa Abwana awa akufuna mnyamata kapena mtsikana woti azigulitsa zovala za mubelo, zina zosokedwa ndi telala ( [email protected])

Ngati ndinu telala, ayankhuleni abwana awa pa Email [email protected] akufuna atelala atatu , mmodzi mu Lilongwe awiri mu Blantyre.

Ntchito izo , sizikufunikira mapepala akusukulu, LUSO BASI

26/05/2025

Tapanga graduation

Panopa basi tabwereranso pabwalo pano.

MUKHALE NDI USIKU WOPAMBANA

Mawa Bwalo liyamba kumva nkhani zosiyanasiyana

Address

Lilongwe
MALAWIBASI

Website

Alerts

Be the first to know and let us send you an email when Mfumu Solomo - Pabwalo posts news and promotions. Your email address will not be used for any other purpose, and you can unsubscribe at any time.

Contact The Business

Send a message to Mfumu Solomo - Pabwalo:

Share