Mfumu Solomo - Pabwalo

Mfumu Solomo - Pabwalo Pabwalo ili pamaikidwa zinthu zosiyanasiyana monga malo achilendo, zachilengedwe komanso nkhani zosi

09/06/2026

MUKHALE NDI USIKU WOPAMBANA

22/05/2026

Pa ana 100 muno mu Malawi , mwana mmodzi amakhala pa chiopsezo chozebetsedwa ndikukagulitsidwa mmayiko akunja.
Ndipo Chaka chatha pa ana 100 mwana mmodzi adasowa, nkupedzeka kuti wagulisidwa ku dziko lina.

Mwachitsanzo, Mu Lilongwe ndi Blantyre muli timabungwe tambiri tomwe timati tikufuna kumathandidza ana amasiye ndi ana amene makolo awo sakukwanitsa kupereka zofunika za umoyo wa tsiku ndi tsiku. Ana amenewa amakakhala kosungira ana a masiye, kumene amaikidwako kumabwera azungu amene amanamiza anthu kuti akudzawatenga anawa azikakhala nawo kunja ngati ana awoawo. Boma limatha kupusisidwa kumene chifukwa cha ziphuphu zimene zafalazi, mwatsoka ilo Chaka chatha ana angapo amakwera mabasi , n'kumapita kunja , anthu osaziwa kuti akubedwa , kumangoti ali mmanja mwa azungu.

Nthawi zina anzathunso akunjawa kumasamala nawo akamayandikira ana. Si onse komano ena ndi akuba.

Ena amabwera mu dzina la mipingo, amati ndi azungu akunja akufuna kutenga atumiki kuno ku MALAWI azikatimikira kunja. Womwewo .... Usabwereranso.

Komano Kodi anthu amene agulitsidwa mmayiko ena , ZIMAWATHERA BWANJI??

20/05/2026

Lero ndinafasa kuona ma message amene ndinkalandira zaka ziwiri zadutsazi, ndipo ndimaonanso ma message amene akubwera mu week inoyi.
Ndazindikira zinthu izi.

1. Pa Malawi pano mchitidwe ozembetsana ukuchulukirachulukirabe. Mayiko monga OmaN/ OMANI ndi Dubai mmmm penapake kuli nkhaza zazikulu. Amene mukupedza ntchito kunja, onanani Kaye ndi aboma kaya ndi a labour musananyamuke, anthu kunjaku ali paukapolo. Ndi ochepa chabe amene akufikira pachinyezi.
Dubai iyi ndi yabwino zedi komano chenjerani. Osaiwala kupewa kwambiri ntchito zina mu dziko la OMAN/ OmaNI

2. Ntchito pa Malawi pano zikusowa komano akubaso achuluka. Ambiri aberedwa mu dzina losakantchito

3. Matenda otupa Masaya / khansa akunka naononga miyoyo ya anthu

4. Mabanja panopa akusowa chifukwa cha kusowa kwa makobidi.

Ndangoyankhula mwachidule, komano zonse ndifotokoza mwatsatanetsatane

23/01/2026

CHIBVOMEREZI ! !

Chaka chino zikuonetsa kuti tayamba ndi zibvomerezi.

Kale tikamaona izi zikuchitika kumayambiliro kwa Chaka anthu amakhulupirira kuti mizimu yakwiya. Ndipo ku Ghana anthu amati Mlungu wa mkazi dzina lake ASASE YAA wapsa mtima ndipo akuyankhula kudzera mu chibvomerezi

Pamene anzathu aku Kenya amati ENKAI ( Mulungu) akuchenjeza anthu za chilala choopsa chimene chichitike, njala ndi kuzuzidwa komwe kubwere kamba ka ziwawa zomwe zichitike mu dzikomo.

Chimozimozinso ku Nigeria , ababalawo kapena kuti ansembe amapemphedwa kuti apemphe kwa mlungu wawo ILE kuti asabweretse tsoka.

MATSIKU AZANA ZINALI MOTERO

16/01/2026

ZIKOMO KWA ONSE AMENE ANATENGAPO MBALI KUTCHULA ZOMWE ZIMAFUNIKIRA KUTI MUNTHU AKHALE NDI BABASHOPU

Lero ndagula katundu yense amene anatchulidwa ndipo wina tinangopitanso pa babashopu Ina kukaonaonapo zoti TIONJEZERE kwangotsala kuti tigule poti tilembepo chikwangwani.

ZIKOMO KWAMBIRI

15/01/2026

NDAKUMANA NDI MNYAMATA amene ndikufuna kuti aziimire payekha mokhala ndi Babashopu

komano funso ndi loti

KODI NDITHA KUMUGULIRA ZINTHU ZITI ZOFUNIKA KWAMBIRI?

iye akuziwapo, machine ometera, mwala onolera Mano a machine, makatani, ma extension.......

ZINA ZITHA KUKHALA ZITI?

Address

Lilongwe
MALAWIBASI

Website

Alerts

Be the first to know and let us send you an email when Mfumu Solomo - Pabwalo posts news and promotions. Your email address will not be used for any other purpose, and you can unsubscribe at any time.

Contact The Business

Send a message to Mfumu Solomo - Pabwalo:

Shortcuts

Share