PBW Online Tv

PBW Online Tv Your trusted source of news and information. PBWtv.

We offer:
-News and Current Affairs
-Music shows and entertainment
-Live streaming of different engagements
-Advert and HD Photos

Located in Lilongwe off-Kachere Road
Contact 0994656612/ 099946342.

  #Timu ya mpira wa miyendo ya Nyasa Big Bullets yaimitsa mkulu wa ochemelera a Stone Mwamadi.Nyasa bullets yachita izi ...
11/10/2025

#

Timu ya mpira wa miyendo ya Nyasa Big Bullets yaimitsa mkulu wa ochemelera a Stone Mwamadi.

Nyasa bullets yachita izi potsatira ma lipoti akukhudzidwa kwa a Mwamadi pa nkhani yomwe ikufufuzidwa ndi apolisi.

Timuyi yati yaimitsa a Mwamadi pofuna kupereka mpata kuti kafuku fuku ayenda bwino komaso pofuna kuteteza mbiri ya timuyi.

Timu ya Bullets yati yasankha Chingeni Gumbala Kadammanja kukhala mkulu wa ochemelera.

Blessings Chikoti.
Pbwtv Lilongwe.

  #Gulu la Youth Alive Mchinji, lapempha apolisi komaso asilikali kuti afufuze zakuonongedwa kwa ku nyumba ya chimfumu (...
11/10/2025

#

Gulu la Youth Alive Mchinji, lapempha apolisi komaso asilikali kuti afufuze zakuonongedwa kwa ku nyumba ya chimfumu (State House) ku Lilongwe.

Gululi lati apolisi akhazikitse ntchito yofufuza ndipo wopeza alandire chilango.

Malinga ndi kalata yomwe gululi latulutsa, yati pa masamba a chenzo pali zithunzi zomwe zikuonetsa kuonongedwa kwa ku nyumba ya chifumu.

Gululi lati nyumbayi iyenderedwe asanabwera mtsogoleri wa dziko lino a Prof. Peter Mutharika kudzakhala.

Youth Alive Mchinji ikudzudzulanso mchitidwe woopseza atolankhani womwe a ndale ena akuchita m'dziko muno

Gululi lati pali ma lipoti oti akulu akulu a ulamuliro wapita wa MCP, akuopseza mtolankhani wa kampani ya Times Group, Cathy Maulidi.

"Tikudzudzula mchtidwe woopseza olemba nkhani kuti uthe ndipo tikupempha apolisi kuti amange onse opezeka akuchita izi.

PBW Online Tv .
Kanema yanu yanu.

11/10/2025

#

Gulu lotchedwa "Youth Alive Mchinji", lati ndilokhumudwa ndi zithunzi zomwe zikuyenda pa masamba achenzo zoonetsa kuonongedwa kwa ku nyumba ya chimfumu (State House) ku Lilongwe.

Blessings Chikoti
Pbwtv Lilongwe.

11/10/2025

Wa luso wanga ndi program yomwe Pbwtv imakupatsirani akatswiri a maluso osiyana siyana mdziko mino.

Kodi ndinu wa luso ndipo mukufuna anthu adziwe za luso lanu? Uwu ndi mwayi wazama wofukula ndi manja.

Tipezeni ife, a Pbwtv ku Lilongwe.

PBW Online Tv,
Kanema yanu yanu.

Mpingo wa Christ-Citadel International, uchita mapemphero othokoza Mulungu komaso kusangalala kuti wachiwiri wa mtsogole...
11/10/2025

Mpingo wa Christ-Citadel International, uchita mapemphero othokoza Mulungu komaso kusangalala kuti wachiwiri wa mtsogoleri wa dziko lino Dr Jane Ansa SC, akwanitsa zaka 70.

Mpingowu uchita izi loweruka pa 11 October ku likuli la mpingowu ku Area 47 mu mzinda wa Lilongwe.

Chikondwelerochi ndi njira imodzi yokumbukira zabwino zomwe Dr Ansa amachita ku mpingowu komaso ku dziko la Malawi.

Zochitikazi ziyamba nthawi ya 1:00 koloko masana.

Blessings Chikoti.
Pbwtv Lilongwe.

mai justice Dr Jane ansah sc omwe ndi vice president wa dziko lino anabadwa lero pa 11 October 1955 pa chipatara Cha Nkh...
11/10/2025

mai justice Dr Jane ansah sc omwe ndi vice president wa dziko lino anabadwa lero pa 11 October 1955 pa chipatara Cha Nkhoma mission hospital ku Lilongwe. happy birthday kwa inu a vice president athu 🎉🎉🎉🎉🎉

Unduna wa maphunziro a Primary komaso Secondary wadzudzula m'chitidwe wakuba zipangizo zophunzirira za makono (Digital L...
11/10/2025

Unduna wa maphunziro a Primary komaso Secondary wadzudzula m'chitidwe wakuba zipangizo zophunzirira za makono (Digital Learning Tablets) womwe wakula m'dziko muno.

Undunawu wanena izi pomwe zipangizo zokwana 57 zabedwa pa sukulu ya Secondary ya Kasolo m'boma la Kasungu lachinai sabata ino.

Unduna maphunzirowu wati m'chitidwewu umabwezeretsa ntchito m'mbuyo ntchito yopereka maphunziro apamwamba m'dziko muno.

Mneneli wa mu undunawu, a Christopher Kapachika Banda, atsimikiza za nkhaniyi ndipo ati izi zachitika m'mawa wa lachinai pa 9 October.

A Banda ati nkhani ngati yomweyi idachitikaso pa sukulu ya Secondary ya Chankhanga m'boma lomweli pomwe ma kompiyuta 5, ma iPad 6 mwa zina zinabedwa.

Iwo nkhani zonse zili m'manja mwa apolisi ndipo ntchito yofufuza katunduyu ili mkati.

Blessings Chikoti.
Pbwtv Lilongwe.

Mtsogoleri wa dziko lino, Prof Peter Mutharika, wati athana ndi anthu onse omwe ali ndi maganizo komaso malingaliro ochi...
10/10/2025

Mtsogoleri wa dziko lino, Prof Peter Mutharika, wati athana ndi anthu onse omwe ali ndi maganizo komaso malingaliro ochititsa ziwonetsero zotsutsana ndi ulamuliro wake m'dziko muno.

A Mutharika ati pali anthu omwe akufua kuti azichita izi pofuna kutsutsa ndi ulamuliro wawo m'dziko muno.

Mtsogoleriyu wanena izi lachisanu pa ulendo wake wochoka ku Balantyre kupita ku nyumba yake m'boma la Mangochi.

"Sindisekelera anthu omwe akufuna kuwononga dziko lino kudzera muziwonetsero", Anatero mtsogoleriyu.

Blessings Chikoti.
PBW Online Tv Lilongwe.

10/10/2025

Mkulu wa nyumba yowulutsa mawu ya boma ya Malawi Broadcasting Cooperation (MBC) a George Kasakula ati akupempha mtsogoleri wa dziko a Prof. Peter Mutharika komaso chipani chonse cha DPP kuti awakhululukire.

A Kasakula akhala akunyoza a Peter Mutharika, mu nthawi ya misonkhano yokopa anthu mu program ya pa kanema yotchedwa Timvetse.

Blessings Chikoti.
PBW Online Tv Lilongwe.

Malawi commemorated the  2025, International Day for Universal Access to Information (IDUAI) under theme; Empowering Com...
10/10/2025

Malawi commemorated the 2025, International Day for Universal Access to Information (IDUAI) under theme; Empowering Communities through Digital Literacy: Access to Information.

The event took place at Katoto Stadium in Mzuzu, provided a platform to raise awareness on the roles of Universal Access to Information and Digital Literacy in promoting human rights.

Blessings Chikoti.
Pbwtv Lilongwe.

Unduna wa maphunziro m'dziko muno ukudziwitsa aphunzitsi, ophunzira komanso makolo kuti chaka cha maphunziro cha 2025/26...
10/10/2025

Unduna wa maphunziro m'dziko muno ukudziwitsa aphunzitsi, ophunzira komanso makolo kuti chaka cha maphunziro cha 2025/26 chidayamba pa 22 September ndipo chidzatha pa 24 July 2026.

Undawu wati chakachi chili ndi masabata ophunzira okwana 40.

Iwo wati kalendala ya maphunziroyi ikugwira ntchito kwa aliyese ndipo wati pasapeze wina wachita zosiyana ndi zomwe kalendala-yi ikunena.

Blessings Chikoti.
Pbwtv Lilongwe.

Nyumba ya malamulo m'dziko muno ikudziwitsa aphungu onse omwe asankhidwa pa chisankho cha pa 16 September kuti mwambo wo...
10/10/2025

Nyumba ya malamulo m'dziko muno ikudziwitsa aphungu onse omwe asankhidwa pa chisankho cha pa 16 September kuti mwambo wolumbira komaso maphunziro a ntchito yawo zidzachitika kuyambira pa 20 mpaka 28 October ku Bingu International Convention Centre (BICC), mu mzinda wa Lilongwe.

Maphunzirowa adzachitika lolemba 20 mpaka lachisanu pa 24 October pa mutu woti ; "Kuchoka ku chisankho kupita ku ntchito, kulimbikitsa aphungu kukhala atsogoleri abwino".

Maphunzirowa adzathandiza aphunguwa kukhala ndi luso komaso kulimbikitsa kudziwa malamulo.

Pambuyo pa maphunzirowa, aphungu adzalumbira mu chamber ya nyumba ya malamulo lolemba pa 27 mpaka lachiwiri pa 28 October.

Aphungu akuyenera kuti afike ku Lilongwe pa 17 October kuti alembetse maina awo ndipo akupemphedwa kubweretsa ziphaso zawo za unzika komaso zitupa (certificate) za maphunziro awo.

Blessings Chikoti.
Pbwtv Lilongwe.

Address

56
Lilongwe

Telephone

+265994924588

Website

Alerts

Be the first to know and let us send you an email when PBW Online Tv posts news and promotions. Your email address will not be used for any other purpose, and you can unsubscribe at any time.

Contact The Business

Send a message to PBW Online Tv:

Share

Category