PBW Online Tv

PBW Online Tv Your trusted source of news and information. PBWtv.

We offer:
-News and Current Affairs
-Music shows and entertainment
-Live streaming of different engagements
-Advert and HD Photos

Located in Lilongwe off-Kachere Road
Contact 0994656612/ 099946342.

21/07/2025

wa chisankho #

M'tsogoleri wa chipani cha UTM a Dr Dalitso Kabambe wati nkhani ya njala, kusowa kwa ntchito pakati pa achinyamata, mavuto a zachuma ndinso kukwera mtengo kwa katundu udzakhala mbiri chabe chipani chake chikalowa m'boma chaka chino.

M'tsogoleriyu wanena izi lolemba la pa 21July m'boma la Dedza pa msonkhano wokopa anthu omwe umachitikira pa bwalo la sukulu ya Umbwi m'bomalo.

A Kabambe ati mavuto osiyanasiyana omwe dziko lino likukomana nawowa adzakhala nthano anthu akadzamuvotera kukhala mtsogoleri wa dziko lino pa chisankho cha pa 16 September.

"Mukuyenera kuponya voti yanu mwanzeru ngati mwatopa ndi mavuto omwe tikukomana nawo mdziko muno posankha chipani cha UTM chomwe chithandize kusintha zinthu mdziko muno kuti ziyambe kuyendaso ngati kale" iwo anatero.

Annie Phiri
PBWtv Lilongwe.
21/07/2025.

  #President Dr Lazarus Chakwera has delegated the Vice President Dr Michael Usi, to represent Malawi nation at the 15th...
21/07/2025

#

President Dr Lazarus Chakwera has delegated the Vice President Dr Michael Usi, to represent Malawi nation at the 15th Meeting of the Conference of the Contracting Parties to the Ramsar Convention on wetlands.

The conference will be held in Victoria Falls, Republic of Zimbabwe on 24th July 2025 under the theme; "Protecting wetlands for our common future".

The conference will strengthen international commitments for wetlands conservation and facilitate crucial discussions on the conservation and sustainable use of Wetlands, serving as a global platform for advancing wetland conservation practices that protect vital ecosystem and their benefits.

Dr Usi will depart Kamuzu International Airport on Tuesday 22nd July 2025 at 10:00am and return on Friday 25th July at 15:00 through the same Airport.

Blessings Chikoti
PBWtv Lilongwe.
21/07/2025.

21/07/2025

wa chisankho #

Wachiwiri kwa mtsogoleri wa dziko lino yemweso ndi mtsogoleri wa chipani cha Odya Zake Alibe Mulandu, a Dr Michael Usi ati manifesto atsogoleri onse amakhala abwino komaso othandiza dziko lino.

Dr Usi ati mfundo zonse zomwe atsogoleri amapereka kwa anthu awo zimakhala zabwino koma vuto limakhala ogwira ntchito m'boma.

Mtsogoleriyu wati ogwira ntchito m'boma ndi omwe amaononga manifesto-wa.

Dr Usi ati manifesto awo adzanathana ndi anthu onse ogwira ntchito m'boma omwe amapendereza manifesto atsogoleri.

Mtsogoleriyu wanena izi lolemba pa msonkhano wandale womwe amachititsa kwa Kauma mu mzinda wa Lilongwe.

Blessings Chikoti.
PBWtv Lilongwe.
21/07/2025.

  wa chisankho  #Mtsogoleri wakale wa dziko lino yemweso ndi mtsogoleri wa chipani cha People's Dr Joyce Banda ati akalo...
21/07/2025

wa chisankho #

Mtsogoleri wakale wa dziko lino yemweso ndi mtsogoleri wa chipani cha People's Dr Joyce Banda ati akalowa m'boma pa 16 September adzakhazikitsa ntchito ya MASAF.

Dr Banda ati adzakhazikitsa ndondomeko ya cash for work yomwe anthu azidzagwira ntchito ngati kukonza msewu ndikulandira ndalama.

Iwo anena zimenezi lolemba ku Lilongwe pamene amakhazikitsa mfundo za chipani chawo (manifesto).

Mtsogoleriyu watiso adzakonza chuma cha dziko lino poonetsetsa kuti mitengo ya katundu pa msika ili bwino kuti anthu apeza phindu pa katundu wawo.

Blessings Chikoti.
PBWtv Lilongwe
21/07/2025.

21/07/2025

wa chisankho #

Khansala wa chipani cha Malawi Congress Party (MCP) ku dera la Mbizi ku Lilongwe, a Jeremiah James Nkhoma ati nthawi yakwana yoti dera la mbizi litukuke.

A Jeremiah ati adasankhidwa ngati khansala pa 16 September adzaonetestsa kuti anthu ku derali akulandira zonse zomwe boma lakonza.

Iwo ati sadalowe ndale ndi cholinga chofuna kukhutitsa mimba ngati momwe ena amachitira koma kutumikira anthu popeza ali ndi zochita zawo zambiri.

"Ndidzaonetsetsa kuti kalikonse komwe boma lakonza anthu anga akufikilidwa", Iwo anatero.

Khansalayu wati anthu kuderali asachedwe ndi otsogoleri omwe sangawathandize koma avotere Dr Lazarus Chakwera ngati mtsogoleri wa dziko komaso Jeremiah Nkhoma ngati khansala wawo.

Blessings Chikoti
PBWtv Lilongwe
21/07/2025.

19/07/2025

wa chisankho #

Khansala yemwe akufuna kuyimira Ward ya Likuni, a Dishen Chitete ati ngakhale a Bridget Chaponda abwera mochedwa ngati phungu ku derali ndiyekhayo amene ali mpulumutsi wa anthu a ku Kamphuno.

A Chitete ayankhula izi loweruka pa sukulu ya Likuni Girls m'dera la Kamphuno pamene phungu wa chipani cha Odya Zake Alibe Bridget Chaponda amakagogoda kwa mafumu a derali.

Khansalayu wati dera lawo lili ndi mavuto ochuluka omwe akufunika kukonzedwa ndi phungu.

Iwo anati anthu a derali akufuna chipatala cha boma komaso ma dera ena ambiri alibe magetsi.

"Wolemekeza kwathu kuno tili ndi mavuto a chipatala, msewu wabwino komaso madera ambiri alibe magetsi, choncho tifuna mukalowa m'boma tidzatikonzere,"Iwo anatero.

A Chitete anati ali wokonzeka kugwira ntchito zotukula dera la Kamphuno limodzi phungu wawo a Bridget Chaponda.

Blessings Chikoti.
PBWtv Lilongwe
19/07/2025.
Kanema Yanu Yanu.

"Mupange chisankho choyenera", Bridget Chaponda.Phungu wa chipani cha Odya Zake wa dera la Kamphuno mu mzinda Lilongwe, ...
19/07/2025

"Mupange chisankho choyenera", Bridget Chaponda.

Phungu wa chipani cha Odya Zake wa dera la Kamphuno mu mzinda Lilongwe, mai Bridget Chaponda ati anthu ku derali akavote mwanzeru.

Phunguyu wati anthu ambiri abwera kudzapempha mavoti kwa anthu koma avotere phungu wa maso mphwenya ngati iwo.

A Chaponda anena izi loweruka pa 19 July, ku Likuni pamene amakayendera mafumu a derali.

Phunguyu wati iye ali ndi maso mphenya otukula derali ndi cholinga choti anthu akhale ndi moyo wabwino.

"Ine ndidzamanga malo omwe achinyamata ndi amayi azikaphunzira maluso osiyana siyana.

Ndidzabweretsa chipatala cha boma choyang'anira uchembere wa azimai ku dera lino.

Msewu wa Likuni- Malingunde ndidzakonza pofuna kuthandiza ntchito za malonda kuno", anatero phunguyu.

A Chaponda ati anthu pa 16 September adzawavotere popeza ali ndi kuthekera kotukula dera lawo.

Blessings Chikoti.
PBWtv Lilongwe
19/07/2025.
Kanema Yanu Yanu.

Apolisi m'boma la Dowa amanga a Pemphero Puleti azaka 24 zakubadwa powaganizira kuti akukhudzidwa pa imfa ya yemwe anali...
19/07/2025

Apolisi m'boma la Dowa amanga a Pemphero Puleti azaka 24 zakubadwa powaganizira kuti akukhudzidwa pa imfa ya yemwe anali msilikali wa Malawi Defence Force a Chiswansangu Nyirongo.

Malingana ndi ofalitsa nkhani ku polisi ya Dowa a Alice Sitima ati, a Puleti akuwaganizira kuti ndi omwe anapita ku nyumba kwa malemuwa pakati pa usiku kukawachita chiwembu powabaya pa mimba ndi Chitsulo kenako ndikuthawa.

Izi ndi zomwe apolisi ya Dowa apeza malingana ndi kafukufuku yemwe apolisiwa anachita.

A Chiswansangu Nyirongo omwe anachitidwa chiwembuchi amachokera m'boma lomweli la Dowa m'mudzi wa Kalazi mfumu yayikulu Chiwere ndipo amagwira ntchito ku Mvera Support Battalion.

Annie Phiri.
PBWtv Lilongwe
19/07/2025.

18/07/2025

wa Ku chisankho Chaponda shadow -MP- Kamphuno Constituency Zake Alibe Mulandu #

18/07/2025

Phungu wa Odya Zake Alibe Mulandu yemwe akufuna kuimira dera la Kamphuno, a Bridget Chaponda, ati mtsogoleri wa chipanichi, a Michael Usi ndi munthu wachifundo.

Phunguyu wati nayenso watengera mzimu womwewo wachifundo wothandiza pofuna kutukula miyoyo ya anthu a dera lake

A Chaponda ati akapambana adzapamanga chipatala cha boma choti amayi oyembekera azikalandilira chithandizo.

Phunguyu wati amai ku derali amavutika kwambiri nthawi yomwe akufuna kuchira.

A Chaponda anena izi lachisanu pomwe amayendera mafumu onse a dera la Kamphuno Kwa Chinsapo mu mzinda wa Lilongwe.

"Ine ndidzamanga chipatala cha boma kuno ku dera la Kamphuno, amai akuvutika ndi ma bilu ku chipatala cha mission cha Likuni", Iye anatero.

Blessings Chikoti.
Pbwtv Lilongwe
18/07/2025.

18/07/2025

zake alibe mulandu #

Khansala yemwe akufuna kuimira dera la Kamphuno pansi pa chipani cha, Odya Zake Alibe Mulandu, a Louis Chiphukusi ati ali ndi malingaliro oti azidzalipilira ana a sukulu ndalama yachitukuko.

A Chiphukusi ati ndi zomvetsa chisoni kuti ana ambiri akulephera kulemba mayeso kaamba kosowa ndalama ya chitukuko.

Khansalayu wanena izi lachisanu pamene yemwe akufuna kuimira ngati phungu ku derali, a Bridget Chaponda, amakumana ndi mafumu onse a dera la Kamphuno.

A Chiphukusi ati pali zambiri zomwe iwo akufuna kuchitira dera la Kamphuno.

"Misewu yomwe ili ndi mavuto ndikonza, choncho ndikupempha sapoti yanu mafumu," Iwo anatero.

Blessings Chikoti.
Pbwtv Lilongwe.
18/07/2025.

17/07/2025

nkhani #

Yemwe akuima ngati phungu woyima payekha Ku dera la Bwaila, a Henry Muyaya, ali nawo pa mwambo wosankha komiti ya chitukuko ya dera la Chipwaira (VDC) kwa Chinsapo mu mzinda Lilongwe.

A Muyaya alandiridwa ndi mafumu ozungulira dera la Chipwaira.

Oyimira zipani komaso mabungwe osiyana siyana abwera kudzachitira umboni pa mwambo wosankha komitiyi.

Kubwera kwa komiti ya chitukukoyi kuthandiza kufufuza mavuto omwe derali limakumana nawo.

Address

Lilongwe

Telephone

+265994924588

Website

Alerts

Be the first to know and let us send you an email when PBW Online Tv posts news and promotions. Your email address will not be used for any other purpose, and you can unsubscribe at any time.

Contact The Business

Send a message to PBW Online Tv:

Share