
14/07/2025
Wapampando wa bungwe loyendetsa chisankho la Malawi Electoral Commission MEC Justice Dr Anabel Mtalimanja wapempha atsogoleri azipani kuti achite ntchito yokopa anthu nyengo imeneyi mwaukadaulo popewa kuphwanya malamulo a zisankho.
Malingana ndi a Mtalimanja, andale asaiwale kuti Malawi ndi m'modzi choncho pakufunika kupewa mchitidwe waziwawa kamba kakuti uli ndikuthekera kosokoneza ungwiro wa dziko lino.
Amtalimanja afotokoza izi lolemba mu nzinda wa Lilongwe pa mwambo otsegulira nyengo yokopa anthu pokozekera chisankho cha pa 16 September pano.
Mwazina wa pampando wa bungwe la MEC yi wati a Malawi atopa ndi mau onyozana opanda mfundo omwe andale ena amalankhula koma kuti akuyembekezela mfudo zothyakuka mu nthawiyi.
Wolemba: Joseph Chibade.