
24/09/2025
Mt'sogeleri wa Democratic Progressive Party-DPP Professor Arthur Peter Mutharika ndi wachiwiri wawo Dr Jane Ansah ndi omwe apamba pachisankho cha pa 16 September 2025.
Malingana ndi nkulu wa bungwe la Malawi Electoral Commission-MEC Justice Annabel Mtalimanja walengeza kuti a Professor Muntharika apambana ndi mavoti 3,035,244 Miliyoni (56.8%) pamene yemwe anali tsogoleri wakale wadziko lino komaso wa Malawi Congress party-MCP Dr. Lazarus Chakwera apeza mavoti 1,765,170 Miliyoni (33.0%).
Professor Arthur Peter Muntharika angonjetsa atsogoleri 16 azipani zina komaso oyima pawokha omwe anatenga nawo mbari pachisankhochi.
Zatelemu a Muntharika omwe anakhalaponso ngati m'tsogoleri mzaka za 2016 kufikira 2020 akuyenera kulumbiritsidwa pakatha masiku 7 owulutsa ndi kusapitilira masiku 31 owulitsira zotsatira zachisankho.
(Wolemba Thom Kamanga)