Timveni Online

Timveni Online Timveni is a child and youth media organisation, which comprises of Radio, Television & Social Media.
(3)

23/09/2025

Timu ya mpira wamanja ya dziko ya osewera osapyola zaka 21 yagonja 64-33 ndi timu ya South Africa mu mpikisano wa Netball World Youth Cup ku Gibraltar.

Izi zikutanthauza kuti zikuvutabe kuti matimu a mpira wamanja a dziko lino azigonjetsa timuyi.

Pamasewero atatu omwe aseweredwa mu gulu D, Malawi yapambana masewero awiri komanso kugonja masewero amodzi pomwe South Africa yapambana masewero atatu onse omwe yasewera.

Wolemba: Richard Tiyesi

23/09/2025




Mitima ya anthu ochita malonda m'boma la Ntcheu ili m'mwamba pamene akuyembekezera kumva zotsatira za chisankho.

A Clement Chitsokonombwe, omwe amapanga bizinezi yogulitsa nsapato, ati bizinezi sinayende bwino kweni-kweni m'sabata imeneyi kamba koti iwo akumangotanganidwa ndi kumvetsera misonkhano ya atolankhani yomwe anthu azipani zosiyana-siyana akumapangitsa.

Mayi ena omwe amagulitsa mbatatesi, a Sellina Kafansiyanji, ati akuona kuchedwa kuti alengeze yemwe wapambana pampando wa mtsogoleri wadziko kamba koti akufuna amve mtengo wa fetereza omwe ulengezedwe ndi yemwe apambane.

Iwo ati ulimi wakhala ovuta kamba kakukwera mtengo kwa fetereza.

Ndipo a James Mtileni, omwe amapanga bizinezi yopha nkhumba, ati iwo ndiokonzeka kumva zotsatira zomwe akhala akuziyembekezera kwa sabata tsopano.

Iwo amema omwe anayimira pa zisankhozi kuti avomereze zotsatira zomwe a MEC alengezetse kuti zinthu zisasokonekere m'dziko muno.

Wolemba Florida Chona

23/09/2025

2025 GENERAL ELECTIONS UPDATE

23/09/2025

2025 GENERAL ELECTIONS UPDATES

Timu ya mpira wamiyendo ya dziko lino ya asungwana osapyola zaka 20 yagonjetsa South Sudan 2-0 pamasewero ofuna kudzigul...
23/09/2025

Timu ya mpira wamiyendo ya dziko lino ya asungwana osapyola zaka 20 yagonjetsa South Sudan 2-0 pamasewero ofuna kudzigulira malo mu mpikisano wa FIFA U-20 omwe analipo lero ku Juba.

Enelesi Fabiano komanso Sarah Mlimbika anagoletsera asungwana a Maggie Chombo.

Masewero achiwiri a matimu awiriwa alipo lachisanu likudzali pa bwalo lomweli m'dziko la South Sudan.

Wolemba: Richard Tiyesi

  Chipani cha Anyamata Atsikana Azimai (AAA) chafunira zabwino mtsogoleri wa chipani cha Democratic Progressive (DPP), P...
23/09/2025




Chipani cha Anyamata Atsikana Azimai (AAA) chafunira zabwino mtsogoleri wa chipani cha Democratic Progressive (DPP), Peter Mutharika pamene akutsogola pa chisankho chomwe chinachitika pa 16 September chaka chino.

Mukalata yomwe yasainidwa ndi mtsogoleri wake, Akwame Bandawe, chipanichi chapemphanso zipani zonse zomwe zimapikisana nawo pa chisankhochi kuvomereza zotsatira za chisankhochi ndikugwirana manja ngati amodzi.

Chipani cha AAA chati apa nkhondo yangoyamba ndipo chidzapikisana nawonso pa chisankho cha 2030.

Olemba Sam Magwira

  Mtsogoleri wakale wabungwe loona za malamulo la Malawi Law Society, Patrick Mpaka, wapempha anthu kuti akhale odekha p...
23/09/2025




Mtsogoleri wakale wabungwe loona za malamulo la Malawi Law Society, Patrick Mpaka, wapempha anthu kuti akhale odekha pamene bungwe la MEC likuyembekezeka kutulutsa zotsatira za chisankho.

Mpaka wati malingana ndi malamulo, bungweli limapatsidwa masiku asanu ndi atatu (8) kuti lilengeze zotsatira zovomerezeka za mtsogoleri wadziko kotero kuti a Malawi adekhe kaamba kakuti masikuwa sadakwane.

Iye wati lamulo limalolanso bungweli kuonjezera masiku atatu kukwanitsa khumi ndi chimodzi (11) ngati pena sipadayende bwino mkati-mkati mwa masiku asanu ndi atatu (8).

Bungwe la MEC langotsala ndi tsiku limodzi lokha kuti lilengeze zotsatira zonse zotsimikizika za mtsogoleri wa dziko.

Wolemba: Comfort Braziz-Nkhoma

23/09/2025




Mkulu wa bungwe la Citizens League m'boma la Chikwawa, Francis Mazinga, wati akufuna kuti pakhale zokambirana ndi aphungu omwe angosankhidwa kumene m’bomalo kuti apitirize zitukuko zomwe zinaimira panjira.

Kudzera mu kalata yomwe Mazinga walemba pa 23 September, 2025, watsindika za kufunika kolimbikitsa kuchitira zinthu poyera ndi kukwaniritsa malonjezano a panthawi yokopa anthu.

Iye watchulapo zitukuko zina zofunika m’bomalo kuphatikizapo mseu wa Gwanda Chakuamba Highway ku East Bank, Chapananga Sidik Mia Highway, ndi chingalande cha nthilira pansi pa Shire Valley Transformation Programme (SVTP).

  Pali kuthekera kuti bungwe loyendetsa chisankho la Malawi Electoral Commission (MEC) lingathe kulengeza zotsatira za c...
23/09/2025




Pali kuthekera kuti bungwe loyendetsa chisankho la Malawi Electoral Commission (MEC) lingathe kulengeza zotsatira za chisankho cha mtsogoleri wadziko lero kutsatira chisankho chomwe dziko lino linali nacho lachiwiri sabata yatha.

Izi zikutsatira mipando ya ulemu yomwe ikuikidwa m'chipinda chomwe bungwe la MEC likulengezera zotsatira za chisankho (National Tally Center).

Mipando yomwe ikuikidwayi, simapezekamo chiyambirembireni wapampando wabungwe la MEC, Annabel Mtalimanja kulengeza zotsatira za chisankho komanso kupereka mauthenga ena kwa anthu.

Bungwe la MEC sinayankhulepo kaye pankhaniyi.

Wolemba: Johans Mumba

23/09/2025

Khalani tcheru pa Timveni Radio kuyambira pano mpaka 4 O'clock masana ndipo muli ndi mwayi opambana ticket ya Lake of Stars 🔥🔥

89.6 MHz
89.8 MHz

22/09/2025





Zotsatila zotsimikizika za chisankho za maboma okwana 24 zili chonchi pakati pa adindo atatu omwe ali m'mwamba.

1. Pro. Arthur Peter Mutharika (DPP) - 2,022,879

2. Dr. Lazarus Chakwera (MCP) - 722,577

3. Dr. Dalitso Kabambe (UTM) - 169,564

Olemba: Sam Magwira

Address

712
Lilongwe
265

Alerts

Be the first to know and let us send you an email when Timveni Online posts news and promotions. Your email address will not be used for any other purpose, and you can unsubscribe at any time.

Contact The Business

Send a message to Timveni Online:

Share