Timveni Online

Timveni Online Timveni is a child and youth media organisation, which comprises of Radio, Television & Social Media.
(8)

The government has urged District Commissioners to help raise awareness about Community Development Fund (CDF) dashboard...
10/08/2026

The government has urged District Commissioners to help raise awareness about Community Development Fund (CDF) dashboards in their respective councils.

Public Relations Officer in the Ministry of Local Government, Chimwemwe Njoloma, said this will help citizens become aware of what is happening in their communities.

The government launched the CDF Dashboard to strengthen transparency, accountability and real-time monitoring of development projects across all 36 local authorities.

Reported by Sam Magwira

Thupi la malemu Brian Banda, yemwe anali mkulu wa Malawi Broadcasting Corporation (MBC),  lalowa m'manda lero m'mudzi mw...
10/08/2026

Thupi la malemu Brian Banda, yemwe anali mkulu wa Malawi Broadcasting Corporation (MBC), lalowa m'manda lero m'mudzi mwa M'banda ku Blantyre.

Anthu osiyana-siyana ayamikira katswiriyu ponena kuti anagwira ntchito yotamandika pa ntchito yowulutsa mawu m'dziko muno.

Mlembi wa boma, Justin Saidi, wati mtsogoleri wa dziko lino amamukonda Banda chifukwa cha ntchito zake.

Banda wamwalira loweruka ku chipatala cha Mwaiwathu ku Blantyre.

Iye wamwalira ali ndi zaka 46 ndipo wasiya mkazi ndi ana asanu ndi m'modzi.

Wolemba: Phillimon Backson

Anthu anayi apambana ndalama zokwana K2.4 million mu mpikisano wa Male Powerball  omwe kampani yochita masewero amuloser...
10/08/2026

Anthu anayi apambana ndalama zokwana K2.4 million mu mpikisano wa Male Powerball omwe kampani yochita masewero amulosera ya Zonse Lotto ikuchititsa.

Martha Kambewa wa ku Lilongwe yemwe ndi m'modzi mwa anthu omwe achita mphumi wati agwiritsa ntchito ndalamazi kukulitsa bizinesi yake.

Enanso omwe achita mphumi atagwiritsa ntchito ndalama zoyambira K1,000 ndi monga Sadick Ibrahim, Madalo Chikavumba komanso Samuel Rodrick.

Kampaniyi yaperekanso K1 million kwa Nelson Mpinganjira atachita mphumi pamayere a Raffle omwe amachititsa loweruka lililonse.

Wolemba: Richard Tiyesi

10/08/2026

Mfumu ya Nzinda wa Blantyre, Isaac Jomo Osman, yati ikulira limodzi ndi akubanja la Brian Banda komanso a Malawi onse.

Polankhula kudzera pa tsamba la Facebook kuchokera m'dziko la Morroco, Jomo wati chisangalalo chake kutsatira kupambana kwa timu ya mpira wa miyendo ya atsikana, Scorchers usiku wa lamulungu sichinali monga mwamasiku onse kamba koti anali okhudzidwa ndi infa ya Banda.

Iye wati akanakonda akanakhala nawo pa mwambo otsazikana ndi Banda, koma poti ali kutali kunali kovuta kutero.

Banda, yemwe wamwalira ali ndi zaka 46, walowa m'manda lero m'mudzi wa M'banda ku Chileka m'boma la Blantyre.

Wolemba Sam Magwira

Police in Nkhata Bay have arrested four people in connection with the murder of Emmanuel Kanyinji, of Chavula Village, T...
10/08/2026

Police in Nkhata Bay have arrested four people in connection with the murder of Emmanuel Kanyinji, of Chavula Village, Traditional Authority Fukamapiri in the district.

According to the Nkhata Bay Police Publicist, Sergeant Devoter Mithi, the suspects are Ackim Phiri, 66, Boston Kanyinji, 60, Sindani Kanyinji, 27, and Charles Kanyinji, 26, all from Chavula Village, Traditional Authority Fukamapiri in Nkhata Bay District.

Mithi said they have also recovered a muzzle-loading rifle believed to have been used in the murder, which is reported to have occurred during the night of 8 August, 2026, at the deceased's home in Chavula Village.

"The deceased and his wife were in an open kitchen chatting. The wife heard a gunshot and noticed that her husband had sustained gunshot wounds to the chest and was bleeding," said Mithi.

A postmortem examination established that the cause of death was severe blood loss due to trauma.

Reported by Maureen Moffat

10/08/2026

Wapampando wa nyumba yofalitsa mawu ya Malawi Broadcasting Corporation (MBC), Ben Tembo, wati Brian Banda anali mtsogoleri wachitsanzo chabwino yemwe anali wodzipereka pa ntchito yake komanso ankafunitsitsa kusintha maganizo a anthu ndi kuwalimbikitsa kukhala ndi maganizo abwino pa moyo komanso pa nkhani za dziko.

Tembo wati kudzipereka kwa Banda pa ntchitoyi kudzapangitsa kuti anthu adzamukumbukire kwa nthawi yaitali.

Wolemba: Japhet Kang'ombe

M'modzi mwa  ana a malemu Brian Banda, Hope, wati ndikovuta kukhala wolimba mtima pa imfa ya bambo ake popeza anali mzat...
10/08/2026

M'modzi mwa ana a malemu Brian Banda, Hope, wati ndikovuta kukhala wolimba mtima pa imfa ya bambo ake popeza anali mzati wawo.

Hope wati bambo ake anali wodalirika ndi atsogoleri a dziko lino.

Wolemba Phillimon Backson

10/08/2026

Wapampando wa bungwe la Media Institute of Sourthen Africa-MISA Malawi Chapter, Felix Washon, wapempha atolankhani m'dziko muno kuti atengere chitsanzo cha Brian Banda.

Washon wayankhula izi lero pa mwambo wa maliro a malemu Banda omwe ukuchitikira ku Chileka m'boma la Blantyre.

Komabe, Washon wati ndi zomvetsa chisoni kwambiri kuti Banda wamwalira ali wachichepere.

Wolemba: Phillimon Backson

Chisoni chakuta mudzi wa M'banda ku Chileka, m'boma la Blantyre pamene mwambo wa maliro wa muwulutsi komanso mkulu wa bu...
10/08/2026

Chisoni chakuta mudzi wa M'banda ku Chileka, m'boma la Blantyre pamene mwambo wa maliro wa muwulutsi komanso mkulu wa bungwe la Malawi Broadcasting Corporation (MBC), Brian Banda uli mkati.

Wolemba Phillimon Backson

National Bank of Malawi (NBM) plc has called for the creation of platforms for journalists to scale up their professiona...
10/08/2026

National Bank of Malawi (NBM) plc has called for the creation of platforms for journalists to scale up their professional skills.

NBM's Marketing and Corporate Affairs Manager, Akossa Mphepo Hiwa, made the remarks at the end of a two-day media learning tour to Gaborone, Botswana, for ten business journalists.

Hiwa said the initiative was aimed at strengthening business and financial reporting capacities in Malawi.

During the trip, journalists engaged directly with the Botswana Stock Exchange (BSE), where its Market Development Expert, Kgotla Sengwe, shared strategies on attracting private investment and cultivating small and medium enterprises (SMEs).

The delegation also toured the Bahurutse Cultural Village in Mmankgodi to experience traditional Setswana cuisine, music and heritage.

Reported by Richard Tiyesi

Address

712
Lilongwe
265

Alerts

Be the first to know and let us send you an email when Timveni Online posts news and promotions. Your email address will not be used for any other purpose, and you can unsubscribe at any time.

Contact The Business

Send a message to Timveni Online:

Shortcuts

Share