
06/07/2025
Omenyera ufulu wa anthu, Billy Malata, walengeza kuti walowa chipani cha Odya Zake Alibe Mlandu, chomwe mtsogoleri wake ndi wachiwiri kwa mtsogoleri wadziko lino, Michael Usi.
Malata wati amakhulupirira kuika chitukuko patsogolo, ndale pambuyo.
Iye wati adzaimira chipanichi ngati khansala wadera la Kasemba kudera la phungu wakunyumba ya malamulo la M'buka ku Lilongwe.
Malata wati akufuna kutukula derali ngati anthu kumeneko adzamusankhe pa chisankho cha chapa 16 September chaka chino.
Wolemba: Johans Mumba