Nkhoma Synod Radio

Nkhoma Synod Radio Contact information, map and directions, contact form, opening hours, services, ratings, photos, videos and announcements from Nkhoma Synod Radio, Broadcasting & media production company, Lilongwe.
(1)

Nkhoma Synod Radio is a christian Radio station under the C.C.A.P Nkhoma Synod, which intends to bring people closer to God using well produced Christian Programs

 Apolisi ku Nkhata-bay amanga bambo wina wa zaka 39 pomuganizira kuti wagona ndi msungwana wa zaka 15 yemwe ali ndi vuto...
15/07/2025



Apolisi ku Nkhata-bay amanga bambo wina wa zaka 39 pomuganizira kuti wagona ndi msungwana wa zaka 15 yemwe ali ndi vuto la mu ubongo.

Malinga ndi apolisi m'bomali, bamboyu wapanga izi pa malo ena ogona alendo.

Iwo ati msungwanayu adapita pa malowa chifukwa amagwira ganyu wotunga madzi.

Mkuluyu atawona msungwanayu nkumukokera mchipinda chomwe iye adali ndi kugona naye.

Pofuna kuti asakaulure kwa anthu, mkosanayu adapereka 800 kwacha kwa mwanayu.

Koma mwanayu adakauza mayi ake, womwe adakanena ku polisi ndipo apolisi agwira mkuluyu akufuna adzithawira ku Mozambique.

 The Malawi National Council of Sports (MNCS) says it will implement effective measures to retain the talent which Team ...
15/07/2025



The Malawi National Council of Sports (MNCS) says it will implement effective measures to retain the talent which Team Malawi showcased during the recent AUSC Region 5 Youth Games, which were held in Namibia.

MNCS Chief Executive Officer Dr. Henry Kamata said this at Kamuzu International Airport in Lilongwe when welcoming the team from Windhoek, Namibia where it participated in the games.

Team Malawi secured a total of 32 medals at the tournament including 7 gold and 13 silver medals.

Dr. Kamata suggests that maintaining and overseeing the athletes will assist the country in developing robust sports disciplines, which in the near future will yield positive results.

He says the council has developed a plan to organize the first camp for Team Malawi in September this year, with the goal of representing the nation in the Region 5 tournament scheduled for next year in Mozambique.

Director in the Ministry of Youth and Sports Jameson Ndalama said government is pleased with the team's performance and will continue to provide adequate financial support for the upcoming competitions.

The captain of Team Malawi Chris Milli expressed gratitude to the government for the support provided which enabled them to prepare adequately and perform well in the tournament.

Photo Credit : MNCS
Reported by Eliot Tandani

15/07/2025



M'modzi mwa anthu omwe amayankhulirapo pa zochitika m'dziko Dr George Chaima wati anthu ena m'boma akuoneka kuti akuchita zinthu zofuna kumuonetsa mtsogoleri wa dziko ngati wolephera.

Iwo ati izi zili chomwechi potengera kuti anthuwa amalephera kuchita zinthu zomwe mtsogoleriyu wayankhula.

Mwa chitsanzo, iwo ati ngakhale mtsogoleri wa dziko lino wakhala akuuza nthambi za chitetezo kuti zigwire ndi kuzenga mlandu anthu omwe amabweretsa ziwawa pa ndale koma mpaka pano palibe yemwe adamangidwa ndi kuzengedwa mlandu.

Mwa ichi, iwo ati akuona kuti zomwe mtsogoleriyu wayankhula ku mtundu wa aMalawi dzulo kukhala kuvuta kuti zikwanilitsidwe ngati mtsogoleriyu sachitapo kanthu pa olephera kukwanilitsa zomwe wanena.

Dr Chaima atinso mtsogoleri wa dziko linoyu pena amaonetsa kulephera posagwiritsa ntchito mphamvu zake za m'malamulo pochotsa ntchito anthu omwe akulephera kukwanilitsa masomphenya ake.

 Mtsogoleri wa chipani cha Odya Zake Alibe Mlandu Dr Michael Usi tsopano atenga kalata zoonetsa chidwi chofuna kupikisan...
14/07/2025



Mtsogoleri wa chipani cha Odya Zake Alibe Mlandu Dr Michael Usi tsopano atenga kalata zoonetsa chidwi chofuna kupikisana nawo pa udindo wa mtsogoleri wa dziko.

Izi ndi malinga ndi uthenga womwe bungwe loyendetsa zisankho la MEC latulutsa.

Izi tsopano zatengera chiwerengero cha anthu omwe akufuna kupikisana nawo pa udindo wa mtsogoleri wa dziko lino pa zisankho za mu September muno kufika pa 18.

 Anthu mdziko muno kuyambira  mawa  akhala akukhamukira  ku Bingu International Convention Center  ( BICC) mu mzinda  wa...
14/07/2025



Anthu mdziko muno kuyambira mawa akhala akukhamukira ku Bingu International Convention Center ( BICC) mu mzinda wa Lilongwe komwe mtsogoleri wa utumiki wa Omega Fire padziko lonse mtumwi Johnson Suleman ochoka mdziko la Nigeria akhale akumwaza uthenga wachipulumutso.

Mtumikiyu yemwe wafika lolemba mdziko muno kudzela Ku bwalo la ndege la Kamuzu akhala akulalikira kuyambira mawa mpaka lachitatu pa 16 July.

A Suleman ati mkumano omwe uchitikewu ukhale mdalitso kwa a Malawi pomwe Mulungu akhale akukumana ndi zosowa zawo.

Iwo awonjezeraso kuti mumasikuwa adzala akuyankha mafuso omwe anthu amakhala nawo okhudza umoyo wa uzimu.

Wolemba: Zephaniah Nungu

 Mtsogoleri wa dziko lino Dr Lazarus Chakwera watsindika za kufunika kokhala anthu osunga malamulo adziko lino posaphwan...
14/07/2025



Mtsogoleri wa dziko lino Dr Lazarus Chakwera watsindika za kufunika kokhala anthu osunga malamulo adziko lino posaphwanya ufulu wa ena pa nthawi yovomelezeka yochita misonkhano yokopa anthu pomwe dziko lino likhale ndi zisankho posachedwa.

Iye wayankhula izi lolemba madzulo kutsatira kukhazikitsidwa kwa nthawiyi ndi bungwe la MEC kum'mawa wa tsikuli.

Poyankhula Ku mtundu wa aMalawi a Chakwera ati pa nthawiyi anthu apewe m'chitidwe wophwanya malamulo adziko lino pophwanya ufulu wa anthu ena pomwe akuchita misonkhano ya ndale kapena kuyankhulapo ndemanga zawo.

Iwo ati ngati mtsogoleri wa dziko lino akhala akuwona maiko ena momwe zisankho zimasokonekera ngati anthu aphwanya ufulu wa ena m'nyengo yoponya voti.

Pomaliza a Chakwera ati akuwafunira aMalawi zabwino zonse pa nthawi yomwe akhale akumva mfundo zosiyanasiyana kuchokera kwa omwe akudzayimira nawo pa chisankho chomwe chikudzachi.

14/07/2025



The Team Malawi, which traveled to Namibia to compete in the AUSC Region 5 Youth Games in various sports disciplines, has arrived at Kamuzu International Airport today.

A total of 165 athletes from Malawi went to Namibia to compete in categories of football, netball, athletics, volleyball, boxing, e-sports, karate, Paralympics, judo, basketball, and more.

In this tournament, Malawi has managed to win 32 medals, with 7 gold medals and 13 silver medals.

The team has received a warm welcome from fans who are chanting different songs for their wonderful performance in this tournament.

Reported by Eliot Tandani ( KIA)

14/07/2025



YAM'KWANA NGUWO, MULEKENI AVALE

M'modzi mwa anthu omwe amayankhulirapo pa zochitika m'dziko Francis Liyati Phiri akuyembekezeka kuti adindo achitapo kanthu pa kalata yomwe General Assembly ya mpingo wa CCAP yalemba.

A Liyati ati iwo sakuyembekezera kuti adindo aloza chala atsogoleri a mipingo pa zolakwika zomwe aziona mu ulamuliro ulipo-wu.

Iwo ati kalatayi kupatula kuloza zofooka, yaunikiraso ma gawo omwe boma likuchita bwino ndi momwe angachitire pa magawo omwe zinthu sizikuyenda bwino.

General Assembly ya mpingo wa CCAP yatulutsa kalatayi lamulungu ndipo inawerengedwa m'mipingo yonse ya CCAP.

 Mtsogoleri wa dziko lino Dr Lazarus Chakwera akuyembekezeka kuyankhula ku mtundu wa aMalawi lero.Malinga ndi uthenga ku...
14/07/2025



Mtsogoleri wa dziko lino Dr Lazarus Chakwera akuyembekezeka kuyankhula ku mtundu wa aMalawi lero.

Malinga ndi uthenga kuchokera ku nyumba ya chifumu, Dr Chakwera akuyembekezeka kuyankhula kuyambira nthawi ya 7 koloko madzulo.

14/07/2025



Bambo wa zaka 24 Jericho Mayeso, yemwe adali ndi vuto la mu ubongo, wapezeka atafa m'mudzi mwa Ligomba mfumu yaikulu Kanyenda ku Nkhotakota.

Malinga ndi apolisi, thupi la mkuluyu lapezeka pa ntchire lina loweruka lapitali.

Zotsatira za chipatala zaonetsa kuti mkuluyu wamwalira kaamba ka vuto la kuchepa kwa shuga m'thupi.

14/07/2025



Bambo wina wa zaka 41 wamwalira atadziyatsa ndi petulo ku Nkhotakota ati poti mkazi wake anamukanira kuti agulitse thumba limodzi la chimanga.

Mneneli wa polisi ya Nkhunga Sub Inspector Andrew Kamanga wati malemuwa, Shadrick Phiri loweruka lapitali adapita ku mowa komwe adaononga ndalama zonse.

Apa mkuluyu adaganiza kuti apite ku nyumba kuti akagulitse thumba limodzi kuti akamweleso koma mkazi wake adamukanira.

Apa mkuluyu adatenga petulo nkudzithira, kenako n'kupita ku malo ena komwe adadziyatsa.

Thupi la mkuluyu lapezeka m'bandakucha wa dzulo lili ndi zilonda za moto.

14/07/2025




Wapampando wa bungwe loyendetsa zisankho mdziko muno la MEC Justice Annabel Mtalimanja wati bungweli sililora kuti akuluakulu a zipani zandale adzichita zosemphana ndi malamulo ake pomwe akukopa anthu kuti adzawavotere.

A Mtalimanja ati mwazina akuluakulu a bungweli adziyendera m'madera onse a mdziko muno pofuna kudziwa momwe ntchito yokopa anthu ikuyendera.

Iwo apempha akuluakulu a zipani za ndalezi kuti apewenso kuchitira nkhanza amayi komanso magulu ena pa nthawiyi.

Apapa a Mtalimanja apemphanso mafumu mdziko muno kuti apereke mpata kwa andale onse kuti achititse misonkhano yawo yokopa anthu m'madera awo.

Wolemba: Billy Amos

Address

Lilongwe

Alerts

Be the first to know and let us send you an email when Nkhoma Synod Radio posts news and promotions. Your email address will not be used for any other purpose, and you can unsubscribe at any time.

Contact The Business

Send a message to Nkhoma Synod Radio:

Share