TWR Malawi

TWR Malawi A non-denominational, not-for-profit Christian radio network reaching Malawians and beyond.

30/07/2025

Mwadzuka bwanji okondedwa omvera?
Inu ndi mdalitso ku TWR,ndichifukwa chake timakunyadilani ndi program ya Chimwemwenmmawa from 06:10 mpaka 07:00 mmawa(Mon- fri)

Lero tikambilane nkhani ya anthu amene safuna kukhazikika pamalo antchito,business even pa banja kumene ena sakhalitsa😂
Kuyamba ntchito osatha chaka unva akuti asiya.

Komatu mawu a Mulungu pa Miyambo 22 v 29 amati " Kodi ukumuona munthu wa luso pa ntchito yake?
Iye adzatumikira mafumu sadzatumikira anthu wamba."Koma anthu tikulephera kupezeka pamaso pa mafumu ndiko kupeza zabwino chifukwa chosakhazikika,kudekha pamalo antchito.

Kudekha pamalo kumapangitsabkuti otilemba ntchito atikhulupilire.Pa malo pamakhala zinthunzina zimene zimachitika ife osadziwa kumakambilana za promotion yako we ukuganiza zosiya ntchito.
Know that trust is earned and its a long term work setting.

Ena tasemphana ndi mwayi chifukwa chakusakhazikika pa malo.Abwana kuti afike pokusiila ma Key akuchipinda,ai galimoto mukhoza kumakagona nayo kwanu it means akukhulupilira.
Koma izi sizingachitike kwa kanthawi kochepa.
Kumadekha😂
Ndemanga zanu nzotani?
fans

    A MEC atavomeleza kalata zawo, a Banda ati kupikisana nawo pa chisankho cha pa 16 September akufuna kusintha miyoyo ...
29/07/2025




A MEC atavomeleza kalata zawo, a Banda ati kupikisana nawo pa chisankho cha pa 16 September akufuna kusintha miyoyo ya anthu m'Malawi muno.

Iwo ati akuyimira zofuna za anthu osati chipani pakubweresanso kusintha vuto la nkhani ya chuma. Powonjezerapo a Banda ati mayi Vera Kaludzu awasankha kamba koti wonse ali ndi chidwi pofuna kukonza chuma cha dziko lino.

Wa pa mpando wa bungwe la MEC a Anabel Mtalimanja, ayamikira a Banda kamba kolimba mtima kwawo posankha kuyima pawokha pa chisankho cha mtsogoleri wa dziko lino.

Wolemba: Glory Mvula - Lilongwe.

 The Malawi Congress Party (MCP) has announced that its members who are contesting in the primary elections for the parl...
29/07/2025


The Malawi Congress Party (MCP) has announced that its members who are contesting in the primary elections for the parliamentary seat in Mzimba Central Constituency should run as independent candidates in the upcoming September elections.

This means that Trade Minister Vitumbiko Mumba and Adamson Mkandawire will contest in the upcoming election as independent candidates, but both will continue to be members of the MCP.

According to a letter written by the party’s legal affairs director, George Jivason Kadzipatike, addressed to Mumba’s Khumbo Soko.

In the letter, Kadzipatike says the MCP will not discipline the two candidates, but it will take action against its members who disrupted the party’s primary elections in the constituency back in May and more recently on July 26, 2025.

A Thokozani Manyika Banda, omwe akudzapikisana nawo pa chisankho cha pa 16 September ngati mtsogoleri woyima pawokha afi...
29/07/2025

A Thokozani Manyika Banda, omwe akudzapikisana nawo pa chisankho cha pa 16 September ngati mtsogoleri woyima pawokha afika kudzapereka kalata zawo ku bungwe la MEC ndi kuti awonetse yemwe akhale wachiwiri wawo pa zisankho zimenezi.

A Vera Alinafe Kaludzu ndi omwe asankhidwa ndi a Banda kukhala wachiwiri wawo pa zisankho zimenezi.

Wolemba: Glory Mvula -Lilongwe.

    A Mbewe ati akufuna achinyamata apeze ntchito zosiyanasiyana, mafuta a galimoto adzipezeka, kupezeka kwa mankhwala m...
29/07/2025




A Mbewe ati akufuna achinyamata apeze ntchito zosiyanasiyana, mafuta a galimoto adzipezeka, kupezeka kwa mankhwala mzipatala komanso onse kupeleka ndalama za omwe anapuma ntchito koma ndalama zawo sanalandile.

A Mbewe apempha a Malawi kuti asankhe mwadongosolo yemwe akufuna kuti asankhe kukhala mtsogoleri wa dziko lino posatengera zomwe akulonjeza koma zomwe akuchita.

Powonjezerapo mtsogoleriyu wapempha bungwe la MEC kuti amvere madandawulo a atsogoleri omwe akutenga nawo gawo pa chisankho cha pa 16 September. Izi anayankhula pomwe mkulu wa MEC, Justice Annabel Mtalimanja anawatsimikizila kuti zikalata zawo zalandiladwa ndipo chilichonse choyenelera chilipo m'zikalatamo.

Wolemba: Glory Mvula - Lilongwe.

A Edwards  Kambanje ndi omwe asankhidwa ndi a David Mbewe kukhala wachiwiri wawo.Iwowa asankha a Kampanje kuti athandiza...
29/07/2025

A Edwards Kambanje ndi omwe asankhidwa ndi a David Mbewe kukhala wachiwiri wawo.

Iwowa asankha a Kampanje kuti athandizane mu mpikisano wa utsogoleri was dziko lino komanso kuti atukule dzikoli limodzi

    Motsagana ndi khamu la anthu a David Mbewe omwe ndi a chipani cha Liberation for Economic Freedom Party (LEFP) afika...
29/07/2025




Motsagana ndi khamu la anthu a David Mbewe omwe ndi a chipani cha Liberation for Economic Freedom Party (LEFP) afika pa malo opelekera kalata zawo ku bungwe la MEC ku BICC pomwe akhale akutiwonesera wachiwiri wawo komanso komanso kukambapo zina mwafundo zomwe akufuna a Malawi adzawasankhe pa zisankho za pa 16 September.

29/07/2025


Kwa mphindi zochulukirapo mabizinesi anayima kaye pa msika wa Chinamwali mu mzinda wa Zomba kaamba ka mdipiti wa galimoto omwe unanyamula otsatira a Davie Maunde, womwe akukapereka kalata zawo ku bungwe la Malawi Electoral Commission (MEC).

A Maunde womwe akudzapikisana nawo ngati phungu wa nyumba ya malamulo m'dera la Zomba City North m'chipani cha United Democratic Front (UDF) anayamba wakhalapo ngati mfumu ya mu mzinda-wu zaka zapitazo.

Zina mwa zochitikazi mu kanema yemwe mtolankhani wathu wajambula mphindi zapitazo.

Wolemba ndi kujambula: Taona Steven Mkandawire, Zomba.

29/07/2025


Nthambi yowona za nyengo ndi kusintha kwa nyengo yalangiza anthu ogwiritsa ntchito Nyanja ya Malawi kuti akhale osamala ndi kudziteteze kaamba ka mphepo ya Mwera yomwe ikhale ikuwomba panyanjayi ndi madera ena omwe azungulilidwa ndi nyanjayi.

Mphepoyi ikuyembekezeka kuwomba pa liwiro lalikulu la 50 kilomitas pa ola, ndipo panyanja pakhala mafunde amphamvu masiku akubwera.

Malinga ndi kalata yomwe mkulu wa nthambiyi Dr. Lucy Mtilatila wasainila, mphepoyi ikhala ikuwomba madera osiyanasiyana, kuphatikizapo Karonga, zomwe zikubweretse chiopsezo kwa asodzi, ogwiritsa ntchito mabwato, komanso anthu okhala m’mphepete mwa nyanja.

 Minister of Agriculture Sam Kawale who is also the aspiring candidate for Dowa North East yesterday presented his nomin...
29/07/2025


Minister of Agriculture Sam Kawale who is also the aspiring candidate for Dowa North East yesterday presented his nomination papers at Msakambewa TDC as he seeks to return to parliament after 16th September polls.

Kawale has also launched a K22 million Sam Kawale Premier League at Msakambewa ground.

The minister paid a courtesy call at Inkosi Msakambewa headquarters and met chiefs in Dowa North East constituency before the launch of the league.

Kawale has served for 11years as an MP for the area.

After its launch in 2024, Sons of Valour Summit is back in 2025!Under the theme "Forged for More: Rising in Strength, Id...
29/07/2025

After its launch in 2024, Sons of Valour Summit is back in 2025!

Under the theme "Forged for More: Rising in Strength, Identity and Purpose", this one-day summit is designed to empower and shape young men for greatness. It's happening on 2nd August 2025, from 8:00 AM to 4:00 PM.

Register your boys aged 12 to 25 years for this impactful event. It will take place at the Presbyterian Church of Malawi – Lilongwe (LL-PCM), along the KCH Road. Artists like A'chanza, Beuce Africa, Tact & CS are lined up for performances during the event.

This is more than just an event—it’s a life-shaping experience! Get ready for mentorship, inspiration, and practical wisdom to help you grow into a man of purpose.

📞 Register Now:
0888879200 | 0881741681 | 0998750681 | 0888956622

  A Timothy Kayendera ndi omwe asankhidwa kukhala wachiwiri wa a Jordan Sauti omwe akupikisana nawo pa mpando wa utsogol...
29/07/2025



A Timothy Kayendera ndi omwe asankhidwa kukhala wachiwiri wa a Jordan Sauti omwe akupikisana nawo pa mpando wa utsogoleri wa dziko lino. A Sauti ndi m'modzi wa iwo amene ali ndi ukadawulo pa ntchito za migodi ya miyala m'dziko muno ndi mayiko ena osiyanasiyana.

Poyankhulapo pomwe amapereka kalata zawo a Sauti ati ndale zawo atsatira ndondomeko yomwe bungwe la MEC lakhazikitsa komanso kuti ndale zawo zikhala za bata ndi mtendere.

Powonjezerapo iwo ati akufuna kupindulitsa a Malawi kudzera m'migodi ya miyala yosiyanasiyana yomwe ili m'dziko muno.

Iwo ati migodi ya miyala yosiyanasiyanayi ithandizira dziko lino kupeza chuma chochuluka chomwe chithandizire kumanga sukulu, kusitsa mtengo wa feteleza komanso kutsitsa ndalama zophunzilira mu sukulu za ukachenjede zomwe mtsogolomu atha kuzazipanga kukhala zaulele.

Wolemba: Glory Mvula - Lilongwe.

Address

Lilongwe

Opening Hours

Monday 08:00 - 16:00
Tuesday 08:00 - 16:00
Wednesday 08:00 - 16:00
Thursday 08:00 - 16:00
Friday 08:00 - 16:00

Telephone

+265992048990

Alerts

Be the first to know and let us send you an email when TWR Malawi posts news and promotions. Your email address will not be used for any other purpose, and you can unsubscribe at any time.

Contact The Business

Send a message to TWR Malawi:

Share