TWR Malawi

TWR Malawi A non-denominational, not-for-profit Christian radio network reaching Malawians and beyond.

Komiti ya nyumba ya malamulo yoona zamalonda yapempha bungwe la zamalonda la Malawi Confederation of Chambers of Commerc...
10/06/2026

Komiti ya nyumba ya malamulo yoona zamalonda yapempha bungwe la zamalonda la Malawi Confederation of Chambers of Commerce and Industry (MCCCI) kuti likonze malo omwe pamachitikira chionetsero cha zamalonda ku Blantyre.

Wapampando wa komitiyi Ackim Kumwenda wapeleka pempholi pomwe akuluakulu a MCCCI anakaonera ku komitiyi lachitatu.

Kumwenda wati malowa akufunika azioneka mwa pamwamba pofuna kukopa a malonda ochuluka ochokera kunja kuti azakhala nawo pa chionetserochi.

Iwo ati bungweli likuyeneranso kudzipezeketsa mmadera ochuluka pofuna kufikira amalonda ochuluka mdziko muno.

Kumwenda wauza MCCCI kuti itsekule ofesi zatsopano mmaboma ambiri a dziko lino kuti chiwelengero cha mamembala awo chikwere.

Poyankhapo, mkulu wa MCCCI Daisy Kambalame anati nkhani yokonza malo omwe chionetsero chamalonda chimachitikira ili kale mkati.

Kambalame wati posachedwapa bungwe lawo lifikira a malonda ochuluka pomwe likukonza zotsekula ofesizi kuti amalonda azilifikira mosavuta.

Pakadali pano bungwe la MCCCI lili ndi mamembala pafupifupi 350.

  Concerned Civil Society Organisations have questioned reported plans by the Director of Public Prosecutions and the An...
10/06/2026


Concerned Civil Society Organisations have questioned reported plans by the Director of Public Prosecutions and the Anti-Corruption Bureau to withdraw corruption-related charges against convicted Chinese wildlife trafficker Lin Yun Hua.

Addressing a news conference in Lilongwe, the organisations said such a move would undermine Malawi's progress in the fight against illegal wildlife crime and could weaken public confidence in the justice system.

Speaking on behalf of the grouping, Indigenous Conservation of Nature representative Zilanie Gondwe and Centre for Environmental Policy and Advocacy representative Alfred Kambwiri questioned what they described as a possible conflict of interest involving the DPP, noting that he previously formed part of Lin Yun Hua's legal team.

Lin Yun Hua was sentenced to 14 years' imprisonment in 2021 after being convicted of offences involving rhino horns and money laundering. In 2025, he was granted a presidential pardon after serving four years but was later re-arrested over allegations that he bribed prison officials and sought to secure a lighter sentence during his original trial.

The 12 civil society organisations are demanding a clear, evidence-based explanation for any decision to discontinue the corruption-related charges, saying transparency and accountability are essential to maintaining public trust in the justice system.

The organisations have also called on both the Director of Public Prosecutions Fostino Mayere and the Anti-Corruption Bureau Director genera general Gabriel Chembezi, to publicly explain the reported plans to withdraw the charges and say they will seek intervention from the Malawi Law Society and other relevant authorities if no satisfactory clarification is provided within 14 days.

When contacted, ACB public relations officer, Jacqueline Ngongonda asked for more time before commenting on the matter.

 : Timu ya FCB Nyasa big bullets yalemba ntchito Wedson Nyirenda (Wada Wada) ngati mphunzitsi wamkulu wa timuyi. Nyirend...
10/06/2026

: Timu ya FCB Nyasa big bullets yalemba ntchito Wedson Nyirenda (Wada Wada) ngati mphunzitsi wamkulu wa timuyi.

Nyirenda wasaina mgwirizano wa zaka ziwiri ndi maule.

Mphunzitsiyu ndi wa m'dziko la Zambia.

Bungwe la Medical Council of Malawi latseka chipinda chochitira opaleshoni pa chipatala chachin'gono cha Monkey Bay ku M...
10/06/2026

Bungwe la Medical Council of Malawi latseka chipinda chochitira opaleshoni pa chipatala chachin'gono cha Monkey Bay ku Mangochi kaamba kosatsatira zina mwa ndondomeko za zipindazi.

Akuluakulu omwe anayendera chipatalachi dzulo ati achita izi pofuna kuteteza miyoyo ya anthu omwe amathandizidwa pa chipatalachi.

Bungweli linapeza kuti chitseko cha malo ochirirawa chinaongeka kalekale ndipo mpaka pano sichinakonzedwe.

Pakadali pano, mkulu wa bungwe la Malawi Health Equity Network a George Jobe ayamikira ganizoli ponena kuti lithandiza kuika chikhulupiriro mwa a Malawi pa momwe zipatala zikugwirira ntchito zake.

Wolemba: Horace Tebulo, Dedza.

Khonsolo ya mzinda wa Lilongwe ayipatsa malire pa 31 August 2026 kuti isamutse mtaya wa ku Area 38. Komiti ya nyumba ya ...
10/06/2026

Khonsolo ya mzinda wa Lilongwe ayipatsa malire pa 31 August 2026 kuti isamutse mtaya wa ku Area 38.

Komiti ya nyumba ya malamulo yoona za chilengedwe ndi kusintha kwa nyengo ndi yomwe yalamula khonsoloyi pomwe imaonekera ku nyumbayi lero.

Wapampando wa komitiyi Tiaone Hendry wati khonsoloyi ikuyenera kuchita machawi popeleka lipoti la momwe ndondomekoyi iyendere pofuna kuti umoyo wa anthu omwe akhale kufupi ndi mtaya watsopanowu ukhale wabwino.

Hendry wati awuza unduna wa za nyengo ndi kusintha kwa nyengo kuti uthandizire pa ntchitoyi kuti iyende msanga.

Mlembi wamkulu mu undunawu Dr. Misheck Munthali wati iwo ayesetsa mbali yawo pokumbutsa khonsoloyi kuti ikwanilitse ntchito yomwe yapatsidwa.

Munthali wati unduna wawo ndi okonzeka kugwira ntchito limodzi ndi khonsoloyi pofuna kuonetsetsa kuti umoyo wa anthu a ku Area 38 ukupita patsogolo.

Mtaya watsopanowu ukuyembekezeka kukakhala malo ena mmbali mwa msewu wa Salima.

 Dziko la Democratic Republic of Congo lati anthu omwe ali ndi matenda a Ebola afika pafupifupi 600. Kufalikira kwa mate...
10/06/2026


Dziko la Democratic Republic of Congo lati anthu omwe ali ndi matenda a Ebola afika pafupifupi 600.

Kufalikira kwa matenda a Ebola kunalengezedwa pa 15 May mdzikolo.

Mu lipoti lake laposachedwa la pa X, boma la DRC lati chiwerengero cha anthu omwe afa ndi Ebola chafika pa 115.

Odwala 22 achira ku matendawa mdzikolo.

Zina mwa zizindikiro za Ebola ndi: Kutentha ndi kuphwanya kwa thupi, kusanza, kutsegula m'mimba, kapenanso kufooka kwambiri.

Wolemba: Hennock Malinda, Lilongwe.

Sukulu ya Maranatha Academy yati ipeleka mwayi wa maphunziro (Scholarship) kwa Duwama Muhammad yemwe ndi ophunzira yekha...
10/06/2026

Sukulu ya Maranatha Academy yati ipeleka mwayi wa maphunziro (Scholarship) kwa Duwama Muhammad yemwe ndi ophunzira yekhayo wa mkazi yemwe akulemba mayeso a 8 pa sukulu ya Mangale Primary ku Mangochi.

Mkulu wa Maranatha Academy, Ernest Kaonga wati ngati Duwama akhoze mayesowa, adziwiretu kuti malo ake alipo ku sukuluyi kuyambira Form 1 mpaka 4.

Kaonga wati Duwama azikalandiranso ndalama yokwana 500, 000 kwacha pa teremu yomuthandizira zina ndi zina zofunika pa sukulu.

Kuchokera chaka cha 2017, aka nkoyamba kuti mtsikana afike 8 ndi kulemba mayeso pa sukuluyi.

Ambiri mwa atsikana mderali safika Standard 8 kaamba kotenga pakati.

10/06/2026

Galimoto ina yatseka msewu opita ku Kamuzu Central pomwe trailer yake yagwa.

Galimotoyi imachokera mu Dr. Saulos Klaus Chilima Highway kulowera mbali ya ku Mchesi.

Pakadali pano galimoto zina sizikukwanitsa kudutsa pa malopa.

Ntchito yosamutsa katundu yemwe anali mgalimotoyi ili mkati pano.

Wojambula:Alfred Maida, Lilongwe.

Somali referee Omar Abdulkadir Artan has returned to Mogadishu after being excluded from the 2026 FIFA World Cup followi...
10/06/2026

Somali referee Omar Abdulkadir Artan has returned to Mogadishu after being excluded from the 2026 FIFA World Cup following a decision by US immigration authorities.

Artan, named Africa’s Best Male Referee in 2025, was set to become the first Somali official to referee a World Cup match.

FIFA confirmed he will not officiate at the tournament, saying entry decisions are made by host governments.

Speaking after his return, Artan said he was not upset by the setback and would continue to work hard and remain focused on his career.

DW Africa

10/06/2026


The Taekwondo Association of Malawi has announced the appointment of six additional officials to bolster administration, technical development, and promotion of the sport nationwide.

The Executive Board said the appointments take effect immediately, according to a press release signed by TAM President Major Louis Msokwa on 8 June 2026.

The statement says Andrew Soole has been named National Technical Director. His duties include coordinating athlete development, coaching, officiating standards, technical seminars, gradings, competitions, and ensuring compliance with Taekwondo rules and regulations.

Two Assistant Technical Directors were also appointed to support regional coordination. Valerie Ntula will serve for the Southern Region while Victor Msonga takes the Central Region.

The association also filled key administrative and communications roles where Vester Banda was appointed Safeguarding Officer, Chikambotho Banda comes in as Marketing Director to drive visibility and growth through sponsorship, branding, partnerships, and event marketing, and Mike Lyson Zgambo will serve as Media Officer.

Msokwa urged all heads of dojangs and TAM members to extend cooperation to the new officials as they carry out their mandates.

He said the appointments are aimed at improving technical delivery, safeguarding, and public visibility of Taekwondo in Malawi.

Reported by Dumisani Prince Tembo, Mzuzu

Address

Lilongwe

Opening Hours

Monday 08:00 - 16:00
Tuesday 08:00 - 16:00
Wednesday 08:00 - 16:00
Thursday 08:00 - 16:00
Friday 08:00 - 16:00

Telephone

+265992048990

Alerts

Be the first to know and let us send you an email when TWR Malawi posts news and promotions. Your email address will not be used for any other purpose, and you can unsubscribe at any time.

Contact The Business

Send a message to TWR Malawi:

Share