10/06/2026
Komiti ya nyumba ya malamulo yoona zamalonda yapempha bungwe la zamalonda la Malawi Confederation of Chambers of Commerce and Industry (MCCCI) kuti likonze malo omwe pamachitikira chionetsero cha zamalonda ku Blantyre.
Wapampando wa komitiyi Ackim Kumwenda wapeleka pempholi pomwe akuluakulu a MCCCI anakaonera ku komitiyi lachitatu.
Kumwenda wati malowa akufunika azioneka mwa pamwamba pofuna kukopa a malonda ochuluka ochokera kunja kuti azakhala nawo pa chionetserochi.
Iwo ati bungweli likuyeneranso kudzipezeketsa mmadera ochuluka pofuna kufikira amalonda ochuluka mdziko muno.
Kumwenda wauza MCCCI kuti itsekule ofesi zatsopano mmaboma ambiri a dziko lino kuti chiwelengero cha mamembala awo chikwere.
Poyankhapo, mkulu wa MCCCI Daisy Kambalame anati nkhani yokonza malo omwe chionetsero chamalonda chimachitikira ili kale mkati.
Kambalame wati posachedwapa bungwe lawo lifikira a malonda ochuluka pomwe likukonza zotsekula ofesizi kuti amalonda azilifikira mosavuta.
Pakadali pano bungwe la MCCCI lili ndi mamembala pafupifupi 350.