TWR Malawi

TWR Malawi A non-denominational, not-for-profit Christian radio network reaching Malawians and beyond.

14/09/2026

Loya Sylvester Ayuba James wati kupepesa kwa chipani cha MCP kwa zipani za mu mgwirizano wa Tonse nkosakwanira ngati Dr....
14/09/2026

Loya Sylvester Ayuba James wati kupepesa kwa chipani cha MCP kwa zipani za mu mgwirizano wa Tonse nkosakwanira ngati Dr. Lazarus Chakwera akutsogolelabe chipanichi.

Ayuba James wati Dr. Chakwera ndi omwe sanatsatire mfundo za mu mgwirizano ndipo amayenera achoke kuti zipanizi zikhulupilirenso chipani cha MCP.

Katswiri wa za malamuloyi wati mtsogoleri ndi yemwe amalozedwa chala pa momwe zinthu zikuyendera mchipani.

Ayuba James wati mau opepesa okha osachotsa a Chakwera pa mpando wa utsogoleli ngosakwana.

Iwo aloza chala Dr. Chakwera kuti amakonda kugwira ntchito ndi anthu a pa banja lawo, azibale awo komanso anzawo.

Chipani cha MCP kudzera mwa mneneri wake Dr. Jessie Kabwira chapepesa zipani monga UTM ndi zina zomwe anali nazo pa mgwirizano otchedwa Tonse kuti chinalakwa posatsatira mfundo za mu mgwirizano.

PSALM 69:17Do not hide your face from your servant;answer me quickly, for I am in trouble.
14/09/2026

PSALM 69:17
Do not hide your face from your servant;answer me quickly, for I am in trouble.

Tikuchoka ku Weeekend komwe ambiri tinapita ku Church. Kumeneku kumabwela ena amene akufuna kudzakhala nawo pa mapempher...
14/09/2026

Tikuchoka ku Weeekend komwe ambiri tinapita ku Church. Kumeneku kumabwela ena amene akufuna kudzakhala nawo pa mapemphero kapenanso kudzayamba nawo mpingo wathu. Nthawi zinatu maweluzidwe athu ndi omwe abweza ena kubwela kunyumba ya Mulunguyi. Kungomuona muthu mmene akuonekela taweluza kale kuti uyu akungofuna kudzasokoneza mapemphero athu, koma pamene takhala tikufuna ndithu Mpingo wathu utakula. Ngati tiwabweza otelewa kodi nanga Mpingo ukula bwanji?

Tiyeni tikhale limodzi mu Program ya Chimwemwe mmawa nthawi ya 06:10 mpaka 07:00 momwe muli zambiri za nkhani imeneyi. Mukhozanso kupeleka maganizo anu pano kapena kudzela pa SMS/Whatsapp 0888500222. TWR 90.4 kapena 90.6. Muthanso kumvela TWR online: https://onlineradiobox.com/mw/twrmalawi/

Member of Parliament for Ntcheu Central East Norman Chisale has supported 33 boarding students with K200,000 each, trans...
13/09/2026

Member of Parliament for Ntcheu Central East Norman Chisale has supported 33 boarding students with K200,000 each, translating into a total contribution of K6.6 million.

Each of the students received K200,000, an expanded school bag, hard-cover notebooks and pens to support their education.

The initiative is aimed at helping students meet some of their educational needs and encouraging them to remain focused on their studies.

The support demonstrates Chisale’s commitment to promoting education and improving opportunities for young people in his constituency.

Chisale then called upon the students to work hard in school in order for them to produce good grades.

A Malawi akupitiliza kuwapempha a Rodwell Lumbe kuti adzionetse okha "Live" pa tsamba lawo la mchezo ngatidi ali kunja. ...
13/09/2026

A Malawi akupitiliza kuwapempha a Rodwell Lumbe kuti adzionetse okha "Live" pa tsamba lawo la mchezo ngatidi ali kunja.

Izi zikuchitika pomwe a Lumbe lero aponyaso zithunzi zina zoonetsa kunja komwe ali.

Anthu ochuluka akufuna kuti a Lumbe abweze ndalama kapena awapatse malo omwe anagula ku kampani yawo omwe mpaka lero sanawaone.

Koma polemba pa tsamba lawo la mchezo, Lumbe wati akuthokoza anthu onse omwe akwanitsa kulankhula nawo pa nkhani za malo awo.

Iwo akuti anthu ena akufunabe kugula malo kuchokera ku kampani yawo ndipo akonzeka kuwathandiza.

Lumbe wati wayamba kupeleka malo kwa omwe analipira kale, ndipo walimbikitsa makasitomala ake kuti asunge kalata zogulira malo pabwino kaamba koti alandira ndithu.

Komabe, anthu ena afunsa a Lumbe kuti adzijambule ngatidi ali kunja kapena ayi.

"Ingolowani LIVE man kuti tione ngati mulidi kumeneko."

Anthu 6 afa sitima ina yotchedwa Virgo Transport 8, yomwe inanyamula anthu oposera 240 itatembenuzika m’nyanja ya Java k...
13/09/2026

Anthu 6 afa sitima ina yotchedwa Virgo Transport 8, yomwe inanyamula anthu oposera 240 itatembenuzika m’nyanja ya Java ku Indonesia kaamba ka nyengo yoipa pa madzi.

Apolisi ndi opulumutsa anthu ati anthu 107 apulumutsidwa ndipo ena pafupifupi 130 akusowa.

Sitimayi imachokera ku Surabaya kupita ku Banjarmasin.

Ntchito yopulumutsa anthu ili mkati pakadali pano.

Akuluakulu ati chiwelengero chenicheni cha anthu omwe anali m’ngalawamo chikhoza kusiyana ndi zomwe zili pa m’ndandanda wa okwera.

Wolemba: Hennock Malinda, Lilongwe.

 Mkulu oona zamalamulo m'chipani cha DPP Chipiliro Mpinganjira wati mtsogoleri wa dziko lino a Peter Mutharika akuyendet...
13/09/2026


Mkulu oona zamalamulo m'chipani cha DPP Chipiliro Mpinganjira wati mtsogoleri wa dziko lino a Peter Mutharika akuyendetsa bwino dziko lino chitengereni boma chaka chatha.

Poyankhula pa msonkhano omwe wachitikira pa bwalo la sukulu ya pulayimale ya Makhetha mu mzinda wa Blantyre, a Mpinganjira ati atangotenga boma a Mutharika anathana ndi vuto la kusowa kwa chakudya komanso mafuta a galimoto.

Iwo ati zinthu zambiri zomwe zinaonongeka ziyambanso kuyenda bwino posachedwa, ndipo apempha anthu kuti agwirane manja pothandiza boma kukwaniritsa masomphenya ake.

"Kukonza zinthu kuti ziyambenso kuyenda bwino si ntchito ya tsiku limodzi, kotero ndikupempha kuti mudekhe chifukwa a pulezidenti akukonza," atero a Mpinganjira.

A Mpinganjira omwe ndi wachiwiri kwa nduna ya zachilengedwe ayamikira anthu aderali povotera chipani cha DPP pa chisankho cha pa 16 September 2025.

Wolemba: Francis Mkawihe, Blantyre

 58' Erling Haaland scores!Man United 0-1 Man City
13/09/2026


58' Erling Haaland scores!

Man United 0-1 Man City

"Timangomenya kuti chichitike nchomwecho"- Mtetemera. Mphunzitsi wa Mighty Wanderers MacDonald Nginde Mtetemera wati ndi...
13/09/2026

"Timangomenya kuti chichitike nchomwecho"- Mtetemera.

Mphunzitsi wa Mighty Wanderers MacDonald Nginde Mtetemera wati ndi okhumudwa ndi osewera ake ena omwe sanadzipeleke mmasewero omwe agonja 6-1 ndi timu ya Simba SC.

Mtetemera wati osewera ake ambiri analibe mtima odzipeleka.

Iye akuti anyamatawa anali mtima olimbikira kaamba koti amazitenga zinthuzi ngati zophweka.

Mtetemera: Simnayembekezere, ndipo ndaona zinthu zodabwitsa kwambiri, I expected us to win this game."

"Koma some of the players aaah amazitenga zopepuka kwambiri, komabe tisaloze chala anthu ambiri."

"Zimaoneka ngati mtima pa mpirawu palibe, timangomenya kuti kaya chichitike nchomwecho.",

Address

Lilongwe

Opening Hours

Monday 08:00 - 16:00
Tuesday 08:00 - 16:00
Wednesday 08:00 - 16:00
Thursday 08:00 - 16:00
Friday 08:00 - 16:00

Telephone

+265992048990

Alerts

Be the first to know and let us send you an email when TWR Malawi posts news and promotions. Your email address will not be used for any other purpose, and you can unsubscribe at any time.

Contact The Business

Send a message to TWR Malawi:

Shortcuts

Share