The Beast.

The Beast. News + entertainment

02/08/2025

.

Pomwe kumacha loweruka, anthu ena omwe akuti adamanga mipanda yawo yanjerwa mosatsatira malamulo ku area 3 adzuka atabalalika kamba koti khosolo ya mzindawu yagwetsa mipandayo.

Mipanda yomwe ayigwetsayi ati adayimanga pamwamba pamalo omwe ma payipi a madzi a bungwe Lilongwe water board adadutsa, zomwe ati ndi chiopsyezo ku miyoyo ndi katundu wa anthu komaso kuphwanya malamulo a malo adziko lino.

Malinga ndi nduna ya malo m'dziko muno a Deus Gumba boma likuonetsetsa kuti aliyese m'dziko muno akutsatira malamulo pochita ntchito za zomangamanga ndipo ati iwo akukhulupilira kuti aliyese ayamba kutsatiradi malamulowa.

Sabata ziwiri zapitazi unduna wa malo wagwetsa zomangamanga zingapo zomwe ati sizinatsatire ndondomeko ndi malamulo a malo adziko pozikhazikitsa, ndipo nduna mu undunawu yafusa aliyese kuti azitsatira ndondomeko komaso kufusa nzeru kwa adindo asadayambitse chitukuko chirichonse cha zomangamanga.

Tiyeni!
29/03/2025

Tiyeni!

Church leaders in Malawi have been challenged to adopt servant leadership principles to better serve their congregations...
29/03/2025

Church leaders in Malawi have been challenged to adopt servant leadership principles to better serve their congregations with humility.

Clara Mhango, Ministry Centre Director for Development Associates International (DAI) in Malawi, conveyed this on Friday, when religious leaders from various denominations were issued certificates after successfully completing a five-day workshop by Development Associates International (DAI) in collaboration with the Evangelical Association of Malawi (EAM) at Malawi Assemblies of God University (MAGU) in Lilongwe.

Mhango emphasized the need for religious leaders to provide top-notch services in the ministry that focus on serving people in God's kingdom.

Pastor Kingston Stima, one of the attendees from the Dedza CCAP church, hailed the timely engagement, stating that the training has equipped them with key skills in servant leadership.

President of the Republic of Malawi
27/02/2025

President of the Republic of Malawi

APOLISI AKUTI ANTHU OCHULUKA ADZIPHA MCHAKA CHA 2024 POYEREKEZA NDI CHAKA CHA 2023Chiwerengero cha anthu omwe adadzipha ...
09/02/2025

APOLISI AKUTI ANTHU OCHULUKA ADZIPHA MCHAKA CHA 2024 POYEREKEZA NDI CHAKA CHA 2023

Chiwerengero cha anthu omwe adadzipha m'chaka cha 2024 chaposa anthu omwe adadzipha m'chaka cha 2023

Wachiwiri wa mneneri wa polisi mdziko muno Harry Namwaza wati anthu 597 ndiwo adadzipha chaka chatha poyerekeza ndi 527 mchaka cha 2023 ndipo mwa anthuwa 522 ndiabambo komaso amayi 75.

Malinga ndi kalata yomwe apolisi atulutsa, yasonyeza kuti mu mchaka cha 2023 abambo 447 adadzipha ndipo amayi 48 okha ndiwo adachotsa miyoyo yawo mchakachi.

A Namwaza ati achinyamata azaka za pakatikati pa 20 mpaka 40 ndiwo akuchita mchitidwewu mowirikiza ndipo a Namwaza amena gulu la achinyamata azaka zotere kuti azifusa maganizo kwa anthu okhwima mzeru zinnthu zikawapsyinja pofuna kuthana ndi vutoli.

Apolisi komaso akatswiri m'mbuyomu adatiuza kuti umphawi, ngongole komaso mavuto a m'banja ndi nkhani zokhudza Chikondi kuti ndizo zikukolezera kudzipha maka pakati pa abambo ndi anyamata.

09/02/2025

Child rights activists say they are stunned by what they term the suspicious disappearance of a case file concerning Jan Williem Akster, which led to the postponement of the trial.

The trial, which was scheduled to commence on February 7, 2025, failed to proceed after court officials at Blantyre Magistrate Court reported that they had lost some crucial documents related to the case.

Akster is accused of so**my and sexual abuse, having molested students and employees at Timotheos Foundation between January 2018 and April 2020.

Reacting to the development, child rights activists Memory Chisenga and Caleb Ng’ombo, in a joint statement, said that in their inquiry with the Blantyre Magistrate regarding the delay of the case, officials admitted to the missing case documents, hence the situation.

The officials further acknowledged that the file had been at the High Court since June 2024 following a constitutional ruling.

However, the Chief Resident Magistrate assured to recover the file within the day and a new date will be set for the trial.

Meanwhile, the two children's rights activists have assured that they will closely monitor the progress of the case until justice is served in the matter.

SABATA YATHUNTHU OPANDA MAGETSI PA CHIPATALA CHA BWAILA.Sabata ya nthunthu ndimasiku angapo adutsa, chipatala cha Bwaila...
22/12/2024

SABATA YATHUNTHU OPANDA MAGETSI PA CHIPATALA CHA BWAILA.

Sabata ya nthunthu ndimasiku angapo adutsa, chipatala cha Bwaila chikukakamizika kubweza odwala omwe avutika mano kamba koti mbali imodzi ya chipatalichi magetsi adazima.

Tsamba lino lapeza kuti odwala mano akuwabweza kapena kuwauza kuti apite ku chipatala kwina chifukwa ku nthambi yoona za Mano ya chipatalachi kulibe magetsi.

Tsono ife tinafusa mneneri pa chipatalachi a Richard Mvula kuti tivetsetse, ndipo iwo atsimikizadi kuti zinthu zavutadi ku nthambiyi.

Iwo ati chipatalachi chikutumiza odwala akayakaya ku zipatala zapafupi kuphatikizapo za Kawale ndi Area 25 kuti akalandire thandizo kumeneko.

Komabe a Mvula ati adapereka kale uthega wokhudza vutoli ku unduna wa zaumoyo kuti uwathandize pa vutolo kamba koti ndi lalikulu ndithu.

21/12/2024

Manoma manoma
Flawless heart - nkhani plus

AKUTI ATHETSA BANK YA RESERVE KOMASO MALAMULO ADZIKO LINO NDIKUYALA ENA- MAHATIDennis Mahata yemwe wati ali ndi chidwi c...
21/12/2024

AKUTI ATHETSA BANK YA RESERVE KOMASO MALAMULO ADZIKO LINO NDIKUYALA ENA- MAHATI

Dennis Mahata yemwe wati ali ndi chidwi chodzapikisana nawo pa udindo wa mtsogoleri wa dziko lino chaka chamawa, wafanizira dziko lino ndi matenda akayakaya ochita kuwonera pakhosi ndipo ofunika thandizo la chipatala lamsanga.

Mahata walankhula izi pamsonkhano wa atolankhani omwe unachitika lero chakummawaku munzinda wa Lilongwe komwe anati zafikapa dzikoli silikufunikaso kuchita kudikira chisankho chachaka cha mawa kuti zinthu zisinthe, koma kuti aliyese afafanize kalikose ndikuchita kuyambiraso.

Mwazina mkuluyu wati mpofunika kuthetsa banki yaikulu mdziko muno ya Reserve ndikukhazikitsa ina yatsopano, ponena kuti ilipoyi palibe chomwe ikuchita pa chuma cha dziko lino.

Watinso malamulo akulu a dziko lino a Constitution m'chingerezi akufukikanso kukhazikitsa ena atsopano kuchotsa omwe alipo pakadali pano ponena kuti malamulo omwe alipo pakadali pano sakupindulira dziko la Malawi.

Ngakhale alankhula izi ndi mtsogoleri wa dziko yekha yemwe ali ndi mphamvu zochitira izi. Komabe Mahata watsindika kuti sakutengela malamulo m'manja mwawo ponena izi, koma kuti mavuto a m'dziko muno ndiwo akuwayankhulitsa zonsezi.

MPHEZI YAPHA OPHUZIRA ANAYI KU DOWA-UNDUNA WA MAPHUZIROMphezi yapha ophuzira anayi a pa sukulu yoyendera ya Kaungwe(CDSS...
30/11/2024

MPHEZI YAPHA OPHUZIRA ANAYI KU DOWA-UNDUNA WA MAPHUZIRO

Mphezi yapha ophuzira anayi a pa sukulu yoyendera ya Kaungwe(CDSS) ku Mponela m'boma la Dowa masana a lero.

mneneri mu unduna wa zamaphuziro Mphatso Mkuonera ndiye watitsimikizira zangoziyi.

Malinga ndi Mkuonera, mwaophuzirawa awiri ndi a form 1, komaso m'modzi wa mu form 2 ndi wina mu 3.

Mkuonera wati izi mzodandaulitsa kuti dziko lataya adindo a mtsogolo muno, ndipo undunawu wapempha makolo kuti azisamalira bwino ana maka nyengo ya mvulayi.

MUNTHU ASAKUBWATIKENI, MUNGAGWIRE THANGATA M'MAYIKO A ENI- CALEB THOLE.Pomwe anthu ochuluka akukhamukira m'maiko ena kus...
24/11/2024

MUNTHU ASAKUBWATIKENI, MUNGAGWIRE THANGATA M'MAYIKO A ENI- CALEB THOLE.

Pomwe anthu ochuluka akukhamukira m'maiko ena kusaka mwayi wa ntchito kamba ka mavuto a zachuma omwe alipo pa dziko lapansi, akatswiri odziwa bwino nkhani zokhudza kuba ndi kuzembetsa anthu achenjeza nzika za dziko lino ku matchela a atambwali ena omwe akutengera mwayi pomagulitsa anthu ku ukapolo m'mayiko akunja.

M'modzi wa akatswiriwa, Caleb Thole wati anthuwa amabwera ndi kunyengerera kozama maka pa nkhani yamalipiro zomwe zimakopa mosavuta anthu omwe alibe kalikose kuti akapita kunjako akatola chikwama mosavuta.

A Thole ati zafika poti anthu ena akungoyenda njira za chibulaki, wopanda ndi pasipoti yomwe, pomweso ambiri ena akugwirizana ndi ma ajenti osavomerezeka popita kumayikowa komwe zikawavuta kumeneko amasowa chochita.

Malinga ndi a Thole izi zimapereka mpanipani wopandapake pa chuma cha boma pomwe anthuwa akufuna kubwerera kumudzi zikawathina

Posachedwapa mzika zina zinachita kakasi mdziko la Kuwait, komwe adazindikira madzi atafika m'khosi, kuti amagwira thangata kumeneko akatchyali ena atawabwatika kuti akagwira ntchito zapamwamba kumeneko.

Pasuwa ndi mphuzitsi wa Flames wogwirizira, FAM yateroKinna phiri ndi young Chimodzi ndiwo ma technical advisor pomwe Pe...
01/11/2024

Pasuwa ndi mphuzitsi wa Flames wogwirizira, FAM yatero

Kinna phiri ndi young Chimodzi ndiwo ma technical advisor pomwe Peter Mponda ndi Pritchard Mwansa ndiwo othandizira Pasuwa

Address

Lilongwe

Telephone

+265991113334

Website

Alerts

Be the first to know and let us send you an email when The Beast. posts news and promotions. Your email address will not be used for any other purpose, and you can unsubscribe at any time.

Share