Luntha television

Luntha television Luntha TV A Catholic Television located in Malawi. Promoting Spiritual and Integral development of the viewers.

  Kuli mpungwepungwe ku dera la Dedza boma kutsatira zotsatira za bungwe la MEC zotsimikizika pomwe wapampando wa bungwe...
01/10/2025




Kuli mpungwepungwe ku dera la Dedza boma kutsatira zotsatira za bungwe la MEC zotsimikizika pomwe wapampando wa bungweli Annabel Mtalimanja analengeza kuti amene wapambana ku derali ndi a Howard Mzambweuluemba oyima pa okha omwe apeza ma voti 6, 174.

Yemwe anayimira chipani cha MCP a Gerald Kampanikiza ati ndi odabwa ndi zotsatirazi poti nkhani yi ili ku bwalo la milandu.

Iwo atinso Anapereka madando ku bungwe la MEC kutsatira zotsatirazi zomwe amafuna kuti azidzukutenso.

[Olemba Bridgette Mwanoka]

[Chithunzi cha a Kampanikiza]

 Mphuzitsi watimu ya Blue Eagles FC Deklek Msakakuona wati timu yawo ndiyokozeka kuteteza mpikisano wa FDH Bank Cup wach...
01/10/2025



Mphuzitsi watimu ya Blue Eagles FC Deklek Msakakuona wati timu yawo ndiyokozeka kuteteza mpikisano wa FDH Bank Cup wachaka chino.

Msakakuona walakhula izi pamene Lachinayi pa 2 October akhale akusewera nditimu ya Silver Strikers FC pa bwalo la Nankhaka.

Kumbali yake mphuzitsi watimu ya Silver Strikers FC Peter Mgangira wati nthawi yakwana tsopano yobweza chipogwe kamba koti timu ya Blue Eagles FC ndiyomwe inatulutsa timu ya Silver Strikers FC mu mpikisanowu.

Opanga mpikisano wa FDH Bank Cup adzatenga ndalama zokwana 35 Million kwacha.

(Olemba Patrick Phupha)

*Democracy ikukhwima*Wachiwili kwamtsogoleli wadzikolino yemwe akupita Dr.Micheal Usi lelo wakumana ndi wachiwili kwamts...
01/10/2025

*Democracy ikukhwima*

Wachiwili kwamtsogoleli wadzikolino yemwe akupita Dr.Micheal Usi lelo wakumana ndi wachiwili kwamtsogoleli wadzikolino yemwe akhale akulumbila loweluka likubwelali Dr .Jane Ansah.

Malingana ndizomwe Usi walemba patsambalake la Mchezo, iye wachita izi pofuna kuonetsetsa kuti Pali dongosolo posinthana ma office pomwe boma la DPP likhale likutenga chiongolelo

" Nthawi yochita ndale yatha, tsopano ndithawi yoika amalawi patsogolo" watelo usi.

Katswili wazandale Mavuto Bamusi wati kulolelana pakusinthana kwa ulamulilo komwe kukuchitika mdzikomuno kukusonyeza kuti democracy yamalawi ikukhwima.

Wolemba Robert Edward .

     International South African opposition leader Julius Malema has been found guilty on five counts related to the dis...
01/10/2025




International

South African opposition leader Julius Malema has been found guilty on five counts related to the discharge of a firearm during the Economic Freedom Fighters’ (EFF) 2018 anniversary celebrations in East London. The court ruled that Malema’s actions breached firearm control laws, putting public safety at risk during the crowded rally. The charges stemmed from widely circulated footage that appeared to show him firing a rifle into the air while addressing supporters.

While Malema has not yet been sentenced, the conviction carries a minimum sentence of two years and a maximum of 15 years in prison. Legal experts note that the severity of the punishment will depend on factors such as intent, circumstances, and whether the court considers him a repeat offender. The case has drawn nationwide attention, given Malema’s high-profile role as leader of the EFF and a vocal critic of South Africa’s ruling African National Congress.

01/10/2025

Banja Loyera Chilinde Choir 2

  Amayi awiri ndiwo apeza mipando ya aphungu anyumba yamalamulo m'boma la Neno pachisankho chomwe chinachitika pa 16 Sep...
01/10/2025


Amayi awiri ndiwo apeza mipando ya aphungu anyumba yamalamulo m'boma la Neno pachisankho chomwe chinachitika pa 16 September chaka chino.

Malingana ndi zotsatila zomwe bungwe la MEC lalengeza lachiwiri sabata ino, a Mary Maulidi Khembo omwe amayimila kum'mawa kwabomali apambana ndi mavoti 3,406 pomwe a Mutani Elliam Tambala omwe amayima kum'mwela kwabomali apambana ndi mavoti 4,841.

Yemwe anali phungu kumpoto kwa bomali a Thoko Tembo nawo ateteza mpando wawo pomwe apeza mavoti 11,305.

Nkulu oyensetsa ntchito za NICE ku Neno a Wallace Kudzala ati izi zasonyeza kuti ntchito yomwe bungweli limagwila yolimbikitsa amayi kutenga mbali pandale yotchedwa Nthawi Yawo, yakhala yopindula.

Aphungu onse omwe atenga mipandoyi ndi a chipani Cha Democratic Progressive Party (DPP).

Jane Chinkwita- correspondent
Credit: nation

  NsanjeWachiwiri kwa mkulu woona zilingazo zabungwe la Churches Action in Releif and Development (CARD) a Lameck Nkhoma...
01/10/2025


Nsanje

Wachiwiri kwa mkulu woona zilingazo zabungwe la Churches Action in Releif and Development (CARD) a Lameck Nkhoma anati akufuna kugwira ntchito yokonzekeretsa anthu womwe amayiwalidwa pokonzekera ntchito zangozi zogwa mwadzidzi.

A Nkhoma ayankhula izi Lachiwiri pomwe apereka chilinganizo kwa akuluakulu anthambi zaboma ku Nsanje ntchito yomwe ayigwire kwa Senior Chief Mlolo kuyambira October mpaka December chaka chino.

A Nkhoma anati "Tikufuna kufikira mawanja 350 anthu amaulumali, wokalamba, amayi woyamwitsa ndi ena womwe saganiziridwa powapatsa ndalama zamtukula pakhomo zokwanira K105 000 kwamiyezi yiwiri. Kupereka ndalama kumadera zomangira matchinga amadzi aja amati ma d**e popeza kuli mitsinje yayikulu yambiri monga Shire, Ruo, Milole, Muona - Thangadzi ndi Namichimba yomwe yimasefukira nthawi yamvula. Tikufuna kugwiritsa ntchito mauthenga azanyengo powasamutsira anthuwa kumtunda."

Bungweri likugwira ntchitoyi yomwe ndi yoyesera ndi ndalama zokwanira K166 miliyoni kuchokera kumabungwe a Norwegian Church Aid ndi DanChurchAid (NCADCA).

Wolemba: Martin Gela Jnr, Correspondent.
Credit: Nation

NsanjeYemwe amulengeza kuti wapambana ngati phungu wanyumba yamalamulo kumpoto kwaboma la Nsanje a Francis Folley athoko...
01/10/2025

Nsanje

Yemwe amulengeza kuti wapambana ngati phungu wanyumba yamalamulo kumpoto kwaboma la Nsanje a Francis Folley athokoza anthu am'derali powapatsa mwayi woti awatumikire ngati phungu.

Poyankhula ndi NationOnline m'mawa wa Lachitatu a Folley anati akalumburitsidwa ntchito yoyamba yikhala yokonza msewu wam'derali womwe umakatulukira ku Thabwa m'boma la Chikwawa.

A Folley anati ndiwokhumudwa kuti ku Muona - Fatima kuli anthu wolombikira pantchito zaulimi popeza amalima kwambiri mpunga, nyemba ndi mbewu zina koma amangopereka kwa mavenda potengera kuti misewu ndiyoonongeka kwambiri kuderali.

"Ndikufuna kuno kukhale kumalo kofikirika ndi wina aliyense. Ndilimbikitsa ntchito zaumoyo potengera kuti chipatala chomwe tilinacho pa Muona Fatima nchampingo, kulimbikitsa maphunziro popitiriza ntchito yomwe ndinayamba kale yopereka sukulu fizi komanso ulimi wamthilira pokonzanso ndi kukulitsa masikimu." Anatero a Folley.

Wolemba: Martin Gela Jnr, Correspondent.

NsanjeAtangolengeza wapampando wabungwe loyendetsa chisankho Justice Annabel Mtalimanja kuti a Walter McMillan Nyamiland...
01/10/2025

Nsanje

Atangolengeza wapampando wabungwe loyendetsa chisankho Justice Annabel Mtalimanja kuti a Walter McMillan Nyamilandu Manda woyima pawokha ndiwomwe apambana ngati phungu wanyumba yamalamulo m'dera lakummwera chakuzambwe kwaboma la Nsanje cham'ma 11 koloko usiku kunali phokoso paboma la Nsanje.

Nyimbo ngati "Mwana Ndimwana, Galamukani yoyimbidwa ndi Khumbo Kamba komanso Pangolin ya Jetu zimamveka kuyimbidwa m'magalimoto awiri womwe amayenda mosiyana kuzungulira paboma kukafika kwa Mbenje kwa TA Ngabu komanso ku Chididi ndi kwa Lambwe TA Malemia m'bomali.

Yemwe amathandizira ntchito zokopa anthu a Nyamilandu Manda a Gregory Sandram anati ndiwokondwa kuti ntchito yomwe anagwira yabereka zipatso ndipo anati akonzeka kutumikira anthu am'derali ndi chitukuko.

M'mawu awo a Nyamilandu Manda mwachidule anati akuyamikira Mulungu powathandiza ntchito yoti apambane ndipo alonjeza kutumikira anthu womwe awavotera m'derali.

A Nyamilandu Manda anati "Siine wopambana pa anthu asanu ndi atatu womwe timapikisana koma wopambana ndi anthu aku Nsanje kum'mwera chakuzambwe popeza asankha chitukuko. Ndiyesetsa kuti ndiyende nawo limodzi, tigwire ntchito limodzi potukula dera lathu. Mwazina ndikufuna kuti tikonze sekondale yathu ya Nsanje pakhale malo abwino woti ana adziti tili ndi sukulu wosati pano momwe ilili ndi bwinja."

Wolemba: Martin Gela Jnr, Correspondent.
Credit: Nation

NsanjeM'modzi mwa akuluakulu akunthambi zanyengo ndi kusintha kwanyengo Meteorogical Services a Edwin Fanuel Tadeyo ati ...
01/10/2025

Nsanje

M'modzi mwa akuluakulu akunthambi zanyengo ndi kusintha kwanyengo Meteorogical Services a Edwin Fanuel Tadeyo ati ulosi wanyengo dzinja yamvula yamchaka 2025 mpaka 2026 boma la Nsanje likhonza kulandira mvula yamulingo wokhazikika kapena kupyolera mulingo wokhazikika.

A Tedeyo ayankhula Lachiwiri ku Nsanje pomwe amakumana ndi atsogoleri wonwe amakghudzidwa ndi nkhani yamvula m'bomali.

A Tadeyo anati "M'miyezi ya November chaka chino ndi February mchaka cha 2026 mvula yikhonza kudzagwa chopera komanso tikhonza kudzakhala ndi ng'amba kwa sabata yimodzi yomwe yidzathandizire kuti alimi adzapalire komanso nthawi zina yimawaula zinthu zakumunda."

"Komabe mu January momwemo tikuyenera kudzakhala ndi mvula yochuluka kwambiri yofika pamlingo wa mamililitala 300 zomwe zofunika paulimi pothilira mbewu komanso zikupereka chiopsezo chamadzi wosefukira. Mvulayi yikuyenera kugwa kwamasiku 120 ndi 130 ndiye alimi akuyenera kugwiritsa ntchito mbewu zocha msanga." Anatero a Tadeyo.

Wolemba: Martin Gela Jnr, Correspondent.

  Karonga Apolisi m'boma la Karonga amanga bambo wa zaka 26 a Undule Mwakikunga, kaamba kogonana ndi mtsikana wa zaka 9 ...
01/10/2025


Karonga

Apolisi m'boma la Karonga amanga bambo wa zaka 26 a Undule Mwakikunga, kaamba kogonana ndi mtsikana wa zaka 9 yemwenso ndi mwana wa oyandikana nawo m'mudzi wa Mwambuli m'bomali.

Nkhaniyi ikuti mayi ake a mtsikanayu amachita bizinesi ya zophika mtauni zomwe zimapangitsa kuti asamapezeke kwambiri pakhomo komanso kuti bamboyu azitengerapo mwayi pompatsanso mtsikanayu ndalama kuti asamaulure.

"Pa 26 September 2025 monga mwa chizolowezi, a Mwakikunga analowetsanso mtsikanayu m'nyumba mwawo ndipo akwawo anayamba kumuyang'ana mpaka m'mawa wa pa 27 September, pamene mtsikanayu anaulura kuti wagona m'nyumba ya a Mwakikunga, zomwe iwonso sanakane atafunsidwa," mneneri wa polisi m'bomali, a Margret Msiska adatero poyankhulapo.

Nazo zotsatira za kuchipatala zinaonetsa kuti mwanayu wakhala akuchitidwa zimenezi kokwana ka 6 konse.

A Mwakikunga, omwe akuchokera m'mudzi wa Mwambuli, mfumu yaikulu Kyungu m'boma la Karonga, akawonekera ku bwalo la mlandu kukayankha mlanduwu womwe ukusemphana ndi gawo 138 la malamulo m'dziko lino.

(Wolemba: Sekile Kitalu-Correspondent)
Credit: Nation

  Mlembi wa komiti ya chitukuko cha m'mudzi ya Lusani 1 m'boma la Rumphi a Moses Nyoni apempha adindo kuti apeze njira z...
01/10/2025



Mlembi wa komiti ya chitukuko cha m'mudzi ya Lusani 1 m'boma la Rumphi a Moses Nyoni apempha adindo kuti apeze njira zothesera mchitidwe ogwiritsa ntchito ana mu minda ya fodya zomwe zikuchititsa kuti ana azisiyira sukulu pa njira komanso kukwatiwa ali achichepere mdera lawo.

A Nyoni anena izi pa zokambirana zomwe bungwe la Chikulamayembe Women Forum linakonza ndi thandizo la ndalama kuchokera ku Action Aid Malawi kuti adindo apereke mayankho a mavuto osiyanasiyana omwe anthu akukumana nawo makamaka nkhani za nkhanza zomwe amayi, atsikana ndi ana amakumana nazo.

Iwo ati mchitidwe ogwiritsa ntchito ana mu minda ya fodya komanso ma banja a ana achichepere wakula kwambiri mdelari ndipo pakufunika adindo achite machawi pothana ndi mavutowa.

Mkulu owona za chisamaliro cha anthu ku khonsolo ya boma la Rumphi a Zindawa Lungu ati akudziwa za mavutowa ndipo akugwira ntchito limodzi ndi unduna owona za ntchito komanso ma bungwe m'bomali kuti athane ndi mavutowa.

Mkulu wa bungwe la Chikulamayembe Women Forum, a Tiwonge Gondwe ati iwo ndiwokhutira ndi ndondomeko zomwe adindo ayika kuti athandize kuthana ndi mavuto omwe anthu akukumana nawo m'bomali.

(Wolemba: Taonga Chizinga Nyirenda-Correspondent)

Address

Luntha Tv, Area 2
Lilongwe

Alerts

Be the first to know and let us send you an email when Luntha television posts news and promotions. Your email address will not be used for any other purpose, and you can unsubscribe at any time.

Contact The Business

Send a message to Luntha television:

Share

Category