01/10/2025
Kuli mpungwepungwe ku dera la Dedza boma kutsatira zotsatira za bungwe la MEC zotsimikizika pomwe wapampando wa bungweli Annabel Mtalimanja analengeza kuti amene wapambana ku derali ndi a Howard Mzambweuluemba oyima pa okha omwe apeza ma voti 6, 174.
Yemwe anayimira chipani cha MCP a Gerald Kampanikiza ati ndi odabwa ndi zotsatirazi poti nkhani yi ili ku bwalo la milandu.
Iwo atinso Anapereka madando ku bungwe la MEC kutsatira zotsatirazi zomwe amafuna kuti azidzukutenso.
[Olemba Bridgette Mwanoka]
[Chithunzi cha a Kampanikiza]