Luntha television

Luntha television Luntha TV A Catholic Television located in Malawi. Promoting Spiritual and Integral development of the viewers.

29/10/2025



Bwalo la Principal Resident Magistrate ku Lilongwe lati lipeleka chigamulo chake mawa, papempho la belo lomwe anthu 9 omwe akuwaganizila kuti adamenya, kukhapa ndikuchita chipongwe Sylvester Namiwa apeleka.

Anthu asanu ndi anayiwa akana milandu yonse isanu ndi umodzi (6).

Mmodzi mwaoimila milandu mbali yaboma Senior supretendent Moja Phiri wati iwo atsutsa pempho labeloli chifukwa anthuwa akatuluka akhonza kuthawa mwazina, pomwe yemwe akuimila oganizilidwawa Chrispine Mndala wati oganizilidwawa sangathawe chifukwa ali ndi mawanja, komanso amachita malonda awo mu Lilongwe mommuno mwazina.

Wolemba Robert Edward.

  The 28 Malawian pilgrims who traveled to Rome last week have safely landed back into the country through Kamuzu Intern...
29/10/2025


The 28 Malawian pilgrims who traveled to Rome last week have safely landed back into the country through Kamuzu International Airport.

29/10/2025



Aphungu a nyumba yamalamulo akuponya voti yosankha sipikala wa nyumba ya malamulo.

Phungu wa nyumba ya malamulo wa dera Dowa East Richard Chimwendo Banda anapempha Mlembi wamkulu wa nyumbayi kuti aphungu asamalowe ndi foni mubokosi lovotera, zomwe Mlembi yu anavomerezana nazo.

Olemba Gift Kalonga

29/10/2025



Phungu wa Dedza Mlunduni Constituency Moses Kunkuyu wati kusankhidwa kwa a Peter Dimba kuti aimire pa mpikisano wa sipikala wa nyumba ya malamulo kwadza ataunikira maphunziro awo komanso ukadaulo omwe alinawo pa ntchito

A dimba anakhalapo wachiwiri kwa nduna ya za mayendedwe.

Maphunziro awukachenjede komanso kudziwa kagwiridwe ka ntchito mwa ukadaulo ndiye mtsanamira ya Dimba, anatero a Kunkuyu .

Wolemba Moses Makawa

29/10/2025



Phungu wa nyumba ya malamulo ku Karonga Central Frank Tumpale Mwenifumbo ndiye anaima kufotokoza mbiri ya a Sameer Suleman a chipani cha DPP, ndipo m'mawu ake Iye waikila kumbuyo ganizo loti a Suleman asankhidwe pa udindo wa sipikala wa nyumba ya malamulo ponena kuti ali ndi ukadaulo komanso mtima olimbikira pa chitukuko cha dziko lino.

Phungu wa Thyolo Thava Mary Navitcha naye waikira kumbuyo Suleman ponena kuti ndi munthu yemwe alindi khalidwe komanso osaonetsa mbali pogwira ntchito ndipo amatsogoza zofuna za anthu.

Wolemba Moses Makawa

29/10/2025



Aphungu a nyumba ya malamulo okwana 221 ndi omwe abwera kuzatenga nawo mbali pa ntchito yosankha sipikala wa nyumba ya malamulo.

Mlembi wa Nyumbayi Fiona Kalemba walengeza kuti analandila makalata asanu kuchokera kwa a phungu omwe awonetsa chidwi chofuna kukhala sipikala, koma ati kalata ya Kondwani Nankhumwa ayikana chifukwa idachedwa komanso ndizosatheka kuti apikisane aphungu 5 pa mpandowu kotero apikisana aphungu 4 omwe anayambilira kupereka zikalata zawo.

Olemba Gift Kalonga

29/10/2025



Pakadali pano Aphungu anyumba ya malamulo akuchita ndondomeko younika kuti adziwe ngati onse afika mu nyumbayi

Yemwe asankhidwe lero ngati sipikala akuyenera kutsogolera nyumbayi kwa zaka zisanu zikubwerazi.

Wolemba Moses Makawa

29/10/2025



Aphungu a nyumba ya malamulo asonkhana munyumbayi masana ano pomwe akuyembekezera kusankha sipikala wanyumbayi.

Aphungu atatu akupikisana pa mpandowu, omwe ndi Sameer Suleman wachipani cha DPP, Kondwani Nankhumwa wa chipani cha PDP komanso Peter Dimba wachipani cha MCP.

Phungu woyima payekha George katunga Million walengeza kuti sapikisana nawo ndipo wati asankha Sameer Suleman.

Wolemba Gift Kalonga

29/10/2025

LUNTHA TV | Election of the Speaker and Deputy Speakers of the National Assembly | 29 OCTOBER 2025

29/10/2025

LUNTHA TV | Group four Swearing in of Members of Parliament Elect | 29 OCTOBER 2025

29/10/2025

LUNTHA TV | NEWS UPDATES | 29 OCTOBER 2025

    The Malawi Economic Justice Network (MEJN) has commended the Malawi Government for its stand to ban the exportation ...
29/10/2025



The Malawi Economic Justice Network (MEJN) has commended the Malawi Government for its stand to ban the exportation of raw materials and products from Malawi's minerals.

MEJN Executive Director Bertha Lipipa Phiri said this during an interview on the sidelines of an annual partners meetings of all NCA DCA partners in Malawi held at the Sunbird Lilongwe Hotel.

Lipipa Phiri noted that it was disheartening to see Malawi's economy nosediving while others are milking from it.

MEJN is implementing a project that is fighting inequalities in Mangochi with funding from the NCA DCA Malawi.

Reported by Sam Kalimba.

Address

Luntha Tv, Area 2
Lilongwe

Alerts

Be the first to know and let us send you an email when Luntha television posts news and promotions. Your email address will not be used for any other purpose, and you can unsubscribe at any time.

Contact The Business

Send a message to Luntha television:

Share

Category