
29/07/2025
Annie Namani Chibwana yemwe akuima payenkha pampando wa phungu wanyumba yamalamulo mdera la pakati m'boma la Dowa walonjeza kusintha zinthu derali komaso kuthana ndi ndale zoopsezana zomwe wati zayipitsa chithuzuthuzi cha derali maka pa Mponela.
Chibwana wanena izi lero pasukulu ya Mponela 2 pomwe amapereka kalata zake zofuna kuima nawo pa mpandowu.
Iye wati muzaka zisanu ndi chimodzi 6 zapitazi palibe chilichose chomwe chachitika ngakhale kuti boma limaika ndalama zokwana 220 miliyoni kwacha zachitukuko.
Apa iye wapempha anthu kuti amuvotere ndicholinga choti ndalama yachitukuko ya CDF idzagwile ntchito yake komaso kuti anthu ayambe kugula mwa mtendere chimanga ku ADMARC komaso feteleza wa AIP mosavuta osati mavenda okha.
Chibwana wapereka kalatazi pamodzi ndi Chisomo Makwecha yemwe akufuna kuimira ku dera la khansala la kumadzulo kwa Mpanda ndi Abraham Samu yemwe akuima ku dera la ku mmawa la khansala la Mpanda.
Wolemba Philord Kamagunda Magalasi