18/10/2025
Timu ya Silver Strikers yapeza chipambano mmasewero ampikisano wa Caf Champions league pa bwalo la zamasewero la Bingu mzinda wa Lilongwe.
Phunzitsi wa mkulu watimu ya Silver Strikers Peter Mgangila wauza Dowa FM Online kuti ngakhale agonjetsa timu ya Young African FC (yanga) wati sizinali zophweka kupeza chipambanochi koma kuti anyamata analimbikila.
Mgangila watiso timu ya Young African FC ndi timu yabwino ndipo wati yawapatsa mpira wabwino.
Silver Strikers inapeza chigoli mchigawo chachiwiri pa mphindi 75 kuchokera kwa Andrew Josephy yemwe analandila mpira kwa Ernest Petrol.
Timu ya Silver Strikers ikuyembekeza kulowera mdziko la Tanzania kukasewera ndi timuyi mmasewero achibwereza pa bwalo la Benjamin mkapa.
Wolemba Peter Kawaza