DOWA FM

DOWA FM A media house that stands on journalistic principles, providing well verified and balanced news.

Timu ya Silver Strikers yapeza chipambano mmasewero ampikisano wa Caf Champions league pa bwalo la zamasewero la Bingu m...
18/10/2025

Timu ya Silver Strikers yapeza chipambano mmasewero ampikisano wa Caf Champions league pa bwalo la zamasewero la Bingu mzinda wa Lilongwe.

Phunzitsi wa mkulu watimu ya Silver Strikers Peter Mgangila wauza Dowa FM Online kuti ngakhale agonjetsa timu ya Young African FC (yanga) wati sizinali zophweka kupeza chipambanochi koma kuti anyamata analimbikila.

Mgangila watiso timu ya Young African FC ndi timu yabwino ndipo wati yawapatsa mpira wabwino.

Silver Strikers inapeza chigoli mchigawo chachiwiri pa mphindi 75 kuchokera kwa Andrew Josephy yemwe analandila mpira kwa Ernest Petrol.

Timu ya Silver Strikers ikuyembekeza kulowera mdziko la Tanzania kukasewera ndi timuyi mmasewero achibwereza pa bwalo la Benjamin mkapa.

Wolemba Peter Kawaza


Mtsogoleri wa dziko lino Professor Arthur Peter Mutharika  wasankha Roza Fatch Mbilizi kukhala nduna ya za ulimi ndi chi...
17/10/2025

Mtsogoleri wa dziko lino Professor Arthur Peter Mutharika wasankha Roza Fatch Mbilizi kukhala nduna ya za ulimi ndi chitukuko cha madzi komanso a George Partridge kukhala nduna ya makampani, malonda ndi zokopa alendo.

A Rose Mbilizi omwe ndi Phungu wa dera la pakati ku Mangochi adagwirapo ntchito ku bungwe lotolera misonkho mdziko muno la Malawi Revenue Authority (MRA) ngati wachiwiri kwa komishinala.

A George Partridge omwe asankhidwa kuti akhale nduna ya makampani, malonda ndi kuona ntchito zokopa alendo amadziwika kwambiri pa nkhani zoyendetsa bwino chuma cha makampani.

A Partridge adakhalapo mkulu wa banki ya National, agwirapo ntchito ndi banki yaikulu ya Reserve kwa zaka zoposa khumi komanso agwirapo ntchito ngati mkulu woyang'anira ntchito za kampani ya Malawian Airlines, Telecom Networks Malawi ndi Sunbird Tourism.

Mlembi wamkulu wa mu ofesi ya mtsogoleri wa dziko lino ndi nduna Dr Justin Saidi ndi omwe atsimikizira za kusankhidwa kwa nduna ziwirizi ndipo pakadali pano nduna zonse zakwana zisanu.

Wolemba: Damiano Fredson Kalajira


13/10/2025

Timu ya mpira wa miyendo ya dziko lino ya Flames yalephera kudzigulira malo a mpikisano wa FIFA World Cup 2026 pomwe yagonja ndi timu ya Sao Tome and Principle masewero omwe anachitika mdziko la Tunisia ndi chigoli chimodzi kwa chilowere.

Timu ya Malawi mugulu H yamaliza pa nambala ya chinayi ndi mapoitsi 13 pomwe Sao Tome and Principle yamaliza ndi mapoitsi 3 pansi pagulu la nambala 6

Timu ya Tunisia ndiyomwe yatsogolera gulu H ndi mapoitsi 28 pa nambala yachiwili pali timu ya Namibia ndi mapoitsi 15.

Timu ya Malawi ikhale ikubwerera kumudzi kuchokera dziko la Tunisia itagonja ndi mchigawo chachiwiri pa mphindi 62 kudzera pa penate yomwe anagoletsa ndi Ronaldo Lumungo Afonso.

Wolemba Peter Kawaza


Dowa District Council has commended Zoe Empowers for its commitment to uplifting the lives of orphaned and vulnerable yo...
11/10/2025

Dowa District Council has commended Zoe Empowers for its commitment to uplifting the lives of orphaned and vulnerable youths in Dowa District.

The Council's Chief of Administration, Mathews Mkandawire, made the remarks during the graduation ceremony of 393 youths from the organization's empowerment program.

Mkandawire noted that Zoe Empowers is making a lasting impact on these young people, thereby also complementing the government's 2063 development agenda.

Esther Chinkhadze, Senior Programme Facilitator for Zoe Empowers Malawi, said the graduation marks the achievement of the organization's goals and expressed commitment to doing more.

One of the graduates Nelson Mandala expressed that his life has changed for the better, thanking Zoe Empowers for the positive impact.

By Gladys Chimphanga


Wailesi ya Dowa Fm yapereka thandizo la njinga komaso katundu osiyanasiyana kwa Innocent Charles wa mmudzi wa Malowa mfu...
10/10/2025

Wailesi ya Dowa Fm yapereka thandizo la njinga komaso katundu osiyanasiyana kwa Innocent Charles wa mmudzi wa Malowa mfumu yaikulu Mponela boma la Dowa.

Motsogozedwa ndi mkulu wa wailesi ya Dowa, wailesi yi yapereka thandizo lanjinga komaso katundu wina monga sopo,zakudya ndi sobo.

Poyakhurana ndi Dowa Fm fm Online Charles Masalanga yemwe ndi bambo ake a Innocent ,iwo ati ndi chisomo cha Ambuye polandira thandizo ngati limeneli ndipo athokoza wailesi ya Dowa.

Mmawu ake mfumu Malowa inati ndiyosangalala komaso othokoza Dowa Fm kamba koti njingayi ithandiza kuti mayendedwe asakhale ovuta kwa mwana yemwe walandira thandizoli

"Njinga imeneyi imuthandiza kuti azitumikira komaso kumacheza ndi anzake mosavuta "anatero Malowa.

Poyakhurapo mkulu wa wailesi ya Dowa Manase Chitedze anati anachiona kuti mchabwino kuti mwana yemwe walandira thandizo li akhale nawo opindura ndi wailesi ya Dowa kuti asakhale ndi vuto la mayendedwe .

Wolemba : Patrick Chafukira


Mkulu wa bungwe lomenyera ufulu wa atolankhani mdziko muno la Media Institute of Southern African( MISA)- Malawi   Golde...
10/10/2025

Mkulu wa bungwe lomenyera ufulu wa atolankhani mdziko muno la Media Institute of Southern African( MISA)- Malawi Goldern Matonga wadandaula ndi mchitidwe wonyazitsa, kuopseza komanso kuzunza atolankhani omwe zipani zina ndi otsatira ake akuchita.

Dandauloli likudza kutsatira kalata yomwe chipani cha Malawi Congress Party (Mcp) idatulutsa posachedwapa yodzudzula nyumba yowulutsira mau ya Times ndi mtolankhani wake Cathy Maulidi ponena kuti adalemba nkhani yopanda umboni kweni-kweni yokhudza kuonongeka kwa nyumba ya chifumu( State house) yomwe ili mu mzinda wa Lilongwe.

Anthu omwe akuganiziridwa kuti ndi wotsatira chipani cha Mcp akhala akuopseza komanso kulemba mau womunyoza mtolankhaniyu pa masamba a mchezo chifukwa chakuti adalemba ndi kuulutsa nkhani ya kuonongedwa kwa nyumba ya chifumuyi mu nthawi yomwe mtsogoleri wa kale wa dziko lino Dr Lazarus Chakwera amafuna kupereka mphamvu kwa mtsogoleri wa dziko lino Professor Peter Mutharika.

A Matonga akumbutsa anthu mdziko lino kuti gawo 36 la malamulo akulu a dziko lino limateteza ufulu wa atolankhani wolemba ndi kuulutsa nkhani mopanda kuopsedwa ndipo wa pempha anthu kuti ngati ali ndi madandaulo a momwe atolankhani akugwirira ntchito azikapereka madandaulowa ku nthambi zoyenerera monga MISA- Malawi.

A Matonga ati posachedwapa ena mwa atolankhani wogwira ntchito ku wailesi ya Malawi Broadcasting Corporation(MBC) akhala akulandiranso zipongwe kuchokera kwa anthu otsatira zipani zina kuti adalembedwa ntchito motsatsata malamulo chifukwa choti amamvana kwambiri ndi boma lapitali zomwe a Matonga adandaula kuti mchitidwewu ngosayenera chifukwa uli ndikuthekera kosoneza ntchito za atolankhani mdziko muno.

Wolemba: Damiano Fredson Kalajira.

09/10/2025

Ana atatu ku Dowa amwalira pomwe wachinayi wapulumuka nyumba yomwe amasewereramo itayaka moto.

Izi zachitika pa 8 October nthawi ya 6 koloko madzulo mmudzi mwa Kachisa kwa senior Dzoole m'boma la Dowa.

Sergeant Macpatson Msadala mneneri wa polisi ya Mponela wauza Dowa FM kuti omwalirawa ndi Joas Gledson, Onesiano Eliya, azaka zisanu ndi Sydney Josephy wazaka zitatu.

Msadala wati patsiku latsokali anawa adapita kukasewera m'nyumba ya mayi wina Abiti Manesi yomwe imamangidwa.

Iye anapitiliza kunena kuti pomwe amasewera, mwana wina anayatsa udzu mwangozi, ndipo mapeto ake anapsa ndi motowo.

Zotsatira za kuchipatala zaonetsa kuti anawa amwalira kamba kobanika ndi moto.

Wolemba Khumbo Chiudzu


Ogwila ntchito ku kampani ya zomangamanga ya Sanga Construction atchinga pachipata cholowera ku kampani ya Smed yomwe im...
09/10/2025

Ogwila ntchito ku kampani ya zomangamanga ya Sanga Construction atchinga pachipata cholowera ku kampani ya Smed yomwe imathandiza anthuwa kulandira malipiro awo apamwezi kamba kosawapatsa malipiro munthawi yoyenera.

Polankhula ndi Dowa Fm Online m'modzi mwa ogwila ntchito, yemwe wati tisamutchule dzina wati iwo amayenera kulandila makobidi awo pa 27 mwezi watha ndipo kufika lero alibe chiyembekezo chilichonse izi ndi malingana ndizomwe akulu akulu awo akuwayankha.

Anthuwa ati moyo wawo ukukumana ndizokhoma maka pa nkhani ya chakudya, malo ogona, komaso chisamaliro chamawanja awo.

Wolemba Chifuniro Smoke


Bungwe la Football Association of Malawi  (FAM) yati  masewero a FIFA World Cup odzigulira malo omwe amayenera kusewered...
09/10/2025

Bungwe la Football Association of Malawi (FAM) yati masewero a FIFA World Cup odzigulira malo omwe amayenera kuseweredwa madzulo a tsiku la lero pa 9 October 2025 pa bwalo la Bingu mu mzinda wa Lilongwe apakati pa timu ya Malawi komaso Equatorial Guinea sakhalapo kamba koti timu ya Equatorial Guinea yalephera kufika chifukwa cha vuto la mayendedwe

Izi ndi malinga ndi chikalata chomwe FIFA yatulutsa masanawa.

Football Association of Malawi ikhala ikufotokoza za m'mene achitile angakhale kuti anthu ochuluka anaguliratu matikiti oti akaonerere masewero omwe alepherekawa.

Wolemba Peter Kawaza


#

Mwambo wachisangalaro omwe umatchedwa Tumain festival ku msasa wa Dzaleka m'boma la Dowa wabweraso chaka chino kuyamba p...
09/10/2025

Mwambo wachisangalaro omwe umatchedwa Tumain festival ku msasa wa Dzaleka m'boma la Dowa wabweraso chaka chino kuyamba pa 30 October mpaka pa 1 November.

Kumwambowu kumakhala oyimba osiyanasiyana akuno ku Malawi ngakhaleso a mayiko ena, magule achikhalidwe monga gule wankulu, mganda, chimtali ndi ena ambiri.

Mutu wa chaka chino pa mwambowu ndi "Kukwera, kukhazikika, ndikupilira pa zovuta"

Tumain festival idayamba mu chaka cha 2016 ndi cholinga chofuna kubweretsa umodzi, kuphunzitsana za chikhalidwe pakati pa anthu okhala mu msasa wa Dzaleka ndi madera ozungulira ndipo imakhalako chaka chilichonse.

Wolemba : Patrick Chafukira


08/10/2025

Bungwe lomenyera ma ufulu a azimai, ana ndi azibambo la Coalition for the Empowerment of Women and Girls CEWAG kudzera kwa mmodzi wa akuluakulu ku bungweri Elijah Kawonga, wati atsikana akuyenera kusamalitsa pochita maubale pamene anthu omanga msewu wa M1 kufika ku Kasungu akugwira ntchito yawo mdelari.

Izi zalankhulidwa pamene bungwe la CEWAD limakumana ndi ana akazi pa sukulu ya Mataka kwa TA Chimutu ku Lilongwe.

Polankhulana ndi Dowa FM Online iye watsindikanso kunena kuti atsikana apa sukulu yi apewe kuchita zibwezi ndi anthu ogwira ntchito ponena kuti zitha kuwabweretsera mavuto pa nthawi yomwe akuchita maphunziro awo.

Wolemba Gracious Jumbe


M'modzi mwa adindo ku bungwe la M1 Rehabilitation Project GBV Service, Child Protection Worker, Moreen Banda wati atsika...
08/10/2025

M'modzi mwa adindo ku bungwe la M1 Rehabilitation Project GBV Service, Child Protection Worker, Moreen Banda wati atsikana apasukulu ya Mataka kwa mfumu yaikulu Chimutu ku Lilongwe akuyenera kupewa kupereka thupi lawo kwa anthu amene akugwira ntchito yomanga nsewu powanyengelera ndi zinthu zosiyanasiyana.

Polankhula ndi Dowa FM, Iye wati atsikana ndi golide ndipo sakuyenera kugulitsa thupi lawo mophweka ponena kuti akugwira ntchito wo si anthu akuno ndipo ali ndi mawanja awo.

Mlembi wabungweri Mary Kutchire waonjezera kunena kuti makolo apewe kuwatuma ana kuti adzikafika pamene ntchito yomanga nsewu ikuchitikira maka nthawi ya makalasi kuwopa kuchita zosakhala bwino ndi ogwira ntchitoyo.

Izi zalankhulidwa pamene amakumana ndi ana asukuli yi ku Lilongwe pamene akuyembekezera kuyamba kumanga nsewu umene udulitsire kufupi ndi sukulu yi.

Wolemba Gracious Jumbe


Address

Mponela

Telephone

+265991561861

Website

Alerts

Be the first to know and let us send you an email when DOWA FM posts news and promotions. Your email address will not be used for any other purpose, and you can unsubscribe at any time.

Contact The Business

Send a message to DOWA FM:

Share