DOWA FM

DOWA FM A media house that stands on journalistic principles, providing well verified and balanced news.

Annie Namani Chibwana yemwe akuima payenkha pampando wa phungu wanyumba yamalamulo mdera la pakati m'boma la Dowa walonj...
29/07/2025

Annie Namani Chibwana yemwe akuima payenkha pampando wa phungu wanyumba yamalamulo mdera la pakati m'boma la Dowa walonjeza kusintha zinthu derali komaso kuthana ndi ndale zoopsezana zomwe wati zayipitsa chithuzuthuzi cha derali maka pa Mponela.

Chibwana wanena izi lero pasukulu ya Mponela 2 pomwe amapereka kalata zake zofuna kuima nawo pa mpandowu.

Iye wati muzaka zisanu ndi chimodzi 6 zapitazi palibe chilichose chomwe chachitika ngakhale kuti boma limaika ndalama zokwana 220 miliyoni kwacha zachitukuko.

Apa iye wapempha anthu kuti amuvotere ndicholinga choti ndalama yachitukuko ya CDF idzagwile ntchito yake komaso kuti anthu ayambe kugula mwa mtendere chimanga ku ADMARC komaso feteleza wa AIP mosavuta osati mavenda okha.

Chibwana wapereka kalatazi pamodzi ndi Chisomo Makwecha yemwe akufuna kuimira ku dera la khansala la kumadzulo kwa Mpanda ndi Abraham Samu yemwe akuima ku dera la ku mmawa la khansala la Mpanda.

Wolemba Philord Kamagunda Magalasi

Dr Michael Usi omwe ndi mtsogoleri wa chipani cha Odya zake wabwereza kunena kuti akadzalowa m'boma adzachotsa ntchito k...
29/07/2025

Dr Michael Usi omwe ndi mtsogoleri wa chipani cha Odya zake wabwereza kunena kuti akadzalowa m'boma adzachotsa ntchito kapena kumangitsa anthu onse omwe sadzigwira ntchito zawo mwadongosolo.

Polankhula ku khwimbi la anthu omwe adasonkhana kuja kwa BICC Dr Usi ati pali adindo ena a boma amene ali ndi khalidwe logwira ntchito mwachidodo ndipo khalidweli lili ndikuthekera kobwezeretsa chitukuko cha dziko m'mbuyo komanso zopangitsa kuti anthu kuyamba azinyoza mtsogoleri wa dziko.

Dr Usi wapempha womusatira ake kuti asakopeke ndi ndalama kapenanso zovala za zipani zomwe anthu omwe akufuna kupikisana nawo pa mpando wa utsogoleri wa dziko akupereka chifukwa zoterezi zili nkuthekera kodzavotera atsogoleri omwe sadzakwanitsa kuphula anthu pa moto omwe ambiri akuumva chifukwa chakusayenda bwino kwa chuma.

Mtsogoleri wa Odya zake-yu wabwerezanso kunena kuti iye sadzatukwana atsogoleri omwe adalamulirapo dziko lino kuphatikizapo mtsogoleri wa dziko lino Dr Lazarus Chakwera komanso wapempha womusatira ake kuti asamaimbe nyimbo zonyoza atsogoleri a zipani zina.

Dr Usi wati adzaika ndondomeko za bwino zothanirana ndi mavuto omwe akuta dziko lino ndipo adafunira za bwino zonse atsogoleri a zipani zina omwe akupikisana nawo pa zisankho zikubwerazi.

Wolemba: Damiano Fredson Kalajira.

Mtsogoleri wa chipani cha Odya zake Alibe Mulandu Dr Michael Bizwick Usi asankha mai Grace Nazitwere kukhala wa chiwiri ...
29/07/2025

Mtsogoleri wa chipani cha Odya zake Alibe Mulandu Dr Michael Bizwick Usi asankha mai Grace Nazitwere kukhala wa chiwiri wawo pa chisankho chomwe chikhaleko pa 16 September chaka chino.

Dr Usi ati akakamizika kupikisana nawo pa mpando wa utsogoleri pa zisankho zikubwerazi chifukwa ukadaulo omwe aphunzira wokhudza kayendetsedwe ka ntchito za boma kuchokera pomwe malemu Dr Saulosi Chilima adawasankha kukhala wachiwiri wawo.

Dr Usi ati anthu onse omwe akufuna kupikisana nawo ali ndi mfundo za bwino zokopa anthu koma chomwe chikupangitsa kuti dziko lino lisamachite bwino pa chitukuko ndikulephera kwa adindo kochita zinthu molondola.

Mtsogoleri wa Odya zake-yu walangiza anthu omwe akupikisana pa zisankhozi kuti athe kupanganso pulani ya zomwe atachite akadzalephera zisankho.

Wolemba: Damiano Fredson Kalajira.

# KubweretsaChiyembekezoKuDera

Dr Cassim Chilumpha yemwe ndi mtsogoleri wa chipani cha Assembly For Democracy and Development (ADD)  sapikisana nawo pa...
29/07/2025

Dr Cassim Chilumpha yemwe ndi mtsogoleri wa chipani cha Assembly For Democracy and Development (ADD) sapikisana nawo pa mpando wa utsogoleri wa dziko lino pa zisankho zomwe ziliko mu September ndipo m'malo mwake agwira ntchito ndi chipani cha People's Party.

Dr Chilumpha omwe lero amayembekezereka kupereka zikalata zawo ku bungwe la Malawi Electoral Commission (MEC) ati chiganizochi chabwera ndi cholinga chofuna kupulumutsa a Malawi ku mavuto omwe akukumana nawo.

Mneneri wa ADD a Lameck Sapuwa auza Dowa FM Online kuti chipani chawo chapanga mgwirizano ndi chipani cha PP chomwe chikutsogoleredwa ndi Dr Joyce Banda kuti agwire ntchito limodzi yofuna kutukula miyoyo ya a Malawi.

Dr Joyce Banda adali munthu woyamba kupereka zikalata zake zosonyeza kuti apikisana nawo pa mpando wa utsogoleri wa dziko lino pa zisankho zikubwerazi ndipo adasankha a Khumbo Kachali yemwe ndi mtsogoleri wa chipani cha Freedom Party (FF) kukhala wachiwiri wake.

Wolemba: Damiano Fredson Kalajira.

Yemwe akufuna kuima nawo ngati phungu wanyumba yamalamulo mdera la pakati m'boma la Dowa pansi pa chipani cha Malawi Con...
28/07/2025

Yemwe akufuna kuima nawo ngati phungu wanyumba yamalamulo mdera la pakati m'boma la Dowa pansi pa chipani cha Malawi Congress Darlington Harawa lero wapereka kalata zake zofuna kuimira pampandowu pachisankho chapa 16 September.

Harawa wati ndiokondwa kamba koti bungwe loyendetsa chisankho la MEC lavomera kalatazi ndipo walonjeza kuti achita ntchito yokopa anthu mderali mwabata ndi mtendere.

Apa iye wapempha anthu kuti adzamuvotere pachisankhochi ndi cholinga choti apitilize zitukuko ku derali zomwe wati adayamba kale kuchita.

Ndipo kumbali yake oyimira bungwe la MEC Ku derali Joyce Makwecha walimbikitsa oyimilawa kuti atsamile kwambiri mfundo pa ntchito yokopa anthu osati kunyozana.

Pakali pano bungwe loyendetsa chisankho mdziko muno la Malawi Electoral Commission (MEC) lili pakalikiliki kulandila kalata kuchokera kwa omwe akufuna kuyimira pachisankho chaka chino, ntchito yomwe yayamba pa 24 July ndipo ikutha pa 30 mwezi omwe uno.

Wolemba Philord Kamagunda Magalasi


Mtsogoleri wa chipani cha United Transformation Movement (UTM) Dr Dalitso Kabambe asankha Dr Mathews Mtumbuka kukhala ch...
27/07/2025

Mtsogoleri wa chipani cha United Transformation Movement (UTM) Dr Dalitso Kabambe asankha Dr Mathews Mtumbuka kukhala chiwiri wawo pa chisankho cha pa 16 September.

Dr Kabambe ati mavuto omwe akupangitsa dziko lino kukhala losauka kwambiri mu zaka 61 zomwe dziko lino likuzilamulira ndi kusowekera kwa adindo wozikindira bwino pa kagwiridwe ka ntchito,Katangale komanso kusankhana mitundu.

Dr Kabambe ati iwo ndi chipani chawo akadzalowa m'boma adzayetsetsa kuthana ndi mavuto a njala,chuma, katangale komanso kusankhana mitundu.

Pamene a Kabambe amafika ku BICC kukapereka mapepala awo adafika atakwera pa thirakitala yokonsa mi ndipo amayendetsa okha.

Wolemba: Damiano Fredson Kalajira.

.

Mtsogoleri wa chipani cha Democratic progressive Party( Dpp) Professor Arthur Peter Mutharika asankha mai Jane Ansah kuk...
25/07/2025

Mtsogoleri wa chipani cha Democratic progressive Party( Dpp) Professor Arthur Peter Mutharika asankha mai Jane Ansah kukhala wachiwiri wake yemwe aime nawo pa chisankho chikubwerachi.

Mutharika wati wasankha mai Jane Ansah chifukwa chakuti ndi munthu wokhwima mu nzeru, woopa Mulungu, ndipo akudziwa bwino momwe boma limayendera, ndiposo wati katswiri wa za malamulo komanso ali ndi ukadaulo woyendetsa bwino zinthu.

Polankhula ku BICC atapereka mapepala awo a Mutharika ati chipani chawo ndi chomwe chili ndi mayankho a mavuto omwe a Malawi akukumana nawo.

A Mutharika apempha anthu otsatira chipani chawo kuti achite kampeni wa mtendere osati kampeni womatemana ndi zikwanje.

M'chaka cha 2019 mai Jane Ansah adakhalapo wa pa mpando wa bungwe loyendetsa zisankho mdziko muno la Malawi Electoral Commission (MEC).

Wolemba: Damiano Fredson Kalajira.

.

Democratic Progressive Party has announced that Mayamiko Nkoloma is now a newly appointed Malawi Electoral Commission (M...
25/07/2025

Democratic Progressive Party has announced that Mayamiko Nkoloma is now a newly appointed Malawi Electoral Commission (MEC) commissioner.

In a Facebook post, Dpp described Nkoloma as an expert in technology, innovation and development.

He was upon his appointment serving as a lecturer in Telecommunications at Malawi University of Business and Applied Sciences (MUBAS) and he is now pursuing a PhD in innovation and development.

Nkoloma is a founder and director of iMosys, a Malawian Tech company that deal with the development of internet of Things (IoT) solutions.

Recently president Dr Lazarus Chakwera disapproved Mackford Somanje, the DPP's nominee for the Malawi Electoral Commission (MEC) due to questionable academic credentials.

Reported by Damiano Fredson Kalajira.

.

Timu ya mpira wamiyendo ya Mponela Fc yomwe ikutumikira nawo mu mpikisano wa Central Region Football Association Divisio...
24/07/2025

Timu ya mpira wamiyendo ya Mponela Fc yomwe ikutumikira nawo mu mpikisano wa Central Region Football Association Division One yaika pamsika malaya amakaka (Jerseys) a timuyi kuti yemwe angawafune agule.

Malinga ndi mkulu oyang'anira timuyi Dzimkambani Sitolo, wauza Dowa FM Online kuti ganizoli labwera pofuna kuti timuyi izidzidalira kumbali ya zachuma komaso ngati mbali imodzi yoti anthu ayidziwe timuyi.

Sitolo watiso kwa amene akufuna makakawa ali ndi ufulu oti atha kulembetsa dzina lawo kumbuyo komwe kunalembedwa kale kuti 'Mponela FC.'

Dzimkambani Sitolo wapitiliza kunena kuti mitengo yoyambila kugula malayawa (Jersey) olembedwa Mponela FC mtengo ukusiyana kutengera ndi nsalu yake ya jersey yo ndipo wati zovalazi zikhale zikupezeka pa msika mosavuta posachedwapa.

Chaka chatha timu ya Mponela Fc idamaliza pa nambala ya chitatu mu mpikisano wa Castel Challenge Cup omwe udachitika pansi pa bungwe loyendetsa masewero m'boma la Dowa.

Wolemba Peter Kawaza


24/07/2025

Katswiri pa ndale George Chaima wati chipani cha AFORD chapanga ganizo labwino lopanga mgwirizano ndi chipani cha DPP potengera kuti chipanichi chili ndi mphamvu ku mpoto pamene DPP ili ndi mphamvu madera ambiri mdziko muno.

Chipani cha AFORD kudzera mwa mtsogoleri wawo Enock Chihana, chalengeza kuti chapanga mgwirizano ndi chipani cha DPP.

Izi zanenedwa pa msonkhano wa atolakhani womwe umachikira ku Lilongwe.

Mmau ake Chihana wati izi zadza pamene komiti yaikulu ya chipanichi inali ndi zokambirana.

Wolemba Gracious Jumbe


Dr Joyce Banda, president of the People's Party (PP) has chosen Khumbo Kachali as her running mate for the September, 20...
24/07/2025

Dr Joyce Banda, president of the People's Party (PP) has chosen Khumbo Kachali as her running mate for the September, 2025 elections.

Dr Banda revealed the development after presenting her presidential nomination papers to the Malawi Electoral Commission (MEC) in Lilongwe this morning.

The former president said that her party and its electoral alliance partners are ready to address the economic crisis in Malawi.

Malawi Electoral Commission chairperson Justice Annabel Mtalimanja has assured Malawians that the commission will do their best to make sure that the elections are free and fair.

She urged candidates and party supporters to accept the election results after voting on September,2025.

Reported by Damiano Fredson Kalajira.

24/07/2025

The Mponela First Grade Magistrate's Court has sentenced and jailed a 36 years old man identified as Pilirani Kachimanga to 12 years imprisonment for having sexual in*******se with a girl child.

The Court heard through the state Prosecutor Ophia Ng'ambi that on April 1, 2025, the victim met the convict, who is also a witchdoctor to assist her because she was not experiencing monthly periods.

Ng'ambi further told the court that the victim was told to go together with the convict to his house and get some charms and while there, Kachimanga grabbed her and had sexual in*******se with her.

In Court Kachimanga pleaded not guilty to the charge leveled against him which prompted the state to parade three witnesses to prove beyond reasonable doubt.

The state asked the court to give the stiffer punishment to deater others would be offenders.


Address

Mponela

Telephone

+265991561861

Website

Alerts

Be the first to know and let us send you an email when DOWA FM posts news and promotions. Your email address will not be used for any other purpose, and you can unsubscribe at any time.

Contact The Business

Send a message to DOWA FM:

Share