DOWA FM

DOWA FM A media house that stands on journalistic principles, providing well verified and balanced news.

A polisi ku Lilongwe amanga anthu awiri omwe amadziwika kuti ndi mbava zotheratu chifukwa chopezeka ali ndi mfuti yokhal...
27/05/2026

A polisi ku Lilongwe amanga anthu awiri omwe amadziwika kuti ndi mbava zotheratu chifukwa chopezeka ali ndi mfuti yokhala ndi zipolopolo zinayi popanda chilolezo ku Bwalolanjovu nthawi ya nkhomaliro Lachiwiri lapitali.

Anthu omwe amangidwawo ndi Steven Kanongola Kambwiri wa zaka 54 komanso Phillip Lazaro wa zaka 51, pomwe munthu wachitatu yemwe akungodziwika ndi dzina loti Jack Semu Kapilikitsa anathawa ndi galimoto ya mtundu wa Suzuki Swift.

Mneneri wa polisi ku Lilongwe Inspector Hastings Chigalu wati apolisi omwe amazungulira mu mzinda pofuna kukhwimitsa chitetezo adayimitsa galimoto yomwe anthuwo amagwiritsa ntchito ndipo atafufuza anapeza mfuti yodzaza ndi zipolopolo zinayi.

Wofalitsa nkhani za polisiyu wati Kambwiri ndi Kapilikitsa anali pa belo ya khoti pa mlandu wakuba ndi kuvulaza nzika ya ku India mu mwezi wa February chaka chino ku Area 9 mu mzinda wa Lilongwe pamene munthuyo ankachokera ku bizinesi zake.

Kambwiri omwe amachokera ku Dedza komanso Lazaro omwe amachokera ku Ntcheu akuyembekezeka kukaonekera ku khoti posachedwa kukayankha mlandu wopezeka ndi mfuti popanda chilolezo.

Wolemba: Damiano Fredson Kalajira

Bungwe la Malawi Electoral Commission( MEC) lalengeza kuti mkulu woyang'anira zisankho, Andrew Mpesi, wasiya ntchito ndi...
27/05/2026

Bungwe la Malawi Electoral Commission( MEC) lalengeza kuti mkulu woyang'anira zisankho, Andrew Mpesi, wasiya ntchito ndipo mwa malamulo iwo adzachoka pa 21 August 2026.

Wa pa mpando wa bungweli Anabel Mtali wati a Mpesi adapereka kalata yosiya ntchito pa 24 May 2026 ndipo pakadali pano akhala akugwirabe ntchito kwa miyezi itatu ku bungweli monga mwa malamulo a pa ntchito kufikira atamalizitsa ntchito zonse zomwe amayenera kugwira .

Polankhula kudzera mu kalata yomwe bungweli latulutsa a Mtalimanja ayamikira a Mpesi chifukwa chogwira ntchito mozipereka ndi mwa dongosolo pa nthawi yomwe dziko lino limakonzekera zisankho za pa tatu zomwe zidachitika chaka chatha.

A Mpesi anatsogolera kusintha kwa malamulo a zisankho komanso anathandiza kwambiri pa kupanga ndi kugwiritsa ntchito njira yatsopano yoyendetsera chisankho cha 2025.

A Mtalimanja awafunira zabwino a Mpesi pa ntchito zawo za mtsogolo pamene akukonzekera kuchoka ku bungweli.

Wolemba: Damiano Fredson Kalajira

A polisi ku Lilongwe amanga Thomson Banda wa zaka 55 yemwe amagwira ntchito pa chipatala cha Bwaila ngati wothandizira d...
27/05/2026

A polisi ku Lilongwe amanga Thomson Banda wa zaka 55 yemwe amagwira ntchito pa chipatala cha Bwaila ngati wothandizira dotolo wa za mafupa chifukwa chomuganizira kuti waba mankhwala ndi zipangizo za opaleshoni pa chipatalacho.

Mneneri wa a polisi ku Lilongwe, Inspector Hastings Chigalu, wati Lolemba lapitali a polisi adagwira Sudala Mdazika atanyamula thumba lomwe munali mankhwala ndi zipangizo zochitira opaleshoni pamene ankayesera kutuluka pa chipata cha chipatalacho.

Mneneriyu wati Mdazika atafunsidwa komwe adatenga zinthuzo, adauza a polisi kuti adagula katunduyo kwa Banda omwe amagwira ntchito ngati wothandizira dotolo wa za mafupa ndipo izi zomwe zinachititsa kuti a polisi akamange Banda.

A polisi adakwanitsa kupeza ma sodium chloride intravenous infusions 20, ma povidone iodine topical solutions asanu, ma ceftriaxone sodium injections BP 11, komanso ma jakisoni 100.

Thomson Banda omwe amachokera m’mudzi mwa Njoka, mfumu yaikulu Masumbankhunda, komanso Sudala Mdazika ochokera m’mudzi mwa Malili, mfumu yaikulu Malili m’boma la Lilongwe, akaonekera ku bwalo la milandu kuti akayankhe milandu yokhudza kupezeka ndi mankhwala opanda chilolezo komanso zinthu zomwe zikuganiziridwa kuti zinabedwa.

Wolemba: Damiano Fredson Kalajira

Nduna ya kale yoona za zofalitsa nkhani Moses Kunkuyu apempha komiti ya Nyumba ya Malamulo yomwe ikufufuza ngozi ya ndeg...
27/05/2026

Nduna ya kale yoona za zofalitsa nkhani Moses Kunkuyu apempha komiti ya Nyumba ya Malamulo yomwe ikufufuza ngozi ya ndege ya Malawi Defence Force (MDF) Dornier kuti iyambe kaye kufufuza nkhani yokhudza “black box,” ponena kuti imeneyi ndi nkhani yofunika kwambiri kuti choonadi pa ngoziyi chidziwike.

Polemba pa tsamba lawo la Facebook, a Kunkuyu ati anthu ambiri ali ndi chiyembekezo chachikulu pa kafukufuku amene akuchitika pakadali pano, makamaka pofuna kudziwa chomwe chinachititsa ngoziyi komanso kuti mabanja a omwe anataya abale awo apeze chitonthozo.

A Kunkuyu, omwe ndi phungu wa dera la Dedza Mlunduni, ati ali wokonzeka kukaonekera pamaso pa komiti yomwe ikufufuza nkhaniyi kuti akayankhe mafunso okhudza mawu omwe akuti adayankhula pa nkhani ya “black box.”

Mneneri wakale wa boma ameneyu ananenanso kuti chinthu choyamba chomwe komiti yotsogoleredwa ndi Walter Nyamilandu iyenera kuchita ndi kufufuza mozama nkhani ya “black box,” chifukwa kudikira mpaka pakati kapena kumapeto kwa kafukufukuyu kungapangitse anthu ambiri kuona ngati komitiyi ikungotaya nthawi pa zinthu zosafunika.

A Kunkuyu ati akukhulupirira kuti kafukufukuyu abweretsa poyera choonadi chokhudza ngoziyi komanso kuti aliyense amene apezeke wolakwa ayenera kulangidwa motsatira malamulo.

Wolemba: Damiano Fredson Kalajira

Ngati njira imodzi yokonzekera kutulutsa chimbale cha nyimbo chotchedwa 'Dziko la wonongeka' Shadreck Chisale akugawa ma...
22/05/2026

Ngati njira imodzi yokonzekera kutulutsa chimbale cha nyimbo chotchedwa 'Dziko la wonongeka' Shadreck Chisale akugawa ma t-shirt ku ma wailesi osiyanasiyana.

Chisale yemwe adatchona mdziko la South Africa akuyembekezera kutulutsa chimbale cha nyimbo chomwe muli nyimbo zokwana khumi ndipo mawailesi osiyanasiyana monga Dowafm,Yetu community radio komaso Ntchisi FM kungotchulapo ochepa chabe ndi omwe alandire ma t-shirt wa.

Poyankhurapo mkulu amene akuyendetsa madongosolo onse kuno kumudzi Ausi Chabwera anati tsiku komaso malo okachitira mwambo okhazikitsa chimbale alengezabe.

Chisale yemwe kwao ndi ku Nkhotakota koma adatchona mdziko la South Africa komwe akugwira tchito zina ndipo watsimikiza kuti pa tsiku lokhazikitsa chimbale chake adzakhalapo.

Wolemba Peter Kawaza


Miyoyo ya anthu ikumbekezeka kusintha m'dera la Kasese m'boma la Dowa kutsatira kutsekulidwa kwa nyumba imene anthu akha...
21/05/2026

Miyoyo ya anthu ikumbekezeka kusintha m'dera la Kasese m'boma la Dowa kutsatira kutsekulidwa kwa nyumba imene anthu akhale akuphunziliramo zinthu yosiyanasiyana yomwe akuitcha kuti Golden Community Centre mchingerezi ndi bungwe la Orant Charities Africa.

Pamalowa anthu azikhala ndi mwai okaphunzira zinthu yosiyanasiyana monga mawu amulungu, luso la makono pamakina a komputa ,maphunziro akuluakulu kungotchulako zochepa chabe.

Poyankhula pamwambo otsekulira malowa wapampando wa khonsolo ya boma la Dowa khansala Billy Mtika wayamikira bungweli ponena kuti miyoyo ya anthu isintha makamaka achinyamata ndipo wapempha anthu kuti atenge udindo owonetsetsa kuti katundu amene ali pamalopa akusamalidwa.

Mmawu ake mkulu wa bungwe la Orant Charities kuno ku Malawi Gabriel Kapanda wati ndichiyembekezo chawo kuwona anthu akusinthika ndizochitika yosiyanasiyana zomwe zizichitika pamalowa ndipo wapempha anthu kuti ayesetse kumapita kukagwiritsa ntchito malowa.

Mfumu yaikulu Chakhala inathokoza bungweli pokhazikitsa malowa ponena kuti zithandizira kuti delari likhale lotukuka muzambiri.

Wolemba Chiletso Kabwazi Chaima


Mneneri wa boma, Shadreck Namalomba, achenjeza anthu mdziko muno kuti kugwiritsa ntchito dzina la Purezidenti Arthur Pet...
21/05/2026

Mneneri wa boma, Shadreck Namalomba, achenjeza anthu mdziko muno kuti kugwiritsa ntchito dzina la Purezidenti Arthur Peter Mutharika popanda chilolezo ndi kuphwanya malamulo a dziko lino.

A Namalomba anena izi kudzera mu kalata yomwe atulutsa potsatira uthenga wabodza womwe ukuyenda pa masamba a internet, womwe ukunena kuti a Mutharika adatumiza uthenga woyamikira timu ya ku England ya Arsenal F.C. chifukwa chopambana chikho cha English Premier League cha chaka cha 2025/2026.

Malinga ndi a Namalomba, uthengawu ndi wabodza ndipo cholinga chake ndi kusokeretsa anthu komanso ati boma silinatulutse uthenga uliwonse wokhudza nkhaniyi ndipo Purezidenti sanalembe uthenga womwe ukukambidwawo.

A Namalomba awonjezera kuti kugwiritsa ntchito dzina la mtsogoleri wa dziko pa nkhani zosakhudza boma kumachotsa ulemu komanso kumanyozetsa ofesi ya Purezidenti.

Boma lapempha munthu amene wapanga uthengawu kuti awuchotse mwachangu pa masamba a internet ndipo boma lachenjeza kuti aliyense amene apezeka akuphwanya lamuloli akhoza kulandira chilango chopereka chindapusa kapena kumangidwa.

Wolemba: Damiano Fredson Kalajira

A polisi ku Lilongwe amanga nzika ya ku Tanzania ya zaka 56 chifukwa chopezeka ndi mankhwala osiyanasiyana komanso zida ...
19/05/2026

A polisi ku Lilongwe amanga nzika ya ku Tanzania ya zaka 56 chifukwa chopezeka ndi mankhwala osiyanasiyana komanso zida za chipatala opanda chilolezo.

Wofalitsa nkhani za apolisi ku Lilongwe, Hastings Chigalu, wati apolisi adamanga a Josephat Kamundu ku Falls Estate Lolemba lapitali kutsatira uthenga womwe adalandira kuchokera kwa anthu akufuna kwa bwino.

Mneneriyu wati pa ntchito yomangayo apolisi apeza katundu wina wa chipatala monga zida zoyezera matenda a HIV, malungo komanso mankhwala akulera, kungotchula zochepa chabe.

A Chigalu ati apolisi akuchita kafukufuku kuti apeze komwe a Kamundu adatenga mabokosi 100 a Triclofen, mabokosi 40 a zida zoyezera matenda a HIV komanso mabokosi 58 a Orchid Paracheck, limodzi ndi katundu wina wa chipatala.

Iwo ati apolisi atengera a Kamundu ku bwalo la milandu posachedwapa bungwe la Pharmacy and Medicines Regulatory Authority (PMRA) likamaliza kufufuza mankhwala ndi zipangizozo, kuti akayankhe mulandu wopezeka ndi mankhwala komanso zida za chipatala opanda chilolezo.

Wolemba: Damiano Fredson Kalajira

Apolisi ku Mponela m'boma la Dowa amanga mayi wazaka 53 Aliste Adson pogwirira nyamata wazaka 16.Sergeant Macpatson Msad...
18/05/2026

Apolisi ku Mponela m'boma la Dowa amanga mayi wazaka 53 Aliste Adson pogwirira nyamata wazaka 16.

Sergeant Macpatson Msadala mneneri wapolisi ya Mponela wauza Dowa Fm Online kuti izi zinachitika pa 11 May, mmudzi mwa Mondwe m'dera la Senior Chief Kayembe.

Msadala wati mayiyu anakumana ndi nyamatayu panjira akupita ku dimba kwake masana apa tsikuli ndipo anamuuza apite kunyumba kwake madzuro komwe anakamunyengerera nyamatayu kuvula zovala zake ndikumugwirira.

Patatha masiku awiri nyamatayu anauza msuweni wake za nkhaniyi pakuti anazindikira kuti anavulala maliseche ake.

Adson akaonekera kubwalo la milandu posachedwapa kukayankha mulandu wogwiririra.

Wolemba Khumbo Chiudzu


Boma kudzera mu unduna wa zofalitsa nkhani latsutsa zomwe chipani cha Malawi Congress Party (MCP) chikunena kuti boma li...
15/05/2026

Boma kudzera mu unduna wa zofalitsa nkhani latsutsa zomwe chipani cha Malawi Congress Party (MCP) chikunena kuti boma lidachita dala kuletsa chipanichi kupezeka pa mwambo wokumbukira mtsogoleri wakale wa dziko lino, malemu Dr Hastings Kamuzu Banda, womwe unachitika Lachinayi lapitali.

Nduna ya zofalitsa nkhani yemwenso ndi mneneri wa boma, a Shadreck Namalomba, yati mwambo wokumbukira Dr Kamuzu unakonzedwa ndi a Ken Kandodo limodzi ndi banja la Kamuzu osati boma monga ena akulankhulira ndipo chiganizo chosaitana chipani cha MCP chidapangidwa ndi omwe ankakonza mwambowu.

Polankhula kudzera mu kalata yomwe undunawu watulutsa lero, a Namalomba ati okonza mwambowu adayitana mtsogoleri wa dziko lino, Professor Arthur Peter Mutharika, ngati mlendo wolemekezeka koma anatumiza nduna ya za masewero Alfred Gangata kuti akawaimirire.

Undunawu wadzudzulanso chipani cha MCP chifukwa chokonza ulendo wawo wopita ku manda a Dr Kamuzu popanda chilolezo cha apolisi ndi khonsolo ya mzinda wa Lilongwe, zomwe ati ndikuphwanya malamulo a dziko.

Undunawu waikiranso kumbuyo apolisi ponena kuti adagwira ntchito yawo mwa ukadaulo, moleza mtima komanso motsatira malamulo poletsa atsogoleri ndi otsatira a chipani cha MCP kupita ku manda a Dr Kamuzu.

Wolemba: Damiano Fredson Kalajira

Mtsogoleri wa chipani cha United Transformation Movement (UTM) Dalitso Kabambe wapempha anthu mdziko muno kuti aziyika p...
15/05/2026

Mtsogoleri wa chipani cha United Transformation Movement (UTM) Dalitso Kabambe wapempha anthu mdziko muno kuti aziyika patsogolo umodzi osati ndale pa nthawi imene dziko lili ndi zochitika zosiya-siyana.

Polankhula kudzera mu kalata yomwe chipanichi chatulutsa lero, Dr Kabambe ati zomwe zidachitika dzulo pamene dziko limakumbukira kubadwa kwa Hastings Kamuzu Banda zaonetsa momwe ndale zingabweretsere magawano pakati pa anthu.

A Kabambe apemphanso atsogoleri a zipani mdziko muno kuti azilimbikitsa mtendere, mgwirizano komanso kuyanjanitsa anthu pa nthawi yomwe dziko lino likukumana ndi mavuto azachuma.

Chipani cha UTM chatinso pakufunika kukhala malamulo oyendetsera zikumbutso za dziko pofuna kuti anthu onse mdziko muno aziloledwa kutengapo mbali mosayang’ana mtundu kapena chipani.

Chipanichi chati chikukumbukira Dr Kamuzu Banda ngati m'modzi mwa anthu omwe adakhazikitsa maziko a chitukuko komanso amene adalimbana ndi atsamunda kuti Malawi ipeze ufulu wodziyimira pawokha.

Wolemba: Damiano Fredson Kalajira.

Address

Mponela

Telephone

+265991561861

Website

Alerts

Be the first to know and let us send you an email when DOWA FM posts news and promotions. Your email address will not be used for any other purpose, and you can unsubscribe at any time.

Contact The Business

Send a message to DOWA FM:

Share