Mzati Radio & Tv

Mzati Radio & Tv To Entertain, Educate and Inform .. Mzati Limited Company- is registered and licensed with the Malawi Communications Regulatory Authority (MACRA).

The station broadcasts social and developmental programs on the following frequencies: 94.0Mhz & 94.2 MHz
MZATI TV-GO TV CHANNEL 811 & MDBNL 810 ZUKU CHANNEL 75

Radio online: Getmeradio.com, A2Z Malawi App, radio box & radio garden

Apolisi ku Blantyre amanga bambo wina pomuganizira mlandu wokuba ponamiza anthu kuti amagulitsa mbuzi. Wachiwiri kwa m'n...
01/11/2025

Apolisi ku Blantyre amanga bambo wina pomuganizira mlandu wokuba ponamiza anthu kuti amagulitsa mbuzi.

Wachiwiri kwa m'neneri wa Polisi ya Blantyre Doris Mwitha wauza Mzati kuti oganiziridwayu ndi Raphael Saliva wa zaka 45 ndipo amachokera m'mudzi mwa Ngowi m'boma la Chikwawa.

Mwitha wati apolisi amanga mkuluyu lachisanu pa 31 October, ku Chikwawa komwe amabisala.

"tapeza kuti a Saliva akhala akuuza anthu kuti amagulitsa mbuzi ndipo ofuna azilipira kudzera pa lamya kuti awapititsire katunduyu, koma ofuna katundu wawo akatumiza ndalama iwo amadzimitsa lamya zawo", Mwitha watero.

Padakali pano m'neneriyu wati mlanduwu uli m'manja mwa apolisi owona milandu ya ndalama ndipo oganiziridwayu akaonekera ku bwalo lamilandu posachedwapa.

Chithunzi:Oganiziridwayu komanso Doris Mwitha yemwe ndi m'neneri wa apolisi.

Wolemba-Evance Rhonex Matola-Blantyre.

 Bungwe la Southern Africa Development Community (SADC) lati ndilokhumudwa ndi kupitilira kwa ziwonetsero zokhudza zotsa...
01/11/2025



Bungwe la Southern Africa Development Community (SADC) lati ndilokhumudwa ndi kupitilira kwa ziwonetsero zokhudza zotsatira za chisankho chomwe chinachitika pa 29 October chaka chino m'dziko la Tanzania zomwe kufikila pano anthu ambiri afa komanso katundu wambiri waonongeka.

Malingana ndi kalata yomwe bungweli latulutsa kudzera ku nthambi yake yoona za ndale, nkhondo ndi chitetezo ndipo yasainidwa ndi wapampando wake Professor Peter Mutharika, yemwe ndi Mtsogoleri wa dziko lino.

Nthambiyi yati ikutsatila mwa chidwi zonse zomwe zikuchitika mdziko la Tanzania ndipo yapemphanso a nthambi za chitetezo kugwila ntchito yawo mwaukadaulo pofuna kupewa kukolezera ziwawazi.

SADC yapempha Boma la Tanzania komanso magulu okhudzidwa mdzikolo kubwela pamodzi ndikupeza njira zothetsera kusamvana kwao.

Wolemba: Blessings Malunda - Lilongwe

01/11/2025



Apolisi ku Mponela m'boma la Dowa atsimikiza za imfa ya Thomas Chilimbire wazaka 51 yemwe wafa kutsatira ngozi ya moto.

Mneneli wa polisi ku Mponela Macpatson Msadala, wati ngoziyi yachitika pa 31 October, chaka chino m'mudzi mwa Mwakana m'bomali.

Iye wati patsikuli a Chilimbire adali mnyumba ndipo munabuka moto omwe oyamba kuwuzindikira anali m'bale wawo, yemwe adali pafupi.

M'nenriyu wati m'baleyu adadziwitsa anthu oyandikana nawo ndipo ngakhale anthuwa anayesetsa kuzimitsa motowu sizinatheke kupulumutsa Chilimbire kaamba koti motowu unali utayaka kwambiri.

Thupi la Chilimbire linapezeka litapsa kwambiri ndipo zotsatira za chipatala zasonyeza kuti imfa yadza kaamba kakupsa kwambiri ndi motowu.

Chilimbire amachokera m'mudzi mwa Mwakana, Mfumu yaikulu Dzoole, m’boma la Dowa.

Wolemba: Maureen Kanyundo

 Bungwe loyendetsa chisankho mdziko la Tanzania lalengeza kuti Samia Suluhu Hassan apambana pa chisankho cha mtsogoleri ...
01/11/2025



Bungwe loyendetsa chisankho mdziko la Tanzania lalengeza kuti Samia Suluhu Hassan apambana pa chisankho cha mtsogoleri wa dzikolo

Malingana ndi BBC Hassan wapeza 97.66% ya mavoti omwe adaponyedwa lachitatu sabata ino.

Pakadali pano anthu mdziko la Tanzania akuchita zionetsero zosakondwa ndi momwe chisankhochi chayendela.

Mwazina anthuwa akukhulupilira kuti ufulu owalora adindo kupikitsana pa udindowu waphwanyidwa pomwe ena mwa omwe amapikisana nawo amangidwa,kulesedwa komanso kusowesedwa.

Kufikila pano anthu ena afa pa zionetsero zomwe zikuchitika mdzikolo.

Wolemba:Akim Malindi

01/11/2025



Bungwe la Malawi Energy Regulatory Authority( MERA) lati njira ya boma yobweretsera mafuta a galimoto kudzera ku madoko aku Dar es Salaam ndi Tanga mdziko la Tanzania, yakhudzidwa ndi mavuto kutsatira zionetsero zokhudza chisankho zomwe zikuchitika mdzikolo.

Izi ndi malingana ndi kalata yomwe bungweli latulutsa pa 31 Okotobala 2025, pokambapo zamafuta agalimoto.

MERA yati sabata ikuthayi mabungwe a National Oil Company of Malawi( NOCMA) ndi Petroleum Importers Limited ( PIL) anadandaula kuti mathankala amafuta okwana 120 anayimitsidwa ku doko la Dar es Salaam.

Kalatayi yawonjezera kuti doko la Tanga ntchito yolandira sitima yayimitsidwa zomwe zakhudza sitima yomwe yanyamula mafuta a petulo ndi dizilo okwana 48 million litazi obwera ku Malawi.

Padakali pano kalatayi yati boma likuyetsesa kukambirana ndi boma la Tanzania pofuna kupeza thandizo komanso ndipo padakali pano lapeza njira yobweretsa mafuta ena kudzera ku madoko a Beira ndi Nacala ku Mozambique komanso Msasa ku Zimbabwe.

Wolemba-Evance Rhonex Matola..

01/11/2025



Mwambo olumbilitsa mlangizi wa boma pa nkhani zamalamulo komanso nduna zatsopano zomwe mtsogoleri wa dziko lino Professor Arthur Peter Mutharika wazisankha kumene, ausintha kuchoka lero kufika mawa pa 2 November 2025.

Izi ndi malingana ndi uthenga kuchokera kwa mlembi ofalitsa nkhani ku ofesi ya mtsogoleri wadziko lino, Cathy Maulidi.

Maulidi wati kupatula kusintha kwa tsiku, ndondomeko yonse yamwambowu sinasinthe.

Mwambowu ukuyembekezeka kuchitikira ku Bingu International Convention Centre (BICC) mu nzinda wa Lilongwe kuyambira nthawi ya 2 koloko masana.

Wolemba: Austin Katunga - Lilongwe.

 Ofesi yoona kuti pasakhale  kusiyana pakati pa amayi ndi abambo m'boma la Thyolo yati kutsogoza amayi m'ma udindo osiya...
01/11/2025



Ofesi yoona kuti pasakhale kusiyana pakati pa amayi ndi abambo m'boma la Thyolo yati kutsogoza amayi m'ma udindo osiyanasiyana kungathandize pa ntchito yolimbikitsa bata ndi kuthetsa mikangano kumadera.

Mkulu wa ofesiyi a Gerald Zgambo anena izi pawayilesi ya Mzati kudzera mupologalamu yapadera yomwe amakamba za ntchito yolimbikitsa bata komanso kuthetsa mikangano yomwe ikugwiridwa ndi bungwe la Chipembere Community Development (CCDO) m'boma la Thyolo.

Mkulu wa komiti yolimbikitsa umodzi ndi mtendere a Martin Kavalo ati pakadali pano boma la Thyolo likuchita bwino pankhani ya umodzi ndi mtendere kaamba ka mgwirizano omwe ulipo pakati pa anthu osiyanasiyana komanso magulu omwe akukhazikitsidwa olimbikitsa umondi ndi bata.

M'mau ake, mkulu wa bungwe la CCDO a Dalitso Chiwayula ati anakhazikitsa ntchitoyi poona mavuto omwe amayi komanso atsikana amakumana nawo monga nkhanza ndipo mwazina akukhazikitsa magulu amayi, atsikana ndi adindo ena pofuna kuthana ndi mchitidwewu.

Bungwe la CCDO likugwira ntchito yolimbikitsa bata komanso kuthetsa mikangano m'madera a mafumu akuluakulu asanu m'boma la Thyolo ndipo ntchitoyi inayamba mwezi wa September chaka chatha.

Wolemba: Chikondi Kuphata

  Good morning
01/11/2025


Good morning

 Mtsogoleri wa dziko lino professor Peter Mutharika pa 1 November akuyembezeleka kukakhala nawo pamwambo olumbilitsa ndu...
31/10/2025



Mtsogoleri wa dziko lino professor Peter Mutharika pa 1 November akuyembezeleka kukakhala nawo pamwambo olumbilitsa nduna zaboma zomwe zasankhidwa kumene komanso mlangizi wa boma pa nkhani za malamulo.

Izi ndi malingana ndi kalata yomwe boma latulutsa kudzera mwa mlembi wake wamkulu a Justin saidi lachisanu pa 31 October chaka chino.

Malingana ndi kalatayi mwambowu udzachitikila ku Bingu International Convention Centre BICC munzinda wa Lilongwe kuyambila nthawi ya 2 koloko masana.

Wolemba: Blessings Malunda - Lilongwe

 Mtsogoleri wa dziko lino Professor Peter Mutharika wasankha counsel Gabriel Chembezi kukhala mkulu wa bungwe lothana nd...
31/10/2025



Mtsogoleri wa dziko lino Professor Peter Mutharika wasankha counsel Gabriel Chembezi kukhala mkulu wa bungwe lothana ndi katangale ndi ziphuphu la Anti- Corruption Bureau.

Mtsogoleriyu wasankha a Chembezi kukhala mkulu wa ACB, mopatsidwa mphamvu ndi malamulo a dziko lino gawo 89, (1) (d).

A Muthalika asankhanso a Chimwemwe Chipungu kukhala nduna ya za chitetezo omwe dzulo anasankhidwa kukhala wachiwili kwa nduna ya zaumoyo ndi ukhondo.


Izi ndi malingana ndi kalata yomwe boma latulutsa ndipo yasainidwa ndi mlembi wamkulu wa boma Justin saidi.

Wolemba: Blessings Malunda - Lilongwe

 Ophunzira a msukulu za sekondale zoyendera m'dziko muno ati ali ndi kuthekera komachita bwino pamayeso a Malawi School ...
31/10/2025



Ophunzira a msukulu za sekondale zoyendera m'dziko muno ati ali ndi kuthekera komachita bwino pamayeso a Malawi School Certificate of Education (MSCE) ndikusankhidwira m'sukulu zaukachenjede, ngati ataika chidwi chochuluka pamaphunziro awo.

M'modzi mwa akuluakulu ku nthambi ya zamaphunziro chigawo cha Shire Highlands Education Division (SHED) a Vincent Kaunda ndiwo anena izi lachisanu sabata ino pamwambo opereka mphatso kwa ophunzira 11 omwe akhonza ma points oyambira 13 mpaka 20 pasukulu ya Mulanje Mission CDSS m'boma la Mulanje.

M'mau ake m'modzi mwa ophunzirawa yemwenso wachita bwino kuposa onse pokhoza 13 points, Ernest Masasa wayamikira aphunzitsi pa sukuluyi komanso makolo ake pomuthandizira zomwe zathandiza kuti achite bwino.

Pothirilapo ndemanga mphunzitsi wa mkulu pa sukuluyi Lovemore Manjolo wati ndiokondwa kuti akwanitsa kukhonzetsa ophunzira ochuluka mchakachi.

Sukulu ya Mulanje Mission CDSS yapereka ma Laptop atsopano kwa ophunzira awiri omwe akhonza bwino kuposa anzawo ndipo ophunzira onse omwe sanadutse ma points 20 pa mayesowa apasidwa mphatso ya zikwama.

Wolemba: Innocent Mutipe

 Nduna ya zaulimi a Roza Mbilizi pa 1 November chaka chino akhazikitsa ndondomeko yopereka thandizo kwa maanja okhudzidw...
31/10/2025



Nduna ya zaulimi a Roza Mbilizi pa 1 November chaka chino akhazikitsa ndondomeko yopereka thandizo kwa maanja okhudzidwa ndi njala mchaka cha 2025 mpaka 2026 Lean Season Food Insecurity Response Programme pachingerezi).

Malingana ndi nthambi yoona ngozi zogwa mwadzidzidzi ya DODMA mwambowu ukachitikira pa Sukulu ya pulayimale ya Chinguni m'dera la T/A Sitola, m'boma la Machinga.

Mwambowu ukudza patangotha masiku ochepa mtsogoleri wa dziko lino Prof. Arthur Peter Mutharika atalengeza kuti maboma 11 a m'dziko muno ndi malo a ngozi potsatira kukhudzidwa ndi kusowa kwa chakudya.

Wolemba: Bernike Gomani

Address

P. O. Box 372
Mulanje

Opening Hours

Monday 06:00 - 00:00
Tuesday 06:00 - 00:00
Wednesday 06:00 - 00:00
Thursday 06:00 - 00:00
Friday 06:00 - 00:00
Saturday 06:00 - 00:00
Sunday 06:00 - 00:00

Telephone

+265996492211

Alerts

Be the first to know and let us send you an email when Mzati Radio & Tv posts news and promotions. Your email address will not be used for any other purpose, and you can unsubscribe at any time.

Contact The Business

Send a message to Mzati Radio & Tv:

Share