Daily Bible Verses With Prophet Oswald Chizala

Daily Bible Verses With Prophet Oswald Chizala THIS PAGE IS SPECIFICALLY FOR GOD'S KINGDOM ADVANCEMENT THROUGH BIBLE TEACHINGS
(1)

MAINA ATHU NDI OMWE AMALEMBEDWA KUMWAMBA OSATI A MPINGO Luka 10:2,20 Ndipo ananena kwa iwo, Dzinthu dzicuruka, koma anch...
18/10/2025

MAINA ATHU NDI OMWE AMALEMBEDWA KUMWAMBA OSATI A MPINGO

Luka 10:2,20 Ndipo ananena kwa iwo, Dzinthu dzicuruka, koma anchito acepa; potero pemphani Mwini dzinthu, k*ti akankhe anchito kuk*tuta kwace. Koma musakondwera nako k*ti mizimu idakugonjerani, *koma kondwerani k*ti maina anu alembedwa m'Mwamba.*

Hallelujah 🙏 🙏 🔥

Eklesia wa Mulungu kuli ziphunzitso zonyoza mipingo ina k*t ngati timapemphera mpingo umenewo sitikapulumuka ndipo amatha kumapereka mavesi ngati zoona koma k*t muwafunse k*t ndi malemba ati amene amanena choncho sangakuuzeni k*tanthauza k*t chiphunzitso chawo chilibe umboni mmau a Mulungu ndipo mavesi omwe amapereka ndi osiyana ndi zinene amanena choncho mau a Mulungu ak*t tidzikondwera k*t maina athu alembedwa kumwamba kapena kunena k*t kumwamba munthu sadzaitanidwa ndi dzina la mpingo umene amapemphera koma lake iyeyo ndi ntchito zake ndi zimene ziti zidzamuchitire umboni choncho anthu atha kunyoza maina a mipingo ina koma sizik*tanthauza k*t mu mpingo umene amapemphera iwowo onse akapulumuka ayi opulumuka ndi amene maina awo alembedwa mu buku la moyo alembedwa kumwamba ndi ntchito zawo zabwino choncho ino ndi nthawi yolembetsa maina mu buku la Ambuye Yesu Khristu polapa machimo ndi k*tsikimizadi mtima kusiya zoipa mu dzina la Ambuye Yesu Khristu.

Apostle FM on 🎤🎙️

NSANJE YA UMULUNGU YA UMUNTHU NDI YA CHIKONDI Eksodo 20:5 usazipembedzere izo, usazitumikire izo; cifukwa *Ine Yehova Mu...
17/10/2025

NSANJE YA UMULUNGU YA UMUNTHU NDI YA CHIKONDI

Eksodo 20:5 usazipembedzere izo, usazitumikire izo; cifukwa *Ine Yehova Mulungu wako ndiri Mulungu wansanje,* wakulanga ana cifukwa ca atate ao, kufikira mbadwo wacitatu ndi wacinai wa iwo amene akudana ndi Ine;

AMEN MPINGO

Eklesia wa Mulungu msanje ndi kuipidwa kapena kusakondweretsedwa kapena kunyasidwa ndi zimene wina akuchita choncho msanje mu baibulo zilipo za mitundu itatu *1* ndi nsanje ya Umulungu imene Mulungu amachita munthu akapembedza zinthu zina zak*t sizingamuthandize sizingamupulumutse sizingamuyankhe ndiy Mulungu amaipidwa nazo amanyasidwa nazo sakondwera nazo monga anena mu vesi limeneli ndiy *2* pali nsanje ya umunthu imene munthu amamva kuwawa akaona mzake zikumuyendera bwino akamatukuka anthu ena akamayankhula zabwino za iye pa *1 Samueli 18:7-9* pali mau amene amaonetsa msanje ya umunthu imene Sauli amkaipidwa ndi Davide komanso *Mateyu 27:18* mau a Mulungu ak*t Amsembe ndi afarisi adamupereka Ambuye Yesu chifukwa cha msanje kuipidwa k*t amatchuka amalalikira bwino kusiyana ndi iwowo amachita zamphamvu kusiyana ndi iwowo ndiy *3* pali msanje ya chikondi imene umamuchitira wachikondi wako ukaona akichita zoipa ndi ena ukamva k*t akupanga zibwenzi umamva kuwawa umaipidwa umanyasidwa sukondwera mu mtima *Numeri 5:11-31* ndi miyambo *6:34-35* choncho Mulungu amamva kuwawa akaona ife tikuchita zoipa amachita msanje akaona tikupembedza mafano msanje ya Mulungu ndiyomukonda munthu imasiyana ndi msanje ya umunthu imene yachuluka masiku ano ngakhale mmipingo wina zikamamuyendera choncho ukakhala ndi msanje ya umunthu ukamaipidwa chifukwa mzako zikumuyendera dziwa k*t ndiwe omangidwa ndi satana ndithu ukufunika mamasulidwe ndithu ndipo msanje ya Umulungu mwa munthu umamva kuwawa ukaona wina akusocheretsa anthu akumunamiza wina

*Apostle FM on 🎤🎙️🎤🙏🔥🙏🔥🙏*

🔥 UNENELI WA CHISOMO  PA INU🔥🕊️Amene anatsekula maso a Batumeo k*ti awone, alinazo zochuluka m’manja mwake, ndipo dzanja...
16/10/2025

🔥 UNENELI WA CHISOMO PA INU🔥🕊️

Amene anatsekula maso a Batumeo k*ti awone, alinazo zochuluka m’manja mwake, ndipo dzanja lake silinaufoke lero. Dzanja lomwelo likufika pa moyo wako lero 🕊️kukonza zonse zomwe zasokonekera, kukhetsa mphamvu pa moyo wako, ndi kubwezeretsa ulemerero womwe udabedwa ndi mdani. 🙌

🕊️ Dzanja la Yehova likugwira ntchito pa moyo wako:
❤️Likukonzerani umoyo wanu wam’thupi ndi wauzimu.
❤️ Lik*tonthoza umphawi ndi chilichonse chimene chinakulepheretsani kupita patsogolo.
❤️ Lik*tsegula chitseko cha mimba yanu, cha bizinesi yanu, ndi cha moyo wanu wonse.
❤️ Chilichonse chimene chidamwalira m’kati mwanu chikuyambanso moyo lero!

🔥 Chinachake chatsopano chikuchitika!
Mulungu akukubwezeretsani mphamvu, ulemu, ndi chisomo.
Zomwe zidawoneka ngati zosatheka zikukhala zotheka lero.
M’malo mwa kulira, Mulungu akupatsani kuseka.
M’malo mwa manyazi, akupatsani ulemu wosatha.

Mdzina lamphamvu la Yesu Khristu,
dzanja lililonse lolemba k*ti musapite patsogolo
lidzakhala likukwezani lero ndi Yehova Wamphamvuzonse! ✋🔥

AMEN 🙏🔥

Apostle FM on 🎙️🎤🙏🙏🔥🔥

LIMBANI MTIMA 🙏🏾🔥🔥 Mukhalabe olimba mtima, pak*ti Yehova Mulungu wanu akupitilira kumenyera nkhondo pa inu.📖Deuteronomo ...
15/10/2025

LIMBANI MTIMA 🙏🏾🔥🔥

Mukhalabe olimba mtima, pak*ti Yehova Mulungu wanu akupitilira kumenyera nkhondo pa inu.
📖Deuteronomo 20:4

Mizimu yonse yomangirira ntchito, bizinesi, ndi banja ikulandidwa mphamvu lero!
Mulungu akuyika njira zatsopano, k*tsegula zitseko zomwe zatsekedwa kwa nthawi yayitali.
Chaka chino chikhala cha umboni wako! 🔥

Ndithu, nawenso uikile umboni wako mudzina lamphamvu la Yesu Khristu! 🙌🏾🖐️🙌🙌🔥🔥

Apostle FM on 🎤🎙️🎤🙏

15/10/2025

UDINDO WA AMAYI

Tsogolo la mwana limadalira ntchito ya mayi wachipembedzo

M’buku la 2 Timoteyo 1:5 timawerenga za udindo wa amayi a Timoteyo ndi agogo ake. Eyunike ndi Loisi anafalitsa chikhulupiriro cholimba cha Chikhristu kwa Timoteyo. Udindo wapamwamba wa mayi ndi kukhala chitsanzo chabwino choyenera k*tsatiridwa m’banja lake.
Mayi wachipembedzo, musabisire kuwala kwanu kunyumba kwanu. Mabanja anu ndi nthaka yabwino yobzalamo mbewu za uthenga wabwino. Lolani banja lanu la pafupi ndi la k*tali lidziwe za chikhulupiriro chanu mwa Yesu ndipo liwone chikondi ndi chimwemwe cha Khristu mwa inu.

M’mavesi athu a lero (Tito 2:1–5), Mtumwi Paulo analimbikitsa akazi akulu k*ti aphunzitse atsikana ndi amayi achichepere ndi mawu komanso ndi chitsanzo.
Amayi kaya achichepere kapena okalamba muyenera kulemekeza amuna anu, kusamalira ana anu, ndi kuwaphunzitsa kukhala moyo wolemekeza Mulungu.
Mayi wachipembedzo ayenera kukhala wopemphera. Mayi amene amapemphera nthawi zonse ndi mayi wamphamvu. Palibe mphamvu ya gehena yomwe ingakwatule ana a mayi wopemphera (Akolose 4:2)

Udindo wina wapamwamba wa mayi wachipembedzo ndi kuphunzitsa ana ake njira za Mulungu.
Miyambo 22:6 imati, “Phunzitsa mwana njira imene ayenera kuyendera, ndipo akakalamba sadzasiyapo.”
Momwemonso, mayi wachipembedzo ayenera kukhala woyang’anira mwanzeru wa banja lake monga mkazi wa Miyambo 31:27, amene amasamalira banja lake pa nthawi yoyenera.

Udindo wa mayi wachipembedzo umaphatikizanso kuopa Mulungu ndi kumukhulupirira. Ndi ntchito yake kulera banja lake m’mantha a Mulungu.
Miyambo 14:1 imati, “Mkazi wanzeru amamanga nyumba yake, koma wopusa amaiwononga ndi manja ake.”

Mayi wachipembedzo ayenera kulera ana ake ndi Mawu a Mulungu. Ayenera kukhala wokhutira ndi zomwe ali nazo ndipo aphunzitse ana ake kukhala choncho.
Ndipo ndi wophunzitsa ophunzira, amene amalera ana ake k*ti akhale a Mulungu – monga momwe Hana anachitira.

Apostle FM on 🎙️🎤

15/10/2025

Happy happy mother's day 🙏😇, Ambuye oziwa kudalitsa adalise amayi nonse omwe muli pa page pano.💯🙏🙏💐🎉🌹

🌴MOYO NDI UDZU🌾Anthu onse ali ngati udzu, ulemerero wawo uli ngati duwa la k*thengo.Udzu umafota ndipo duwa limathothoka...
13/10/2025

🌴MOYO NDI UDZU🌾

Anthu onse ali ngati udzu, ulemerero wawo uli ngati duwa la k*thengo.
Udzu umafota ndipo duwa limathothoka
📖1 Petro 1:24📝

Mwaswera bwanji,,, ?
ABWENZI mukuziwa inu k*ti udzu🌾 umauma, moyo umatha.
👉Chuma
👉Maphunziro
👉Kutcuka
👉Luso etc
Zonsezi ndi maluwa🌺💐🌼 ndipo zizatha pamene moyo watha.
Konzani njira zanu lero, tisanafike pa malire amoyo wathu.

Chenjezo...🤔🤷
Duwa silimasunga mtengo🌴 koma mtengo ndiumene umasunga duwa💐, musalore mtendere wampasi pano ukupusiseni ai, tsiku lina uzatha uwu📖 1 Yohane 2 vc 15 to 17📖. Amen

🙏, Mulungu wamoyo amakukondani 💞

Mulungu akhale ndinu🙋

Apostle FM on 🎤🎙️🎤🙏🔥🔥

🐉satana🐍wachita manyazi amawona ngati Mulungu wagona Uli ndi Mulungu iwe m'dzina la Yesu khristu🕊️ Amen 🙌🔥🐉🐍Satana amany...
12/10/2025

🐉satana🐍wachita manyazi amawona ngati Mulungu wagona Uli ndi Mulungu iwe m'dzina la Yesu khristu🕊️

Amen 🙌🔥🐉🐍
Satana amanyozedwa, mphamvu zake zapera!
Mulungu wathu sakhala tulo, sakhala kugona (Salimo 121:4),
Iye ndiye mphamvu, chitetezo ndi mpulumutsi wathu.

✝️ Uli ndi Mulungu amene ali mkulu kuposa mavuto onse.
✝️ Uli ndi mphamvu ya Yesu yomwe imagonetsa mdani.
✝️ Uli ndi Mzimu Woyera amene amayenda nanu.

🕊️ Ndipo lero tikulengeza k*ti:
➡️ Satana wachita manyazi.
➡️ Udani wafooketsedwa.
➡️ Mpandopando wa Mulungu wayimilira.

Imfa imagonjetsedwa, moyo umapambana, ndipo iwe uli ndi chigonjetso!

Apostle FM on 🎤🎙️🎤🙏🔥🔥🔥

SATANA SAMALIMBANA NDI ANTHU OTI ANATHANA NAWO KALE.Satana akamalimbana nawe usamakhumudwe ..uziziwa k*ti pa iwe akuwona...
11/10/2025

SATANA SAMALIMBANA NDI ANTHU OTI ANATHANA NAWO KALE.

Satana akamalimbana nawe usamakhumudwe ..uziziwa k*ti pa iwe akuwonapo chinachake chomwe Mulungu anayika mwa iwe.

Mu ground la mpira, munthu opanda mpira samamakidwa.
Adani amalimbana ndi munthu yemwe ali ndi mpira.

Nkhondo zina usamadzadabwe nazo.
Uli ndi kanthu komwe satana akulimbana nako pa iwe.

Uli ndi tsogolo la bwino iweyo.
Uli ndi ntchito ya bwino iweyo.
Uli ndi banja la bwino iweyo.
Ndiwe munthu ofunikira kwambiri padziko pano iweyo.

Koma afiti amangolimbana nawe, kumak*tchingatcinga k*ti usabowoleze koma ndikukuuzadi k*ti m’dzina la Yesu ubowoleza ndipo Mulungu akupasa chimene ukhumbira mtima wako.

Usamadandaule nyengo zikamawawa… pali kanthu pa iwe.
Komwe kudziko la kumidima akuwopa k*ti ukangobowoleza zinthu ziwadera.

Chofunika ndikuponya kwa kuya pemphero basi.

Kumwamba kuchite nawe mwamphamvu.

AMEN.

Apostle FM on 🎙️🎤🙏🔥🔥

🌹Ndimafuna ndiyankhule ndi opemphera nonse amene muli pa banja. Nthawi ya banja ndi nthawi ya banja, okondedwa anu asama...
11/10/2025

🌹Ndimafuna ndiyankhule ndi opemphera nonse amene muli pa banja. Nthawi ya banja ndi nthawi ya banja, okondedwa anu asamakusoweni kumati ndili busy kulingalira za moyo wanga.
Ngati munapanga chitsankho chokwatira kapena kukwatiwa muli born again weniweni. Panganinso chitsankho chokonda mkadzi wanu kapena mwamuna wanu ndipo mumumvere.

🌹Ndi kupeza k*ti ma banja a anthu opemphera mu kukhala nkhondo zosatha chifukwa cha mkulirano wa pa ma pemphero ndipo banja silikumapezeka ayi. Amakhala ooneka pa nseu kapena ku church limodzi kumakhala banja la chitsanzo koma mtendere m'ma banja a opempherawo ukusowa. Please, pangani k*ti ena akhumbire kupemphera Poona mtendere ndi zipatso za bwino zotuluka pa banja lanu.

🌹Musayankhulane za chipongwe Muli opemphera. Khalani chitsanzo cha bwino. Pena zikavuta mwina simukumvetsetsana, aliyense amapalira mbali yake k*ti sakulakwitsa, apezeni opemphera okhulupirira k*ti ak*thandizeni vuto lanu. Mvetserani kumwamba zokhuzana banja lanu, osati pamene mzako wakusowa ndi pamene u k*tenga Bible kuyambanso k*ti ndikufuna kupemphera. Zoterezi ma banja ena a atsogoleri sakuyenda bwino ngakhale abusa omwe. Mulungu akhale mbali ya onse amene muli pa udindo komanso opemphera nonse. Mulungu ndiye mwini banja. Lemekezanani wina ndi mzake k*tinso kulemekeza ndI kulambira kwanu mukhale koona ndi komveka pamaso pa Mulungu.
God bless your families.🎈🎈

Apostle FM on 🎤🎙️🎤🙏🔥🔥🔥
MABANJA alimbe basi

MULUNGU ALI NAFE .Muzonse zimene tikuchita mulungu alinafe ndipo salola k*ti loto lanthu lifele mazira .Za zomanga Manga...
10/10/2025

MULUNGU ALI NAFE .

Muzonse zimene tikuchita mulungu alinafe ndipo salola k*ti loto lanthu lifele mazira .

Za zomanga Manga zanthu ali momo .

Ma business anthu ali momo

Za utumiki wanthu ali momo .

Za program ya ukwati wanu ali momo

Za machilitso anu ali momo .

Za kalikonse kanu kamene mukukachita ali momo ndipo simunkhumudwa or pang'ono koma kumalizitsa kufikila kumapeto .

Palibe choyipa chitsate moyo wanu ndipo kulibe chowawa ndi cholilitsa chigwele banja lanu .

Mantha anthu saopa iwo anyanga , otembelera, ndi akaduka koma iye wakulenga zakumwamba ndi dziko lapansi.

MATEYU 1:23

Onani namwali adzaima, nadzabala mwana wamwamuna, ndipo adzamutcha dzina lake, Imanuele. Ndilo losandulika, Mulungu nafe.

Ndikunenera kuntchito kwanu Emmanuel, pa banja lako Emmanuel, pa zama project ako Emmanuel.

Kuyambila lelo let the name of Emmanuel be with you and give you victory.

Apostle FM on 🎙️ 🎤 🙏 🔥

Shalom

09/10/2025

Hezekiya atadwala nthenda yakufa nayo Mulungu anati uzafa ndithu komatu Hezekiya sanateye chikhulupiliro zamoyo wake koma anaima ndipemphero kufikira Mulungu atampatsanso moyo.

TANVESERANI
Kuntheka nyengo zanu zafika pa Hezekiya mukakhala mukumaona banja lanu litatha,business ikugwa,nthenda zavuta,abale anu akukudani, chinachake chakukhazikani kakasi ine apostle FM ndik*t kubwezelesa zonsezi kuli mu week ino ndikunenera chinachake chichitike painu LANDILANI amen

Apostle FM on 🎤🎙️🎤🙏

Address

Blantyre

Telephone

+265887096964

Website

Alerts

Be the first to know and let us send you an email when Daily Bible Verses With Prophet Oswald Chizala posts news and promotions. Your email address will not be used for any other purpose, and you can unsubscribe at any time.

Contact The Business

Send a message to Daily Bible Verses With Prophet Oswald Chizala:

Share