BIBLE STUDY

BIBLE STUDY BIBLE STUDY
CHOLINGA CHANGA NDI
2 Timoteyo 3:16
othandiza pophunzitsa, podzudzula, pokonza cholakwika ndi polangiza za chilungamo
(3)

TAPHUNZIRANI KUWERENGA MAU AMULUNGU NDIKUWACHITA.Odala iye amene awerenga   ndi iwo akumva  mau achinenero nasunga zolem...
07/09/2025

TAPHUNZIRANI KUWERENGA MAU AMULUNGU NDIKUWACHITA.

Odala iye amene awerenga ndi iwo akumva mau achinenero nasunga zolembedwa momwemo pakuti nthawi yayandikira Chivumbulutso 1:3.

Mau AMulungu ndi moyo ukawadziwa sunganamizidwe tikuyenera kumawerenga mau ndikuwachita tsiku ndi tsiku .

Munthu amene amawerenga mau AMulungu ndikuwachita amakhala munthu amene moyo wa uzimu umakula.

Choyamba mukafuna Kuwerenga mau a Mulungu mupemphere kuti Mulungu akutsogolereni ndi mphamvu ya Mzimu oyera.mukayamba Kuwerenga musanapemphere sumumvesesa bwino.

Lapani Machimo mulandire chisomo cha Ambuye wathu Yesu khristu ndi mphamvu ya Mzimu oyera.
Mtendere wa Ambuye wathu Yesu khristu ukhale Nanu.

Follow BIBLE STUDY

06/09/2025

PA NYANJAYI YA MOYO
Pa nyanjayi ya moyo, Namondwe ali pi!
Nangula wanga ali chiyembekezochi,
Mayeso akabwera, mphepo zikaopsa,
Mwa Yesu ndipumulatu koposa.

Chorus
Nangula ndi Yesu, m’namondwe ndiri nji,
Nangula ndi Yesu, mkati mwa mphepozi
Nangula ndi Yesu, ndiye Mpulumutsi,
Ndaphimbidwa ndi Thanthwe Lakale.

Asunga moyo wanga ndi mtendere wake,
Madzi achita bata ndi liulo lake,
Woongolera bwato, ndi wondilanditsa,
Ndi Yesu yemwe amandikwanitsa.

Bwenzi ndi Mpulumutsi, ndi Nangula wanga,
Amanditchinjiriza naingitsa mantha,
Ndiyang’ana Kumwamba kuseri kwa nyanja,
Alikundikonzera malo anga.

Thanks brother Evangelist Cosmas Chizula
Received your 🌷🌷🌹🌹🥀🌹🏵️🏵️🥀🥀
Kuti nanuso musakhe nyimbo yanu ya mu buku yomwe yimakusangalasani tiyike pano pangani follow BIBLE STUDY by Denzo Mo Sakuwa
Praise and worship mix hymn
Follow WhatsApp 0887096964

CHENJEZO KWA AKATOLIKA Okodedwa Nthawi yantha kwambiri ndipo ngati Nthawi yantha ife tiyenera kukuuzani choonadi chifukw...
06/09/2025

CHENJEZO KWA AKATOLIKA

Okodedwa Nthawi yantha kwambiri ndipo ngati Nthawi yantha ife tiyenera kukuuzani choonadi chifukwa ndi tsoka ngati sitikuuzani choonadi

Inde palibe kanthu kaya mumva kaya simumva,kaya munyoza,kaya mutsutsa, Kaya mulapa kaya simulapa koma ife sitisiya kukuuzani choonadi mpaka lipenga la mkwatulo litalira

Okodedwa ngakhale munamva kale koma Lero Mulungu akufunaso kukuchenjezani maka abale athu Akatolika

Mpamene ndangotchula za mpingo wa katolika yena akwiya yena akulakalaka ataponya chimbakera pafoni pomwepa chifukwa akuona ngati ndikuwanyozera mpingo wao

Okodedwa kaya zikuwawani kaya zikukomerani koma dziwani kuti Mulungu amakukondani ndipo ukuntha moyo wuno nanunso Mulungu akufuna kuti mukapezeke mu ufumu wake

Chonde! Pano sitikufuna kunyoza mpingo wa munthu ayi koma tikufuna kuvumbulutsa satana kumene wabisala ngati wolowa m'mpingo ife timalowa ndikumusanthula ndikumuyika poyera

Pamene ndikulemba uthengawu nkati mwanga mukulengeza misonzi powona mmene anthu akuchitila makani ndipo ndikudziwa kuti wina Anyoza

Akatolika! Mulungu amakukondani chifukwa chake sakufuna kuti mudzakanthele kugehena

Katolika ndi mpingo umene Mulungu awudzudzula kwanthawi yaitali kupyolera mu maumboni kapena mwa azitumiki osiyanasiyana koma palibe amamva kuyitana kwa Ambuye

Mateyu 7:15
Yang'anirani mupewe aneneri onyenga, amene adza kwa inu ndi zobvala zankhosa, koma m'kati mwao ali afisi alusa.

Vs 16 Mudzawazindikira ndi zipatso zao. Kodi achera mphesa paminga, kapena nkhuyu pamtula?

Vs 17 Comweco mtengo wabwino uli wonse upatsa zipatso zokoma; koma mtengo wamphuci upatsa zipatso zoipa,

Apa Baibulo likutitsimikizira kuti ngati inuyo mukufuna kudzalowa mu ufumu wa Mulungu MUPEWE ANENERI ONYENGA (ABODZA) AMENE AMABWERA KWA INU NGATI NKHOSA KOMA NKATI MWAO MULI AFISI

Mwanjira ina aneneri onyenga pobwera kwa inu amadziwonetsa ngati iwowo ndi anthu a Mulungu koma ali a satana KOMA MUDZAWAZINDIKIRA NDIZIPATSO ZAWO

Ichi ndichimodzimodzi mpingo wakatolika umanamizira kuti ndi mpingo wa Mulungu umanama kuti ndi mpingo umene unayambitsidwa ndi paulo kapena petro mtumwi kapena Ambuye Yesu KOMA ZIPATSO ZA MPINGOWO ZIKUTSUTSA BAIBULO

Kondi Mulungu angayambitse chinthu chotsutsa mawu ake yankho ayi chifukwa chinthu chotsutsa mawu a Mulungu ndi cha satana

Eeee pamene ndangonena izi wina wakwiya komaso sakumvetsa, hiii anangozo mudakakhala wina mudakaukonda moyo wanu chifukwa Nthawi tilibe

Popeza baibulo likuti MUDZAWAZINDIKIRA NDIZIPATSO ZAWO Lero tikufuna tiwone ZIPATSO ZOIPA ZA MPINGO WAKATOLIKA ZIMENE ZIMATSUTSA BAIBULO

1**Mpingo wakatolika umanena kuti munthu akamwalira amasungidwa malo yena otchedwa Purgatory atha kumupemphelera kuti achoke malo amenewa amuyike kumwamba

Pamene baibulo limati Kwaikika kwa Munthu kufa kamodzi ndipo atafa chiweruziro (Ahebri 9:27)

2** Mpingo wakatolika amakumbukira anthu akufa amene anafa kalekale

Pamene baibulo limati Palibe ubale pakati amoyo ndi akufa (Yeremiya 22:10)

3**Mpingo wakatolika umalambila chifaniziro cha Mayi maria kapena cha Yesu opachikidwa

Pamene baibulo limati usalambile chifaniziro chilichonse cha kumwamba kapena chapasi panthambo (Deuteronomo 5:8)

4** Mpingo wakatolika popemphela umatchula dzina la mayi maria

Pamene baibulo limati palibe dzina lapatsidwa pasi panthambo kapena kumwamba limene liyenera kutchulidwa koma dzina La Yesu lonkha m'bondo lilironse lipinde ngakhale satana amagwada pa dzina limeneri (Afilipi 2:10;Machitidwe 4:12)

5**Mpingo wakatolika umaphuzitsa kuti imwani koma musaledzere

Pamene baibulo limati ku mowa nditchimo kaya uledzera kaya suledzera koma ngati wamwa wachimwa (Yesaya 5:11;Yeremiya 25:27)

Mutani Brother and sister pamene mwamva uthenga uwu mutuluka simutuluka tamvetserani!!!

Ahebri 10:26
Pakuti tikacimwa ife eni ace, titatha kulandira cidziwitso ca coonadi, siitsalanso nsembe ya kwa macimo,

Vs 27 koma kulindira kwina koopsa kwa ciweruziro, ndi kutentha kwace kwa mota wakuononga otsutsana nao.

Baibulo apa likutitsimikizira kuti munthu akachimwa atantha kumva choonadi siyitsalaso nsembe ya kwamachimo koma kudikira kwina ndikutetha kwa Gehena

Chonde! musafe musanalape kapena muli Mpingo wumenewu chifukwa kugehena kulibe kulapa ,moti abale anthu amene anafa asanalape kapena ali mmpingo wakatolika pano akuzizuzika usiku ndi usana chonde lapani Nthawi yantha

Lapani! lapani! lapani!

lamulo la zonse ndiye chikondi ngati mwawerenga chonde akondeni azanu powatumizira uthengawu ma gruop onse muli kuti nawonso awerenge nawo

ngati mukufuna kuti nkhani zotsitsimutsa moyozi zisakuphonyeni pangani zinthu ziwiri izi
Follow BIBLE STUDY
By Denzo Mo Sakuwa

GAHENA YILIKONADZAWATAYA  MNG'ANJO YA MOTO KOMWEKO KUDZAKHALA KULIRA NDI KUKUKUTA MANO. MATEYU 13:50.Chivumbulutso 21:8K...
03/09/2025

GAHENA YILIKO

NADZAWATAYA MNG'ANJO YA MOTO KOMWEKO KUDZAKHALA KULIRA NDI KUKUKUTA MANO. MATEYU 13:50.

Chivumbulutso 21:8
Koma amantha, osakhulupirira, okonda zonyansa, opha anthu, achiwerewere, amatsenga, opembedza mafano ndi abodza, malo awo adzakhala nyanja yamoto ya sulufule wotentha. Iyi ndi imfa yachiwiri.”....

Mateyu 25:46
“Amenewa adzapita ku chilango chosatha pamene olungama ku moyo wosatha.”

Chivumbulutso 20:14
Kenaka imfa ndi Hade zinaponyedwa mʼnyanja ya moto. Nyanja yamoto ndiyo imfa yachiwiri.
Chivumbulutso 20:15
Ngati dzina la wina aliyense silinapezeke mʼBuku Lamoyo, anaponyedwa mʼnyanja yamoto.

2 Atesalonika 1:9
Adzalangidwa ndi chiwonongeko chamuyaya ndipo sadzaonanso nkhope ya Ambuye ndi ulemerero wamphamvu zake
2 Petro 2:4
Pakuti Mulungu sanalekerere angelo atachimwa paja, koma anawaponya mʼndende, nawayika mʼmaenje amdima, kuwasunga kuti adzaweruzidwe.

GEHENA IRIPO NDITHU KWA ONSE SAFUNA KUMVERA MULUNGU AMENE ASAKHA KUCHITA ZOFUNA MOYO WAO.

MULUNGU SAFUNA KUTI UZAKAKHALE KU GEHENA KOMA NTCHITO ZAKO ZOIPA ZA TSIKU NDI TSIKU NDIZOMWE UKUSAKHA GEHENA WEKHA .

UWU NDI MOTO UNAKONZEDWA KWA ONSE AMENE SAFUNA KUMVERA MULUNGU.

CHITANI CHIFUNIRO CHA MULUNGU LERO POLAPA MTCHIMO KUTI MUSAZAKHALE KU GEHENA.KOMA MUZAKHALE KU PARADIZO.

PAMENE NTHAWI IRIPO LERO LAPANI MULANDIRE CHISOMO CHA AMBUYE WATHU YESU KHRISTU POPEZA AKUBWERA POSACHEDWA.

MTENDERE WA AMBUYE WATHU YESU KHRISTU UKHALE NANU.

FOLLOW BIBLE STUDY

01/09/2025

KHALA chete ziwa kuti iye NDI mulungu oyakha 🙏🙏❤️❤️❤️❤️❤️❤️🙏🙏
Thanks brother Vin Chizuzu
🥀🥀🥀🥀🥀🥀🥀

DZULO NDINAPONYA POST YA MWANA UYU ANAPSA NDI MOTO KUTI TIZIMUPEPHERERA 🙏😢lero akuti akupezako bwino kusiyana NDI mmene ...
31/08/2025

DZULO NDINAPONYA POST YA MWANA UYU ANAPSA NDI MOTO KUTI TIZIMUPEPHERERA 🙏😢

lero akuti akupezako bwino kusiyana NDI mmene zinakhalira , apa tiyamike mulungu kuti apitilize kugwira ntchito yake ,komaso tisasiye kumuyikiza mmapephero ,
Mr Gama amene NDI bambo wa mwanayu ayakhula izi lero

Kuchoka chamawa panopa ndipomwe akupasano mazi koma ndiyamike kumwaba chifukwa amakanika kundya ngakhali kumwa pano wamwako zakumwa pang' ono ndikumuyamika mulungu akhale mulungu ,amen

Ifeso tikuti mulungu apitilize kumuchilitsa tamufunileni zabwino mwanayu NDI mau achilimbikitso

Zambiri tikupasirani
🙏🙏🙏🙏🙏🙏🙏🙏🙏🙏🙏
BIBLE STUDY

31/08/2025
MISAPHA YA SATANA.Tavalani zida zonse za Mulungu  kuti muzakhoze kuchilimika pokana machenjerero mdierekezi Aefeso 6:11....
31/08/2025

MISAPHA YA SATANA.

Tavalani zida zonse za Mulungu kuti muzakhoze kuchilimika pokana machenjerero mdierekezi Aefeso 6:11.

Kusakonda kupemphera msapha wasatana
Kukonda kusitha amuna ndi akazi ndi zibwenzi zambiri mbiri misampha yasatana.
Kuzikweza msapha wasatana.

Kuonera zolaula mu phone mwakomo misapha ya satana
Kusakonda Kuwerenga baibulo msapha wasatana

Kuyakhula bodza ndi umbombo misampha yasatana.

Kunyada,mwano, ufiti misapha ya satana.

Kusakonda kumvera mau AMulungu msapha wasatana.

Kukonda kumapanga zigololo komanso kusirira kazi kapena mwamuna aliyense msapha wasatana

Kukhala opanda chifundo ndi chikondi ndi azako kumenyana banja ,Kumwa mowa ndi njunga msapha wasatana.

Kumango kwiya kwiya NDI kupsa mtima misapha ya msatana.miseche

Satan ali ndi misapha yambiri yofuna akole akhristu ake AMulungu chonde mukaneni powerenga mau AMulungu ndi kupemphera.

Chenjerani satana akupetani chifukwa iye sakondwera ndi anthu opembeza mu Mzimu ndi choonadi.

Mukazawerenga ndi kusunga mau AMulungu ndikuwachita satana azakuopani

Lapani Machimo mulandire chisomo cha Ambuye wathu Yesu khristu ndi mphamvu ya Mzimu oyera.
BIBLE STUDY

PLEASE TIYENI TITHANDIZANE KUPEPHERERA MWANA ALI MU ULULU OOPSA KWAMBIR 😢Agwa pa moto mmawa Zambiri tikupasirani ,apa al...
30/08/2025

PLEASE TIYENI TITHANDIZANE KUPEPHERERA MWANA ALI MU ULULU OOPSA KWAMBIR 😢

Agwa pa moto mmawa
Zambiri tikupasirani
,apa ali ku chipatala kulandira THANDIZO lamankhwala zambiri ✍️✍️

Yakobo 5:14
Kodi alipo wina mwa inu akudwala? Ayitane akulu ampingo kuti adzamupempherere ndi kumudzoza mafuta mʼdzina la Ambuye.
Yakobo 5:15
Ndipo pemphero lachikhulupiriro lidzachiritsa munthu wodwalayo ndipo Ambuye adzamuutsa. Ngati wachimwa adzakhululukidwa...

Yesaya 41:10
Tsono usaope, pakuti Ine ndili nawe; usataye mtima chifukwa Ine ndine Mulungu wako. Ndidzakupatsa mphamvu ndipo ndidzakuthandiza, ndidzakutchinjiriza ndi dzanja langa lamanja logonjetsa.

😭😭😭😭😭😭😭😭😭
MULUNGU AMUCHILITSE

30/08/2025

THANKS FOR 32K FOLLOWERS GOD BLESS FANS 🙌🙌🙌🙌

1 Atesalonika 5:18
Yamikani mu zonse, pakuti ichi ndi chifuniro cha Mulungu kwa inu mwa Khristu Yesu.

PAKUTI ZONSE NDI CHIFUNIRO CHA MULUNGU TIKUYAMIKA MULUNGU

Masalimo 136:26
Yamikani Mulungu wakumwamba, pakuti chikondi chake chosasinthika nʼchamuyaya.

Masalimo 103:2
Tamanda Yehova, iwe moyo wanga, ndipo usayiwale zabwino zake zonse.

Aefeso 5:20
Muziyamika Mulungu Atate nthawi zonse chifukwa cha zonse, mʼdzina la Ambuye athu Yesu Khristu.

*MULUNGU AKUDALITSENI NONSE*

Numeri 6:24
“ ‘Yehova akudalitse ndi kukusunga;
Numeri 6:25
Yehova awalitse nkhope yake pa iwe, nakuchitira chisomo;
Numeri 6:26
Yehova akweze nkhope yake pa iwe, nakupatse mtendere.’ ”
Numeri 6:27
Choncho akadzatchula dzina langa podalitsa Aisraeli, Ine ndidzawadalitsadi.

Masalimo 121:8
Yehova adzayangʼanira kutuluka kwako ndi kulowa kwako; kuyambira tsopano mpaka muyaya.

Aroma 15:13
Mulungu amene amatipatsa chiyembekezo adzaze mitima yanu ndi chimwemwe ndi mtendere pamene mukumudalira Iye, kuti chiyembekezo chanu chisefukire mwamphamvu ya Mzimu Woyera.

*CHISAKHO CHANU SICHOLAKWIKA KOMA MULUNGU ALI NAWE CHOLINGA*

Miyambo 16:9
Mtima wa munthu umalingalira zochita, koma Yehova ndiye amakhazikitsa njira zake.

Miyambo 19:21
Munthu amakonzekera zambiri mu mtima mwake, koma cholinga cha Yehova ndiye chidzachitike.

*ALI NDI MWAYI AMENE ASATA NJIRA YA CHIPULUMUTSO*

Miyambo 14:12
Pali njira ina yooneka ngati yabwino kwa munthu, koma kumatsiriziro kwake ndi ku imfa.

Mateyu 7:13
“Lowani pa chipata chopapatiza. Pakuti chipata cholowera kuchiwonongeko nʼchachikulu ndipo msewu wake ndi waukulunso. Ndipo anthu ambiri amalowera pamenepo.

Mateyu 7:14
Koma chipata ndi chopapatiza ndi msewu ndi waungʼono umene utsogolera anthu ku moyo wosatha ndipo ndi owerengeka okha amene ayipeza njirayo.

BIBLE STUDY
SHAROM SHAROM ZIKOMO

Thanksto aunt NELIGO for Good song
,💜💜💜💜💜💜💜💜💜🔥BIBLE STUDY
Follow BIBLE STUDY KUTI muzilandira nawo mauthenga osisimusa awa 💜✍️

MPEPHERO LA UTSIKU❤️🙏Ambuye wathu wakumwamba mutamandike.  Nthawi ino ya kumadzulo uno zikomo kuti Munali nafe munyengo ...
29/08/2025

MPEPHERO LA UTSIKU❤️🙏

Ambuye wathu wakumwamba mutamandike. Nthawi ino ya kumadzulo uno zikomo kuti Munali nafe munyengo zonse
Tikupempha muzichepesa Pamaso panu ndichikhulupiriro kuti mfumu ya mafumu simumatisiya tokha nthawi zonse mutikhululukire zochimwa zathu zonse.

Mwayenera Kulambiridwa Yehova mwini zonse tikuthokoza mapemphero athu mumatiyakha nthawi zonse zikomo kwambiri.

Kuli azathu sakupeza bwino matupi awo kawakhunzeni ndi machiritso ena akukalowa ku operation mawa mukhale nao,

Pangani zotheka madokotala ndi anamwino akhale achifundo zipatalamu, awa alibe chakudya komanso alibe podalira paliponse apatseni chakudya.

Zafika posauzana ntchito yikuvuta perekani ntchito ndimphamvu yanu,
Awa ndalama yolipirira rent alibe chonde kawapatseni.
Business sikuyenda chonde chonde pangani iyambe Kuyenda bwino,

Onse amene akhala akulira kutaya okondedwa awo apukuteni misozi yao.

Mphamvu ya Mzimu oyera ikhale nafe mu utsiku umenewu tigone bwino Kupereka chitetezo ma nyumba mwanthu ndipanjira zanthu.

Onse alinyengo zowawa zonse nkhalani bwenzi lao ndikuwapatsa zosowa zao,koma amasiye, olumala, ophinjika, okalamba akundende ndi ali pa nkhondo Mukhale nao ndikuwapatsa zosowa zao.

Lembani maina athu buku la moyo ndipo musachotsemo zisomo ndi chifundo chanu ziyendere wina aliyense mwa Yesu khristu amen.

FBIBLE STUDY

Address

Mzimba

Telephone

+265887096964

Website

https://youtube.com/@denzomosakuwa-kg6lm?si=ldEEGb5QHdz77kka

Alerts

Be the first to know and let us send you an email when BIBLE STUDY posts news and promotions. Your email address will not be used for any other purpose, and you can unsubscribe at any time.

Contact The Business

Send a message to BIBLE STUDY:

Share