27/10/2019
Wakufuna kwabwino amanga mpanda pachipatala cha Chibavi
Aubrey Thom Vakhani
Mawu a nzeru zakuya amati "mkono wamanja ukapereka, wakumanzere usadziwe."
Mawuwa agwirizana kwatunthu ndizomwe wachita munthu wina ku Chibavi mumzinda wa Mzuzu yemwe wazipereka kumanga mpanda kuzungulira chipatala cha Chibavi mumzindawu.
Potsimikiza zankhaniyi, khansala wa dera la kumvuma kwa Chibavi, a Edward Kashololo Simwaka anati nkhani yomanga mpandayi yadzetsa chimwemwe chophwatula tsaya kwa iye komanso anthu a mdera lake (Chibavi East Ward) ponena kuti chipatalachi chiyamba kugwira ntchito posachedwapa.
"Munthu wina wakufuna kwabwino titamupempha anazipeleka kuti amanga mpanda. Nkhaniyi ndinailandira ndi manja awiri.
Uthenga kwa anthu aku [Chibavi East] ndiwakuti pompano vuto la chipatala litha ndipo azipita pafupi kukalandila mankhwala akadawala," anatero Simwaka.
Simwaka anati malowa akhala wotetezeka ndikumangidwa kwampandawu.
"Anyamata amagwiritsa ntchito malowa molakwika monga kusutira chamba. Pano pakhala chitetezo chokwanira," iye anatero.
Iye anatengerapo mwayi kuthokoza munthu wakufuna kwabwinoyu.
"Izi ndizinthu zotamandika kwambiri. Uwu ndiye umunthu. Akanakhala ena akanayima pachulu kulengeza koma munthuyu sanafune kutero. Ndipemphenso anthu ena kutengera chutsanzo chabwinochi. M'dela langa kuli ntchito zambiri zachitukuko zomwe zikufunika kugwira. Sitingangodikira boma kapena mabungwe akunja kutithandiza. Tingathe kutenga nawo gawo pachitukuko chammadrla mwathu," anafotokoza motero Simwaka.
Khansala Simwaka yemwe anayimira chipani cha Malawi Congress (MCP) pachisankho cha pa 21 May, anati chipatalachi chikayamba kugwira ntchito
chidzathandiza anthu a Chibavi [yomwe ili ndi madela awiri a khansala], Mchengatuwa, Chibanja komanso Sonda omwe amadalira chipatala chaching'ono cha Mapale.
Chipatala cha Chibavi chinamangidwa zaka zammbuyomu ndipo chimangogwira ntchito yokweza sikelo ana osapitilira zaka zisanu zakubadwa.