Nkhani Mchichewa

Nkhani Mchichewa Kukupatsirani nkhani zenizeni zochitika mdziko muno komanso kunja kwa dziko lino. Nkhani monga zamaphunziro, zaumoyo, zaulimi komanso zamasewero.

17/03/2026

Shout out to my newest followers! Excited to have you onboard! Brighton Mubanga, Wayit Njalasi, Willias Palimtima Maxwell, Cares Biziwick, Kachere Chisomo, Tatenda Manyenje, Michiel Kachitsa, Munthu Msyene, Darlington Simunye, Jonas Godfrey

Wakufuna kwabwino amanga mpanda pachipatala cha ChibaviAubrey Thom VakhaniMawu a nzeru zakuya amati "mkono wamanja ukape...
27/10/2019

Wakufuna kwabwino amanga mpanda pachipatala cha Chibavi

Aubrey Thom Vakhani

Mawu a nzeru zakuya amati "mkono wamanja ukapereka, wakumanzere usadziwe."

Mawuwa agwirizana kwatunthu ndizomwe wachita munthu wina ku Chibavi mumzinda wa Mzuzu yemwe wazipereka kumanga mpanda kuzungulira chipatala cha Chibavi mumzindawu.

Potsimikiza zankhaniyi, khansala wa dera la kumvuma kwa Chibavi, a Edward Kashololo Simwaka anati nkhani yomanga mpandayi yadzetsa chimwemwe chophwatula tsaya kwa iye komanso anthu a mdera lake (Chibavi East Ward) ponena kuti chipatalachi chiyamba kugwira ntchito posachedwapa.

"Munthu wina wakufuna kwabwino titamupempha anazipeleka kuti amanga mpanda. Nkhaniyi ndinailandira ndi manja awiri.
Uthenga kwa anthu aku [Chibavi East] ndiwakuti pompano vuto la chipatala litha ndipo azipita pafupi kukalandila mankhwala akadawala," anatero Simwaka.

Simwaka anati malowa akhala wotetezeka ndikumangidwa kwampandawu.

"Anyamata amagwiritsa ntchito malowa molakwika monga kusutira chamba. Pano pakhala chitetezo chokwanira," iye anatero.

Iye anatengerapo mwayi kuthokoza munthu wakufuna kwabwinoyu.

"Izi ndizinthu zotamandika kwambiri. Uwu ndiye umunthu. Akanakhala ena akanayima pachulu kulengeza koma munthuyu sanafune kutero. Ndipemphenso anthu ena kutengera chutsanzo chabwinochi. M'dela langa kuli ntchito zambiri zachitukuko zomwe zikufunika kugwira. Sitingangodikira boma kapena mabungwe akunja kutithandiza. Tingathe kutenga nawo gawo pachitukuko chammadrla mwathu," anafotokoza motero Simwaka.

Khansala Simwaka yemwe anayimira chipani cha Malawi Congress (MCP) pachisankho cha pa 21 May, anati chipatalachi chikayamba kugwira ntchito
chidzathandiza anthu a Chibavi [yomwe ili ndi madela awiri a khansala], Mchengatuwa, Chibanja komanso Sonda omwe amadalira chipatala chaching'ono cha Mapale.

Chipatala cha Chibavi chinamangidwa zaka zammbuyomu ndipo chimangogwira ntchito yokweza sikelo ana osapitilira zaka zisanu zakubadwa.

FCB U20 iyamba ku Mzuzu• Oyendetsa akuti akuyembekezera mpikisano wamkulu kuchokera ku matimuWolemba: Aubrey Thom Vakhan...
04/06/2019

FCB U20 iyamba ku Mzuzu
• Oyendetsa akuti akuyembekezera mpikisano wamkulu kuchokera ku matimu

Wolemba: Aubrey Thom Vakhani

Pamene ligi ya mpira wamiyendo ya anyamata achisodzera osapyola zaka makumi awiri (FCB U20) yayamba mumzinda wa Mzuzu Lamulungu lapitali pa 2 June, 2019, mlembi wamkulu wa Mzuzu Youth Football Committee, Mwayi Mavado Kumwenda wati ali ndi chikhulupiliro kuti ligiyi ikhala yapamwamba kwambiri chakachino.

Kumwenda wati ngati komiti akuyembekezera mpikisano waukulu kuchokera ku matimu omwe akutenga nawo gawo muligiyi yomwe ikulandira thandizo la ndalama kuchokera ku First Capital Bank.

"Ligi yathu yayamba bwino kwambiri. Lero (Lamulungu lapitali) pokhala tsiku loyamba Taonga matimu akuonetsa mpira wabwino kwambiri zomwe zatipatsa chithunzithunzi ife oyendetsa ligiti kuti tikhala mpikisano waukulu pakati pamatimu," anatero Kumwenda.

Iye anatinso mavuto okhudza oyimbira anawunikira ndipo sipakhala matimu kudandaula kwina kulikonse kuchokera kwa oyimbira.

"Tisanayambe ligi, tinakahala pansi ndi amnzathu yimbira masewero a mpira wamiyendo ndicholinga chowunikira mavuto zomwe analipi mmbuyomu ndikupeza njira zothanirana nawo ndipo ndinene pano pokondwa kuti chaka chino sipakhala madando okhudza oyimbira kamba koti zonse zili mchimake," anatsindika moteromo Kumwenda.

Mlembiyu anathokoza banki ya First Capital popitiliza kuthandiza ligiyi ndi ndalama.

"Ichi ndichyambi chotukula mpira wamiyendo mdziko muno. Anawa ndiomwe adzatumikire matimu osiyanasiyana m'dzikomuno komanso timu ya dzikolino. Kutero ndiwathokoze a First Capital Bank popitiliza kuthandiza. Kuthokoza kwakukulu ndikoti tionetsetsa ngati komiti kuti matimu akhale osunga mwambo ndipo ngati pangapezeke timu yophwanya malamulo oyendetsera ligi yathuyi, malamulo adzagwira ntchito mosayang'ana nkhope. Ndikuwafunira matimu zabwino zonse ndipo akhale olimbikira," anatero Kumwenda.

Mmasewero omwe aseweredwa musabata yoyamba, timu ya Sanwecka inagonjetsa timu ya Mbahewe ndi zigoli ziwiri kwa duu.

13/01/2016

Achinyamata a chipani cha United Democratic Front (UDF) mchigawo chapakati aopseza kuti achita chinthu chomwe sanachitchule.

Achinyamatawo motsogozedwa ndi Alex EmWaziri anena izi mupempho lawo lopita kwa akuluakulu a chipanichi kuti ayitanitse mkumano wapadela pasanathe masiku makumi awiri ndi limodzi (21).

09/01/2016

Bwalo la milandu la High Court Ku Mzuzu masiku apitawa linakana pempho la ophunzira ochokera ku sukulu ya ukachenjede ya Mzuzu (Mzuzu University) omwe anakasumira ganizo la akuluakulu a sukuluyi lowayimitsa kuphunzira potsatira zipolowe zonwe ophunzirawo anachita chaka chathachi.

Pa 29 November ndi pa 1 December, 2015 ophunzira APA Mzuzu University anachita zipolowe posagwirizana ndizonwe akuluakulu a Mzuzu University pochedwetsa kuwapatsa ndalama zawo za alawansi. Izi zinawapatsa mangolomera akuluakulu a university kuimitsa ena mwa ophunzira othandizidwa ndi boma amchaka chachiwiri, chachitatu ndi chachinayi pomwe komiti yosungitsa mwabo pasukuluyi imadikira kuti iwunike nkhaniyi.

Potsutsana ndi ganizo lomwe a university anapanga popereka zilango zowayinitsa sukulu KWA zaka ziwiri komanso ena zitatu, ophunzira asanu ndi anayi (9) anakatenga chiletso ku Mzuzu High Court.

Zionetserozo zinaonongetsa katundu ndipo ophunzirawo analipilitsidwa K200 000 aliyense zokonzetsera katubdu anawonongeka paziwonetserozo.

Ophunzirawo anatsutsana ndi chiganizo cha university ponena kuti university'yo inaphwanya malamulo akulu a dziko lino chifukwa choti sanafune kumva kumbali yawo.

Mmawu awo akuluakulu a Mzuzu University anatsutsa kwa mtu wa galu pazomwe ophunzirawo anawuza khoti ponena kuti zinali zammaluwa kaamba koti university inawalembera kalata zomwe zinafotokoza mwatsatanetsatane milandu yomwe amayenera kuyankha.

Popereka chigamulo pankhaniyi, Justice Dingiswayo Madise anati sanapeze cholakwika kumbali ya akuluakulu oyendetsa university poyimitsa sukulu ophunzirawo chifukwa choti ndondoneko zones zoyenera zinatsatidwa pamene komiti yosungitsa mwambo inapereka. Justice Madise anati konitiyo sinaphwanye malamulo a dziko lino popereka chigamulo chake kwa iphunzirawo.

09/01/2016

MCP IYAMIKIRA GANIZO LA BOMA

Chipani chachikulu chotsutsa cha Malawi Congress (MCP) chati boma liyenera kupitiliza kugwiritsa ntchito zinthu zomwe zipani zotsutsa zimalilangiza ponena kuti zambiri mwa izo zimakhala zomwe anthu zikuwakhufzs mdziko muno.

Wofalitsa nkhani za chipanichi Dr. Jessie Kabwila ndi amene anena izi kwa atolankhani mumzinda wa Lilongwe ponwe anayamikira boma kuti layamba layimitsa ganizo lokweza ndalama zolipilira malipiro msukulu za sekondale.

Mwazina Dr. Kabwira anaiza atolankhaniwo kuti zomwe boma lachita pankhaniyi, zapindulira mzika za dziko lino osati chipani cha MCP.

Iwo anati ntchito ya zipani zotsutsa sikulimbana kapena kufuna kugwetsa boma koma kulithandiza bomalo ndi upangiri wopititsira patsogolo chitukuko chadziko lino.

Boma, kudzera mu unduna wa zamaphunziro linalengeza zakusintha kwake ganizo lokweza dalama zolipira malipiro msukulu za sekondale kufikira mtsogolomu.

08/01/2016

Mmodzi mwamkhalakale pandale mdziko muno , a Humphreys Mvula wati ndiwodandaula ndikunjatidwa kwa mwana wawo Dumisani yemwe ndimmodzi wa anthu omwe anamangidwa pamilandu yakuba galimoto ndi kupha mumzinda wa Blantyre.

Mmawu awo a Mvula anati ngati kholo, iwo apitiliza kumuthandiza mwana wawoyo pandondomeko yopeza chilungamo pankhaniyi ngakhale kuti Dumisani amumanga pamilandu yoopsa chomwechi
Iwo anati Dumisani yemwe amachita maphunziro ake a ukachenjede ku susukulu ina yake, anakula ngati mwana wabwino komanso ngochilimika pazochitika zakumpingo.

Dumisani yemwe ndiwazaka makumi awiri ndi mphambu zitatu (23) zakubadwa, anamangidwa limodzi ndi anthu ena atatu powaganizira kuti amaba galimoto komanso kuoha anthu komwe amalanda galimotozo.

05/01/2016

Ntchito yomanga msewu wa Jenda-Edingeni mboma la Mzimba yayamba yayima chifukwa bungwe la Roads Fund Administration Fund likulephera kuperka ndalama za chipepeso kwa mabanja atatu omwe nyumba zawo zinaonongeka chifukwa champhamvu ya makina omangira msewu.

Tsamba lino lagwira mawu a mmodzi wa anthu omwe mabanja awo akhudzidwa ndi nkhaniyi a Mathias Kampango omwe anena kuti analetsa kampani ya ku China kupitiliza kumanga msewu umenewu mpaka atawapatsa ndalama zawo zomwe anagwirizana ndi a Roads Authority atachita kalembera wawo.

05/01/2016

Chigawo chazaumoyo kumpoto chalimbikitsa ntchito younika komanso kuphinzitsa anthu njira zosiyanasiyana pofuna kupewa kufalikira kwa matenda a kolela omwe abuka m'boma la Nkhata Bay.

Mbomali pofika Lolemba pa 4 January, 2016, mwapezeka anthu khumi ndi awiri (12) ndimatenda a kolela ndilomwe kumachokera zakudya zambiri zopita mumzinda wa Mzuzu choncho pali mantha kuti matendawo akhoza kufika mwamsanga mumzindawu.

05/01/2016

Chipani cha Peoples (PP) chasankha a Kamlepo Kalua kukukhala wachiwiri wina wa pulezidenti wa chipanichi.

Mneneri wa chipanichi, a Ken Msonda ati a Kamlepo Kalua awasankha ndi a Joyce Banda atakambirana ndiyemwe akugwirizira mpando wa pulezidenti wa chipanichi a Uladi M***a.

A Uladi M***a anawasankha sabata yatha kukhala wogwirizira mpando wa pulezidenti wa PP potsatita kuti mtsogoleri wachipanichi a Jocyce Banda alikunja kwadziko lino kuyambira mchaka cha 2014 atalephera pachisankho cha pulezidenti wa dziko lino.

Address

Mzuzu

Alerts

Be the first to know and let us send you an email when Nkhani Mchichewa posts news and promotions. Your email address will not be used for any other purpose, and you can unsubscribe at any time.

Share