30/05/2026
Mfumu yaikulu ya Angoni m'maiko a Zambia ndi Malawi ,Inkosi ya ma Nkosi Mpezeni yamwalira lero mdzikolo.
Malingana ndi nyumba zofalitsa nkhani mdziko la Zambia, Inkosi Mpezeni yamwalirira ap University Teaching Hospital ndipo thupi lake lasunthidwa kupita ku chipatala cha Maina Soko.
Inkosi ya ma Nkosi Mpezeni yomwe dzina lake lenileni ndi David Njengembanso Jere inalowa pa udindowu mchaka cha 1982 mdziko la Zambia ndipo yalamulira zaka zodutsa 40.
Inkosi Mpezeni imadziwika ndi mbiri yoteteza chikhalidwe cha angoni m'maiko a Zambia ndi Malawi.