Umunthu FM

Umunthu FM Broadcasting and Media production company. Advertising/Marketing

  Mfumu yaikulu ya Angoni m'maiko a Zambia ndi Malawi ,Inkosi ya ma Nkosi Mpezeni yamwalira lero mdzikolo. Malingana ndi...
30/05/2026


Mfumu yaikulu ya Angoni m'maiko a Zambia ndi Malawi ,Inkosi ya ma Nkosi Mpezeni yamwalira lero mdzikolo.

Malingana ndi nyumba zofalitsa nkhani mdziko la Zambia, Inkosi Mpezeni yamwalirira ap University Teaching Hospital ndipo thupi lake lasunthidwa kupita ku chipatala cha Maina Soko.

Inkosi ya ma Nkosi Mpezeni yomwe dzina lake lenileni ndi David Njengembanso Jere inalowa pa udindowu mchaka cha 1982 mdziko la Zambia ndipo yalamulira zaka zodutsa 40.

Inkosi Mpezeni imadziwika ndi mbiri yoteteza chikhalidwe cha angoni m'maiko a Zambia ndi Malawi.

30/05/2026


Wapampando wa komiti ya masapota a Arsenal ku Nkhotakota, Wilson Kambeja wati khumbo lawo ndilofuna kuti gululi lipite patsogolo.

Iwo ati akufuna kuti kupatula kukambirana za mpira, kutsogoloku akulingalira zomachita ntchito za chifundo, kuphatikizapo kuthandizana wina akagwedwa mavuto.

Iwo atsindika kuti mpira ndi chida chomwe chimapanga anthu osiyanasiyana kukhala pa ubale, choncho agwiritsa ntchito mwayiwu polimbikitsa ubale wabwino pakati pawo.

  Otsatira timu ya Arsenal m'boma la Nkhotakota akuchotsa dalazi komanso kumwerera posangalalira chipambano cha timuyi p...
30/05/2026


Otsatira timu ya Arsenal m'boma la Nkhotakota akuchotsa dalazi komanso kumwerera posangalalira chipambano cha timuyi pomwe yakhala akatswiri a ligi ya ku mangalande.

Kupatula kukhwasula, anthuwa akukadziwana, pambali pokambirana mapulani a momwe angapititsire patsogolo ubale womwe wayambawu komanso gululi.

30/05/2026


Social commentators are weighing opposing views on a decision by President Professor Arthur Peter in separating the Ministry of Energy and Mining into two standalone ministries.

One of the analysts, Peter Mumba says the decision increases the number of cabinet ministers, which calls for additional financial resources.

Mumba believes that besides laying a financial burden on already strained economy, it violates the 2025 campaign promise by the current administration of serving with a lean cabinet.

On the other hand, Dr. George Chaima welcomes the decision, arguing it will ensure efficiency in service delivery, saying the country needs the two ministries to commit themselves to transforming the energy and mining sectors.

In the statement yesterday, President Mutharika has appointed Dr. Jean Mathanga Minister of Energy, while Thoko Tembo MP has been appointed Minister of Mining.

30/05/2026


Apolisi ku Kasungu amanga m'phuzitsi wa zaka 32, Gerald Banda, pomuganizira kuti anali pa ubwezi wogonana ndi ophunzira wa zaka 16 wa standard 7 pa sukulu yomwe amaphunzitsa kuchokera mu April chaka chatha kufikira mwezi wa February chaka chino.

Wachiwiri kwa wofalitsa nkhani za apolisi m'bomali, Miracle Hauli, wati ophunzirayu adaneneza za nkhaniyi kwa makolo ake m'mwezi wa January chaka chino koma makolowa sadachitepo kanthu, zomwe zidapangitsa m'sungwanayu kukanena nkhaniyi kwa aphunzitsi akazi pa sukuluyi omwe adamulangiza kuti akatule nkhaniyi ku polisi ya Chinsinga

Hauli wati zotsatira zachipatala zasonyeza kuti msungwanayu amagonedwadi, zomwe zapangitsa kuti woganiziridwayu anjatidwe ndipo akaonekera ku bwalo la milandu posachedwapa kukayankha mlandu.

Banda ndi m'phuzitsi wachiwiri kumangidwa m'mwezi wa May ku Kasungu kutsatira kunjatidwaso kwa Jonathan Mponda Banda, m'phuzitsi wa sukulu ya sekondale ya Chankhanga pa mlandu ogonana ndikupereka mimba kwa msungwana wa zaka 17 wa pa sukuluyi.

Gerald Banda amachokera m'mudzi mwa Nkhuzenje mfumu yaikulu Simulemba ku Kasungu.

30/05/2026


One of the country’s transparency and accountability watch group has objected request by the Electricity Supply Corporation of Malawi (ESCOM) to Malawi Energy Regulatory Authority (MERA) to transfer a single buyer license for electricity generation to the Power Market Limited (PML).

The Center for Democracy and Economic Development Initiatives (CDEDI) argues the decision will likely cause electricity tariffs hike in near future, as PML will need human and financial resources to commence its operations.

CDEDI Executive Director, Sylvester Namiwa stresses that he sees no reason to have three companies: Electricity Generation Company (EGENCO), PML, and ESCOM working separately on a similar mission at a time Malawians are swimming in prolonged blackouts due to operational challenges facing these companies.

Namiwa says the organization has formally written the Malawi Energy Regulatory Authority (MERA) to block the process, saying it is not in the best interest of power consumers.

  Mkulu wa apolisi m'boma la Mchinji Dr. David Pheremero wayamikira ubale wabwino omwe ulipo pakati pa anthu ndi apolisi...
30/05/2026


Mkulu wa apolisi m'boma la Mchinji Dr. David Pheremero wayamikira ubale wabwino omwe ulipo pakati pa anthu ndi apolisi m'bomali.

Pheremero wayankhula izi la chisanu pomwe ophunzira ndi aphuzitsi pa sukulu ya pulaimale ya Nthunzi m'bomali anayendera komanso kupereka thandizo la chakudya kwa anthu omwe akusungidwa mchitokosi cha apolisi.

Iye wati izi zikusonyeza m'gwirizano wabwino pakati pa mbali ziwirizi, ndipo wathokoza sukukuyi kaamba ka zomwe yachita.

Mphunzitsi wamkulu pa sukulu ya pulaimale ya Nthunzi Nestory Kamude wati anachita izi ngati udindo omwe anthu okhala m'bomali akuyenera kumachita, pomwe wapempha anthu ena kuti azikhala ndi chikondi wina akakhala m'mavuto.

M'modzi mwa omwe akusungidwa mchitokosi cha apolisi yemwe walandira nawo thandizoli, Charles Chimombo wathokoza sukukuyi kaamba ka thandizo la chakudya, pomwe wapemphaso ena akufuna kwabwino kuchita chimodzimodzi kaamba koti ambiri pa malopa akusowekera chakudya.

  Mtsogoleri wa dziko lino Professor Arthur Peter Mutharika wagawa unduna owona za mphamvu za magetsi ndi mafuta komanso...
29/05/2026


Mtsogoleri wa dziko lino Professor Arthur Peter Mutharika wagawa unduna owona za mphamvu za magetsi ndi mafuta komanso migodi kukhala ma unduna awiri.

A Jean Mathanga MP, omwe amatsogolera undunawu usanagawidwe aikidwa ku unduna oona za mphamvu za magetsi komanso mafuta.

Pomwe a Thoko Tembo MP asankhidwa kukhala nduna yoona za migodi.

Aka ndi kachiwiri kuti undunawu ugawidwe kaamba koti ulendo oyamba kudachokaso unduna wa za chilengedwe komwe kuli a Patricia Wiskes.

  Komiti yomwe yakonza mwambo osangalalira chipambano cha timu ya Arsenal m'boma la Nkhotakota yati zonse zili mchimake ...
29/05/2026


Komiti yomwe yakonza mwambo osangalalira chipambano cha timu ya Arsenal m'boma la Nkhotakota yati zonse zili mchimake kuti achite ulendo wa ndawala komanso chisangalalo mawa pa 30 May m'bomali.

Ofalitsa nkhani za komitiyi, Edward Kuwacha wauza Umunthu FM kuti onse okonda ma 'Gunners' m'bomali akakumane pa bwalo la masewero la St. Paul's ndipo akayenda kudutsa pa boma mpaka kunyanja ku Kariba Beach Resort komwe kukakhala zisangalalo monga kudziwana komanso kukhwasula nyama.

Kuwacha wati khonsolo komanso apolisi m'bomali apereka chilolezo kuti kuyendaku kuchitike mwa bata ndi mtendere ndipo zonse zikayamba nthawi ya 1 koloko masana.

Iye wapempha ma Gunners onse m'boma la Nkhotakota kuti abwere pa chikondwererochi atavala makaka a timuyi.

Mawa lomweli, timu ya Arsenal ikhala ndi masewero a ndime yotsiriza ya chikho cha UEFA champions, ndipo okonda timuyi ati ali ndi nkhawa yoti chiwapweteke ndi chimwemwe pomwe akuti apambanaso chikhochi.

Timu ya Arsenal yakhala akatswiri a English Premier League ku England patatha zaka 22.

  Regional Manager for Ujama Pamodzi Africa, Susan Ngwira Phiri says the organization seeks to train teachers who will t...
28/05/2026


Regional Manager for Ujama Pamodzi Africa, Susan Ngwira Phiri says the organization seeks to train teachers who will then equip learners on how they can defend themselves against any form of violence in Nkhotakota.

Phiri told Umunthu FM Thursday after the Nkhotakota district council executive committee approved its 'Empowerment Transformation Training (ETT) Country-wide Scale up program'.

She says the project targets all schools in the lakeshore district, with 100 teachers from 50 schools earmarked for the first phase, adding figures will keep growing as the program progresses.

She adds that the project will, among others, help in linking survivors of violence, including those that are gender-based, to different service providers for assistance.

Address

Umunthu FM, P. O Box 26
Nkhotakota

Alerts

Be the first to know and let us send you an email when Umunthu FM posts news and promotions. Your email address will not be used for any other purpose, and you can unsubscribe at any time.

Contact The Business

Send a message to Umunthu FM:

Share