Umunthu FM

Umunthu FM Broadcasting and Media production company. Advertising/Marketing

  A polisi m'boma la Nkhotakota amanga bambo Richard Lazarus wazaka 52 yemwe  akuganizilidwa kuti anachita mchitidwe ogo...
01/09/2026



A polisi m'boma la Nkhotakota amanga bambo Richard Lazarus wazaka 52 yemwe akuganizilidwa kuti anachita mchitidwe ogonana ndi mwana wake omupeza wazaka 14.

Mneneri wa polisi ya bomali Sergeant Chisomo Chuma wati bambowa anachita izi usiku omwe akazi awo anali atapita kumaliro.

"Bambowa analowa kuchipinda chomwe mwanayo amagona limodzi azibale ake, ndikuchita zosaweruzikazo. Mayi ake atabwera m'mawa, mwanayo anaulula zomwe zinachitika ndipo mayiwa atamva izi, anakatula nkhaniyi ku polisi ya Benga," watero Chuma.

Atatengeledwa kuchipatala cha Benga, azaumoyo anatsimikiza kuti mwanayo anachitilidwadi nkhanza yogonedwa.

Bambowa omwe ndi a m'mudzi mwa Bonga, Senior Chief Mwadzama m'boma lomweli akuyembekezereka kukaonekera ku bwalo la milandu posachedwa.

  Gulu lochuluka lasonkhana kwa Senior Chief Nkhanga komwe mwambo operekeza thupi la malemu Senior Chief Nkhanga m'manda...
01/09/2026



Gulu lochuluka lasonkhana kwa Senior Chief Nkhanga komwe mwambo operekeza thupi la malemu Senior Chief Nkhanga m'manda ukuchitika.

Ena mwa anthu odziwika pamwambowu ndi monga ndina yoona za masewero ndi achinyamata, Alfred Gangata.

Senior Chief Nkhanga inamwalira loweruka lapitali pachipatala chaboma la Nkhotakota itadwala nthenda yofa ziwalo kwa kanthawi.

Mfumuyi yomwe dzina lenileni ndi Lex Ngaunje inabadwa pa 25 August, 1952.

  The body of Senior Chief Nkhanga of Nkhotakota District will be laid to rest today, following his death on 29th August...
01/09/2026



The body of Senior Chief Nkhanga of Nkhotakota District will be laid to rest today, following his death on 29th August 2026.

According to earlier communication from the Ministry of Local Government, signed by its Secretary, Rev. Moses Owen Chimphepo, Senior Chief Nkhanga was transferred from Malowa Health Centre to Nkhotakota District Hospital, where he was pronounced dead upon arrival.

Senior Chief Nkhanga, born Lex Ngaunje on 25th August 1952, had been sick for almost two years following a stroke.

He was appointed Sub Traditional Authority on 5th August 2016, elevated to Traditional Authority in 2019 and installed as Senior Chief in April 2025.

He is survived by his wife and six children.

 Mtsogoleri wa dziko la Zambia Hakainde Hichilema akhale akulumbilitsidwa lero ku bwalo la masewero la Heroes mu nzinda ...
01/09/2026



Mtsogoleri wa dziko la Zambia Hakainde Hichilema akhale akulumbilitsidwa lero ku bwalo la masewero la Heroes mu nzinda wa Lusaka, ndipo mwambowu ukudza pomwe Brian Mundubile mtsogoleri wa chipani chotsutsa boma, wapititsidwa ku ndende ya Mukobeko pomwe akuyimbidwa mlandu owukira boma.

Mkulu wa mabwalo a milandu Chief Justice Dr. Mumba Malila ndi yemwe akuyembekezereka kulumbilitsa Hitchelema ndi wachiwiri wake Mutale Nalumango.

Ena mwa alendo olemekezeka omwe akhale nawo pa mwambuwo ndi monga mtsogoleri wa dziko la Botswana Duma Boko komanso yemwe akuyimira mtsogoleri wa dziko la China Xian Hui.

Hakainde anapamba chisankho cha mdziko la Zambia chomwe chinachitika pa 13 August, 2026 ndi mavoti 60 pa 100 aliwonse, malingana ndi zotsatira zomwe zinalengezedwa ndi bungwe loyendetsa chisankho mdzikolo.

 Ofesi yoona za ntchito pa khonsolo ya boma la Nkhotakota yalangiza anthu okhala m'bomali kuti apewe kugwiritsa ana ntch...
31/08/2026


Ofesi yoona za ntchito pa khonsolo ya boma la Nkhotakota yalangiza anthu okhala m'bomali kuti apewe kugwiritsa ana ntchito zodutsa msinkhu wawo, makamaka m'migodi.

Mkulu wa ofesiyi, Charity Mwambira, walankhula izi lolemba pomwe anayendera m'godi wa Nambale kwa T/A Mwansambo m'bomali.

Mwambira wati ndizokhumudwitsa kuti ana azaka za pakati pa 11 ndi 16 akugwira ntchito m'migodi opanda zodzitetezera komanso nthawi yaitali zomwe zikuika miyoyo yawo pachiopsezo.

Polankhulapo, mkulu woyang'anira zachisamaliro cha anthu m'bomali, Macdonald Mpichi, wati iwo limodzi ndi ofesi yowona za ntchito apitiriza kugwira ntchito yodziwitsa anthu za kuipa kwa mchitidwewu komanso zotsatira zomwe zimadza kwa anthu omwe amalemba ntchito anawa.

Iye wati pomwe sukulu zikutsegulira posachedwapa, mafumu komanso makolo awonetsetse kuti mwana aliyense akupezeka mkalasi osati kumagwira ntchito m'malo osiyanasiyana monga migodi.

  Katswiri wa zamaphunziro Victor Chikoti wapempha boma kuti liyike chidwi chochuluka  pamaphunziro ozera pamakina a int...
31/08/2026



Katswiri wa zamaphunziro Victor Chikoti wapempha boma kuti liyike chidwi chochuluka pamaphunziro ozera pamakina a internet ndi cholinga chofuna kupereka danga kwa anthu ochuluka.

Chikoti wayankhula izi pomwe dziko lapansi lero likukumbukira tsiku la maphunziro apa internet.

Iye wati tsikuli likuyenera kuthandizira magulu osiyanasiyana kuwunikira za ndondomeko ya maphunzirowa powonetsetsa kuti akufikilika kwa aliyense.

Chikoti wati kupereka zipangizo zochuluka zophunzirira ndi nsanamira yopititsa patsogolo maphunziro komanso mwayi kwa ena.

  Civil Society Organizations (CSOs) in Nkhotakota District have announced plans to hold interface meetings with Nkhotak...
31/08/2026



Civil Society Organizations (CSOs) in Nkhotakota District have announced plans to hold interface meetings with Nkhotakota District Council to map the way forward ahead of the effective implementation of Constituency Development Funds (CDF).

The move comes in response to the last Local Authority Performance Assessment (LAPPA) report, which ranked the district poorly. The CSOs say, among other concerns, they were not actively engaged in GESD projects, making monitoring difficult.

Chairperson for Nkhotakota CSOs Dan Nthara told Umunthu FM that the committee recognizes that various factors contribute to LAPPA scores, one of which is stakeholder engagement for effective project implementation.

Nthara further added that from Wednesday this week, the committee will write to the Nkhotakota District Commissioner requesting to hold interface meetings on the matter.

 Timu ya Mighty Wanderers yaimitsa mphunzitsi wamkulu wa timuyi Bob Mpinganjira.Izi zikudza timuyi itagonja ndi Ekhaya F...
31/08/2026


Timu ya Mighty Wanderers yaimitsa mphunzitsi wamkulu wa timuyi Bob Mpinganjira.

Izi zikudza timuyi itagonja ndi Ekhaya FC mundime yotsiriza ya chikho cha Airtel Top 8 lamulungu pa Bingu National Stadium.

Malingana ndi mlembi wa bodi ya timuyi, Chancy Gondwe, masiku awiri akudzawa akhala akulengeza mpunzitsi wogwirizira komanso kusintha ena omuthandizira.

29/08/2026



Senior Chief Nkhanga ya m'boma la Nkhotakota yamwalira.

Malingana ndi uthenga ochokera ku ofesi yoona zochitika pa khonsolo ya bomali, mfumuyi yamwalira m'mawa wa lero loweruka itadwala kwa nthawi yaitali.

Zambiri zokhudza mwambo onse wamaliro zilengezedwabe.

 Khonsolo ya Boma la Mchinji yalangiza achinyamata m'bomali kuti akhale ochilimika pa ntchito zamanja kuti akhale odzida...
28/08/2026



Khonsolo ya Boma la Mchinji yalangiza achinyamata m'bomali kuti akhale ochilimika pa ntchito zamanja kuti akhale odzidalira komanso kupewa makhalidwe omwe angawononge moyo wawo.

Wapampando wa khonsoloyi Kennedy Peter Chipanga ndiye wanena izi pa mkumano wa masiku awiri wa achinyamata omwe khonsoloyi inachititsa pa sukulu yosula aphunzitsi m'bomali.

Chipanga wati achinyamata akuyenera kusintha kaganizidwe pa kachitidwe ka zinthu kuti moyo wawo upite patsogolo komanso pofuna kukwanilitsa masomphenya a mchaka cha 2063.

Iye wadzudzulanso mchitidwe ogonana ali ana achichepere womwe ati ukukolozela kukula kwa mimba zochuluka m'bomali ndipo wapempha anthu m'bomali kuti azineneza kwa adindo oyenera izi zikachitika.

M’mawu ake, woyang'anira achinyamata ku bungwe la Kacodo Dyson Chikoti wati apitiriza kulimbikitsa achinyamata kukhala odzidalira pantchito zamanja komanso kuwalangiza kuti apewe makhalidwe ogonana omwe angawononge tsogolo lawo.

Mkumano omwe unakonzedwa ndi khonsolo ya Mchinji unabweletsa pamodzi achinyamata oposa 300 ndicholinga chofuna kuwasula m’ntchito zosiyanasiyana zamanja komanso kuwaphunzitsa zakuipa kochita mchitidwe ogonana ali achichepere.

Address

Umunthu FM, P. O Box 26
Nkhotakota

Alerts

Be the first to know and let us send you an email when Umunthu FM posts news and promotions. Your email address will not be used for any other purpose, and you can unsubscribe at any time.

Contact The Business

Send a message to Umunthu FM:

Shortcuts

Share