Gaka FM

Gaka FM Gaka FM is a community licensed radio station based at Bangula, Nsanje District.

Gaka radio targets different types of people such as farmers, mothers, under five, youths, business communities, civil servants, pensioners, bankers, entrepreneurs, people with physical challenges, and local communities. The radio focuses on several thematic areas such as food and nutrition security, education and awareness, disaster risk management, health, water and sanitation, HIV and Aids, eco

nomic empowerment, and entrepreneurship. Some of the programs on Gaka radio are conducted live on the radio while others are recorded through the use of local journalists who produce almost all programs in our local languages of Sena and Chichewa hence unique in Malawi.

Job Opportunity at Gaka FMGaka FM, a radio station based in Nsanje District, is inviting applications from qualified and...
21/09/2025

Job Opportunity at Gaka FM

Gaka FM, a radio station based in Nsanje District, is inviting applications from qualified and passionate individuals to join its editorial team as Radio presenters and Reporters.

Gaka FM Team, testing testing the micto cover 2025 General Election
15/09/2025

Gaka FM Team, testing testing the mic
to cover 2025 General Election

28/08/2025


Wapampando wa gulu la amayi ndi mkomya pa wayilesi ya Gaka Fm, a Zephyrine Mkhutche apempha amayi kuchita malonda ang'onoang'ono kuti akhale odzidalira pa chuma.

A Mkhutche alankhula izi ku Bwabwali Community Day Secondary School m'boma la Chikwawa komwe gululi linali ndi mkumano wawo waukulu wa pa chaka.

Mwa zina pa tsikuli kumakhala ziphunzitso zosiyanasiyana monga za malonda, mabanja, ukhondo komanso amayi amagulirana mphatso zosiyanasiyana.

Polankhulapo pa mwambowu, mayi Loveness Moffat ochokera kwa Bereu anati ndiokondwa kuti chaka chino amayi abwera ku dera lawo kudzapanga mkumano waukulu wa pa chaka.

Aka ndikoyamba kuti amayi akumane kuderali, mikumano ngati iyi yakhala ikuchitikirapo Malo osiyanasiyana monga Bangula, Ngabu, Nchalo, Dyeratu, Livunzu ndi Madziabango.

Wolemba: Charity Alufinali

 Ophunzira aku pulayimare ochokera midzi yozungulira sukulu ya Hope Christian Boarding kwa nyakwawa yayikulu Konzere ku ...
26/08/2025


Ophunzira aku pulayimare ochokera midzi yozungulira sukulu ya Hope Christian Boarding kwa nyakwawa yayikulu Konzere ku Chikwawa apatsidwa mwai wa maphunziro a ulele ku sukuluyi.

Mkulu wa sukuluyi, Lapson Mbewe ndiye wanena izi pa mkumano wa makolo ndi a nyakwawa a m'derali lachiwiri ku sukuluyi.

Malinga ndi Mbewe, ganizoli ladza pofuna kuti ana a midzi yozungulira sukulu yake apindule nkupeza maphunziro a pamwamba kuti adzakhale ndi tsogolo labwino.

Iye anati ndi okhudzidwa kwambiri kuona ana a m'derali asakuchita bwino pa maphunziro awo zomwe anati zikusemphana ndi masomphenya ake pomwe ankayambitsa sukulu ku derali.

"Ganizo langa loyambitsa sukuluyi kuno kwa Konzere ndinkafuna kuti ana a kuno akhale oyamba kupindula. Zikundiwawa kuti ana ochokera kutali ndi omwe akupindula kwambiri ndi malo ano", anatero Mbewe.

Anyakwawa ndi makolo omwe anafika ku mkumanowu motsogozedwa ndi nyakwawa yayikulu Konzere, analulutira ndi kuombera manja pa ganizoli.

Kudzera mu ndondomekoyi, ophunzira ku sukuku ya pulayimale adzingolipira ndalama yokwana K30,000 yokha pa mwezi ya chakudya cha kadzutsa ndi nkhomaliro ndipo adzitha kulipira pang'ono pang'ono.

Wolemba: Charity Dzongwe

 ESCOM employee dies after falling from an electric Pole in NsanjeA 31-year-old man, employee from Electricity Supply Co...
25/08/2025


ESCOM employee dies after falling from an electric Pole in Nsanje

A 31-year-old man, employee from Electricity Supply Corporation of Malawi Limited (ESCOM) has died after falling from an electric pole while working at the Mbenje CR20 campsite in Nsanje District.

Confirming the incident, Nsanje Police Station Deputy Public Relations Officer, Sergeant Jabulani Ng’oma, said the deceased has been identified as Josephy Chilowa from Machinjiri in Blantyre.

Jabulani states that a report filed by his colleague, Mr. Jimy Katekesa, 36, an operations engineer with Escom based in Lilongwe, the tragic incident occurred at around 5:00 p.m.

Preliminary findings indicate that Chilowa was conducting maintenance work when he fell.

Following the incident, police have dispatched Criminal Investigation Department (CID) officers to the scene to establish the circumstances surrounding the accident.

Meanwhile, authorities have stated that a comprehensive report will be released after a postmortem examination has been conducted.

Reported by: Emmanuel Alufazema



 Yemwe akupikisana nawo mpando wa phungu wanyumba ya malamuro kudera la Nsanje Lalanje ngati woyima payekha, a Annie Olg...
25/08/2025


Yemwe akupikisana nawo mpando wa phungu wanyumba ya malamuro kudera la Nsanje Lalanje ngati woyima payekha, a Annie Olgha Sheha ati ndikhumbo lawo kudzatukula derali pokhazikitsa zitukuko zosiyana siyana ndipo apempha anthu kuti adzamuvotere pa 16 September kuti akwanilitse masomphenya awo.

Iwo amayankhula izi pa sukulu ya Pulayimale ya Bangula m'dera la mfumu yayikulu Mbenje m'bomali pamapeto amtsutso omwe bungwe la NICE unakonza kwa anthu omwe akupisana nawo pa mpando wa phungu wanyumba ya malamuro ndi udindo waukhalansala pazomwe adzawachile akadzawaika pa mpando.

Mayi Sheha ati kuderali kuli mavuto ambiri ofuna kukonzedwa monga vuto la njala lomwe limasautsa kwambiri anthu chifukwa akalima mbewu zawo zimakokoledwa ndi madzi osefukira kapena kukhudzidwa ndi ng’amba, choncho ati akawayika pampando adzakhazikitsa chitukuko chaulimi wamthilira kuti anthu azidzakolola mbewu zochuluka ndikukhala ndi chakudya chokwanira m’mawanja mwawo.

Iwo anaonjezera kuti adzaonetsetsa kuti akutukura achinyamata pa ntchito yowonjezera mphamvu ku zokolola za alimi pogwilira ntchito limodzi ndi alimi, zomwe zidzathandizire kupeza phindu lochuluka akagulitsa mbewu zawo.

Iwo ati kosowekera kwa madzi abwino ndi ena mwa mavuto omwe akukhudza derali, ndipo adzakhazikitsa chitukucho cha madzi monga kuyiyika mijigo m’malo momwe mulibe ndi momwe ilipo yochepa, komanso kukhazikitsa madzi amipopi m’mawodi onse awiri m’derali chifukwa anthu akumwa madzi anchere. Mwachitsanzo iwo atchura dera la Sorgin kuti likusalira mbuyo chifukwa kulibe madzi amipopi.

Mayi Sheha omwe mbuyomu anayomanso pa mpandowu, mwazina anaonjezera kuti adzakonza misewu yoonongeka kuti anthu adziyenda bwinobwino, adzakhazikitsa sukulu yaukachenjede ya ntchito zamanja kuti achinyamata azidzaphunzira ntchito zamanja, adzabweretsa magetsi kudera la Mitoni komanso kutukura azimayi kuchita mabizinesi ndikukhala odzidalira pachuma.

M’mawu ake, a Mack Mathenga omwenso akuyima paokha ngati khansala ku wodi ya Lalanje yemwenso akuyendera limodzi ndi mayi sheha pamisonkhano yomema anthu kudzawavotera ati anthu akuderali awakhulupilire powapatsa mavoti ochuluka ndicholinga choti chitukuko chaulimi wamthilira chidzatheke kuti vuto la njara idzakhale mbiri yakale kuderali.

Pakadalipano anthu omwe akupikisana pa mpando wa phungu wanyumba ya malamuro ku Nsanje Lalanje alipo asanu ndi awiri (7) pamene anthu asanu ndi atatu (8) ndiomwe akupikisana nawo pa mpando wa ukhansala ku wodi ya Lalanje m’derali.

Wolemba: Emmanuel Alufazema

24/08/2025


Malawian man drowns in Mozambique while returning home with dry Fish – Nsanje Police Confirm

A 20-year-old Malawian man from Nsanje District has drowned in Mozambique’s Shire Province after a canoe he boarded to return home capsized.

Nsanje Police Station’s Deputy Public Relations Officer, Sergeant Jabulani Ng’oma, has confirmed the incident and identified the deceased as Innocent Neva, first-born son of Mr Neva Petulo, 60, of Nkhundi Village under Traditional Authority Malemia.

According to Ng'oma, Neva left home on 22 August 2025 at around 6:00 a.m. to buy dry fish at Nyaphwatha fishing dock in Mozambique. On his return journey, the canoe capsized midstream. While the operator managed to swim to safety, Neva, who could not swim, was swept away by strong currents.

His body was later recovered and taken to his home village.

Postmortem results confirmed that death was due to suffocation caused by drowning.

Meanwhile, police have ruled out foul play and described the incident as a tragic accident.

Reported by: Emmanuel Alufazema

 Bungwe loyendetsa zisankho mdziko muno la MEC lapempha anthu a m’dera la Nsanje Lalanje kuti adzaponye voti motsatira n...
23/08/2025


Bungwe loyendetsa zisankho mdziko muno la MEC lapempha anthu a m’dera la Nsanje Lalanje kuti adzaponye voti motsatira ndondoko yachisankho ndicholinga choti voti yawo idzagwire ntchito moyenera poyika pa mpando atsogoleri akumtima kwawo.

Mphunzitsi wazisankho wabungwe la MEC kudera la Nsanje Lalanje, a Edith Kazingatchire wapeleka pempholi lachisanu patsutso wandale omwe unakonzedwa ndi bungwe la NICE pa sukulu yapulaimale ya Bangula.

Cholinga cha mtsutsowu kunali kubweretsa pamodzi anthu akuderali kuti adzamve mfundo zachitukuko zomwe anthu akufuna kupikisana pa mpando wauphungu wanyumba yamalamuro komanso ukhansala adzawachitire akadzapambana zisankho zapa 16 September chaka chino.

Kazingatchire walimbikitsa anthu akuderali kuti adzitenga gawo pokhala nawo pa mtsutso wandale kuti adzitha kumva mfundo zachitukuko ndikupanga ziganizo zoyenera kusankha adindo oyenera omwe angatukule kudera lawo.

“Mtsutsu umenewu ndi ofunika kwambiri, chifukwa umatipatsa ife a Malawi mwayi wokhala ndi nthawi yokumva mfundo zosiyanasiyana kuchokera kwa anthu amene akufuna kupikisana nawo m'mipando yosiyanasiyana. Nthawi zambiri timalephera kupezeka pa misonkhano yomwe amapanga kuti timve mfundo zawo, nthawi zina chifukwa timakhala busy ndi zinthu zina. Nde, kukakhala nawo pa mtsutso ngati umenewu, nkofunikira kwambiri kuti tidziwe kuti, tikawasankha ngati khansala kapena ngati phungu wadera lathu, adzatipangiranji,” adafotokoza motero Kazingatchire.

Iwo anapitilira kulangiza anthu ochuluka omwe anasonkhana pa malowa kuti apange kampeni ya bata ndi mtendere ndipo izi kuti zitheke akuyenera apewe kuchita ziwawa komanso kunyozana.

M'mawu ake, Mfumu Nyang’a ya m’dera la Mfumu yayikulu Mbenje m’bomali ayamikira bungwe la NICE kamba kokonza mtsutsowu wapamwamba ponena kuti wazindikiritsa anthu ambiri kuti apange chisankho chodzavotera adindo pachisankho chikudzachi.

Nkumanowu unabweretsa pamodzi omwe akufuna kuyimira mmipando ya makhansala, aphungu anyumba ya malamuro akuderali, mafumu, apolisi, atsogoleri azipani ndi azipembedzo zosiyanasiyana komanso akuluakulu ochokera ku khonsolo la boma la Nsanje.

Wolemba: Emmanuel Alufazema



 Wachiwiri kwa mtsongoleri wachipani cha DPP Dr Jane Ansah wafika pa Bangula Trading Centre pamene akhale akulankhula an...
13/08/2025


Wachiwiri kwa mtsongoleri wachipani cha DPP Dr Jane Ansah wafika pa Bangula Trading Centre pamene akhale akulankhula anthu omwe asonkhana pa malowa pa ulendo wawo wandale woyimayima kumema anthu kuti adzavotere chipanichi pa 16 September.

Pakadalipano, anthu ochokera madera osiyanasiyana kuphatikizapo a midzi yozungulira Bangula m'bomali afika pa malowa.

Tikupatsilani zambiri

 Wachiwiri kwa mtsongoleri wachipani cha DPP, Dr. Jane Ansah wafika pa Bangula Trading Centre pamene akhale akulankhula ...
13/08/2025


Wachiwiri kwa mtsongoleri wachipani cha DPP, Dr. Jane Ansah wafika pa Bangula Trading Centre pamene akhale akulankhula anthu omwe asonkhana pa malowa pa ulendo wawo woyimayima.

Anthu amidzi yozungulira derali afika pa malowa.

 Yemwe akupikisana nawo ngati khansala woyima payekha ku Mlonda wadi dera la Nsanje Lalanje, a Jackson Jussah alimbikits...
13/08/2025


Yemwe akupikisana nawo ngati khansala woyima payekha ku Mlonda wadi dera la Nsanje Lalanje, a Jackson Jussah alimbikitsa anthu a derali kuti azawavotere ngati akufuna kuti derali lipite patsogolo pachitukuko.

A Jussah ati kwa nthawi yayitali anthu akhala akuvutika kupeza zitukuko zosiyanasiyana kamba koyika anthu adyera pa mpandowu.

Poyankhula ndi Gaka_online, a Jussah ati akazapambana pa mpandowu azaonetsetsa kuti miyoyo ya anthu a derali ikutukuka.

Iwo ati azalimbikitsa ntchito za maphunziro,kupitisa patsogolo ulimi wanthirira,kusamalira olumara komanso okalamba.

Iwo anapitilira kutsindika kuti azayikanso achinyamata ndi amayi m'magulu momwe azizawapezera ngongole zoyambira bizinezi zing'onong'ono ndicholinga chotukula miyoyo yawo.

M'modzi mwa atsogoleri a ndale kuderali, a Patrick Saizi ati Jussah ndi munthu yekhayo oyenera kukhala khansala wawo chifukwa mfundo zake ndizogwira mtima komanso amamva zofuna za anthu. Iwo apempha anthu kuderali kuti azavotere a Jussah pa 16 September ngati khansala wawo.

Wolemba: Peterson Adam

 Nsanje, Malawi — Pulogalamu ya Nyafisi Irrigation Scheme yomwe ili kwa Group Village Head Anne Petro, Mfumu Mbenje m’bo...
09/08/2025


Nsanje, Malawi — Pulogalamu ya Nyafisi Irrigation Scheme yomwe ili kwa Group Village Head Anne Petro, Mfumu Mbenje m’boma la Nsanje, yasanduka chithunzithunzi cha chiyembekezo kwa alimi, ikuwonetsa mmene ntchito za ulimi wothilira pogwiritsa ntchito mphamvu ya dzuwa zikhoza kusintha miyoyo ya anthu kumudzi komanso kulimbikitsa ulimi wothandiza chaka chonse.

Kuchokera ku Mavuto Kupita ku Chiyembekezo: Alimi Afotokoza Zomwe Akukumana Nazo

Kwa zaka zambiri, alimi ang’onoang’ono m’madera amenewa akumanapo ndi kusowa kwa mvula yokwanira, zokolola zochepa komanso ndalama zochepa. Lero, chifukwa cha dongosolo la solar-powered irrigation, alimi akhoza kulima ndi kukolola masamba chaka chonse komanso kupeza ndalama zokwanira.

“Tsopano ndimalipira ndalama za sukulu za ana anga, ndimagula sopo ndi chakudya,” watero Ruth Elias, m’modzi mwa amayi omwe akupindula ndi polojekitiyi. Iye akufuna kupititsa patsogolo nkhani zachuma pochita ulimi wa mbuzi.

Jambo Simon, mlimi wachinyamata, anenanso kuti pulogalamuyi ikulimbikitsa achinyamata ndi akulu mofanana. “Ife achinyamata tikutenga nawo mbali zonse, tili ofunitsitsa. Timagwira ntchito limodzi ndi akulu athu kuti pulogalamuyi ipitirire komanso tikhale ndi tsogolo labwino,” adatero Simon.

Zotsatira Zake Zapindulira Alimi ochuluka
Paul Mafambisa, wapampando wa Nyafisi Irrigation Scheme, anauza Gaka online kuti polojekitiyi yasintha kwambiri miyoyo ya alimi, ndipo tsopano amatha kukwaniritsa zosowa zawo za tsiku ndi tsiku komanso kupanga mapulani a nthawi yayitali.
“Kusiyana kuli poyera. Mabanja athu amakhala bwino, amadya bwino komanso tili ndi chiyembekezo,” adatero Mafambisa.

Chofunika kwambiri, zabwino zomwe zikubwera ndi polojekitiyi sizimangokhudza alimi omwe ali m’pulogalamuyi.

Mlangizi wazaulimi ku Magoti EPA, Collins Walasi wati ngakhale anthu a m’madera ozungulira akugula masamba pa mtengo wotsika. Alimi sakukoloranso mbewu kamodzi pachaka, ena akukolora mpaka katatu chaka chimodzi.

“Izi ndi zomwe Malawi imafunikira,” adatero Walasi. “Zikugwirizana bwino ndi zolinga za Malawi Vision 2063, makamaka pa chakudya chokwanira komanso kusintha moyo wa anthu kumudzi.”

Thandizo la Othandizira Latsegulira Njira Yachitukuko Chokhazikika
Yoyambitsidwa mu 2023, Nyafisi Irrigation Scheme inathadizidwa ndi bungwe la Foundation for Active Civic Education (FACE), ndi thandizo la ndalama kuchokera ku bungwe la ALL WE CAN, la ku UK. Thandizo la alawo la solar irrigation system lalimbikitsa zokolola komanso lapatsa anthu m’mudzi zida zokhazikika za chitukuko komanso kupeza chuma mosalekeza.

Kusanthula: Pulogalamu Yoyenera Kuyesedwa m’madera Ena a Kumudzi


Pulogalamu ya Nyafisi si nkhani yoti ingopezeka kuderai kokha ayi, ndi chitsanzo choyenera kuyesedwa m’madera ena ambiri a Malawi. Ikuwonetsa kuti ngati dziko likonzekera kugwiritsa ntchito mphamvu zochokera ku dzuwa (renewable energy) komanso kuthandiza anthu osauka, ulimi wa kudalira mvula ukhoza kusintha kukhala ulimi wothandiza nthawi zonse.

Funso lalikulu ndi kuti pulogalamuyi ingatengedwe bwanji ku madera ena kumene alimi ambiri akadadalira mvula. Mgwirizano wa boma, ma NGO, ndi mabungwe othandizira ndiwo ofunika kwambiri.

Pomaliza: Kuchokera pa Kudalira Kupita ku Kudziyimira
Nkhani ya Nyafisi ikutiuza kuti kusintha kwenikweni kumachitika ngati anthu apatsidwa zida, mphamvu komanso chithandizo choyenera. Pamene alimi akukolola zotsatira za ntchito yawo, uthenga ndi uwui: ulimi wothiriridwa ndi madzi si madzi okha — ndi ulemu, mwayi, ndi chiyembekezo.

Wolemba; Yohane Chipula

Address

Nsanje

Alerts

Be the first to know and let us send you an email when Gaka FM posts news and promotions. Your email address will not be used for any other purpose, and you can unsubscribe at any time.

Contact The Business

Send a message to Gaka FM:

Share

Category