Gaka FM

Gaka FM Gaka FM is a community licensed radio station based at Bangula, Nsanje District.

Gaka radio targets different types of people such as farmers, mothers, under five, youths, business communities, civil servants, pensioners, bankers, entrepreneurs, people with physical challenges, and local communities. The radio focuses on several thematic areas such as food and nutrition security, education and awareness, disaster risk management, health, water and sanitation, HIV and Aids, eco

nomic empowerment, and entrepreneurship. Some of the programs on Gaka radio are conducted live on the radio while others are recorded through the use of local journalists who produce almost all programs in our local languages of Sena and Chichewa hence unique in Malawi.

 Nsanje, Malawi — Pulogalamu ya Nyafisi Irrigation Scheme yomwe ili kwa Group Village Head Anne Petro, Mfumu Mbenje m’bo...
09/08/2025


Nsanje, Malawi — Pulogalamu ya Nyafisi Irrigation Scheme yomwe ili kwa Group Village Head Anne Petro, Mfumu Mbenje m’boma la Nsanje, yasanduka chithunzithunzi cha chiyembekezo kwa alimi, ikuwonetsa mmene ntchito za ulimi wothilira pogwiritsa ntchito mphamvu ya dzuwa zikhoza kusintha miyoyo ya anthu kumudzi komanso kulimbikitsa ulimi wothandiza chaka chonse.

Kuchokera ku Mavuto Kupita ku Chiyembekezo: Alimi Afotokoza Zomwe Akukumana Nazo

Kwa zaka zambiri, alimi ang’onoang’ono m’madera amenewa akumanapo ndi kusowa kwa mvula yokwanira, zokolola zochepa komanso ndalama zochepa. Lero, chifukwa cha dongosolo la solar-powered irrigation, alimi akhoza kulima ndi kukolola masamba chaka chonse komanso kupeza ndalama zokwanira.

“Tsopano ndimalipira ndalama za sukulu za ana anga, ndimagula sopo ndi chakudya,” watero Ruth Elias, m’modzi mwa amayi omwe akupindula ndi polojekitiyi. Iye akufuna kupititsa patsogolo nkhani zachuma pochita ulimi wa mbuzi.

Jambo Simon, mlimi wachinyamata, anenanso kuti pulogalamuyi ikulimbikitsa achinyamata ndi akulu mofanana. “Ife achinyamata tikutenga nawo mbali zonse, tili ofunitsitsa. Timagwira ntchito limodzi ndi akulu athu kuti pulogalamuyi ipitirire komanso tikhale ndi tsogolo labwino,” adatero Simon.

Zotsatira Zake Zapindulira Alimi ochuluka
Paul Mafambisa, wapampando wa Nyafisi Irrigation Scheme, anauza Gaka online kuti polojekitiyi yasintha kwambiri miyoyo ya alimi, ndipo tsopano amatha kukwaniritsa zosowa zawo za tsiku ndi tsiku komanso kupanga mapulani a nthawi yayitali.
“Kusiyana kuli poyera. Mabanja athu amakhala bwino, amadya bwino komanso tili ndi chiyembekezo,” adatero Mafambisa.

Chofunika kwambiri, zabwino zomwe zikubwera ndi polojekitiyi sizimangokhudza alimi omwe ali m’pulogalamuyi.

Mlangizi wazaulimi ku Magoti EPA, Collins Walasi wati ngakhale anthu a m’madera ozungulira akugula masamba pa mtengo wotsika. Alimi sakukoloranso mbewu kamodzi pachaka, ena akukolora mpaka katatu chaka chimodzi.

“Izi ndi zomwe Malawi imafunikira,” adatero Walasi. “Zikugwirizana bwino ndi zolinga za Malawi Vision 2063, makamaka pa chakudya chokwanira komanso kusintha moyo wa anthu kumudzi.”

Thandizo la Othandizira Latsegulira Njira Yachitukuko Chokhazikika
Yoyambitsidwa mu 2023, Nyafisi Irrigation Scheme inathadizidwa ndi bungwe la Foundation for Active Civic Education (FACE), ndi thandizo la ndalama kuchokera ku bungwe la ALL WE CAN, la ku UK. Thandizo la alawo la solar irrigation system lalimbikitsa zokolola komanso lapatsa anthu m’mudzi zida zokhazikika za chitukuko komanso kupeza chuma mosalekeza.

Kusanthula: Pulogalamu Yoyenera Kuyesedwa m’madera Ena a Kumudzi


Pulogalamu ya Nyafisi si nkhani yoti ingopezeka kuderai kokha ayi, ndi chitsanzo choyenera kuyesedwa m’madera ena ambiri a Malawi. Ikuwonetsa kuti ngati dziko likonzekera kugwiritsa ntchito mphamvu zochokera ku dzuwa (renewable energy) komanso kuthandiza anthu osauka, ulimi wa kudalira mvula ukhoza kusintha kukhala ulimi wothandiza nthawi zonse.

Funso lalikulu ndi kuti pulogalamuyi ingatengedwe bwanji ku madera ena kumene alimi ambiri akadadalira mvula. Mgwirizano wa boma, ma NGO, ndi mabungwe othandizira ndiwo ofunika kwambiri.

Pomaliza: Kuchokera pa Kudalira Kupita ku Kudziyimira
Nkhani ya Nyafisi ikutiuza kuti kusintha kwenikweni kumachitika ngati anthu apatsidwa zida, mphamvu komanso chithandizo choyenera. Pamene alimi akukolola zotsatira za ntchito yawo, uthenga ndi uwui: ulimi wothiriridwa ndi madzi si madzi okha — ndi ulemu, mwayi, ndi chiyembekezo.

Wolemba; Yohane Chipula

  Kutumikira Alimi Bwino: Uthenga wa Extension ndi Mfungulo Yopititsira Patsogolo Zaulimi ku MalawiDziko la Malawi likup...
02/08/2025


Kutumikira Alimi Bwino: Uthenga wa Extension ndi Mfungulo Yopititsira Patsogolo Zaulimi ku Malawi

Dziko la Malawi likupitirira kulota za chitukuko kudzera mu Malawi Vision 2063, koma akatswiri a zaulimi akuchenjeza kuti ngati ntchito yopereka uthenga kwa alimi (extension services) sikukonzedwa mwamphamvu, zokambirana za zokolola zambiri ndi malonda aulimi zidzangokhalabe m'maloto.

Mphamvu Yoyendetsa Chitukuko cha Zaulimi

Polankhula ndi Gaka Online, katswiri wa zaulimi Leonard Chimwaza wati ntchito ya extension ndiyofunika kwambiri ngati dziko likufuna kuwonjezera zokolola ndi kulimbikitsa malonda muulimi.
“Kupambana kwa ntchito ya extension kumadalira momwe alimi amathandizidwira kudziwa ufulu wawo wofuna chithandizo.

Popanda kuwaphunzitsa bwino, alimi sangapindule ndi ntchito zomwe zikuwalimbikitsa,” adatero Chimwaza.
Ukadaulo ndi Mawayilesi: Njira Zotsekulira Chidziwitso kwa Alimi
Chimwaza adafotokoza kuti dziko la Malawi liyenera kugwiritsa ntchito njira zosiyanasiyana, kuphatikiza ukadaulo (ICT) ndi mawayilesi, pofalitsa uthenga kwa alimi. “Sititha kulankhula za zokolola zambiri kapena malonda pomwe alimi ambiri ali m’mkati mwa mdima wa kusadziwa. Kusadziwa ndiko kumachepetsa zokolola,” adachenjeza motero.

Izi zikugwirizana ndi Pillar One ya Malawi Vision 2063, yomwe imalimbikitsa malonda aulimi. Koma popanda njira zolimba zothandizira alimi, Vision 2063 ingangokhalira mu pepala.
Zovuta M’munda: Ogwira Ntchito a Extension Akunyanyala pa Ntchito

M’mbali ya alimi, zinthu sizikuyenda. Francis Mvula, Mkulu woona zaulimi m’boma la Chikwawa, adati zinthu zikuvuta kwambiri kumidzi. “Kusowa kwa mayendedwe, nyumba zosasangalatsa za antchito, komanso maphunziro akale kwa ogwira ntchito, zikuchititsa kuti ntchito ya extension isamayende bwino,” adafotokoza.

Mvula adawonjeza kuti chiŵerengero cha alimi pa extension worker ndichachikulu kwambiri. “M’malo mopereka chithandizo kwa alimi 750, tsopano munthu m'modzi akuyenera kuthandiza alimi 3,000. Izi n’zosatheka,” adatero.

Kodi Malawi Itani?
Akatswiri onse akuvomereza kuti ngati Malawi ikufuna kusintha ulimi kukhala wa malonda komanso wothandiza pa chuma, extension services ziyenera kulimbikitsidwa. Pali kufunikira kodzaza mipata: kulimbikitsa ntchito za extension, kugwiritsa ntchito ukadaulo, komanso kulemba antchito ochulukirapo ndi ophunzitsidwa bwino.

Ngati Vision 2063 ikufuna kukhala zenizeni, nthawi yoti dziko liyambirepo ntchito ndiyino, osati kulankhula chabe.
Extension ndi chinsinsi cha chitukuko — osati chotchedwa chabe. Popanda kuthandiza alimi kudziwa ndi kuchita bwino, chitukuko cha zaulimi ndi malonda chidzangokhala maloto chabe.

Wolemba: Yohane Chipula


30/07/2025


Minibus fares have unmercifully gone up in Chikwawa and Nsanje due to the scarcity of fuel.

A spot check conducted by Gaka FM on tuesday and wednesday has shown that passengers were paying more than expected as the fares were too high.

Nchalo to Bangula, passengers were paying K10,00 on tuesday, a journey normally costs K3000 to K4000.

Reported by Charity Dzongwe

 Mtsongoleri wachipani cha UTM, Dr Dalitso Kabambe, wafika ku Bingu International Convention Centre mu nzinda wa Lilongw...
27/07/2025


Mtsongoleri wachipani cha UTM, Dr Dalitso Kabambe, wafika ku Bingu International Convention Centre mu nzinda wa Lilongwe kukapeleka ku MEC mapepala osonyeza kuti ayimira pa u president wa dziko lino pa zisankho zikudzazi pa 16 September 2025.

Dr Kabambe wafika pa malowa akuyendetsa okha Tractor motsogozedwa ndi dipiti wa galimoto za ntunduwu amodzi ndi otsatira chipanichi.

Polankhula ku ntundu wa amalawi Dr Kabambe asankha a Dr Mathews Mtumbuka ngati running mate wawo.

Poyankhulapo powalandira a Kabambe, mkulu wa bungwe la MEC, a Andrew Mpesi wati akufika kwawo kuzapeleka zikalata zawo ku bungweli ndi chitsimikizo chofuna kuwatumikira amalawi akapambana chisankho chikudzachi.

Iwo apempha chipanichi kuti chikuyenera kupanga kampeni ya Bata ndi mtendere pogwiritsa ntchito mfundo osati kulankhula mawu onyoza kapena odzetsa ziwawa.

Wolemba: Emmanuel Alufazema

 Mtsongoleri wa chipani cha UTM,  Dalitso Kabambe tsopano akufika  ku Bingu International Convention Centre akuyendetsa ...
27/07/2025


Mtsongoleri wa chipani cha UTM, Dalitso Kabambe tsopano akufika ku Bingu International Convention Centre akuyendetsa okha Thilakitala.

Wolemba: Emmanuel Alufazema

Mtsongoleri wachipani cha UTM, Dr Dalitso Kabambe, akuyembekezeleka  kufika ku Bingu International Convention Centre mu ...
27/07/2025

Mtsongoleri wachipani cha UTM, Dr Dalitso Kabambe, akuyembekezeleka kufika ku Bingu International Convention Centre mu nzinda wa Lilongwe kukapeleka ku MEC mapepala osonyeza kuti ayimira pa u president wa dziko lino pa zisankho zikudzazi pa 16 September 2025.

Pakadalipano otsatira chipanichi afika kale pa malowa ndipo afika mwa Bata kusiyana ndi zipani zina zomwe zapeleka kale zikalata zawo.

Anthu ambiri akufuna amve komanso kuona okha kuti a Kabambe asankha ndani ngati running mate wawo lero.

Zambiri tikupatsilani

 Pamene bungwe loona zachisankho mdziko muno la Malawi Electoral Commission (MEC) likupitilira kulandira zikalata za ant...
26/07/2025


Pamene bungwe loona zachisankho mdziko muno la Malawi Electoral Commission (MEC) likupitilira kulandira zikalata za anthu omwe awonetsa chidwi kudzapikisa nawo pa chisankho cha pa 16 September, yemwe akuimira chipani cha Democratic Progressive (DPP) pachisankho cha aphungu m'dera la Lalanje m'boma la Nsanje, a Gladys Ganda ati akonzeka kukapeleka zikalata zowayeneleza kuima nawo pachisankho ku bungweli lachita pa 30 July sabata la mawa.

A Ganda alengeza izi kudzera pa tsamba lawo la Facebook, ndipo wapempha anthu m'derali kuti adzamuvotelenso pa mpandowu pachisankho chikudzachi.

Mayiyu wati anthu akuderali akuyenera kumupatsanso mwayi wina owatumikira ngati phungu wawo kuti amalizitse ntchito zachitukuko zomwe anaziyambitsa pofuna kupitiliza kutukula derali.

Phungu wakaleyu anatumikira derali kwa zaka zisanu ndi chimodzi.

Pa chisankho chikudzachi, mayi Ganda akuyembekezeleka kudzapikisana ndi a Jim Chaola oima paokha, a Anne Ngwali oima paokha, a Bilal Karim oima paokha, a Edward Gamba achipani cha Malawi Congress (MCP) ndi a Nthandamwezi Given Khumbanyiwa achipani cha United Transformation Movement (UTM).

Wolemba: Emmanuel Alufazema

 M'modzi mwa ophunzira akale pa sukulu ya Bangula pulayimale, a Bilaal Karimu yemwenso akudzaima nawo pa chisankho cha p...
26/07/2025


M'modzi mwa ophunzira akale pa sukulu ya Bangula pulayimale, a Bilaal Karimu yemwenso akudzaima nawo pa chisankho cha pa 16 september ngati phungu woima payekha walimbikitsa ophunzira apa sukuluyi kuti alimbikire maphunziro kuti adzakhale nzika zodalilika.

A Karimu alankhula izi lachisanu pa Bangula pulayimale sukulu m'dera la mfumu yayikulu Mbenje m’boma la Nsanje pa mwambo wotsekera teremu yotsiriza mu kalenda yamaphunziro ya chaka cha 2024 ndi 2025.

A Karimu anapitilira kupempha ophunzira akale kuti adzitha kupezeka mu zochitika ngati zimenezi pofuna kulimbikitsa ophunzira a sukulu za pulayimare kuti apite patsogolo ndi maphunziro awo.

Polankhulapo pa mwambowu , a Costa Nkhani yemwe ndi khala pampando wa komiti yamakolo aphunzitsi ndi ana pa sukulu ya Bangula ayamikira ntchito yabwino yomwe aphunzitsi akugwira komanso adandaula Kamba mavuto omwe akukumana nawo pasukuluyi.

Wolemba: Yohane Chipula

 Wamkulu wa bungwe la Malawi Electoral Commission (MEC), a Andrew Mpesi ati bungwe lawo lipitiliza kugwira ntchito yawo ...
26/07/2025



Wamkulu wa bungwe la Malawi Electoral Commission (MEC), a Andrew Mpesi ati bungwe lawo lipitiliza kugwira ntchito yawo mosakondera chipani kapena munthu wina aliyense mu nyengo yonse ya chisankho.

A Mpesi alankhula izi lero masana ano ku Bingu International Convention Conference Centre mu nzinda wa Lilongwe pamene amalandira zikalata kuchokera ku chipani cha Peoples Development Part (PDP) chomwe chikutsogoleledwa ndi Dr Kondwani Nankhumwa.

Pakadalipano, Mtsongoleri wachipani cha People Development Party (PDP), Dr. Kondwani Nankhumwa wapeleka zikalata zawo ku bungwe la MEC kutsimikizira chidwi chawo chopikisana nawo pa mpando wautsogoleri wadziko pa chisankho chikudzachi pa 16 September chaka chino.

Polankhulapo atapatsidwa mpata pa mwambowu, a Nankhumwa auza ndi kuonetsera ku ntundu wa a Malawi mayi Bertha Ndebele kuti ndi wachiwiri wawo pa ulendo wa chisankho chikudzachi.

Dr Nankhumwa wati mayi Ndewere ndiwophunzira bwino omwe anapanga maphunziro osiyanasiyana ku sukulu zaukachenjede komanso kugwira ntchito nthambi zosiyanasiyana. Iwo ati mayiwa amachokera m'mudzi mwa Magombela Mfumu yayikulu Nsamala m'boma la Balaka.

Pakadalipano, mwambowu ikupitilirabe.

Wolemba: Emmanuel Alufazema

 Mtsogoleri wa chipani cha United Democratic Front (UDF), a Atupele Muluzi ati chipani chawo cha UDF chakonzeka kupikisa...
26/07/2025


Mtsogoleri wa chipani cha United Democratic Front (UDF), a Atupele Muluzi ati chipani chawo cha UDF chakonzeka kupikisana nawo pa chisankho chikudzachi pofuna kutumikira a Malawi akapambana chisankho cha pa 16 September chaka chino.

Polankhula ku mtundu wa amalawi, a Muluzi ati lero ndi tsiku lopambana kwambiri pamene apeleka zikalata zawo ku MEC komanso ndi mayankho kwa otsatira chipani cha UDF.

A Muluzi alankhula izi mu nzinda wa Lilongwe pamene amapeleka zikalata zawo ku bungwe la MEC komanso kuwonetsa ku ntundu wa amalawi wachiwiri wawo Dr. Lex Kalolo.

Iwo ati Dr Kalolo amachokera mu nzinda wa Lilongwe, ndi munthu waphunziro apamwamba ndipo anagwira ntchito ku unduna wazaumoyo, komanso anadziwana zaka zisanu zapitazo.

Iwo adzudzura nchitidwe wa nkhanza womwe anthu ena akhala akuchitira ena pa ndale, ndipo apempha nthambi ya chitetezo mdziko muno kuti akhwimitse kupeleka chitetezo mu nyengo yonse ya chisankho.

A Muluzi omwe ndi mwana wa mtsogoleri wakale wa dziko lino Dr. Bakili Muluzi, wapemphanso bungwe la MEC kuti liyendetse bwino chisankho chikudzachi posakondera chipani china chilichonse pa chisankho chikudzachi.

M’mawu ake atalandira zikalata za chipani cha UDF, wapampando wa bungwe la MEC, Justice Anabel Mtalimanja, wathokoza a Muluzi komanso wachiwiri wawo kamba kowonetsa chidwi pofuna kutumikira amalawi.

Iwo auza awiriwa kuti kubwera kwawo ku bungweli kudzapeleka zikalata zawo ndi chinthu cha mtengo wapatali chomwe ndichitsimikizo chofuna kutumukira mtundu wa amalawi.

A Mtalimanja atsimikizira amalawi kuti bungwe lawo lipitilira kuunikira zikalata zonse zomwe azilandira kuchokera ku zipani ndi oyima paokha motsatira malamuro.

Wapampandoyi wapempha atsogoleri azichipani kuti alimbikitse mtendere, apewe kupanga kampeni yonyozana kapena kulankhula zinthu zodzetsa ziwawa mdziko muno. Iwo apemphanso chipanichi kuti chilimbikitse anthu awo kudzavoleza zotsatira za chisankho zikadzatuluka.

Iwo anapitilira kuchenjeza zipani kuti zisaphwanye ndondomeko ya malamuro oyendetsera chisankho (Code of Conduct) chifukwa kutero ndi mulandu ndipo adzalipilitsidwa ndalama yokwana 5 million kwacha.

Wolemba: Emmanuel Alufazema

 Kunali kululutira, kuvina ndi kuombera m'manja pamene Phungu wa kunyumba ya malamuro kumwera kwa boma la Chikwawa, Ilya...
15/07/2025


Kunali kululutira, kuvina ndi kuombera m'manja pamene Phungu wa kunyumba ya malamuro kumwera kwa boma la Chikwawa, Ilyasi Abdul Karim analengeza lolemba kuti ayimanso pa chisankho chikubwerachi koma payekha.

Karim analengeza izi kwa Ngabu ku mpingo wa Baptist komwe mafumu, atsogoleri a mipingo, achinyamata ndi anthu ena aku derali anamuyitanitsa kuti awayankhe pempho lao lomuumiriza kuti apitirize kuwatumikira pomwe iye anaganiza zoima kaye ndale kuti ayendetse mabizinesi ake nkupereka mwai kwa ena.

Mbusa wa mpingo wa Nazarene kwa Mwananjobvu, Henry Khuleya anati ndi okondwa kuti tsopano Karim walengeza kuti adzayima nawo pachisankho cha pa 16 September chaka chino ponena kuti wachita zitukuko zambiri mu nthawi yake ndipo zitukuko zina zikufunika zomwe ena sangakwanitse.

Karim wakhala Phungu kuderali kwa ma teremu awiri ndipo atalengeza kuti sayima nawonso zidakwiyitsa magulu a anthu ochuluka.

Wolemba: Charity Dzongwe

15/07/2025


Pamene shuga ikupezeka movutirako, kampani ya Illovo ku Nchalo sinagaye mzimbe lolemba potsatira zionetsero zomwe oyendetsa galimoto zonyamula mzimbe za Unitrans akuchita.

Woyendetsawa anakaniratu kwa mtuwa galu kulowa ndi mzimbe zopakila kale mu galimoto ku fakitale ya kampani ya Illovo ku Nchalo.

Iwo akuchita izi ati pofuna kukakamiza kampani yawo kuti iwakwezere malipiro.

Malinga ndi m'modzi ogwira ntchito ku kampaniyi yemwe anati tisamutchule dzina wati mabwana awo akudziwa za madandaulo awo koma sakuonetsa chidwi chowakwezera malipiro. Ndipo iwo ati aganiza zonyanyala ntchito mpaka akuluakulu a kampaniyi ku dziko la South Africa abwere kudzawayankhula.

Pakadali pano, akuluakulu ena akuyesetsa kuyankhula ndi ogwira ntchitowa komabe sizikuphula kanthu ponena kuti sangagwire ntchito mokondwa pomwe malipiro awo ndi ochepa ndipo akulephera kupeza zosowa zawo pa moyo chifukwa mitengo ya zinthu njokwera kwambiri.

Wolemba: Charity Dzongwe.

Address

Nsanje

Alerts

Be the first to know and let us send you an email when Gaka FM posts news and promotions. Your email address will not be used for any other purpose, and you can unsubscribe at any time.

Contact The Business

Send a message to Gaka FM:

Share

Category