Gaka FM

Gaka FM Gaka FM is a community licensed radio station based at Bangula, Nsanje District.

Gaka radio targets different types of people such as farmers, mothers, under five, youths, business communities, civil servants, pensioners, bankers, entrepreneurs, people with physical challenges, and local communities. The radio focuses on several thematic areas such as food and nutrition security, education and awareness, disaster risk management, health, water and sanitation, HIV and Aids, eco

nomic empowerment, and entrepreneurship. Some of the programs on Gaka radio are conducted live on the radio while others are recorded through the use of local journalists who produce almost all programs in our local languages of Sena and Chichewa hence unique in Malawi.

 Timu ya Mpira  wa miyendo ya Dziko lino ya Scorchers lero yagonja ndichigoli chimodzi kwa duu pamasewero opimana mphamv...
03/06/2026


Timu ya Mpira wa miyendo ya Dziko lino ya Scorchers lero yagonja ndichigoli chimodzi kwa duu pamasewero opimana mphamvu ndi Tanzania omwe anachitikira pa bwalo la zamasewero la KMC Complex mu mzinda wa Dar es Salaam m'dziko la Tanzania .

Poyankhula atatha masewero onse, M'phunzitsi wankulu wa Scorchers, Lovemore Fazili wati ndiokhutira ndimene asungwanawa asewerera ngakhale agonja koma maseweredwe awo apereka chilimbikitso choti akhoza kuchita bwino m'masewero omwe akubwera mtsogolo.

Fazili wati walimbikitsika ndimene Timuyi yachitira pamene inakwanitsa kupita kutsogolo ndikukwanitsa kusewera mwamphamvu masewero onse, choncho kugonjaku sikukugwirizana ndimomwe Timuyi yasewerera .

“Masewero analibwino sindikudandaula kwambiri ndizotsatirazi chifukwa chomwe chandisangalatsa ndichoti tinakwanitsa kupita kutsogolo ndikupanga mwayi ochuluka opeza zigoli komanso takwanitsa kuwasunga adani kwa Mphindi zonse 90,"watero Fazili.


Timu ya Scorchers ikuyembekezereka kukumanaso ndi Tanzania Loweruka masewero ena opimana mphamvu ngati mbali imodzi yokonzekera mpikisano wa 2026 Women Africa Cup of Nations ( WAFCON).

Wolemba : Lawrence Chiononga

 From Studio Struggles to Rising Reggae Star: Shadreck Chisale Chasing His DreamUpcoming reggae artist Shadreck Chisale ...
02/06/2026


From Studio Struggles to Rising Reggae Star: Shadreck Chisale Chasing His Dream

Upcoming reggae artist Shadreck Chisale says his journey in music has been filled with determination, sacrifice and hope despite facing financial challenges along the way.

Born in Lilongwe but raised and educated in Nkhotakota District, Chisale developed a passion for music in 2003. He later entered BK Studio in 2007 to begin recording his songs, but his dream was temporarily put on hold due to financial difficulties.

However, the artist has now made a strong comeback in 2026 with the release of new songs, including “Chimenechi” and “Dziko Laonongeka.” The tracks were recorded at Real Sound Studio and produced by Apex.

Chisale, who specializes in reggae music, says his ambition is to reach greater heights and achieve what many artists have not yet accomplished in Malawi’s music industry.

In a unique move aimed at promoting his brand, the musician says he is among the first local artists to distribute branded T-shirts and caps using his own money without external sponsorship.

Looking ahead, Chisale dreams of establishing his own band and music studio to help nurture and promote different talents across Malawi.

Chisale who is currently residing in South Africa has also thanked his management team in Malawi for their continued efforts in promoting his music and supporting his career growth.

Fans can access his music on various online platforms.

Reported by Emmanuel Alufazema

 Ntchito yomanga chingalande cha ulimi wa mthirira cha Shire Valley Transformation Program (SVTP) yayambiranso mwezi wa ...
01/06/2026


Ntchito yomanga chingalande cha ulimi wa mthirira cha Shire Valley Transformation Program (SVTP) yayambiranso mwezi wa February, 2026 itayima chaka chatha kwa miyezi ingapo kamba ka mavuto a zachuma.

Izi zadziwika lolemba ku Chikwawa pomwe akulu akulu ndi adindo ku nthambi zina m'boma la Nsanje anayendera ntchitoyi ndi kukhala ndi mkumano ndi akulu akulu aku SVTP.

Kuchedwa kwa chingalandechi kwadandaulitsa akulu akulu omwe anali nawo pa mkumanowu.

Mfumu yayikulu Tengani yomwe ndi yotsogolera akulu akulu ndi adindo okhudziwa ndi SVTP, yati anthu atopa nkudikira kuti ayambe kupindula ndi chingalandechi.

"Zaka zachuluka kwambiri chiyambireni ntchitoyi koma ikadali m'mbuyo kwambiri. Sitili siliyasi ngati dziko", yatero Mfumu yayikulu Tengani.

M'mau ake, m'modzi mwa akulu akulu ku SVTP, Felix Tukula wavomereza kuti ntchitoyi yachedwadi ndipo nawonso akudandaula nkuchedwaku koma anafulumira kunena kuti mavuto monga akusowa ndalama zakunja, mafuta, matenda a Covid 19 ndi Cyclone Anna zinawabwezeretsa m'mbuyo pomwe malo otengera madzi anakokoloka zomwe zinachititsa kuti ndalama zopitiriza mtunda wa kumanga chingalande zigwire ntchito ku mbali yoti inali inatha kale.

Tukula wati pakadali pano banki ya African Development yapereka ndalama zokwana 50 million USD zothandizira ntchitoyi ndipo pomafika mwezi wa okotobala chaka chino, madzi ayamba kuyenda mu chingalandechi kuti ma cooperative oyamba a Kambadwe ndi Mwanaalirenji ayambe ulimi wa mthirira.

Wolemba: Charity Dzongwe

 Katswiri wakale pankhani yokankha chikopa, Yamikani Fodya yemweso amadziwika bwino ndi dzina loti “The Headmaster” wape...
31/05/2026


Katswiri wakale pankhani yokankha chikopa, Yamikani Fodya yemweso amadziwika bwino ndi dzina loti “The Headmaster” wapempha adindo amene akuyendetsa masewero ampira m'dziko muno kuti aganizire kwambiri zolowa m'madera akumidzi ponena kuti maderawa ndikomwe kuli achinyamata aluso kunkhani ya masewero ampira .

Fodya wayankhula izi Loweruka pa bwalo lazamasewero la Mpatsa CDSS kwa Tengani m'boma la Nsanje pamene anali mulendo olemekezeka pamasewero otsiliza apakati pa Mnthembwe FC ndi Tengani Academy FC mu Bonaza yotchedwa Jah Boy yomwe imathandizidwa ndi Khansala wadera la Chigumukire, Kafumphe Dzowa m'bomali.

Fodya walimbikitsa achinyamata ochokera m'derali kuti alimbikire ndi kusaziyang'anira pansi pa luso la mpira wamiyendo lomwe alinalo ponena kuti iyeyo ndi munthu m'modzi amene mpira wake adachoka nawo kutali mpaka kufikira adayamba kusewera mu Team yaikulu ya dziko lino ya Flames .

“ Taonera mpira wabwino kwambiri, anyamata ali ndi luso, choncho ndiwapemphe kuti alimbikire ndingopemphanso adindo omwe akutiyendetsera masewero ampira kuti ayang'ane kwambiri kumamidzi ngati kuno, komanso ndipemphe anthu akufuna kwabwino kuti abwere ndikumathandiza masewero ampira ngati mene akuchitira Khansala wadera lino, ”watero Fodya.

Mau ake, Khansala wadera la Chigumukire, Kafumphe Dzowa yemwenso ndimwini wake wa Bonanzayi wati anaganiza zobweretsa masewero ampira m'derali osati chifukwa choti ndi Khasala koma iye amakonda masewero ampira, komanso ngati njira imodzi yowathandiza achinyamata.

Bonanzayi yomwe inali ya ndalama zokwana 1 Million Kwacha, anaigawa musukulu za mdera la Chigumukire ward komanso matimu a m'mudzi.

Ndipo pa ma Timu am'mudziwa, Tengani Academy FC yathambitsa Mnthembwe FC ndi zigoli 8 kwa 7 kudzera mu mapenote ndipo yapatsidwa ndalama zokwana k200,000 ndi msapato zosewerera mpira, pomwe Mnthembwe yapita ndi ndalama zokwana K130,000, Kailedzi fc yomwe inathera panambala yachitatu yatenga k90,000 ndipo panambala yachinayi pali Mizimu United yomwe yatenga k50,000.

Wolemba: Lawrence Chiononga

 Anthu okonda zachikhalidwe kuchigwa cha mtsinje wa Shire Loweluka likudzali pa 30 May akhamukire pa Ngabu community gro...
27/05/2026


Anthu okonda zachikhalidwe kuchigwa cha mtsinje wa Shire Loweluka likudzali pa 30 May akhamukire pa Ngabu community ground kumwambo wotchedwa "Shire Valley Giants Memorial Show" womwe umakonzedwa chaka chilichonse ndi Khulubvi Arts and Cultural Festival.

Mkuku owona za msangulutso mugululi, John Maganizo wauza Gaka online kuti chilichonse chokhudza zokonzekera za mwambowu zafika kumapeto ndipo akumema anthu onse kuti afike mwaunyinji.

Maganizo wauzanso wati chaka chino ayitana akatswiri oyimba monga Kaka, Moses Makawa, Agoroso, Jay Maga komanso ena ochokera m'madera osiyanasiyana kuchigwa cha mtsinje wa Shire.

Kumwambowu kuzakhala kuyatsa makandulo, kuvina nyimbo za oyimba ochokera kuchigwa cha mtsinje wa Shire omwe anamwalira, komanso zionetsero zachikhalidwe cha asena ndi amang'anja monga magule, zakudya, mbiri komanso chiyankhulo.

Khulubvi Arts and Cultural Festival imakonza mwambo wa "Shire Valley Giants Memorial Show" chaka chilichonse pofuna kukumbukira komanso kupereka ulemu ku ntchito zimene aluso komanso anthu odziwika bwino pa ndale ochokera kuchigwa cha mtsinje wa Shire anachita m'dziko muno.

Wolemba: Peterson Adam.

 Masewero a ndime yotsiliza mu Ligi ya Kaombe Estate  pakati pa Timu ya Bangula United ndi Nyamitalala FC pabwalo la Sor...
25/05/2026


Masewero a ndime yotsiliza mu Ligi ya Kaombe Estate pakati pa Timu ya Bangula United ndi Nyamitalala FC pabwalo la Sorgin m'boma la Nsanje athera ziwawa chifukwa cha Masapota a Timu ya Nyamitalala omwe sanagwirizane ndi Chiganizo cha oimbira.

Masewerowa omwe anachitika Lamulungu, anayamba bwinobwino ndipo chigawo choyamba chinathera kufanana mphamvu pamene ma Timuwa anagoletsana chigoli chimodzi chimodzi .

Atayambika masewero mchigawo chachiwiri, Bangula United inamwetsa chigoli chake chachiwiri pa Mphindi 55 kudzera mwa Macphally Stimah, ndipo masewero anapitilira mwabata koma patatsala Mphindi zitatu kuti masewero onse athe, osewera kutsogolo ku Timu ya Nyamitalala, Mada Chisomba, anazigwetsa mu 6 yard box mchigawo cha Bangula United ndipo oimbira anati mpira upitillire.

Izi zinakwiitsa ochemerera Timu ya Nyamitalala omwe amayembekezera oimbirayu kupereka penoti ndipo analowa m'bwalo la zamasewero ndikuyamba kumenya Oimbira .

Zinatengera a Polisi omwe anali pabwaloli kupereka Chitetezo kuthawitsa oimbirawa ndipo m'modzi mwa akuluakulu oyendetsa masewerowa a Grace Tchongwe omwe ndi Mlembi wa komiti yoyendetsa masewero M'bomali anayesera kuwauza ma timu onse kuti alowe m'bwalo kuti mpira upitillire koma Timu ya Nyamitalala imafuna masewero apilitire pokhapokha atasewera penote zomwe zinali zosemphana ndi oimbira choncho Mlembiyu analamula kutiasewero aimire pompo zomwe zinakomera Timu ya Nyamitalala yomwe imatsallira koma sizinasangalatse Bangula united yomwe imatsogola panthawiyi.

Mawu ake Mlembi wamkulu mu komiti yoyendetsa masewero ampira m'boma la Nsanje ,Grace Tchongwe yemwe anaimilira chair wa komitiyi pamasewerowa wati anthu adikire chigamulo kuchokera ku komiti yawo .

“Ngati komiti ya district tikhala pansi ndikuunikira zamene masewerowa ayendera ndipo ngati zingakomere Bangula united tipanga tsiku chikho chiperekedwa ku timuyi ,ndimene zimayendera mu mpira.” anatero a Tchongwe

Timu yowina ikuyembekezereka kupita ndichithumba Cha ndalama zokwana 1 million kwacha ndipo yachiwiri yake imayenera kupatsidwa 5 00 thousand kwacha.

Ligi ya Kaombe Estate yomwe ndiyandalama zokwana 16 million inayamba chaka chatha mu mwezi wa October imathandizaso mpikisano wa masewero ampira wamanja omwe mndime yotsiliza Timu ya Atsikana ya One Love yatenga ukatswiri wa Ligiyi itagonjetsa Atsikana atimu ya Nyamitalala ndi zigoli 25 kwa 14 pabwalo lomweli la Sorgin.

Wolemba: Lawrence Chiononga

 Nthambi ya apolisi m'dziko muno yati amanga anthu 92 powaganizira kuti akukhudzidwa ndi zipolowe zomwe zinachititsa kut...
22/05/2026


Nthambi ya apolisi m'dziko muno yati amanga anthu 92 powaganizira kuti akukhudzidwa ndi zipolowe zomwe zinachititsa kuti anthu asanu ndi atatu (8) kuchigwa chamtsinje wa Shire aphedwe powaganizira kuti amasowetsa ziwalo za anthu zobisika.

Mkulu wa apolisi mchigawo chakumwera chakum'mawa, Frank Kumukumu, walankhula izi Lachinayi pa msonkhano wa olemba nkhani m'boma la Nsanje omwe bungwe la Malawi Human Rights Resources Centre (MHRRC) linachititsa m'bomali.

Kumukumu ati mwa anthuwa, 27 ayankha mulandu okupha, 25 ayankha mulandu ofalitsa nkhani zabodza, 4 ayankha mulandu oyambitsa ziwawa, ndipo zadziwika kuti anthu 30 mwa anthu omwe anamangidwa sanapalamule mulandu ulionse.

Iwo anapitilira kunena kuti apolisi apitiliza ntchito yofufuza anthu ena omwe akukhudzidwa ndi zaupanduzi ndicholinga choti onse alandire chilango mokhudzana ndi milandu yomwe anapalamula.

Mkulu wabungwe la MHRRC, Emma Kaliya, wati ndiokhumudwa ndikukula kwamchitidwe ofalitsa nkhani zabodza ponena kuti izi zachititsa kuti anthu ena ataye miyoyo kaamba konamiziridwa kuti akukhudzidwa ndi zinthu zomwe sanachite.

Kaliya wati mkofunika kuti mabungwe, amipingo ndi magulu ena okhudzidwa agwirane manja ndi boma pofalitsa mauthenga oyenera omwe angapereke mbiri yabwino yadziko lino ndikudzudzula khalidwe la anthu lotengera malamulo m'manja mwawo.

Wolemba: Ethel Mashonga

 Job opportunity advertisement at Foundation for Active Civic Education (FACE). Don't miss it try your lucky now!
19/05/2026


Job opportunity advertisement at Foundation for Active Civic Education (FACE). Don't miss it try your lucky now!

18/05/2026
 Mtsogoleri wa Utumiki wa achinyamata mu Mpingo wa Seventh Day Adventist mchigawo chakum'mwera  chakumadzuro m'dziko mun...
16/05/2026


Mtsogoleri wa Utumiki wa achinyamata mu Mpingo wa Seventh Day Adventist mchigawo chakum'mwera chakumadzuro m'dziko muno, m'busa Elisha Chikumbi walimbikitsa makolo mu mpingowu kuti akhale patsogolo kuthandizira achinyamata pautumiki wawo, ponena kuti izi zimapereka chilimbikitso kwa achinyamata kutumikira Mulungu ndi mtima wawo onse.

Chikumbi wayankhula izi Loweluka pa Mpingo wa Bangula Seventh Day Adventist m'boma la Nsanje pamene anakhala nawo pa mapemphero okondwerera kuti gulu la Achinyamata la Adventurer mu Mpingowu pa dziko lonse lapansi lakwanitsa zaka makumi atatu, mphambu zisanu ndi ziwiri(37) akutumikira mu mpingowu.

“Lero ndi tsiku la mtengo wapatali mu Mpingo wathu padziko lonse lapansi limene tikukondwerera kuti gulu la achinyamata azaka zapakati pa 4 ndi 9 akwanitsa zaka 37 akutumikira, choncho uthenga wanga kwa akhirisitu ndikungowalimbikitsa kuti aziwapanga support achinyamatawa monga mene Baibulo limanenera pa Miyambo 22 verse 6, kuti phunzitsa mwana poyamba njira yake ndipo angakhale atakalamba sadzachokamo," atero achikumbi.

Mau ake, mkalapampando mu utumiki wachimatawu mchigawochi omwe anayenda limodzi ndi a Chikumbi, Hastings Kholomana wati achinyamata amakumana ndi anthu osiyanasiyana komanso zinthu zosiyanasiyana choncho ndikofunika kuti makolo akuyenera aziwapempherera ana awo nthawi zonse.

“Tili osangalala ndi uthenga umene achinyamata akuno ku Bangula atipatsa pa mutu woti 'kuyenda ndi Yesu' pempho langa ndingopempha makolo kuti apitilize kumawalangiza ,awaphunzitse njira yabwino yomwe anawo angakhalemo kuphatikiza apo aziwapempherera chifukwa weekend-yi amakhala nawo pakhomo koma mkati mwa sabata achimatawa amakhala ali kusukulu komwe amakumana ndi anthu osiyanasiyana kuona komanso kumva zosiyanasiyana, ndipo asatope kuwapatsa ulangizi kuti akadzakula adzakhale odalilika ngati mene alili makolo awo lero," atero a Kholomana.

Tsiku la Adventurer mu Mpingo wa Seventh Day Adventist padziko lonse lapansi limakondwereredwa mwezi wa May chaka chilichonse ndipo chaka chino tsikuli linaikidwa pa 16 May pa Mutu woti “Kuyenda ndi Yesu.

Patsikuli pokhala lasabata mu Mpingowu Ana azaka zapakati pa 4 ndi 9 amapatsidwa mpata opanga chilichonse okha kuphatikizapo ulaliki motsogozedwa ndi Atsogoleri awo pa Mpingo.

Wolemba : Lawrence Chiononga

Address

Nsanje

Alerts

Be the first to know and let us send you an email when Gaka FM posts news and promotions. Your email address will not be used for any other purpose, and you can unsubscribe at any time.

Contact The Business

Send a message to Gaka FM:

Share

Category