21/08/2022
CHIBVUMBULUTSO PART 2 IJA NDI IMENEYI
muli bwanji?
lero muli ndi ineso mtumiki wanu KING NOHITOH tipitilize pomwe tinalekera
choyamba tidziwe kuti pali aneneri ena omweso analemba zokhuza chilombo amene tikuti ndi satana . daniel anachitchula chilombochi kuti nyanga yaing'ono (little horn pa chingerezi ) yohane anachitchula kuti okana kristu ("Anti Christ ) pamene paulo anachitchula kuti mwana osaweruzika komanso munthu wauchimo ("the son of perdition" and "the man of sin).
tiyeni tilowe deep muzimenezi kaye
kodi chilombo chaku chibvumbulutso ndikuti kwina komwe chikupezeka?
daniel 7:3
ndipo zilombo zinayi zazikulu zinatuluka mnyanga
daniel:7:23
chilombo chachinayi .....chizaononga dziko lapansi (shall devour the whole earth)
daniel 7:8
ndipo pakati pawo panatulukaso nyanga ina yaing'ono. pa nyanga iyi panali maso onga ngati a munthu .
tikaona chilombo ichi sichikusiyanaso ndi chilombo chomwe tinachipeza mu chibvumvulutso 13 , pa chibvumbulutso 13 chilombo chija chinatuluka pa nyanja ndipo ichiso chikutuluka m'nyanja koma chili ndi nyanga khumi ,ndipo chili ndi mphamvuso pa dziko lonse kuphatikiza apo chikusogozedwaso ndi munthu. ndipo nyanga yaing'onoyi itithandiza kuti tidziwe kuti fano la chilombo ndi chani? Mark of the Beast is.
kodi chilombo chija cha ku chibvumbulutso 13 chikufanana pati ndi nyanga yaing'ono ya ku daniel 7 ?
daniel 7:25
adzayankhula mawu amwano motsusana ndi wamwambamwamba..., azakhala mpaka utha kwa nthaawi, ndipo azazunza oyera mtima.
tikutha kuona kuti zomwe chilombo ichi chikuchita ndi ndendende zomwe chilombo chakuchibvumbulutso 12 chikuchita ,,,,taonani
chibvumbulutso 12:6
ndipo mzimayiyo anathawila ku chipululu komwe MULUNGU anamukonzeratu kuti akamudyese kumeneko masiku 1260 .
chibvumbulutso 12:14
mzimayiyo anapasidwa mapiko awiri ...kuti awulukire ku chipululu , kuti akakhaleko ku nthawi za nthawi.
nthawi (time)mu prophetic meaning imayilimira chaka. nthawi za nthawi imayimilira zaka ziwiri.kugawika kwa nthawi imayimilira half ya chaka onani daniel 4:16, 23, 32; 7:25) zaka 7 zinasanduka kukhala zaka 7 '' ndiyeno nthawi ndi nthawi zanthawi ndi kugawika kwa nthawi zimapanga zaka zitatu ndi half yachaka pamene masiku 1260 aja tinanena kuti tsiku limayimiliraso chaka ndiyekuti apo tili ndi zaka 1260 zomwe zikufanana ndi miyezi 42 ya ulosi ija.
kodi nanga nyanga yaing'ono ikukakamizaso kuti anthu alandire fano la chilombo?
daniel 7:25
ndipo azayesera kusintha nthawi ndi malamulo.
kunena za nthawi apapa yomwe ikukambidwa apapa pa Malamulo a MULUNGU aja ndi sabata ,mchifukwa chake ena sadziwa kuti sabata lenileni ndi liti , sunday kapena surturday ? chifukwa ayesera kale kusintha nthawi zomwe zikusokoneza anthu panopa, calender anayitsokoneza kalekale , ngakhale chaka chimayenera chikhale ndi masiku 360 komanso masiku 30 pa mwezi sizodabwisa kumaona mwezi ukufika pa 31 wina kumatha pa 28 iyi ndi tchito ya satana chifukwa anthu oti mukupembedza MULUNGU mmodzi sitimayera kumakangana za tsiku lopemphera. imeneyo ndi action yomwe chilombochi chaonesa .
kodi chilombo (papa ) asinthapo nthawi?
eya
chibvumbulutso 13:6
anatsegula kamwa lake nanena mosusana ndi MULUNGU.
ma papa akuroma anasintha sabata lomwe lili saturday kukhala sunday pa zifukwa zawo umboni? werengani buku lotchedwa the Convert's Catechism of Catholic Doctrine pa page 50 maonekedwe ake titha kutumiza pic ku inbox ndipo anthu analora kumalambira sunday ena chifukwa choopa kuphedwa chifukwa samanyengelera ayi olo pang'ono koma anayiwala kuti kuvomereza sunday akhala akuvomereza lamulo la CHILOMBO kusiya la MULUNGU. werenganiko commentyi("Protestants…accept Sunday rather than Saturday as the day for public worship after the Catholic Church made the change… But the Protestant mind does not seem to realize that in observing Sunday, they are accepting the authority of the spokesman for the Church, the pope." Our Sunday Visitor, February 5, 1950)
chifukwa chani anthu otsusa maganizowa amalambira sunday mmalo mwa saturday?
chibvumbulutso 13:3
dziko lonse linadabwa nacho chilombocho.
dziko lonse ndilozizwa ndi mmene anthufe tikuchisatitilira chilombo. mukawere buku lija mupeza ma details onse a momwe akutipotozela pa chilungamo.
kodi tingatani lamulo la munthu, kaya la mpingo likusemphana ndi laMULO la MULUNGU?
machitidwe 5:29
''bola kumvera MULUNGU kusiyana ndi munthu''
mark 7:7
amandilambira ine pachabe, kumaphunzitsa ziphunzitsa malamulo a wanthu.
kodi tizizadindidwadi 666 monga fano la chilombo pa mphumi kapena pa zanja pathu?
chibvumbulutso 13:16
"chipangisa onse kuti alandire fano lake pa zanja lawo lamanja kapena pa mphumi pawo"
deutronomo 6:6,8
ayi tisayembekezere kudindidwa pa mphumi kapena pa zanja zomwe aliyense sangalole paja tinanena kale kuti mphumi imayimilira maganizo a munthu ndi zokhumba za mtima wanu, pamene zanja zintchito zathu.
kodi fano la chilombo ndi chani ( papa )
chibvumbulutso 14:11-12
"ndipo sapuma usana ndi utsik amene alambira chilombo ndi fano lake , ndi aliyense amene alandira fanolo mu dzina lache . apa pali chifatso cha oyera mtima :apa pali iwo amene asunga malamulo a MULUNGU , ndi chikhulupiliro mwa yesu.
kuchokera pa verseyo tikutha kusiyanitsa pakati pa anthu oyera mtima ndi anthu omwe avomeleza fano la chilombo. oyera mtima amasunga malamulo a MULUNGU kuphatikizapo sabata komano iwo amene akulambira fano la chilombo tamva kuti sakupuma usana ndi utsiku .tinakamba kuti sabata limatanthauza kuti kupumira ntchito (rest from labour ),oyipa sakupuma or mpang'ono chifukwa sabata sakulisunga. tidziwe ichi kupemphera sunday ndiko fano la chilombo tamvaniko ka statement aka "Sunday is our mark of authority. The church is above the Bible and this transference of Sabbath observance is proof of that fact." The Catholic Record, London Ontario, Sept. 1, 1923"
pomaliza fano la chilombo ndinganene kuti ndikumvera papa pamene anasintha tsiku la sabata ndipamene akulamula zinthu zoipa iwe nkumavera.
kodi chilombo kapena papa ali ndi thandizo pamene akukakamiza kuti anthu alandire fano lake?
chibvumbulutso 13:11-12
ndipo ndinaona chilombo china chikutuluka pansi, chinali ndi nyanga ngati zankhosa ndipo chinalankhula ngati chilombo . ndipo chinachita mphamvu zonse za chilombo choyamba pamaso pake ,ndikupangisa iwo akukhala pa dziko ndi iwo akukhalapo kuti akalambire chilombo choyamba chija.
choyamba choyamba chija chinatuluka pa nyanja koma ichi chikutuluka pansi.tinaphunzisana kuti nyanja imataunthauza kuti malo kapena dera lomwe komwe kuli chiwerengero cha anthu chochuluka (chibvumbulutso 17:15) .ngati nyanja ikuyimilira chiwerengero chochuluka cha anthu , ndiye kuti pansi pakuyimilira dera lomwe muli anthu ochepa.chilombo chachiwiri , kapena dziko ili likutuluka pa dera lomwe muli chiwerengero cha anthu ochepa.. komanso tamva kuti akuyankhula ngati nkhosa mwanjira ina ali ndi machitidwe owoneka achi christu kapena akuyankhula ngati au Mulungu. bible likuti chinadzuka pamene bala lake laku imfa lidapola la chilombo choyamba chija mu 1798 werengani verse 10. kodi dziko liti la mphamvu lomwe linadzuka atatha 1798, kuchokera mu dera la chiwerengero chochepa ndipo amene analiyambitsa ndi anthu amachitidwe ngati achi khristu? apa mupeza kuti ndi united states of america USA.
koma bible likuti xhilombochi chinasiya kuyankhula ngati nkhosa ndikuyankhula ngati chilombo.
ndikupangisa anthu okhala pa dziko lapansi kukakamiza kuti akalambire chilombo. bible apa likungolosera kuti USA izasiya kumenyera ufulu zachipembezo ndi machitidwe achi khristu ndikuthandizira papa kukamiza anthu kusatira malamulo omwe azipanga , ngati national sunday lawn (lamulo lokakamiza anthu onse kumapemphera sunday) , dziko limodzi , ndalama imodzi, kukwatirana amuna kapena akazi okha okha.
kodi USA ukuchita chani pochithandiza chilombo choyamba chija (papa)
chibvumbulutso 13:14
"ndikuwanyenga iwo akukhala pa dziko lapansi .... nanena achipangire fano lake chilombocho."
USA ipanga fano la chilombo chomwe ndi papa (chithunzi cha papa) ndipo musaiwale kuti mfumu nebukadinezala nayeso anapanga fano lake kuti anthu azililambira lomwe shadreck , mishek ndi abidinego anakana kulilambira pokana kuphwanya lamulo la MULUNGU loti usalambire milungu ina koma ine ndekha. tikati tione amzathu achikalika anayamba kale kumulambira mkulu ameneyi papa ..ndiye kukakamiza zinthu zomwe tazitchula zija iwe ndikugonjera uzikhala waphwanya malamulo a MULUNGU.
KODI USA Ikukakamiza bwanji fano la chilombo?
chibvumbulutso 13:15
"ndipo anali ndi mphamvu zopereka moyo kwa fano la chilombocho , kuti chilombocho chikayankhule ndikupangisa kuti aliyense amene sakuchilambira aphedwe.
chibvumbulutso 13:16
ndipo chinapangitsa onse , wa mng'ono ngakhale wankulu, olemera ndi osauka , mfulu ndi akapolo , kuti alandire fano la chilombolo pa mphumi zawo ndi pa zanja lawo lamanzere
USA Izi thandizila chilombo poyankhula ndikupangisa kuti anthu alandire fano la chilombo , kodi USA izizayankhula motani? izizayankhula popanga malamulo omwe dziko lonse lizizsatira ndipo chizapangisa dziko lonse kulandira fano la chilombo. kodi tadziwa bwanji kuti ndi catholic ikuyambitsa izi? werengani ka statement aka “Of course the Catholic Church claims the change was her act…and the act is a mark of her ecclesiastical power and authority in religious matters.” Office of Cardinal Gibbons, through Chancellor C.F. Thomas,Nov 11, 1895.
kodi alipo amene walandira fano la chilombochi panopa?
chibvumbulutso 13:17
"kuti palibe munthu amene adzagule ngakhale kugulitsa pokhapokha akhale ndi fano la chilombo."
palibe amene analandira lembo la chilombochi panopa pokhapokha zinthu tachula zija zitayamba kukakamizidwa ..kuphatikizapo economic sanctions kwa iwo amene azakane kuvomereza izi ..( mwanjira ina kuchotsa thandizo ndi zina zonse zomwe ziko limadalira kuti liyende bwino zizachotsedwa zomwe zizayambitse mavuto maiko ndipo mokakamizika maiko onse azavomeleza izi kungosala kuti munthu akane payekha. .. choyamba azapanga zoti musazamagule ngakhale kugulitsa pokhapokha mukhale nalo fano lake chibvumbulutso 13:17 . pomaliza anthu azizaphedwa akakana kulandira onani verse 15. koma panopa palibe amene ali nalo fano ngakhale ena amanena kuti ukabayisa covid 19 walembedwa 666 , mwina jakisoniyo ali ndi mphamvu yochepesa chiwerengero kapena kukupangisa kuti usamaganize mwa umunthu ndikukuononga chikhulupiliro chako.
kodi kuyipa kolandira fano la chilomboko nkotani?
chibvumbulutso 14:9-10
"ngati wina alambira chilombocho ndikulandira fano lake pa mphumi pake kapena pa zanja lake ,yemweyo adzalawa mkwiyo wa MULUNGU."
Mulungu adzasanulira mkwiyo wake pa aliyense olandira fanolo. azalandira mikwiyo isanu ndi iwiri pa chibvumbulutso 6:2 yomwe tiyilongosole bwino mtsogolomu.
pangani chisankho chabwino panokha musafere makolo , banja ngakhale makolo.
pa chithunzicho imeneyo ndi khani yomwe tikambirane mtsogolomu
nambala yanga ndi 0995926996 text only kapena tumizani message ku pageyi
ndipo timatumiza ma message achilimbikitso mungopanga hi pa nambalayo
pangani share kwa amnzanu please please please amve nawo uthengawu.