07/06/2026
Kampani ya m'boma la Salima ya M & B, yomwe imapanga chakumwa cha Tamu Tamu Health Drink Ginger yasankhidwa kuti ndiyomwe yachita bwino pa kampani zomwe zimapanga chakumwa chomwe sicholedzeletsa m'dziko muno.
Mwambowu unachitika loweluka Ku Bingu International Conventional Center (BICC) mu mzinda wa Lilongwe omwe anachititsa ndi a National Product Magazine.
Mkulu wa kampani ya M & B, Sinah Yusufu wati izi zikutanthauza kuti a Malawi akukonda ndikukhulupilira chakumwa cha Tamu Tamu Health Drink Ginger.
A Yusufu ati mphotoyi ndi chilimbikitso kuti apitilize kupanga chakumwa chapamwamba ndi chopeleka thanzi Kwa anthu.
Kampaniyi yatinso ndiyodzipereka kupitiliza ntchito za chitukuko monga kutukula achinyamata ndiza masewero m'dziko muno.