Love Community Radio 104.5 FM - Salima

Love Community Radio 104.5 FM - Salima Abwenzi poteteza kusintha kwa nyengo
(Partners in climate change mitigation and adaptation)

Bungwe la Circle of hope, layamba ntchito yofuna kuthana ndi ntchitidwe ogwilira ana komaso kusiira Sukulu panjira m'der...
10/09/2026

Bungwe la Circle of hope, layamba ntchito yofuna kuthana ndi ntchitidwe ogwilira ana komaso kusiira Sukulu panjira m'dera la mfumu yaikulu Chiwere m'boma la Dowa.

Izi zadziwika pa mwambo otseka ulendo wandalawala omwe bungweri linakoza pa Katengeza wa masiku atatu okhudza kudziwitsa anthu za kuipa kwa kosiira sukulu panjira komaso kugwililira.

Mkulu wa bungweri kuno ku Malawi Edmond Phiri, wati ana oposera atatu msukulu zawo agwiliridwa komaso ena ambiri akumasiya Sukulu panjira choncho achiona chofunika kuti atengepo Gawo pothetsa izi.

M'mawu ake Senior Gulupu Mphita, yati ndizoonadi kuti kumdelari ana ochululuka asiya Sukulu ndipo ntchitidwe ogwilira wakulaso choncho yati zomwe lachita bungweri zithandiza kuti anthu azindikire za kufunika kwa maphunziro pa mwana.

Leston Mwale yemwe ndi nzika komanso chitsanzo chabwino m’derali, wati adzipereka kuthandiza bungweri pa ntchito yomwe layamba komanso wapempha mafumu kuti ayike upangiri wabwino kuti athane ndi nkhanza za ana.

Kupatula kuphunzitsa ana, bungwe la Circle of Hope limagwiranso ntchito zina za chifundo monga kusamala ana a masiye komaso thandizo la chipatala.

Wolemba Christina Mdolo.

10/09/2026

As Malawi commemorates World Su***de Prevention Day on 10 September, Mental Health Advocate Dennis Mwafulirwa has urged government and other stakeholders to collaborate in efforts to reduce su***de cases.

Mwafulirwa called on the government to allocate more funding toward initiatives addressing the rapidly rising number of su***des in Malawi.

He further asked the government, through the Ministry of Education, to introduce lessons in schools on su***de prevention, which is an area where many Malawians currently lack information.

Mwafulirwa also commended government for passing the landmark Mental Health Act Bill number 17 of 2025 which protects the rights and freedoms of individuals living with mental health conditions.

He added that communities must create safe spaces for people experiencing mental health challenges noting that they deserve support and understanding not stigma.

Every year on 10 September Malawi joins the rest of the world in raising awareness that su***de can be prevented

Reported by William Chitengu.

Mfumu ya a chewa m'dziko muno Kalonga Sosola IX yati mafumu ali ndi udindo waukulu pa nkhani yolimbana ndi katangale.Mfu...
10/09/2026

Mfumu ya a chewa m'dziko muno Kalonga Sosola IX yati mafumu ali ndi udindo waukulu pa nkhani yolimbana ndi katangale.

Mfumuyi yati zitukuko zikuvuta madera akumidzi chifukwa cha katangale amene amakhala akuchitika ku khonsolo komwe mafumu amachita kuchondelera kuti zinthu zina zitheke kwa adindo.

Mfumuyi yapempha nyumba yamalamulo kuti ibweretse lamulo lokhazikitsa seneti yamafumu komwe akhonza kumabweranso pamodzi kudzakambilana nkhani za chitukuko.

Woyankhulapo pa zochitika m'dziko, Joseph Kandiyesa wagwirizana ndi mawu a Kalonga Sosola IX ponena kuti mafumu ali ndi udindo waukulu pa ntchito yothana ndi katangale.

Kandiyesa wati mafumu ena amagwiritsidwa ntchito molakwika ndi andale zomwe zimapangitsa kukanika kudzudzula andale akamachita katangale.

Pa nkhani yobweretsa seneti ya mafumu, Kandiyesa wati izi zitha kukhala zovutilapo koma kuti mafumuwa azigwiritsa ntchito mikumano yomwe amakhala nayo ndi adindo kumakhonsolo pokambila njira zabwino za kayendetsedwe ka chitukuko pofuna kupewa katangale.

Gerald Samson Douglas.

Nthambi yandende mdziko muno yati akaidi amene analemba mayeso a Malawi School Certificate of Education (MSCE) Chaka chi...
09/09/2026

Nthambi yandende mdziko muno yati akaidi amene analemba mayeso a Malawi School Certificate of Education (MSCE) Chaka chino achita bwino kwambiri kuposa chaka chatha pamene akayidi 56 ndiomwe akhoza mayeso mwa 74 kuyimira 75.6%.

Mneneri wanthambiyi Steve Charles Meke wati mkayidi yemwe wachita bwino kwambiri wapeza 14 points.

A Meke ati chaka chatha sanachite bwino pomwe chiwerengero chinali 68.7% ndipo okhoza bwino kwambiri anapeza 16 points.

Iye wayamikira boma komanso mabungwe ena amene amathandiza nthambiyi kuti apitilize kutero chifukwa izi zimathandiza magawo osiyana siyana monga akayidi omwe akuwasunga m'ndende zawo samakhala ndinthawi yopanga zinthu zolakwika.

Wolemba Christina Mdolo.

M'modzi mwa anthu omwe amayankhulapo pa zochitika m'dziko, Lucky Mbewe wayamikira bungwe la African Hero Foundation laku...
08/09/2026

M'modzi mwa anthu omwe amayankhulapo pa zochitika m'dziko, Lucky Mbewe wayamikira bungwe la African Hero Foundation laku Botswana pa ganizo lake lomanga midada yophuziliramo yokwana 300, zipatala zing'ono zing'ono 100 komanso sukulu zophuziliramo luso la manja zokwana 50 m'dziko muno.

Izi zinadziwika pamene wachiwiri wina kwa m'tsogoleri wa dziko lino a Enock Chihana wasayinira ndondomekoyi yomwe imatsogoleredwa ndi mtsogoleri wa dzikolo Duma Gideon Boko.

Mbewe wati ndinkhani yabwino chifukwa chakuti ikulumikizana ndimasomphenya omwe dziko lino likuyenda nawo opita ku ulendo wa 2063.

Malingana ndi Mbewe, izi zithandiza kuchepesa mavuto monga kusowa malo omphunzilira pomwe ana ambiri amamphunzilira panja komanso kuchepesa mavuto amene anthu amakumana nawo oyenda Mitunda itali itali kuti akafike kuchipatala kukalandira thandizo.

''Malo ophunzilira aluso lamanja amene angamangidwe athandiza kuti achepese mavuto awulova pakati pa achinyamata amene akusowa ntchito chifukwa chakusowa luso ndi upangiri oyima pawokha,'' anatero a mbewe.

Wolemba Christina Mdolo.

đź“· Malawi Government.

Msonkhano waukulu wa achinyamata mu mpingo wa CCAP mu presbytery ya Mvera uli mkati ku mpingo wa Mvera m'boma la Dowa.Ms...
06/09/2026

Msonkhano waukulu wa achinyamata mu mpingo wa CCAP mu presbytery ya Mvera uli mkati ku mpingo wa Mvera m'boma la Dowa.

Msonkhanowu omwe umachitika kamodzi pa chaka ndipo wasonkhanitsa achinyamata omwe ali pansi pa Mvera presbytery kuchokera ku mipingo ya Mvera, Msalura, Kaphirimtiwa, Mpatsa, Chamkhungu ndi amene akutenga nawo gawo.

Mkumanowu udayamba pa 03 Sepitembala ndipo utha lero pa 06 Sepitembala ndipo ukuchitika pamutu wakuti thamangani kuti mukalandire mphoto, kuchokera m'buku la 1 Akorinto 9 vs 24-27.

Mpingo wa SengaBay CCAP sudapezeke nawo pa msonkhanowu kaamba ka zovuta zina.

Gerald Samson Douglas Mvera-Dowa.

Bungwe la Christian Health Association of Malawi(CHAM)lati maphunziro osamalira anthu amene ali ndi matenda amgonagona n...
04/09/2026

Bungwe la Christian Health Association of Malawi(CHAM)lati maphunziro osamalira anthu amene ali ndi matenda amgonagona ndiofunikira kwambiri Kwa anthu omwe amagwira ntchito zaumoyo.

Wapampando wabungweli, Happy Makala wayankhula Izizi lachisanu pa mwambo wopereka satifiketi kwa omwe aphunzira maphunziro a matenda a mgonagona pachipatala cha ndimoyo palliative care m'boma la Salima.

M'mawu ake woyang'anira mamphunziro a Chisamaliro cha odwala matenda amgonagona pachipatalachi, Dominic Kangachepe wati cholinga chamaphunzirowa chinali kuti aphunzire m'mene angasamalire anthu amene akudwala matenda amgonagona kuti akabwelera malo awo ogwilira ntchito akathandizire kupereka Chisamaliro choyenelera.

M'modzi mwa ophunzira amene amaliza nawo maphunzirowa ochokera kuchipatala cha St John Of God ku Mzuzu ,Charles Nyasulu wati ziwathandizira kupita patsogolo ndintchito yawo chifukwa ena mwa iwo mzipatala zawo sanayambe kupereka thandizo la anthu amene alindi matenda amgonagona.

Chipatala cha Ndimoyo chinayambitsa maphunzirowa m'chaka cha 2015, ndipo anthu 37 ochokera m'zipatala zosiyanasiyana m'dziko muno ndi m'modzi wa m'dziko la Zambia ndiwo amaliza maphunziro a sabata zisanu.

Wolemba Christina Mdolo.

The Malawi Environment Protection Authority (MEPA) has disclosed that it is doing everything possible to enforce the ban...
02/09/2026

The Malawi Environment Protection Authority (MEPA) has disclosed that it is doing everything possible to enforce the ban on the production, importation, and sale of thin plastics, which remain common in the country.

MEPA’s Information and Education Officer, Aubren Chirwa, said the authority is working with district councils nationwide to curb thin plastics that endanger human health, the environment, and livestock.

Environmental expert Edward Chidombe has urged MEPA to collaborate with manufacturers and stressed that protecting the environment is not only government’s responsibility but requires every citizen’s participation.

Thin plastics cause land pollution, air pollution when burned, and flooding as they block drainage systems.

By Williams Chitengu.

Ngati njira imodzi yolimbikitsa maganizo a ngwiro pakati pa abambo m'dziko muno, bungwe la Abambo Tibe Khonde lakonza m'...
02/09/2026

Ngati njira imodzi yolimbikitsa maganizo a ngwiro pakati pa abambo m'dziko muno, bungwe la Abambo Tibe Khonde lakonza m'gonero ndi kuvina omwe cholinga chake ndikusonkhanitsa ndalama zosachepera 100 million kwacha zothandizira bungweli.

Wapampando wabungweli, Jefferson Milanzie wati cholinga chake ndikufuna kukhazikitsa ofesi 14 m'madera osiyana siyana akumidzi m'dziko muno kuti abambo asamavutike kupeza thandizo pankhani zakagananizidwe kangwiro.

A Milanzie ati vuto lamalingaliro angwiro pakati pa abambo m'dziko muno ndilalikulu ndipo limayamba chifukwa cha mavuto osiyana siyana, kuphatikizapo nkhani za m'banja, mavuto azachuma, ngongole komanso mavuto kungotchula zochepa.

Iwo ati ndi chifukwa chake akufuna kukhala ndi Malo ochuluka omwe abambo angapeze thandizo mosavuta pofuna kuchepesa chiwerengero cha abambo omwe amataya miyoyo yawo chifukwa cha nkhawa.

Mwazina ati ofesizi zikakhazikitsidwa zizigwira ntchito mogwirizana ndi unduna wazaumoyo, apolisi, unduna owona kuti pasakhale kusiyana pakati pa amayi ndi abambo.

Mwambowu ukachitikira mu mzinda wa Blantyre pa 3 Okutobala 2026.

Wolemba Christina Mdolo.

01/09/2026

The Non-Communicable Diseases Alliance Malawi has said Non-Communicable Diseases are responsible for approximately 40 percent of all deaths in Malawi.

Chairperson of the Alliance, Maud Mwakasungula, said this as Malawi joins other countries around the world in commemorating Non-Communicable Diseases Week, which runs from 31st August to 04th September every year.

Mwakasungula has said cardiovascular diseases, cancer, diabetes, and chronic respiratory diseases are increasingly becoming common due to to***co smoking, excessive alcohol consumption, unhealthy diets, and lack of physical exercise.

The alliance has however, commended government, through the ministry of health and it's partners including Partners in Health -PIH Malawi for the progress in strengthening NCD prevention and management.

This year, Non-Communicable Diseases are being commemorated under the theme: “Leadership Under Focus: From Commitments to Delivery.”

By Christina Mdolo.

Address

Post Office Box 15
Salima

Telephone

+265999632090

Alerts

Be the first to know and let us send you an email when Love Community Radio 104.5 FM - Salima posts news and promotions. Your email address will not be used for any other purpose, and you can unsubscribe at any time.

Contact The Business

Send a message to Love Community Radio 104.5 FM - Salima:

Shortcuts

Share