10/09/2026
Bungwe la Circle of hope, layamba ntchito yofuna kuthana ndi ntchitidwe ogwilira ana komaso kusiira Sukulu panjira m'dera la mfumu yaikulu Chiwere m'boma la Dowa.
Izi zadziwika pa mwambo otseka ulendo wandalawala omwe bungweri linakoza pa Katengeza wa masiku atatu okhudza kudziwitsa anthu za kuipa kwa kosiira sukulu panjira komaso kugwililira.
Mkulu wa bungweri kuno ku Malawi Edmond Phiri, wati ana oposera atatu msukulu zawo agwiliridwa komaso ena ambiri akumasiya Sukulu panjira choncho achiona chofunika kuti atengepo Gawo pothetsa izi.
M'mawu ake Senior Gulupu Mphita, yati ndizoonadi kuti kumdelari ana ochululuka asiya Sukulu ndipo ntchitidwe ogwilira wakulaso choncho yati zomwe lachita bungweri zithandiza kuti anthu azindikire za kufunika kwa maphunziro pa mwana.
Leston Mwale yemwe ndi nzika komanso chitsanzo chabwino m’derali, wati adzipereka kuthandiza bungweri pa ntchito yomwe layamba komanso wapempha mafumu kuti ayike upangiri wabwino kuti athane ndi nkhanza za ana.
Kupatula kuphunzitsa ana, bungwe la Circle of Hope limagwiranso ntchito zina za chifundo monga kusamala ana a masiye komaso thandizo la chipatala.
Wolemba Christina Mdolo.