Love Community Radio 104.5 FM - Salima

Love Community Radio 104.5 FM - Salima Abwenzi poteteza kusintha kwa nyengo
(Partners in climate change mitigation and adaptation)

Kampani ya m'boma la Salima ya M & B, yomwe imapanga chakumwa cha Tamu Tamu Health Drink Ginger yasankhidwa kuti ndiyomw...
07/06/2026

Kampani ya m'boma la Salima ya M & B, yomwe imapanga chakumwa cha Tamu Tamu Health Drink Ginger yasankhidwa kuti ndiyomwe yachita bwino pa kampani zomwe zimapanga chakumwa chomwe sicholedzeletsa m'dziko muno.

Mwambowu unachitika loweluka Ku Bingu International Conventional Center (BICC) mu mzinda wa Lilongwe omwe anachititsa ndi a National Product Magazine.

Mkulu wa kampani ya M & B, Sinah Yusufu wati izi zikutanthauza kuti a Malawi akukonda ndikukhulupilira chakumwa cha Tamu Tamu Health Drink Ginger.

A Yusufu ati mphotoyi ndi chilimbikitso kuti apitilize kupanga chakumwa chapamwamba ndi chopeleka thanzi Kwa anthu.

Kampaniyi yatinso ndiyodzipereka kupitiliza ntchito za chitukuko monga kutukula achinyamata ndiza masewero m'dziko muno.

Namwino woyang’anira za matenda a Edzi pa chipatala chachikulu cha Salima, Lucia Matambo Amadu walimbikitsa anthu okhala...
06/06/2026

Namwino woyang’anira za matenda a Edzi pa chipatala chachikulu cha Salima, Lucia Matambo Amadu walimbikitsa anthu okhala m’bomali kuti azigwiritsa ntchito mankhwala a PrEP ndi PEP omwe amathandiza kuti munthu asatenge ka chilombo ka HIV.

Amadu wati ndiwosangalala kuti anthu ambiri m’bomali akugwiritsa ntchito njirayi podzitetezera ku matenda a Edzi.

Malingana ndi a Amadu, pakadali pano mankhwala a jekeseni otchedwa Cabra ayamba kupezeka ku Para komanso MAFCO, komwe anthu angapite kukalandira.

Iwo ati PrEP ndi PEP ndi mankhwala omwe angagwiiitsidwe ntchito ndi aliyense amene ali pachiwopsezo chotenga ka chilombo ka HIV, choncho wati aliyense ali ndi ufulu wolandira.

PrEP ndi mankhwala omwe munthu yemwe alibe kachilombo ka HIV amamwa tsiku ndi tsiku asanakumane ndi chiwopsezo chilichonse pamene PEP munthu amayenera kuyamba kumwa mkati mwa maola 72 atakumana ndi chiwopsezo chotenga kachilombo monga kugonana mosadziteteza kapena ngozi mwazina.

Wolemba Christina Mdolo.

Woyang'anira amayi omwe pakati pachoka Post Abortion Care (PAC) ku Chipatala cha Boma la Salima, Peter Pinakuwa, wadanda...
06/06/2026

Woyang'anira amayi omwe pakati pachoka Post Abortion Care (PAC) ku Chipatala cha Boma la Salima, Peter Pinakuwa, wadandaula kuti amayi ena akupitiliza kukana kulandira njira za kulera pambuyo polandira thandizo.

A Pinakuwa ati kuyambira mwezi wa Januwale mpaka Meyi chaka chino, Nthambi yawo yalembetsa odwala 214, koma 85 okha ndi amene analandira njira za kulera, zomwe zikuyimira 40 pa 100 aliwonse.

Iwo ati kukana kulandira njira za kulera kumachitika chifukwa cha zikhulupiriro za chikhalidwe ndi chipembedzo, kusowa kwa chidziwitso, kufuna kukhala ndi ana ambiri.

Iwo ati ndiodzipereka kupitiliza kuthandiza anthu ngakhale pali vuto losowekera zipangizo zoyenera pogwira ntchito yawo.

Njira za kulera pambuyo pa thandizo lomwe amayi amalandira pakati pakachoka zimathandiza kupewa mimba zosakonzekera komanso kuchepetsa mavuto okhudzana ndi kutaya mimba mtsogolo.

Pakadali pano, zipatala za m’boma la Salima zalembetsa amayi 315 omwe alandira thandizo la Post Arbotion Care (PAC), ndipo mwa iwo, 140 analandira njira za kulera, zomwe zikuyimira 44 peresenti, pomwe jakisoni ndi njira yomwe ikugwiritsidwa ntchito kwambiri.

Wolemba Alice Lissa Kamwanje.

Bungwe loyang'anira miyezo la Malawi Bureau of Standards laononga ndikuotcha matumba 300 a Soya Pieces yemwe anamulanda ...
06/06/2026

Bungwe loyang'anira miyezo la Malawi Bureau of Standards laononga ndikuotcha matumba 300 a Soya Pieces yemwe anamulanda ku kampani ya Price Worth Wholesale ku Limbe mu mzinda wa Blantyre ndipo anadutsa masiku ake.

Poyankhula pambali pa ntchito yowotcha katunduyu m'boma la Salima, woyankhulira bungwe la Malawi Bureau of Standards Annie Maliha wati katunduyu yemwe anatha masiku mu mwezi wa March chaka chino amulanda pa 1 June.

A Maliha ati kutsatira izi kampani ya Price Worthy yalipitsidwa chindapusa cha ndalama zokwana 2 million kwacha.

Iwo ati ntchitoyi ndi mbali imodzi yowonetsa kuti bungweli ndilodzipereka kuonetsetsa kuti anthu m'dziko muno akudya zakudya zoyenelera.

Pakadali pano bungweli lalangiza a Malawi kuti azionetsetsa akamagula katundu ngati Ali psatha masiku komanso kuneneza omwe akugulitsa popewa kudya zosayenera.

Kupatula Soya Pieces, wina mwa katundu yemwe waotchedwa ndi monga mafuta ophikira, zakumwa, soda kungotchilapo zochepa.

Ngakhale kuti dziko la Malawi linagwilizana ndi bungwe loyang'anira za umoyo pa dziko lonse la pansi la World Health Org...
05/06/2026

Ngakhale kuti dziko la Malawi linagwilizana ndi bungwe loyang'anira za umoyo pa dziko lonse la pansi la World Health Organization komanso mayiko ena kuti pofika 2030 adzakhala athana ndi matenda akhate zadziwika kuti m'boma la Salima matendawa akadalipobe ngakhale kwatsala zaka zochepa.

Izi ndi malingana ndi mkulu wa ofesi yoyang'anira za matenda apakhungu pa chipatala chachikulu cha Salima, Philibert Mundi yemwe wati pakadali pano matenda akhate alipo m'bomali koma anthu sazindikira.

A Mundi wati matenda a khate limayambitsidwa ndi tizilombo tomwe sitimaoneka ndi maso komanso anthu angathe kupatsilana kudzera m'malovu.

Iwo ati matenda akhate ndiochizika koma ngati odwala sakumwa mankhwala mwandondomeko amatha kukhala a ulumali monga kuduka zala.

Iye wapempha anthu a m'boma la Salima kuti akaona zizindikiro monga pakhungu kuoneka pena poyelelapo kuposa malo ena aliwonse pakhungu pawo komanso akaona zokhala ngati ziwengu athamangire kuchipatala chapafupi akakumane ndima dotolo.

Wolemba Christina Mdolo.

Zithunzi: Internet.

Ofesi yoona za ntchito Komanso ulangizi wa usodzi  m'boma la Salima lero yaotcha maukonde omwe siovomelezeka omwe analan...
05/06/2026

Ofesi yoona za ntchito Komanso ulangizi wa usodzi m'boma la Salima lero yaotcha maukonde omwe siovomelezeka omwe analandidwa Kwa asodzi.

Mkulu woyang'anira ofesiyi Patrick Zakeyu wati katundu okwana 70 million Kwacha Yemwe analanda kwa asodzi Komanso m'ma shopu kuyambira m'chaka cha 2013 ndi yemwe waotchedwa.

Zakeyu wauza wailesi ya Love kuti kuotcha zipangizo zosavomelezekazi kumapereka uthenga wakuti zipangizozi zosafunika.

Iye anati zipangizozi ndizoopsa chifukwa zimapha nsomba zomwe ndi zazing'ono ngakhalenso mazira omwe.

Ngati mbali imodzi yolimbikitsa malamulo
Magistrate Agnes Chirambo wati malamulo amayenera kugwila ntchito ndipo izi zipeleke uthenga kwa omwe satsatira malamulo.

Zina mwa zipangizo zomwe zaotchedwa ndi neti zoteteza ku udzudzu, monotherapin, ngongongo mongotchula ochepa.

Wolemba Chisomo Mpaso.

Ofesi yoona za usodzi m’boma la Salima mogwirizana ndi bungwe la Ripple Africa yati ndiyokondwa ndi m'mene  ntchito yole...
04/06/2026

Ofesi yoona za usodzi m’boma la Salima mogwirizana ndi bungwe la Ripple Africa yati ndiyokondwa ndi m'mene ntchito yoletsa asodzi kugwilitsa ntchito zipangizo zosayenera ikuyendera.

Mkulu wa ofesiyi a Patrick Zakeyo wati akulimbikitsa madera omwe amapha msomba kuti azigwilitsa ntchito zipangizo zoyenera ndicholinga chofuna kuteteza msomba komanso kusamalira chilengedwe.

Zakeyo wati ngakhale asodzi ena asiya kugwilitsa ntchito zipangizo zosaloledwa, ena akupitilizabe mchitidwewu ndipo wati ofesiyi ikupitilira kuwaphuzitsa asodzi komanso kuyendera nyanja kuti athetse mchitidwe ogwilitsa ntchito zipangizo zosaloledwazi.

Mkulu woyendetsa zausodzi ku bungwe la Ripple Africa m’boma la Salima, Brams Munthali, wati pakhala pakuoneka kusintha kwa kukulu chiyambileni ntchitoyi, ponena kuti poyamba pa ntchitoyi asodzi okwana theka m'boma la Salima amagwilitsa ntchito zipangizo za usodzi zosaloledwa.

Munthali wati mavuto omwe akhala akukumanawo ndikuvetsesa kwa asodzi ochepa pa nkhani yogwilitsa ntchito zipangizo zoyenelera.

Wolemba Laziah Block.

Kusowa kwa zipangizo zophunzilira Komanso zophunzitsira ndi vuto lalikulu pa sukulu ya ana omwe ali ndi ulumali osaona y...
04/06/2026

Kusowa kwa zipangizo zophunzilira Komanso zophunzitsira ndi vuto lalikulu pa sukulu ya ana omwe ali ndi ulumali osaona ya Salima Resource Center.

Mkulu woyang'anira ophunzirawa, Andrew Kaphambe Nkhoma wanena izi lachinayi pomwe amayi ampingo wa Seventh Day Adventist mchigawo cha ku m'mawa m'boma la Salima anakacheza komanso kuwapatsa mphatso ophunzirawa.

Kaphambe wati mavutowa amakhudza kakhonzedwe ka ophunzira mkalasi.

Iwo anati ngakhele khonsolo yabomali kudzera ku ofesi ya maphunziro imapeleka thandizo, silimakhala lokwanira chifukwa zosowa za anawa ndizambiri.

Mtsogoleri wa amayi a Dolika mchigawochi, Jenifer Kumwembe Kholiyo wati achita izi ngati mbali imodzi ya ntchito za chifundo m'mwezi wa June.

Kholiyo anati amayi amipingo isanu ndi umodzi omwe anasokha thandizo lomwe apereka pa sukulupo.

"Tabwela ndi sopo mafuta, odzola, ufa Komanso tachapa zovala ndikuwaphikila chakudya cha lero zomwe zakwana ndalama zosachepera 400 sauzande." a Kholiyo anatero.

Salima resource center ili ndi ophunzira okwana 31, atsikana khumi anyamata makumi awili ndi mmodzi.

Wolemba Chisomo Mpaso.

Katswiri pa nkhani zachuma Mike Marvin Banda wati ngakhale kutumiza ndikulandira ndalama pa Airtel Money ndi TNM Mpamba ...
03/06/2026

Katswiri pa nkhani zachuma Mike Marvin Banda wati ngakhale kutumiza ndikulandira ndalama pa Airtel Money ndi TNM Mpamba kwakwera kwambiri, ndalama zodulira zikadali cholepheretsa.

A Banda ati akuluakulu owona za ntchitoyi akuyenera kuunikanso ndalama zimene zimadulidwa kuti anthu ambiri azigwiritsa ntchito bwino ndalama zamu foni.

Iye wayankhula izi pamene anthu Okhala m'boma la Salima adandaula kuti sikokondwa ndi m'mene ndalama yodulira imachotseledwa, pofotokoza kuti izi zimapangitsa kuti anthu asamagule zimene akufuna mokwanira.

M'modzi mwa anthuwa, Triza Kalumbi wati anthu ambiri akusankha kugwiritsa ntchito ndalama za pamanja kuti apewe kudulidwa ndalama zambiri, makamaka pogulira zinthu zapakhomo.

Wogwira ntchito ya Airtel Money, Lekeleni Phiri, wati anthu ambiri amatulutsa ndalama kuposa kulowetsa chifukwa cha ndalama zodulira, zomwe zimapangitsa kusadalira kusunga ndalama mu foni.

Chiwerengero chikusonyeza kuti kugwiritsa ntchito njira zotumizora ndalama pa phone kunakwera kuchokera pa K19.5 trilioni mu 2024 kufika pa K37.9 trilioni mu 2025, komabe anthu sali okondwa ndi m'mene ndalama zimadulidwira potulutsa mu foni.

Wolemba Alice Lissa Kamwanje.

Picture AI generated.

03/06/2026

The Malawi Health Equity Network has urged government to review and remove newly introduced taxes on essential medicines, warning that the measures will undermine public health.

Executive Director George Jobe made the remarks following the Malawi Revenue Authority’s announcement on 27 May 2026 of increased tariffs on medicines.

Under the new measures, Amoxicillin 250mg capsules and 125mg dry suspension will attract a 20 percent tariff, while Artemether‑Lumefantrine (an anti‑malaria drug), paracetamol, aspirin, and ibuprofen will face a 25 percent tariff.

Jobe stressed that the higher costs will hit poor Malawians hardest, especially those who are often directed to private pharmacies when medicines are unavailable in public hospitals.

He warned that many patients will simply not afford treatment, putting lives at risk.

According to Jobe, the new taxes threaten efforts to control diseases and improve the nation’s health and well‑being, calling for urgent government action to safeguard access to affordable medicines.

By Christina Mdolo.

Address

Post Office Box 15
Salima

Telephone

+265999632090

Alerts

Be the first to know and let us send you an email when Love Community Radio 104.5 FM - Salima posts news and promotions. Your email address will not be used for any other purpose, and you can unsubscribe at any time.

Contact The Business

Send a message to Love Community Radio 104.5 FM - Salima:

Share