Love Community Radio 104.5 FM - Salima

Love Community Radio 104.5 FM - Salima Abwenzi poteteza kusintha kwa nyengo
(Partners in climate change mitigation and adaptation)

Timu ya Maland Fc ndi akatswiri pa boma zone pa mpikisano wa yemwe akuimila dela lapakati ngati phungu wa nyumba ya mala...
10/09/2025

Timu ya Maland Fc ndi akatswiri pa boma zone pa mpikisano wa yemwe akuimila dela lapakati ngati phungu wa nyumba ya malamulo kuchokera ku chipani cha DPP Symon Kaunda Junior.

Maland Fc yogonjetsa Msangu Rangers ndi chigoli chimodzi chomwe chinabwera mu chigawo choyamba cha masewero omwe anachitikila pa bwalo la zamasewero la Salima LEA.

Maland Fc yatenga ndalama zokwana K400, 000 pamene Msangu Rangers yatenga K300, 000.

Gerald Samson Douglas

The Malawi Communications Regulatory Authority (MACRA) has conducted a groundbreaking ceremony for an ICT laboratory at ...
09/09/2025

The Malawi Communications Regulatory Authority (MACRA) has conducted a groundbreaking ceremony for an ICT laboratory at Matenje Community Day Secondary School (CDSS) under a project called Connect a School, an initiative aims to bridge the digital gap in schools and rural areas across Malawi.

Licensing Officer for MACRA, Ireen Chiwaula, said the ICT laboratory will help reduce the digital gap existing between individuals across the country.

"This project will not only provide access to easy information to the students and community but also employ people during the construction period." Chiwaula said.

Director of Planning and Development for Salima District, Eric Kenamu, expressed excitement that Salima is one of the districts chosen to benefit from the project.

He further said the project will help in easy and fast dissemination of information for the students as well as for the community.

Guest of Honor at the ceremony, Enock Phale, advised community members and students to take good care of the ICT laboratory as the facility will improve access to information and enhance education standards in the area .

The construction of the Matenje ICT laboratory is expected to last 9 months. Upon completion, people will access the internet within a 100 meter radius.

By William Chitengu.

08/09/2025

Mtsogoleri wa dziko lino Dr Lazarus Chakwera wati feteleza otsika mtengo wa Affordable Input Program wolemera ma kilogalamu 50 azigulitsidwa pa mtengo wa Mk15,000 ndipo feteleza wa alimi ochita malonda koma magulu azigulitsidwa pa mtengo wa Mk90,000.

Chakwera wayankhula izi lolemba ku nyumba ya chifumu komwe amayankhula ku mtundu wa a Malawi.

Poonjezera apo iye anatsindika pa nkhani yokhudza mafuta omwe pakadali pano akusowa m'malo ambiri othilira mafuta ponena kuti ayamba kupezeka kuyambila la chiwiri pa 9 September.

Iye wati anthu ena osafunira dziko lino zabwino ndiomwe akuchedwetsa ntchito yobweletsa mafuta.

Wolemba Chisomo Mpaso.

Ngati mbali imodzi yokonzekera chisankho chapa 16 September, 2025, yemwe akuimira ngati Phungu wa nyumba ya malamulo kom...
07/09/2025

Ngati mbali imodzi yokonzekera chisankho chapa 16 September, 2025, yemwe akuimira ngati Phungu wa nyumba ya malamulo koma oyima payekha mchigawo chapakati mboma la Salima, James Manyetera, waphunzitsa anthu omwe akayang'anire kayendetsedwe kachisankho m'malo ovotera osiyanasiyana mbomali.

Maphunzirowa, anachitikira pa msalura Community Day Secondary School loweluka, pa 6 September, 2025

Poyankhulapo atamaliza kuphunzitsa, Manyetera wati ndiokhutira ndimomwe maphunzirowa ayendera, chifukwa ndichinthu chofunikira kwambiri

Mwa zina, cholinga cha maphunzirowa ndikuti akaonetsetse kuti voti isakatayike komanso kukaonetsetsa kuti palibe chinyengo pa tsikuli.

Iye wandandaula ndi mchitidwe wa anthu ena omwe akumachotsa zikwangwani zake m'malo osiyanasiyana ponena kuti dziko la Malawi muli ulamuliro wa demokalase umene aliyense amakhala ndi ufulu osankha mtsogoleri wakumtima kwake.

Wolemba: Tiyamike Makanga.

Olemba nkhani komanso mabungwe oyima paokha awapempha kuti azigwilitsa bwino ntchito masamba a mchezo omwe amathandizira...
05/09/2025

Olemba nkhani komanso mabungwe oyima paokha awapempha kuti azigwilitsa bwino ntchito masamba a mchezo omwe amathandizira kufalitsa uthenga kwa anthu pamene dziko lino likukonzekera chisankho chapatatu.

Mkulu woyang'anira ma pulogalamu ku Bungwe la Umunthu Plus, Promise Msampha wayankhula izi lachinayi pamapeto pa maphunziro okhudza kagwilitsidwe ntchito ka intaneti omwe anachitika masiku awiri ku Mponela m'boma la Dowa.

Msampha anati olemba nkhani komanso mabungwe akuyenera kudziwa malamulo omwe amayenera kutsatira pomwe akufalitsa nkhani pa masamba a mchezo.

"Pakadali pano anthu ambiri akugwiritsa ntchito masamba amchezo kotelo atolankhani azisamalitsa za malamulo omwe akuyenela kutsatidwa maka pamene tikuyandikira chisankho chifukwa anthu ambili amakhulupilila zolemba za Atolankhani," Msampha.

George Kaunda yemwe ndi wampando wa komiti yoona za ulamuliro wabwino m'boma la Dowa wati maphunzirowa athandiza kuti afalitse uthenga wa umaliro wa bwino komanso akudziwa za Malamulo akagwilitsidwe ntchito ka intaneti.

M'modzi mwa olemba nkhani omwe apindula ndi maphunziro, Isaac Grant ochokela ku Bembeke Radio m'boma la Dedza wati ndiokondwa kuti Ali nawo pa maphunzirowa pamene waonjezela ukadaulo pankhani ya kagwilitsidwe ntchito ka intaneti.

Maphunziro anachitika ndi thandizo lochokera ku Civicus kudzela ku nthambi ya Digital Democracy initiative.

Wolemba Chisomo Mpaso.

05/09/2025

Bwalo la Second Grade Magistrate m'boma la Salima lagamula bambo wa zaka 20, Emmauel Sesiyo Bakali kukakhala kundende kwa miyezi 18 ndikukagwira ntchito ya kalavula gaga kamba kakuba katundu wandalama zokwana K1,187,000 kumalo ogona alendo a Mpatsa ku Senga Bay mbomali.

Malinga ndi mneneri wa polisi ya Salima, Rabecca Ndiwate, khothi, kudzera mwa oyimila boma, Sergeant Grant Chiwalo, linamvetsedwa kuti usiku wapa 13 March, 2025 Bakali yemwe adagwirako ntchito ku malowa, adaphwanya chipinda china chapa malowa ndikuba filiji, television, nthambo, generator, matilesi, decorder ya DSTV komanso zofunda.

Achiwalo anauzaso khothi kuti apolisi akwanitsa kubwezeretsa katundu yense ku Shapevale mboma la Ntcheu komwe Bakili amabisala.

Atakaonekera kubwalo la milandu, Bakali anapezeka olakwa pa mlanduwu ndipo anauza boma kuti libweretse mboni zinayi zomwe zimatsusana naye.

Boma linalamula kuti opalamuyu alandire chilango chokhwima chifukwa mlanduwu ndiwaukulu.

Ngakhale opalamulayu anapempha kuti amuganizire, second Grade Magistrate Agness Chirambo, anagwirizana ndi boma ndikumulamula kukakhala kundende kukakhala kundende kwa miyezi 18 ndikugwira ntchito yakalavula gaga.

Bakali amachokera m'mudzi mwa Maiwaza, Mfumu yaikulu Kachindamoto mboma la Dedza.

Wolemba Tiyamike Makanga

03/09/2025

The Malawi Electoral Commission (MEC) Chairperson, Justice Annabel Mtalimanja, has reassured stakeholders that comprehensive security measures are in place for the upcoming 2025 General Elections.

Speaking during National elections consultative forum (NECOF), Mtalimanja highlighted the collaborative efforts between the Commission, the Malawi Police Service, and the Malawi Defense Force, which are working together under the Elections Security Task Force to ensure a safe electoral process.

She emphasized that robust systems have been established to safeguard electoral materials and installations.

"All warehouses and facilities involved in the elections will be monitored with round-the-clock security, and necessary precautions will be taken to protect and es**rt materials as needed," She said.

In addition to security measures, MEC said it is focused on the effective training of polling staff to ensure a smooth election process.

A total of 121,044 personnel will be required to manage various aspects of the elections, highlighting the Commission's commitment to conducting a transparent and efficient electoral exercise.

By Alinafe Jimmy Mkwezalamba.

03/09/2025

Bungwe la Malawi Electoral Commission (MEC) likupangitsa mkumano wa National Elections Consultative Forum (NECOF), omwe umabweletsa atengambali okhudzidwa ndi zisankho.

Mkumanowu ukuchitikira ku Bingu International Conventional Center (BICC) ku Lilongwe ndicholinga chofuna kufotokoza m'mene zokonzekera zisankho zikuyendera.

Mkulu wa bungweli, Andrew Mpesi, wayamikira anthu onse kamba koonetsa chidwi chokapezeka ku msonkhanowu.

Malinga ndi Mpesi, cholinga cha msonkhanowu ndikufuna kufotokoza za momwe kuyesa kwa makina otumizira zotsatira kunakhalira pa 27 August 2025, momwe ntchito yogula katundu ovotera ilili, kulemba ntchito ndi kuphunzitsa anthu odzathandiza ovota komanso mmene ndondomeko yotumizira katundu kumadera ovotera idzakhalire.

Wapampando wa bungweli, Justice Anabel Mtalimanja wati akufuna chisankho chikhale cha bata ndi mtendere komanso cholingana ndi zokhumba za a Malawi.

Mwa zina, Mtalimanja wati kuunikiraso malire a phungu ndi makhansala, kukhanzikitsa malo a kalemberawa voti, kusintha malo oponyera voti komanso kulandira maina a anthu ofuna kupikisana nawo ndi zina mwa ntchito zimene akwanitsa.

Ena omwe ali pa mwambuwu ndi ma komishonala a bungweli, mafumu, atolankhani, atsogoleri a zipani zandale, atsogoleri a nthambi za boma komaso mabungwe omwe si a boma.

Wolemba: Tiyamike Makanga

Bwana Mkubwa wa boma la Salima, James Mwenda wati kugawana ndondomeko pa kachitidwe ka zinthu pakati pa magulu osiyanasi...
02/09/2025

Bwana Mkubwa wa boma la Salima, James Mwenda wati kugawana ndondomeko pa kachitidwe ka zinthu pakati pa magulu osiyanasiyana kungathandize kufikira anthu ochuluka pakamodzi.

A Mwenda ayankhula izi pa mkumano omwe anali nawo ndi akuluakulu ampingo wa Anglican m'dziko muno komanso akulu akuluakulu a mpingo omwewu kuchokera ku zambia ndipo anatsindika kuti kugawana ndondomeko kumathandiza kuti anthu othandizika asamakhale amodzimodzi.

Mpingo wa Anglican kuno ku Malawi wati ukufuna kukhazikitsa ntchito zosiyanasiyana zotukula miyoyo ya anthu kuphatikizapo ana kuti azithandizidwa mu moyo wawo wa tsiku ndi tsiku.

Bishop William Chombo wa diocese ya upper Shire komanso wapampando wa Anglican council m'dziko muno wati achita m'gwirizano ndi anzawo aku Zambia kuti awaphunzitse bwino machitidwe a ntchitoyi potengera kuti ku zambia idakhazikika ndipo ikubala zipatso.

Gerald Samson Douglas

Mtsogoleri wakale wa dziko lino yemweso ndi mtsogoleri wa chipani cha Peoples (PP), Dr Joyce Banda, akufotokozera achiny...
02/09/2025

Mtsogoleri wakale wa dziko lino yemweso ndi mtsogoleri wa chipani cha Peoples (PP), Dr Joyce Banda, akufotokozera achinyamata zomwe adzapange anthu akamusankha pa 16 September, 2025, ku Cross Roads Hotel ku Lilongwe

Banda wati mmene ankalowa mboma anapeza mavuto ochuluka ndipo anapanga chothekera ndikusintha zinthu

Mwa zina, Banda wati adzapereka ntchiti kwa achinyamata kudzera mu ulimi, komanso migodi

Iye watiso adzapereka zipangizp zogwirira ntchito zamanja, kumanga nyumba mmidzi ndi kumanga banki ya alimi kumudzi

Mwambowu, akonza ndi a Youth and Society pansi pa mgwirizano wa Youth Decide Campaign

Wolemba: Tiyamike Makanga

📷 Dr Joyce Banda.

Anthu ochuluka akusonkhana pa Kamuzu Road m'boma la Salima pomwe pakuyembekezera kudutsa komaso kunva kuyankhula Kwa mts...
01/09/2025

Anthu ochuluka akusonkhana pa Kamuzu Road m'boma la Salima pomwe pakuyembekezera kudutsa komaso kunva kuyankhula Kwa mtsogoleri wakale wadziko lino Professor Author Peter Mutharika.

A Mutharika akupitiliza kuchititsa misonkhano yoyimayima m'dziko muno munyengo yokopea anthu pa zisankho zomwe zikudza pa 16 September chaka Chino.

A Malawi angotsala ndi masiku 15 okha kuti aponye voti.

Wolemba komaso kujambula zithunzi ndi Benjamin Kumphanje.

Masewero a mpira mu ndime  yotsiriza mu league ya yemwe akuimila dera lapakati mboma la salima James Manyetera atha.Mati...
31/08/2025

Masewero a mpira mu ndime yotsiriza mu league ya yemwe akuimila dera lapakati mboma la salima James Manyetera atha.

Matimu a Abaluya komanso Orlando ndi amene anakumana mu ndime yomaliza lero pa Nakondwa Primary school ground.

Pakutha pa zonse timu ya Abaluya ndi yomwe yatenga ukatswiri wa mpikisanowu pogonjetsa Orlando 4-1.

Mmene chigawo choyamba cha masewerowa chimatha Abaluya imatsogola 2-1 ndi mugawo lachiwiri abaluya inaonjezera zigoli ziwiri.

Timu ya Abaluya itenga K200, 000, pamene Orlando itenga K150, 000.

Gerald Samson Douglas.

Address

Post Office Box 15
Salima

Telephone

+265999632090

Alerts

Be the first to know and let us send you an email when Love Community Radio 104.5 FM - Salima posts news and promotions. Your email address will not be used for any other purpose, and you can unsubscribe at any time.

Contact The Business

Send a message to Love Community Radio 104.5 FM - Salima:

Share