Chisomo Radio Station

Chisomo Radio Station Chisomo Radio Station is a Regional Community Radio Broadcasting to the rural areas of central Malawi

  Khonsolo ya boma la Salima yati ndi yokonzeka kugwira ntchito limodzi ndi atenga mbali osiyanasiyana powonetsetsa kuti...
26/06/2025



Khonsolo ya boma la Salima yati ndi yokonzeka kugwira ntchito limodzi ndi atenga mbali osiyanasiyana powonetsetsa kuti amayi omwe akutenga nawo gawo pa ndale ndi otetezeka ku nkhanza pamene dziko lino likukonzekela chisankho cha pa 16 September.

Mmodzi mwa akulu akulu ku nkhonsoloyi Chipiliro Janet Mtambalika ndiye wanena izi pa mkumano omwe unakozedwa ndi mabungwe a Oxfam ndi Warlec ndicholinga chodziwitsa anthu pa za ubwino otengapo gawo pa ntchito yoteteza amayi omwe akupikisana nawo mmadindo osiyana siyana pa ndale.

Malinga ndi Mtambalika nthambi yowona kuti pasakhale kusiyana pakati pa amayi ndi abambo pa khosoloyi yachilimika pophunzitsa anthu pa za ubwino olemekeza amayi pa ndale.

Pothilirapo ndemanga nkulu wa nthambi ya polisi boma la Salima Albert Nyongani wati mikumano yophunzitsa anthu ndi mafumu komanso ochita malonda ku madera iwathandizira kuchepetsa chiwerengero cha nkhanza pa ndale pofuna kudzakhala ndi chisankho cha bata ndi mtendere.

Mau awo senior Chief Karonga adayamikira mabungwe a Oxfam, Worlec ndi atenga mbali osiyanasiyana kamba ka mkumanowu ponena kuti upindulila amayi pa ndale.

Mkumanowu udabweletsa pamodzi atenga mbali osiyana siyana monga mafumu, apolisi, atsogoleri a zipani kungotchurapo ochepa.

(Angella Mwape-Salima)

 Mkulu wa achinyamata ku chipani cha UTM mu chigawo chapakati yemwe ndi wamalonda odziwika bwino m'boma la Kasungu, Tend...
26/06/2025



Mkulu wa achinyamata ku chipani cha UTM mu chigawo chapakati yemwe ndi wamalonda odziwika bwino m'boma la Kasungu, Tendai Richard Gama wapulumuka pa ngozi ya galimoto.

Malingana ndi zomwe Chisomo Radio Online yapeza, ngoziyi yachitika m'bada kucha walero kwa Jenda m'boma la Mzimba.

Malipoti akusonyeza kuti a Gama anali pa ulendo wopita ku nsika wa fodya waku Mzuzu.

Pa wulendowu, galimoto yomwe a Gama amayendera inawomba galimoto ina yomwe inanyamula katundu yomwe ati panthawiyo inalipatsogolo pawo, inangoyima modzidzimutsa.

A Gama apezeka kuti sanavulale modetsa nkhawa ndipo apitilira pa wulendo wawo waku nsika wa fodya ku Mzuzuko.

(Jeamson Joe Kalimba - Kasungu)

 Yemwe akufuna kuzapikisana nawo ngati phungu woyima payekha  m'dera lapakati m'boma la Nkhotakota, Namangale Kakota wat...
26/06/2025



Yemwe akufuna kuzapikisana nawo ngati phungu woyima payekha m'dera lapakati m'boma la Nkhotakota, Namangale Kakota wati kumathero asabatayi akhazikitsa chikho cha ndalama zokwana 5 milion kwacha chamasewero a mpira m'bomali.

Namangale wati waganizo zoika ndalamazi ndicholinga chofuna kupititsa patsogolo masewero a mpira komanso kuwapewesa achinyamata kum'chitidwe kapena makhalidwe osakhala bwino.

Mpikisanowu ukhazikitsidwa pa 27 June chaka chino pa bwalo la zamasewero la Lozi ndipo timu ya Chombo FC idzasewera ndi timu ya Hot Killers FC.

Chikhochi chikuyembekeza kudzatha pa 26 juy 2025.

(Wolemba: Trouble Sector)

  Galimoto ziwiri za anthu omwe amafuna kuchita zionetsero zaotchedwa Gulu la Achinyamata ovala zotchinga kunkhope kwina...
26/06/2025




Galimoto ziwiri za anthu omwe amafuna kuchita zionetsero zaotchedwa

Gulu la Achinyamata ovala zotchinga kunkhope kwinaku litanyamula zikwanje ndilo latentha galimotozi

Gulu la nzika zokhudzidwa motsogozedwa ndi Mkulu wa Bungwe la CDEDi a Silvester Namiwa omwe amafuna kuchita zionetsero lathawa pamalopa.

Iwo amafuna kuchita zionetsero zofuna kuti Mkulu wa bungwe loyendetsa zisankho la Mec Mai Annabel Mtalimanja atule pansi udindo.

 Mabungwe omwe si aboma  m'boma la Salima tsopano ali ndi utsogoleri wa tsopano.Bungwe la KINDLE motsogozedwa ndi Joseph...
25/06/2025



Mabungwe omwe si aboma m'boma la Salima tsopano ali ndi utsogoleri wa tsopano.

Bungwe la KINDLE motsogozedwa ndi Joseph Kandiyesa ndiye mkhala pa mpando wa tsopano wa Mabungwewa, ndipo atenga udindowu kuchoka ku bungwe la Salima Aids Support Organization (SASO) Pansi pa Paul Dancun omwe amaliza nthawi yawo yokhala pa udindowu.

Bungwe la SAMALA pansi pa George Kanyemba ndiye wachiwili kwa mkhala pa mpando wa mabungwe omwe si aboma mbomali.

Paul Duncan yemwe wamaliza nthawi yake yokhala mtsogoleri wa mabungwe omwe si aboma mboma la Salima wati mabungwewa pansi pa utsogoleri wake agwila ntchito zambiri zokhudza ulamuliro wabwino, umoyo, maphunziro komanso za ulimi.

Ma udindo atsopanowa ayamba kugwila ntchito zawo lero atangosankhidwa kumene pa mkumano wawukulu wa Mabungwewa.

(Louis Khama Majamanda)

 Bungwe loyendetsa masewero a mpira wa miyendo  wachisozera m’dziko muno la National Youth Football Association lati ndi...
25/06/2025



Bungwe loyendetsa masewero a mpira wa miyendo wachisozera m’dziko muno la National Youth Football Association lati ndilokondwa kuti lakwanilitsa lonjezo lake lomwe lidapanga logula zipangizo zophunzirira.

Mlembi wa mkulu wa bungweli, Rabson Woodwell ndiye wayankhula izi lachitatu pomwe bungweli lapeleka zipangizo zophunzilira ku SOS mu mzinda wa Mzuzu.

A Woodwell ati zomwe adalonjeza pa masewero a ndime yotsiliza ya masewero a FCB Katswiri Under 20 mu December chaka chatha zakwanilitsidwa ndipo zithandizira kupititsa patsogolo maphunziro.

Katunduyi ndi wa ndalama zokwana 1 million kwacha ndipo ndi monga Makope akuluakulu (college exercise books), zolembera, mapensulo, ma pental marker kungotchulapo zochepa.

(Wolemba: Matthias Nkosi)

 Ngati njira imodzi yopititsa patsogolo masewero a mpira wa manja wa atsikana m’dziko muno, kampani ya NICO ndi bungwe l...
25/06/2025



Ngati njira imodzi yopititsa patsogolo masewero a mpira wa manja wa atsikana m’dziko muno, kampani ya NICO ndi bungwe la Netball Association of Malawi (NAM) loweruka akuyembekezeka kukhazikitsa mpikisano wa ma timu 12 pa bwalo la za masewero la la Blantyre Sports Arena.

Mpikisano watsopano wu akhala akukhazikitsa pofuna kunthandinza komaso kulimbikitsa timu ya mpira wa manja ya dziko lino kukhala ya mphavu ndi yodalilika.

M’modzi mwa akuluakulu ku kampani ya NICO a Mbumba Mlia-Ndasauka ati kukhazikitsidwa kwa mpikisano wu ndi mbali imodzi ya ndalama zokwana K1 billion zomwe adalonjeza kuti akhala akuthandinza masewero kwa zaka zitatu.

Mkhala pa mpando wa komiti yomwe imayang’anira masewero a manja m’chigawo chapakati a Fernando Ligola ayamikira kampani ya NICO, ponena kuti mpikisano wu uthandinzira kutukula luso la manja m’dziko muno.

(Wolemba: Alinafe Nyanda-Lilongwe)

 Bungwe la Malawi Healthy Equity Network (MAHEN) layamikila magulu osiyanasiyana amene akugwila ntchito yolimbikitsa ama...
25/06/2025



Bungwe la Malawi Healthy Equity Network (MAHEN) layamikila magulu osiyanasiyana amene akugwila ntchito yolimbikitsa amayi kubaitsa ana awo katemera osiyanasiyana yemwe ndiwofunikira ku umoyo wa ana.

Nkulu woyendetsa ntchito zosiyanasiyana ku bungweli, Florence Khongongwa ndiye wanena izi lachitatu pamene MAHEN imapeleka njinga ku gulu la amayi la Chiluwa lomwe lili pansi pa chipatala cha Mwangala, kwa mfumu yaikulu Msakambewa m’boma la Dowa.

A Khonyongwa ati ndiwokhutila ndi momwe gulu la Chiluwa likugwilira ntchito yake, ponena kuti chikhazikitsileni guluri, lakwanitsa kukweza chiwelengero cha ana amene abaitsa katemera kuchoka pa 75 kufika pa 100 pa ana 100 alionse.

Poyankhulapo, wapampando wa guluri, a Moreen Chikaiko ati gulu lawo lakwanitsa izi kamba kogwila ntchito limodzi ndi mafumu komanso atengambali osiyanasiyana opezeka kudera lawo. Iwo anawonjezera ponena kuti tsopano, kupatula amayi, nawo abambo ayamba kutenga nawo gawo lopititsa ana awo kuchipatala kukabaitsa katemera.

Iwo atinso kufika kwa njinga kuguluri, kuwathandizira kwambiri ntchito yawo, ponena kuti akhala akuvutika mayendedwe mwa zina.

Bungwe la MAHEN, kuyambila chaka cha 2018, lakhala likugwila ntchito yolimbikitsa makolo kutengera ana awo ku sikero komanso kuwabaitsa katemera. Ntchitoyi ikumbekezeka kufika kumapeto pa 30 mwezi uno.

(Wolemba: Boniface Selemani-Dowa)

 World Vision Malawi yati ndondomeko ya National Multisectoral Nutrition Policy and Strategy m’chingelezi yomwe ikuyembe...
25/06/2025



World Vision Malawi yati ndondomeko ya National Multisectoral Nutrition Policy and Strategy m’chingelezi yomwe ikuyembekezeka kukhazikitsidwa lachinayi ku BICC mu nzinda wa Lilongwe ikugwirizana kwambiri ndi ntchito zomwe bungweli likugwira m’dziko muno.

M’modzi mwa akuluakulu ku bungwe la World Vision a Lizzie Lombe awauza atolankhani dzulo ku Lilongwe kuti kampeni imeneyi inthandizira kunthana ndi njala ,kunyetchera komaso kupinimbira pakati pa ana.

Malinga ndi a Lombe, apempha boma kuti likuyenera kuyika chidwi kwambiri pa ntchito zakadyedwe kabwino ndikuthana ndi vuto lakunyentchera lomwe ndilalikulu kwambiri pakati pa ana.

Bungwe la World Vision likugwira ntchito yomwe ikudziwika ndi dzina loti ENOUGH ndi cholinga chofuna kulimbikitsa atengambali osiyanasiyana,kuyika chidwi,pankhaniyi komanso yothandizira kulimbikitsa ndondomeko yopeleka chakudya kwa ana msukulu za primary ndi za mkomba phala.

Boma kudzera ku unduna wa za umoyo ukhala ukukhazikitsa ndondomeko yoyendetsera ntchito zakadyedwe kabwino yomwe ndi yazaka zisanu.

(Wolemba: Alinafe Nyanda-Lilongwe)

 Chipani cha MCP chati sichikugwedezeka ndi mgwirizano wa zipani za ku mpoto kwa dziko lino zomwe zinali ndi msonkhano s...
25/06/2025



Chipani cha MCP chati sichikugwedezeka ndi mgwirizano wa zipani za ku mpoto kwa dziko lino zomwe zinali ndi msonkhano sabata yapitayi.

Wachiwili kwa mneneli wa chipani cha MCP Ken Msonda wati chipani chawo chalunjika pa chipambano pa chisankho cha pa 16 September.

"Atsogoleri zipani mukuzikambazo zilibe aphungu kunyumba yamalamulo nde chowopela mchani? Mukaphatikiza ma zero 100 yankho limakhalabe zero." Watelo Msonda.

Zipani zochokela mchigawo cha ku mpoto sabata yathayi zinali ndi msonkhano wa ndale komwe mwazina analimbikitsa kufunika kwa umodzi pakati pa zipani zotsutsa.

(Louis Khama Majamanda)

CALL FOR INTERNS!Chisomo Radio Station (CRS) is looking for interns to join our team in Salima. CRS gives equal opportun...
24/06/2025

CALL FOR INTERNS!

Chisomo Radio Station (CRS) is looking for interns to join our team in Salima.

CRS gives equal opportunity to both men and women, including persons with disabilities. If you meet the qualifications, you are encouraged to apply.

 Malawi Archery Association layamikira Malawi National Council of Sports komaso Malawi Olympic Committee potenga gawo la...
24/06/2025



Malawi Archery Association layamikira Malawi National Council of Sports komaso Malawi Olympic Committee potenga gawo lalikulu lonthandizira kuti zipangizo zomwe bungwe li limagwiritsa ntchito zifike m’dziko muno.

Wachiwiri kwa mtsogoleri wa Malawi Archery Association a Henry Sakala ndiye anena izi lero pakutsatira kwakufika kwa zipangizozi zomwe amagwiritsa ntchito masewero awo a chandamale kuchokera ku World Archery.

Malinga ndi Sakala, zina mwa zipangizo zi ndi monga ma uta ndi zina zambiri zomwe zikuyembekezeka kuperekedwa kwa amphuzitsi a masewero wa omwe adamphuzitsidwa ndi bungweli chaka chantha mogwirizana ndi Malawi Schools Sports Assocciation.

Iye wati zipangizozi zomwe zinthandizire kwambiri kupititsa patsogolo masewero a chandamale m’dziko muno ndi za ndalama zokwana K5 million.

(Wolemba: Alinafe Nyanda-Lilongwe).

Address

Chisomo Radio Station P. O Box 266 Salima
Salima

Opening Hours

Monday 05:00 - 22:00
Tuesday 05:00 - 22:00
Wednesday 05:00 - 22:00
Thursday 05:00 - 22:00
Friday 05:00 - 22:00
Saturday 05:00 - 22:00
Sunday 05:00 - 22:00

Telephone

+2651262883

Alerts

Be the first to know and let us send you an email when Chisomo Radio Station posts news and promotions. Your email address will not be used for any other purpose, and you can unsubscribe at any time.

Share

Category