Chisomo Radio Station

Chisomo Radio Station Chisomo Radio Station is a Regional Community Radio Broadcasting to the rural areas of central Malawi

 Ngakhale bungwe  logula ndi kugulitsa mbewu la ADMARC linati liyamba kugula mbewu kuyambira pa 1 mwezi uno, kafuku fuku...
05/06/2026



Ngakhale bungwe logula ndi kugulitsa mbewu la ADMARC linati liyamba kugula mbewu kuyambira pa 1 mwezi uno, kafuku fuku wathu wapeza kuti bungweli silinayambe ntchitoyi m'boma la Ntcheu.

Titayendera pa malo ogulitsira mbewu a Nsipe tapeza kuti palibe chiyembekezo choti ntchito yogula chimanga iyamba pompano.

Alimi analandira uthenga kuchokera ku bungwe la ADMARC ndi chmwemwe, pomwe amayembekezela kugulitsa mbewu zawo pa mtengo wabwimo komanso nthawi yabwino.

Pakadali pano bungwe la ADMARC silindayankhulepo kathu za kuchedwa koyamba kugula mbewu.

(Daniel kaunda-Ntcheu)

 Nduna ya zachilengedwe Patricia Wiskes yati ngati dziko sitikuchita bwino pankhani yosamalira zachilengedwe.Wiskes wala...
05/06/2026



Nduna ya zachilengedwe Patricia Wiskes yati ngati dziko sitikuchita bwino pankhani yosamalira zachilengedwe.

Wiskes walankhula izi pa mwambo okhazikitsa lipoti la zachilengedwe la mchaka cha 2026 mpaka 2030 lomwe likufotokoza zofooka zomwe zilipo pankhani za chilengedwe maka mu zaka 16 zapitazi.

Ndunayi yati ndi zokhumudwitsa kuti dziko lino likulephera kusamalila zachilengedwe zomwe wati izi zikuyenela kusitha.

Ndunayi yati boma ligwila ntchito ndi ma unduna komanso nthambi zaboma zosiyana siyana pofuna kupeza njira zotetezela chilengedwe.

(Alpha Gabriella Tafatatha -Lilongwe)

 Unduna wa zaulimi wati boma layika chidwi chake polimbikitsa ulimi wa mthilila, komanso kulimbikitsa ulimi wa mbewu zom...
05/06/2026



Unduna wa zaulimi wati boma layika chidwi chake polimbikitsa ulimi wa mthilila, komanso kulimbikitsa ulimi wa mbewu zomwe ndizopilila kuchiwawu.

Mmodzi mwa akuku akulu ku undunawu Getrude Kambauwa ndiye wanena izi pa mwambo okhazikitsa lipoti lokhudza za chilengedwe omwe unachitikila ku Capital Hotel mu mzinda wa Lilongwe.

Malinga ndi Kambauwa, kuchita ulimi wa mthilila komanso molingana ndi kusitha kwa nyengo zitha kuthandizila dziko lino kukhala lodzidalila pa chuma.

(Alpha Tafatatha-Lilongwe)

 Atolankhani kuchoka kunyumba zofalitsa nkhani zosiyana siyana amphunzitsidwa momwe angalembele nkhani zokhudza malingal...
05/06/2026



Atolankhani kuchoka kunyumba zofalitsa nkhani zosiyana siyana amphunzitsidwa momwe angalembele nkhani zokhudza malingaliro agwiro.

Maphunzirowa omwe anakonzedwa ndi chipatala cha St. John of God, achitika lero ndipo anabweletsa pamodzi atolankhani omwe ali ndi chidwi chofalitsa nkhani zokhudza malingaliro agwiro.

Mmodzi mwa aphunzitsi omwe anatenga nawo gawo posula atolankhaniwa Dr. Dumanene Silungwe, yemwenso ndi dotolo pa chipatalachi wati atolankhani ali ndi udindo wawukuku pofalitsa ma uthenga omwe adzithandizila nzika kudziwa zokhudza malingaliro agwiro.

Ena mwa atolankhani omwe anatenga nawo gawo pa maphunzirowa ati upangiri omwe awupeza uthandizila kufalitsa mauthenga okhudza malingaliro agwiro moyenela.

(Francis Katengeza-Lilongwe)

 Mtsogoleri wa chipani cha UTM Dr Dalitso Kabambe wati aphungu mdziko muno akuyenera alingalire zobweretsa nthambi yamat...
05/06/2026



Mtsogoleri wa chipani cha UTM Dr Dalitso Kabambe wati aphungu mdziko muno akuyenera alingalire zobweretsa nthambi yamatenda a khasa mzipatala zikuluzikulu za boma zomwe akuchokera.

Iwo ayankhula izi lero pa Maliro a bambo Edson Ngolomi Mpika yemwe anali mlembi wa Chipanichi ku chigawo cha mbali mwanyanja Lakeshore region mchingerezi.

Kabambe wati mzovetsa chisoni kuti matenda a Khasa akupitilira kutenga miyoyo ya anthu ochuluka mdziko muno kutsatila kuti bambo Ngolomi Mpika amwalira atadwala nthendayi.

Mmawu ake phungu wa dera la kumpoto kwa boma la Salima Maxwell Jowasi Mnjemu yemwe anaima mmalo mwa phungu wadera lapakati pa bomali Gerald Kapiseni Phiri anayamika anthu omwe anafika pa Malirowa kamba kosunga bata posatengera kusiyana zipani.

Mnjemu anati nthawi ya ndale inadutsa kotero mzovetsa chisoni kuti anthu madera ena amalowetsa ndale ingakhale pa Maliro zomwe anati izi mzosayera kamba koti nthawi ya mavote inapita ndipo ino ndi nthawi ya chitukuko.

Pamapeto Mnjemu kumbali yake anati malemu Ngolomi adzawakumbukila kamba ka upangili wawo womwe wakhala akuwapatsa pokhala munthu yemwe anagwila nawo ntchito pomwe anali kumabungwe.

.

 Boma lati latenga mfundo zomwe bungwe la Catholic Commission For Justice and Peace CCJP lapeleka mu kalata yake yomwe b...
05/06/2026



Boma lati latenga mfundo zomwe bungwe la Catholic Commission For Justice and Peace CCJP lapeleka mu kalata yake yomwe bungweri latulutsa lero.

Mneneri waboma Shadrick Namalomba wati, boma ndiloyamika kamba koti mabungwe ngati CCJP akutha kuwona ndikuzindikila zomwe boma likuchita pofuna kutukula miyoyo ya a Malawi.

Malinga ndi Namalomba boma lavetsela bwino madandaulo omwe apelekedwa mu kalatayi.

Mwazina, kalata yomwe bungwe la CCJP latulutsa yadzudzula mchitidwe osankhana ndi kupatsana ntchito pa zifukwa za ndale pomwe kumbali ina kalatayi yayamikila ndondomeko zaboma zofuna kukonzaso chuma cha dziko lino ngakhale ati boma likuyenela kuchilimika pa mfundozi.

(Louis Khama Majamanda-Salima)

 Ofesi yowona za usodzi m'boma la Salima lero yawononga ndi kuwotcha zipangizo zosayenela zomwe zimagwilitsidwa ntchito ...
05/06/2026



Ofesi yowona za usodzi m'boma la Salima lero yawononga ndi kuwotcha zipangizo zosayenela zomwe zimagwilitsidwa ntchito pompha msomba pa nyanja ya Malawi.

Mkulu owona za usodzi m'bomali Patrick Zakeyu wati, zina mwazipangizo zomwe zawotchedwa zimalepheletsa msomba kuswana komanso kuwononga chilengedwe cha mmadzi.

Malinga ndi zakeyu, zipangizo zina monga, maneti otetezela ku udzudzu, zimawononga mazila a msomba komanso kupha msomba zingono zingono zomwe ndizosephana ndi malamu okhudza usodzi.

Magistrate Agness Chilambo, kuchoka ku bwalo la milandu la Salima Magistrate ndiwomwe anachitila umbondi ntchito yowotcha ndi kuwononga katunduyu, Chilambo wati ntchito ngati iyi ikupeleka uthenga kwa anthu omwe amagwilitsa ntchito zipangizo zomphela msomba zosavomelezeka kuti boma lili ndi chidwi chofuna kuteteza ndi kulimbikitsa malamulo okhudza usodzi.

Zipangizo zomphela msomba zandalama zoposela 73 million kwacha, zomwe zinalandidwa kuchoka kwa asodzi komanso ochita malonda kuchoka mchaka cha 2013 kufikila chaka chino ndizomwe zawotchedwa, ndipo ntchitoyo yagwilika ndi nthandizo lochoka ku Ripple Africa.

(Louis Khama Majamanda-Salima)

 Electricity supply corporation of Malawi (Escom) has reaffirmed it's commitment in promoting environmental sustainabili...
05/06/2026



Electricity supply corporation of Malawi (Escom) has reaffirmed it's commitment in promoting environmental sustainability in all operations.

The Statutory Corporation has emphasised on Reliable electricity and stewardship, and remains dedicated to protect the environment.

(Alpha Tafatatha-Lilongwe)

‎ ‎‎Apolisi m'boma la Chikwawa amanga anthu anayi powaganizira kuti apezeka ndi matumba makumi atatu komanso asanu ndi a...
05/06/2026



‎Apolisi m'boma la Chikwawa amanga anthu anayi powaganizira kuti apezeka ndi matumba makumi atatu komanso asanu ndi atatu a Makala popanda chilorezo.

‎Wachiwiri kwa mneneri wa polisi ya Chikwawa Chance Mfune Zare wati anthuwa anamangidwa dzulo pamalo opangira chipikisheni galimoto za pa msewu pamene anagwiritsa ntchito galimoto ya mtundu wa lore ponyamula makalawa kupita nawo mu mzinda wa Blantyre.

‎Maliinga ndi Zare, akuluakulu owona za nkhalango, anatsimikiza kuti makalawa ndi a ndalama zokwana 11.5 million kwacha

‎Anthuwa omwe ndi Elizabeth July, azaka 30, Ireen Hassan azaka 31 amachokera m'mudzi mwa Mtombolera pamene , Patrick Damiano azaka 40, ndi McFarlane Winason azaka 41 amachokera m'mudzi mwa changoima m'bomali.

‎(Jones Busuman-Chiradzulu)

 Dziko la Malawi lero likhala likukhazikitsa lipoti la zachilengedwe la mu chaka cha 2026 mpaka 2030.Pa mwambowu mlendo ...
05/06/2026



Dziko la Malawi lero likhala likukhazikitsa lipoti la zachilengedwe la mu chaka cha 2026 mpaka 2030.

Pa mwambowu mlendo olemekezeka ndi nduna ya zachilengedwe Patricia Wiskes.

Mlembi wamkulu ku unduna wa zachilengedwe Dr. Misheck Yagontha Munthali,mkulu wa bungwe loyang'anira za chilengedwe la Malawi environmental protection authority MEPA Dr Wilfred Kadewa,mkalapampando wa bodi ya MEPA Dr Yanira Ntupanyama ndi ena omwe afikaso pamalowa.

Mwambowu umene ukuchitikira ku Capital hotel mu mzinda wa Lilongwe ndi mbali imodzi yokondwelera tsiku lokumbukira zachilengedwe komanso tsiku lokumbukira zamoyo zonse mu Chaka cha 2026.

(Alpha Gabriella Tafatatha -Lilongwe)

Address

Chisomo Radio Station P. O Box 266 Salima
Salima

Opening Hours

Monday 05:00 - 22:00
Tuesday 05:00 - 22:00
Wednesday 05:00 - 22:00
Thursday 05:00 - 22:00
Friday 05:00 - 22:00
Saturday 05:00 - 22:00
Sunday 05:00 - 22:00

Telephone

+2651262883

Alerts

Be the first to know and let us send you an email when Chisomo Radio Station posts news and promotions. Your email address will not be used for any other purpose, and you can unsubscribe at any time.

Share

Category