05/06/2026
Ngakhale bungwe logula ndi kugulitsa mbewu la ADMARC linati liyamba kugula mbewu kuyambira pa 1 mwezi uno, kafuku fuku wathu wapeza kuti bungweli silinayambe ntchitoyi m'boma la Ntcheu.
Titayendera pa malo ogulitsira mbewu a Nsipe tapeza kuti palibe chiyembekezo choti ntchito yogula chimanga iyamba pompano.
Alimi analandira uthenga kuchokera ku bungwe la ADMARC ndi chmwemwe, pomwe amayembekezela kugulitsa mbewu zawo pa mtengo wabwimo komanso nthawi yabwino.
Pakadali pano bungwe la ADMARC silindayankhulepo kathu za kuchedwa koyamba kugula mbewu.
(Daniel kaunda-Ntcheu)