JOHN POXY

JOHN POXY BORN TO EXPRESS, NOT TO IMPRESS.

🇲🇼NKHANI YA NKHONDO YOMWE IKUPITILILA KU UKRAINE Maiko a Russia ndi Ukraine, Dzulo anagwilizana zochita Msintho kuti asi...
27/01/2024

🇲🇼NKHANI YA NKHONDO YOMWE IKUPITILILA KU UKRAINE

Maiko a Russia ndi Ukraine, Dzulo anagwilizana zochita Msintho kuti asinthane Asilikali a Maiko awiriwo omwe anagwidwa pa Nkhondo.
Ndipo Msinthowo umayenera kuchitika pa Malo ena otchedwa Kolotilovka, ku Malire a Maiko a Russia ndi Ukraine.

Koma Ndege ya Asiliakali a Dziko la Russia, a Nkhondo ya Mlenga Lenga, inanyamuka ku Khamba Lokhala Asilikali a Dzikolo, Lotchedwa Chkalovsky, kufupi ndi Mzinda wa Moscow, pa Ulendo opita ku Chigawo cha Belgorod, chomwe chinachita Malire ndi Dziko la Ukraine.

Ndipo Asilikali a Dziko la Ukraine, anaombera ndi kugwetsa pansi Ndegeyo ndi Mabomba atatu a mtundu otchedwa Mizailo, ochokera ku Zida za Nkhondo za Maiko a Germany ndi America, ponena kuti Ndegeyo inanyamura Mabomba a mtundu otchedwa S-300, ndicholinga choti akaphulitsidwe pa Nkhondo yomwe ikupitilira M'dzikolo.

Koma Dziko la Russia, Lati mu Ndegeyo munali Asilikali a Dziko la Ukraine okwana 65, omwe anali pa Ulendo opita ku Msintho, komanso munali Asilikali atatu(3) omwe amapelekeza Ndegeyo, komanso Anthu ena Asanu ndi M'modzi(6) ogwira ntchito mu Ndegeyo.

Ndipo Anthu onse pamodzi anakwana 74, omwe afera pa Malo pomwe Ndegeyo yagwera.

Ndegeyo yagwetsedwa pansi kufupi ndi Tauni yotchedwa Yablonovo, Mchigawo cha Belgorod.

Ndipo poyankhulapo pa Nkhaniyi, Bambo Mark Voyger, yemwe anakhalapo Mlangizi wa Dziko la America pa nkhani zokhudza Dziko la Russia, anati ndizokayikitsa kuti mu Ndegeyo munali Asilikali a Dziko la Ukraine omwe amapita ku Msintho.

Komanso Bambo Muksym Kolesnikov, yemwe anapulumukira Mkamwa mwa Mbuzi kudzera pa Msintho, wati Iye anali mu Gulu la Asilikali a Dziko la Ukraine okwana 50, pa ulendo opita ku Msintho, Ndipo iwo ankatetezedwa ndi Asilikali a Dziko la Russia, okwana 20, choncho ndi zamkutu ndi zopanda pake kuti Asilikali a Dziko la Ukraine 65, angapelekezedwe ndi Asilikali a Dziko la Russia atatu (3) pa Ulendo opita ku Msintho.

Komanso Bambo Dmitro Lubinets, yemwe ndi Mkulu wa Bungwe Lowona za Maufulu a Nzika za Dziko la Ukraine, wati Maina a Asilikali a Dzikolo, omwe Dziko la Russia Likunena kuti amapita ku Msintho, anapeledwa kale ku Dzikolo, pa Msintho omwe unachitika pa 3rd January.

🛑Tippy and Kitty 🛑:Tippy Dog and Kitty Cat lived in Donny’s home. Donny liked them both very much. But Tippy and Kitty a...
22/01/2024

🛑Tippy and Kitty 🛑:

Tippy Dog and Kitty Cat lived in Donny’s home. Donny liked them both very much. But Tippy and Kitty always quarreled with each other. Tippy barked at Kitty whenever she saw her.

One night, a robber came to Donny’s home. Tippy started to bark loudly. Suddenly, the robber took a stick and moved forward to beat Tippy. Kitty was watching this.

“Oh, no! The robber will harm Tippy and Donny," she thought. Kitty ran to the Robber, and scratched his leg hard. The robber shrieked in pain. Tippy barked loudly. Donny and his father came out and caught the robber.

Tippy thanked Kitty for saving her from the robber. Then, they both became good friends.

MY FIRST ACCOUNT WAS HIKED SO THIS IS MY NEW ACCOUNT

🌍🌍🌍🌍🌍🌍🌍🌍🌍🌍🌍
✨➡️𝗝𝗢𝗜𝗡 𝗠𝗬 𝗙𝗔𝗖𝗘𝗕𝗢𝗢𝗞 𝗣𝗔𝗚𝗘 𝗖𝗛𝗔𝗡𝗡𝗘𝗟! ⬅️✨
1. World News🌍💣
2. Success and Failure Stories of Wealthy Individuals🏆📊
3. Environmental Stories 🌵🌳🌱🌿🍃☘️
4. Vacancies 🗒️📃
5.Jokes🤣😀🤔😟
6.𝖲𝗉𝗈𝗋𝗍𝗌⚽
7.𝖳𝖾𝖼𝗁𝗇𝗈𝗅𝗈𝗀𝗒🛴
8.𝖥𝖺𝗌𝗁𝗂𝗈𝗇🧥
9.𝖧𝖾𝖺𝗅𝗍𝗁🍕🌮
10. 𝖡𝗎𝗌𝗂𝗇𝖾𝗌𝗌📉📈
11.𝖯𝗈𝗅𝗂𝗍𝗂𝖼𝗌📜
12.And many More😆
💼 𝗝𝗢𝗜𝗡 𝗠𝗬 𝗙𝗔𝗖𝗘𝗕𝗢𝗢𝗞 𝗣𝗔𝗚𝗘 /𝗣𝗥𝗢𝗙𝗜𝗟𝗘 𝗔𝗡𝗗 𝗦𝗧𝗔𝗬 𝗨𝗣𝗗𝗔𝗧𝗘𝗗 𝗪𝗜𝗧𝗛 𝗙𝗔𝗦𝗖𝗜𝗡𝗔𝗧𝗜𝗡𝗚 𝗦𝗧𝗢𝗥𝗜𝗘𝗦 𝗔𝗡𝗗 𝗘𝗩𝗘𝗡𝗧𝗦 𝗧𝗛𝗔𝗧 𝗪𝗜𝗟𝗟 𝗜𝗡𝗦𝗣𝗜𝗥𝗘 𝗬𝗢𝗨!
https://www.facebook.com/profile.php?id=61555524852779&mibextid=ZbWKwL

😊 Like and follow me right now

❤️ NKHANI YA CHIKONDI KOMA YOKHUNZA KWAMBIRI ❤️Nyamata wina osauka anali muchikondi ndi mwana wabwana wina koma vuto sam...
21/01/2024

❤️ NKHANI YA CHIKONDI KOMA YOKHUNZA KWAMBIRI ❤️

Nyamata wina osauka anali muchikondi ndi mwana wabwana wina koma vuto samamumasula nkaziyu.
Tsiku lina mnyamatayu analimba ntima kukamufikira ntsikanayu kumuuza za muntima mwake ndipo dzinatheka anamuuza.
"Hey, Mvesera Ndalama yako yomwe umalandira pa mwezi, ndindalama yomwe ndimapasidwa tsiku lililonse nde ndi Ngakhale bwanji muchikondi ndi munthu ngati iwe? Zitaye" Anatero mntsikana uja pomuyankha Nyamata uja.

"ndipo sindikuziwa kuti walimba ntima motani, waganiza bwanji kundiuza ine zimenezo, ine singakonde munthu ngati iwe pita ukasake sake akazi ALIKO Ambiri a level (type ) yako iwala zainezo"
Anapitiliza motero mntsikana uja kumuuza Mnyamata uja, koma ngakhale zinali choncho sizinali zophweka kwa mnyamatayu kumuiwala nsikana uja.

Panadutsa dzaka 10 chichitikireni zimenezi kenako tsiku lina anakumananso mu shoprite.
"Hey, uli bwanji Martin" Anatero mntsikana uja.
"Ndili bwino kaya iwe" anayankha Nyamata uja.
"Kaya family yako ili bwanji" Anafunsa motero mntsikana uja.
"mmm ine sinakwatirebe momuja Kaya iweyo lako" Anatero Martin
"ine ndinakwatiwa ukuziwa Ndalama yomwe amalandira mamuna wanga 150pin pa mwezi, ungamake pamenepo komanso ndiwa smart ? Anatero nkazi uja akunyada.

Pamenepo Martin anangomuyang'ana nkaziyu kenako misonzi yachisoni inayamba kugwa mmaso mwake.
Posakhalitsa mamunake wa nkazi uja anatulukira. Nkazi uja asanalakhule mawu.
"Hey, sir mwafikanso kuno komanso mwayi mwakumana ndi nkazi wanga,
Dorothy awa ndi abwana anga omwe a kutiyang'ana ali ndi project ya 100million ndi munthu wabwino kwambiri, Boss uyu ndinkazi wanga Dorothy." Anatero mamuna uja akuwalonjera anthuwa.
"pamenepa alibe nkazi, koma nkazi amene adzakwatirane ndi bwana Eish wamwayi ndithu. Anali muchikondi ndi nkazi wina koma nkazi yo sanawavomere kuyambira pompo anakhala single till now." Anapitiliza motero mamuna uja.

"ndanyadira kukumana nanu" Anatero Martin
Nkazi atanva zimenezi anaweramira pansi osayankhulanso kanthu.

PHUNZIRO

Moyo ndiwaufupi komanso ulingati glass munthu umangoona pokhapo pomwe pawalapo koma suziwa kuti kodi mbali inayo kuli zotani.
Choncho musakhale anthu oipa pomanyoza anthu chifukwa cha maonekedwe okha ayi
Moyo uli ngati nyengo nthawi imatha kusintha Mosayembekezera,
Osanyoza munthu chifukwa cha nyengo zake chifukwa za mmawa siziziwika aliyese analengedwa ndi tsogolo lowala,
MULUNGU AKUDALITSENI 🙏

Mulibwanji??Alikuti?Akupanga chani?Umoyo wake ukuyendela bwanji?Mwachidule.Takubweleselani zokhunza oyimba wathu wapakan...
21/01/2024

Mulibwanji??

Alikuti?
Akupanga chani?
Umoyo wake ukuyendela bwanji?

Mwachidule.

Takubweleselani zokhunza oyimba wathu wapakanthawi oziwika bwino ndi dzina loti
.

Oyimbayu anaziwika ndi nyimbo za m'chamba Cha lokolo ndi nyimbo monga.
'gwanya

Kungotchulapo zochepa chabe.

Kodi pano Namakhwa alikuti?

Pano Namakhwa ndi banja lake amakhala m'mudzi wina moyandikana ndi Chisitu m'boma la Mulanje.

Nthawi ya m'mbuyomo amagwila ntchito ya ulonda koma pano anasiya.
Kotelo amachita timalonda komaso ulimi kuti azipeza zosowa za iye ndi banja lake.

Kukamba za umoyo wake tingati ukuyendabe bwino chomcho.

Tanena izi chifukwa sipanapite nthawi yayitali chichitileni ngozi ya Galimoto.

Pangoziyi panaliziwa moyo ndimso kuvulala modesa nkhawa kotelo Mulungu anamukondela chifukwa sanavulale modesa nkhawa.

Kodi Namakhwa anasiya kuyimba?

Tingati eya poti patenga nthawi kaswiliyu asanatuluse nyimbo iliyose.

Koma titacheza ndi iye mwini anati luso adakali nalo kotelo atha kubwelelaso mumayimbidwe ngati kutakhala kotheka kuti atelo.

Namakhwa amakhala bwanji ndi anthu.

Titacheza ndi anthu angapo anstifotomozela kuti Namakhwa amakhala naye bwino kotelo kuti alibe chipongwe kwa aliyese.

Kufikilaso nthawi ina pomwe tibweleso tingoti zikomo pokhala nafe.

Zitisatilani bwino popanga follow page ino



Onesesani kuti mwapanga
follow
👇👇
(JOHN POXY?)

DPP YACHOSA ANTHU 11Chipani chotsutsa cha DPP chachotsa m'maudindo ena mwa akuluakulu monga; a Kondwani Nankhumwa, aGrez...
21/01/2024

DPP YACHOSA ANTHU 11

Chipani chotsutsa cha DPP chachotsa m'maudindo ena mwa akuluakulu monga; a Kondwani Nankhumwa, aGrezelder Jeffrey, a Mark Botomani, a Nicholas Dausi ndi a Ken Msonda.

Malingana ndi kalata yomwe chipanichi chatulutsa lero, izi ndizotsatira za zokambirana zomwe akulu akulu osungitsa mwambo mchipanichi analinazo masiku apitawo ndi adindowa. Onse ochotsedwa mu DPP ndi 11.

A Uladi M***a awaimitsa mu chipanichi kwa miyezi isanu ndi inayi (9) pongotchulapo ochepa ndipo, a Ralph Jooma, angowachotsa pa udindo wawo wa mkulu owona zachuma mu chipanichi.

21/01/2024
AMANGIDWA KAMBA KOPANGA MAPEPALA OYENDERA PA MSEU  MWACHINYENGO M'BOMA LA MANGOCHIEastern Region Immigration office yama...
21/01/2024

AMANGIDWA KAMBA KOPANGA MAPEPALA OYENDERA PA MSEU MWACHINYENGO M'BOMA LA MANGOCHI

Eastern Region Immigration office yamanga mdzika zaziko lino zokwanira 5 kamba kopanga mapepala oyendera pamseu achinyengo komanso kupanga malisiti ndi zidindo zaboma mwachinyengonso.

Malimgana ndi Mneneri wa Eastern Region Immigration, Edward Chidzalo,anthu ogwidwawa ndi Abdul M'dala a Zaka 36,Rafick M'dala azaka 24 komanso Alie Soya azaka 32 onsewa ochekwra Kwa T/A Mponda M'boma la Mangochi-.

Ena mwa anthuwa ndi Michael Chipojola azaka 36 ochokera ku Chiradzulu ndi Davie Masanjala Wazaka 42 ochokera Kwa T/A Nkhumba M'boma la Phalombe.

Anthuwa atsekeredwa kutsatira kumangidwa kwa mzimayi Wina pa songwe Border yemwe amagwiritsa ntchito mapepala oyendera pamseu okomzedwa munjira zachinyengozi.

Mzimayiyu anauluka Kuti mapepala achinyengowa apangidwa Ku M'boma la Mangochi, apa ndipomwe a immigration analondola kumaloku ndikugwira anthu asanuwa komwenanakawapeza ndizipangizo zochita mchitidweu.

APA NDE NDIKUTHANAKUTHANA - Watero Chitatata MsondaMmodzi mwa anthu omwe atulutsidwa muchipani cha Democratic Progressiv...
21/01/2024

APA NDE NDIKUTHANAKUTHANA - Watero Chitatata Msonda

Mmodzi mwa anthu omwe atulutsidwa muchipani cha Democratic Progressive (DPP) a Ken Chitatata Msonda ati abwenza chiganizo chawo chomwe anapanga popepesa pazomwe iwo ankapanga zomwe zinkanyozetsa chipanichi.

Pa nkumano womwe chipani cha DPP chinachitisa ku Nkopola miyezi yapitayo a Msonda adapepesa kuti sazachitanso chilichonse chokhudza kunyozetsa chipanichi ndicholinga choti chizalamulilenso mu 2025.

Koma kudzera mu uthenga wawo womwe atumiza pa tsamba la mchezo la WhatsApp a Msonda ati abwenza zomwe adapepesa kaamba koti zikuoneselatu kuti chipanichi sichinamve kupepesa kwawo.

"Apa nde andimva zenizeni, wokufa pandale sadziwika, kuthanakuthana," Atero a Msonda.

Dzulo chipani cha DPP chatulutsa mundandanda wa mayi omwe achotsedwa muchipanichi kuyambira a Kondwani Nankhumwa ndi gulu lawo monga a Nicholas Dausi, Mark Botoman, Grelzeder Jeffrey, Joe Nyirongo, Cecilia Chazama ndi ena.

Chipani cha Democratic Progressive(DPP) chachotsa anthu awa mu chipani.1. Kondwani George Malemia Nankhumwa2. Grezelder ...
21/01/2024

Chipani cha Democratic Progressive(DPP) chachotsa anthu awa mu chipani.

1. Kondwani George Malemia Nankhumwa
2. Grezelder Jeffrey
3. Cecilia Chazama
4. Mark Botomani
5. Nicholas Dausi
6. Mark Botomani
7. Otria Moyo Jere
8. Billy Malata
9.Kenneth Msonda
10.Forunate Simeon Phiri.
11. Joe Nyirongo

Chimanga chochokera ku Tanzania tsopano chitha kutumizidwa ku Malawi chifukwa boma kudzera mu unduna wa zamalimidwe lach...
21/01/2024

Chimanga chochokera ku Tanzania tsopano chitha kutumizidwa ku Malawi chifukwa boma kudzera mu unduna wa zamalimidwe lachotsa chiletso choletsa kuitanitsa chimanga kuchokera ku Tanzania.

```¶ Chiletsochi chinakhazikitsidwa chifukwa cha kupezeka kwa Maize Lethal Necrosis Disease (MLND) m’dziko la East Africa.

M'mawu ake, mlembi wa zaulimi a Dickxie Kampani ati undunawu wakhala ukulankhulana mosalekeza ndi bungwe la Tanzania Plant Health and Pesticides Authority kuti ligawane zambiri za kufalikira kwa matendawa.

Ananenanso kuti akuluakulu aku Tanzania adapereka umboni ndikuwonetsa kuti matendawa adapezeka.

“Potengera udindowu, amalonda amaloledwa kuitanitsa chimanga kuchokera ku Tanzania atalandira chilolezo choyenera kuchokera kumayiko ena komanso zikalata zophatikizira za ukhondo ndi ukhondo kuchokera ku boma la Malawi ndi Tanzania,” inatero Kampani.

Pambuyo polengeza za chiletsocho, akuluakulu a m’madoko a Malawi m’chigawo cha kumpoto analanda matumba angapo achimanga kwa amalonda.

Boma lati chimangachi chigayidwe kukhala ufa pofuna kupewa ngozi yomwe anthu angadzalemo m’dziko muno.```

CHIPANI CHA DPP CHACHOTSA A NANKHUMWA, ENA MCHIPANIChipani chotsutsa cha DPP chachotsa muchipanichi mtsogoleri otsutsa b...
21/01/2024

CHIPANI CHA DPP CHACHOTSA A NANKHUMWA, ENA MCHIPANI

Chipani chotsutsa cha DPP chachotsa muchipanichi mtsogoleri otsutsa boma a Kondwani Nankhumwa, yemwe anakhalapo mlembi wachipanichi a Grezelder Jeffrey komanso mneneri wakale wachipanichi a Nicholas Dausi.

Chipanichi chalengeza izi mu chikalata chomwe chatulutsa ndipo chasainidwa ndi mneneri wake a Shadreck Namalomba.

Chipani cha DPP mchikalatachi chati chachotsanso mchipani akukuakuku ake ena monga a Cecilia Chazama, a Mark Botomani, mai Otiria Jere, a Fortune Phiri, a Ken Nsonda, a Joe Nyirongo, a Fredrick Billy Malata, kungotchulapo mwa ena.

A Namalomba ati chipanichichi chachita izi kutsatira zomwe komiti yosungitsa mwambo yachipanichi yapeza itamva milandu yomwe akuluakuluwa anapalamula.

Chipanichi, chaimitsanso ena mmaudindo komanso kukhala mamembala a chipanichi kwa miyezi isanu ndi inayi.

Mtsogoleri wachipanichi a Professor Peter Mutharika akhala asakumvana ndi mtsogoleri wotsutsa boma a Kondwani Nankhumwa pa mfundo zina zoyendetsera chipanichi.

MFUMU YAMANGIDWA KU NTCHEU POCHITA ZACHINYENGOApolisi m'boma la Ntcheu amanga a Shadrick Justice azaka 27 omwe ndi Nyakw...
21/01/2024

MFUMU YAMANGIDWA KU NTCHEU POCHITA ZACHINYENGO

Apolisi m'boma la Ntcheu amanga a Shadrick Justice azaka 27 omwe ndi Nyakwawa Thunga powaganizila kuti anabera anthu powanamiza kuti awagulira feteleza mu ndondomeko ya zipangizo zotsika mtengo.

Malinga ndi m'neneri wapolisi ya Ntcheu a Jacob Khembo, amfumuwa anatenga ndalama zokwana K660,000 ndi ziphaso za unzika zokwana 44 za anthu omwe amayenera kupindula ndi ndondomeko ya zipangizo zotsika mtengo ponena kuti awathandiza kugula feteleza wa NPK.

Pa 4 January, oganizilidwawa anakabweza ziphaso ndi ndalama kwa anthuwa ponena kuti akanika kugula koma anthuwa atapita kuti akagule okha anakapeza kuti maina awo agula kale feteleza.

Anthuwa anakanena za nkhaniyi ku polisi ya Sharpvalley zomwe zinapangitsa kumangidwa kwa ogazilidwawa.

a Justice amachokera mudzi wa Thunga, m'dera la mfumu yaikulu Ganya m'bomali.

Address


Alerts

Be the first to know and let us send you an email when JOHN POXY posts news and promotions. Your email address will not be used for any other purpose, and you can unsubscribe at any time.

Contact The Business

Send a message to JOHN POXY:

Shortcuts

  • Address
  • Telephone
  • Alerts
  • Contact The Business
  • Claim ownership or report listing
  • Want your business to be the top-listed Media Company?

Share