Andy's stories

Andy's stories Cholinga chake ndi kuphunzitsa komanso kusangalatsa

21/08/2022

NDINAONONGA NDEKHA
¢¢¢¢¢¢¢¢¢¢¢¢¢¢¢¢¢¢¢¢¢¢
PART 2 b
Osaiwara kupanga like page ya Andys stories kuti nkhani zisamakuphonyeni.
Kutacha ndinalemba kalata yofunsira chibwenzi ndi kuisiya nkati mwa kope la notes.
Ndinanyamuka kupita ku sukulu, nditafika malo ena ndinakumana naye Emily nayenso akupita ku sukulu.
"Ndisanaiware, ndipase notes nzanga kaye", Uyu anali Emily kufuna notes zake, ndinapereka koma sinamuuze kuti ndasiyamo kalata.
Ku sukulu ndikamuona Emily akundiyang'ana ndimaganizira za kalata ija kuti akufuna andiyankhe koma osadziwa kuti kope lija sanalibvundukure ndipo zoti muli kalata sakuziwa.
Titaweruka ndinanyamuka kumapita kumudzi, "iwe mnyanata wa mantha, taima!!!! "
Ndinadabwa ndi mau onditchura wamantha.
Ukati wamantha ukutanthauza chani?
Mmalo mondiyankha ungomwetulira, komanso ukanamenyedwa uleletu pamene sitili pa chibwenzi.
Emily kuyankhura akumwetulira.
Tinachenza tikuyenda kenako tinasiyana nditakumana ndi Andrew.
" Man Akimu, mkadzi uyo ndimamufuna bwanji, tsiku lina uzandiuzire kuti ndimamufuna, ukuganiza bwanji?
Zimene anayankhura ndinamukanira pomuuza kuti ampitire yekha.
Tinakambirana kuti la mulungu likubweralo tipitire limodzi kokupha nsomba.
Nditamva izi ndinasangalala.
Kodi zinatha bwanji?
Ndikulephera kulemba nkhani yaitali chifukwa sindikudziwa, mulimonse bola nkhani zizikupezani .

21/08/2022

NDINAONONGA NDEKHA
¢¢¢¢¢¢¢¢¢¢¢¢¢¢¢¢¢¢¢¢¢¢¢¢¢
PART 2
Choyamba pangani like page ya andys stories kuti nkhani zisamakuphonyeni.
Ndili wa mng'ono makolo anga anandiyambisa sukulu ya mkomba phala.
Ndinali wa nzeru ndipo anthu ambiri amandikonda chifukwa cha nzeruzo.
Nditayamba sukulu ya primary, sizinasinthe, ndinali kukhonza bwino mpaka standard 7 ndisanayambe chibwana.
Ndinayamba kuchenza ndi anyamata amene sanali kupita ku sukulu, kukacha amapita kowenza nsomba ku nyanja ya chirwa.
Tsiku lina ndikuchokera ku sukulu, ndinakumana ndi Andrew akuchokera kunyanja kokupha nsomba, anandiitana mokuwa amvekere : Akimu!!! taima undidikire!!!!
Anathamanga ndi kundipeza, atafika ananditengera pansi pa mtengo wa mlambe, kenako anatulusa ndalama zimene anagulisira nsomba.
"Ndithandize kuwerenga ndalama zomwe ndapeza lero".
Zinali zambiri ndipo ndinasilira kwambiri.
Titamaliza anandigaira kuti ndikadyere ku sukulu tsiku lotsatira.
Moyo osilira unayamba kumera midzu mwa ine.
Ndinamupempha kuti tsiku losapita ine ku sukulu "holiday "azanditenge.
"Man Akimu musadande, ndizakutchulani " Andrew amayankhura akutsekerera.
Nditafika ku nyumba anandipasa chakudya, nditamaliza ndinapita kwawo kwa Emily kuti akandibwereke notes za English kuti ndikawerenge nawo.
Ndinamupezadi ndipo ndinamuitanira pamene ndinaima.
*Emily,,, ungandibwerekeko notes za English ndikubwezera madzulo ano kuti nawe ndisakusokoneze kuwerenga? *
Asanandiyankhe ndinadabwa wina anandigwira phewa, "ndimadana ndi aliyense oima ndi chemwali wanga ku njira, mukukambirana chani? ndiuze nsanga ndisanakupase pama. "
Ndinacheuka mwa mantha ndipo ndinaona kuti anali mchimwene wake.
"Usandiganizire zimenezo, mwanji osayamba wafunsa kaye? " Emily kuyankhura mokwiya.
Emily anapita kukatenga notes ndikundipasa, anandiuzanso kuti ndisabvutike ndi kubwera kuzamupasa, ndikamupase ku sukulu.
Ndinanyamuka osamusanzikanso mchimwene wake.
Kutacha, ndinalemba kalata yomufunsira chibwenzi,

zinatha bwanji?

15/08/2022

NDINAONONGA NDEKHA
¢¢¢¢¢¢¢¢¢¢¢¢¢¢¢¢¢¢¢¢¢¢
PART 1

"Amayi ndi abambo, bambo ndi Mayi agona apawa asiya ana awiri. " bambowa amwalira ali ndi dzaka 45 za kubadwa pamene mayiwa amwalira ali ndi dzaka 38 za kubadwa.
Mwambo onse wa maliro wachitira pamodzi chifukwa ndi a chipembezo Chimozi komanso nyumba za makolo awo ndi zoyandikana.
Awa anali a mpingo kuyankhura ku chigulu chimene chinasonkhana pa maliro olirisa wina aliyense anabwera.
•ndinali kuona ngati ndikulota pamene mayi ndi bambo anga anamwalira pa ngonzi ya galimoto imene anakwera.

Akimu zoona!!! taona wasala wekha, amene akusamale ndi ndani? agogo anga kulira akuyan'gana pamene ndinakhala.
Maso anga anafiira ngati ndathilidwamo tsabola komanso ndimalephera kulira kotulusa mau chifukwa anasasa. Ondimvesera atha kumamva ngati bakha.
Mwambo wa maliro unachitika komanso mothamangira nthawi chifukwa inali nthawi ya mvura.
Anthu atafika ku manda, zinali za chisoni kuona, adzukulu ali busy kuchosa madzi nzenje la manda pakuti anali kutuluka pansi.
Pajatu musaiware ndanena kale kuti inali nthawi ya mvura.
Nditalingalira kwambiri ndinayamba kulira.
Makolo anga amagona malo abwino ouma, lero akulowesedwa nzenje la manda komanso monyowa, haaaaaa!!!!! kodi moyowu, unkalinda zimenezi kodi?
Ndinayamba kulira ndikulunjika ku zenje la manda la abambo koma anthu anandigwira.
Zonsezi ndimachita koma mosadzindikira tanthauzo lake la zomwe ndimachita.

Makolo anga anaikidwadi ngati zochenza. Titafika kunyumba anthu anabwerera m'nyumba zawo.
Kuyambira tsiku limenero ndinayamba kulingalira zimene ndinali kuchita posafuna kuti ndilangizidwe ndikalakwisa.

Tibwerere mbuyo kuti muziwe za Moyo wanga.
Ine dzina langa ndi Akimu. Ndinabadwa ndi kukura m'boma la Zomba koma pafupi ndi nyanja chirwa.
Ndili wa mng'ono makolo anga anandiyambisa sukulu ya mkomba phala.
Tangoyambapo Tipitilize mawa.

14/06/2022

Kuyambira lero andys stories ikubweranso m'bwalo.
Tiyeni madzulo ano tikhalire limodzi.

07/05/2022

Muli bwanji nonse?

21/05/2021

WANDITAISA NTHAWI
#£√£√£√£√£√£√£√£√£√£√
PART 6

Choyamba ndipepese chifukwa chochedwesa nkhani, izi zachitika chifukwa cha zobvuta zina.
Tiyeni tipitilize;
Tsiku lina Lidia anamuitana Christopher koma ali okhumudwa kwambiri.
Atafika anadabwa kuona chikwama cha zobvala pa mbali pake.
"Bwanji Lidia ukupita kochapa? " anafunsa Christopher,
ayi ulendoyu ndikupita kwanu.
~kwathu !!!!! usamayese zida ukumva!!!! kotani?
anafunsa modabwa.
Mayi anga andithamangisa atamva kuti tinali Ku rest house ndi iweyo komanso pano ndilibe kopita, nyamula chikwamachi tizipita kwanu.

Lidia amayankhura akuzuka kuti azipita kwawo kwa Christopher.
Chonde Lidia, inetu sindinakonzeke kukwatira komanso makolo anga akamva andikmsikanayuIne ndiye ndakuuza kuti ndikufuna banja? ndikanakhala ndi kwina kokhala ndikanapita kuti ndizikakhala nawo.

Christopher anamulumbikisa Lidia kuti apite kwawo mwina akamumvesa kusiyana ndi kulowerera .
Lidia anabwereradi ndi kupita kwawo, atafika anapeza kuti mayi ake kulibe, anaona kuti ndi mwayi chifukwa anapita kukasamba ndi kumapita Ku sukulu.
Pa nthawi imene amapita Ku sukulu sanaziwe kuti Magi ake amuona ndipo anayenda mwa changu, atafika anapeza anzake akupita pa assembly.
Christopher atamuona Lidia anasangalala podziwa kuti zinthu zayenda bwino chifukwa amaganiza kuti mayi ake amukhululukira.

Atalowa mkalasi aphunzitsi anayamba kuphunzitsa, mtima wa Lidia unagunda mwa mphanvu ngati amathamangisidwa atawaona mayi ake akulowa mu office ya ahead.
Zotinso akuphunzira zinamuchokera koma anaona ngati amuzizimusa aphunzitsi atamuuza kuti aimilire ayankhe funso.
"Lidia, tell the class, what is reproduction?
Lidia mmalo moyankha funso akangokanda mmutu.
" Mmmmmm sir kungoti ujeni eeee ujeni!!!!!!!!"
Asanamalize anatulukira a head, "Lidia muno alipo?
Anafunsa ahead, anabvomera ndipo anamuuza kuti akufunika Ku office pamodzi ndi Christopher.

Lidia ananyamuka, koma Christopher sanapite nsanga chifukwa samadziwa chimene chimachitika.
* Christopher !!!!!!!! akuti upite Ku office kodi sukumva?
Mphunzitsi kuyankhura mokalipa.

Anazuka kupita Ku office koma atafika anadabwa kuona mayi wina akumuyangàna kwambiri.
" Mayi, talongosolani chimene mwabwerera, ndi chiyani?"
Ahead anawafunsa mayi ake Lidia chimene abwerera.

"Ndikufuna mnyamatayu anene yekha inu mukumva, mwana wanga akumabwera Ku nyumba mochedwa,, akuti amakhala ndi iyeyu, akumapita Ku rest house ndiye ndikufuna andiuze chilungamo ndisiye kumulipilira sukulu kuti akwatirane.
Mayi ake Lidia asanamalize kuyankhura Christopher anawadura mau powauza kuti ndi zabodza.
Nkhani inali yobvuta kuti ahead akhulupilire zoti anawa ali pa ubwenzi.
Mayi,,,, mukamabwera kuno muzibwera ndi nkhani ya umboni osati kungoganizira komanso ngati mwana wanu sakuyenda bwino mukuyenera kumulangiza komweko chifukwa kubwera kuno ndi nkhani ngati imeneyi zimatanthauza mukufuna timuchose sukulu mwana wanu.
Iwenso Christopher, ngati ndi zoona kuti uli pa ubwenzi ndi msikanayu uyembekezere kuchosedwa sukulu, kaya zikumveka!!!!.
Christopher anabvomera mau ahead chifukwa sanafune kubvomera kuti ali pa ubwenzi ndi Lidia.
Mayi a Lidia anasanzika kwa a head ndikumapita ndipo mwana wawo sanamusanzike pakuti anali okwiya kwambiri.
Anabwerera mkalasi kumakaphunzira koma ophunzira anzawo anali odabwa ndi kufunidwa kwawo Ku office ya a head.

Masiku amapita, Manuel anapita kwa Aisha kukachenza, inali nthawi imene kumagwa mvula ndipo Manuel ananyowa pofika kunyumbako.
Aisha anamulandira mamuna wake wa nsogoloyo kukalowa nave nyumba ina imene amagona.
Anayamba kuchenza koma ngakhale amachenza, Manuel sanali bwino, amanjenjemera ngati Bango limene lili mmadzi koma malo othamanga madzi kwambiri.
Aisha anatenga ma sikumba ake kumubveka Manuel koma sizinathandize.
Manuel akudwala Ku nyumba ya kwa Aisha, kodi zimuthera bwanji?
Kodi amutengera Ku chipatala?
Search Andy's stories kuti muziwerenga nkhani zambiri.

16/05/2021

WANDITAISA NTHAWI
#£√£√£√£√£√£√£√£√£√
PART 5
Choyamba pangani like page ya Andy's stories kuti nkhani zisamakuphonyeni.
Mu part 4 tinalekeza Lidia akukambirana ndi Christopher, tiyeni tipitilize;
Sindingakhulupilire, ngati ukunena zoona poweruka tikumane kuti tione zosatira.
Mmmm lero lomwe lino, wafulumiratu, chabwino, ndibvomera posafuna kukukhumudwisa.

Lidia anabvomera kukapereka thupi lake kwa Christopher , akuti sakufuna kumukhumudwisa.
Nthawi itakwana anatengana kukakhala malo ena pansi pa mtengo.
Kodi Lidia, wasala ndi K100 ?
Ndili nawo, bwanji ukufuna ugure chani?
Ndipase ndionjezere ndi yanga.
Lidia anaperekadi kenako anamuuza kuti azimulondora.
Atafika malo ena anamuuza kuti ulendowo akukagura room kwa nthawi yochepa malo ena ogona alendo.
Zinachitikadi ndipo anawapasa chipinda.
"Christopher, kunotu akadzi awo amachenza ndi Mayi anga ndiye akandiona akawauza mayi anga".
Lidia kuyankhura atazindikira kuti Christopher anagura room kwa anzawo a mayi ake .
Usadandaure, akupanga business ndiye sangaulure chifukwa kupanga zimenezo akhonza kuthamangisa ma customer.

Mnyamata oyangànira nyumba anamulimbisa mtima kuti sangaulure, analowa mchipinda koma atakhala kwa kanthawi Lidia anamufunsa Christopher ngati watenga mdidi.
Sindinatenge komanso usaiware kuti ndife ana a sukulu ndiye sungatenge mimba.
Mmmm anakuuza ndani kuti sukulu imateteza Ku mimba komanso matenda?
Christopher amayankhura kungofuna kuti zake ziyende osati amanena zoona.
Lidia anabvomereza kupanga zimene amafuna ngakhale sanaziteteze, kenako anaganiza zopita kumudzi koma akuti azituluka anamva mau a mayi make a Lidia kenako anabwerera.
" Chris, mayi anga abwera!!!! paja ndinakuuza kuti amachenza kuno ndiye zitha bwanji?"
Amayankhura akuchita mantha.
"Usadandaure ndipeza njira, ndiyamba ndine kutuluka kenako ndikayankhura ndi mnyamata uja kuti apeze njira yoti utuluke".
Atatuluka anapita kukaonana ndi mnyamata uja, anamuuza kuti asadandaule zitheka.
Anachoka kukaima Ku nsewu, kenako mnyamata uja anawaitana madamu ake kuwauza kuti azikachenza kuseri chifukwa anthu ena amakhala oziwika kuopera kuulura kwa anthu ena.
Madamu aja anapitadi kumakachenza kuseri ndi mayi ake a Lidia.
Lidia anapeza mpata otuluka ndi kukakumana ndi Christopher.

Zitatero chibwenzi chawo chinafikapo polephera kudya akasowana.
Nthawi zambiri mmodzi wa iwo akajomba Ku sukulu, wina samasangalala.
Tsiku lina Lidia analephera phunziro la chingerezi " English " ndipo onse amene analephera anapasidwa chibalo kuti agwire.
Nthawi yoweruka onse amene analephera anasalira ndipo Christopher ataona kuti Lidia wasalira, nayenso anasalira.
"Man Chris, tiyeni tizipita";
Manuel kumuuza Christopher kuti azipita koma iye anakana.
Nzanga ndiye wafika nazo polakwika, ungandiuze zosatira zake?
"Iwee sukudziwa,,,,,,,, akamati chikondi amanena chimenechi, dikira ndikamuthandize chibalo uone.
Ngati zochenza, anapita pamene anali Lidia kuyamba kumuthandiza kulima malo amene anapasidwa.
*Zikatere ndiye chani? ndapereka chibalo kuti agwire cholinga akaona kuphweteka ntchitoyi azilimbikira kuwerenga iwe ndiye ukumuthandiza!!!!!!! mphunzitsi amayankhura ali okwiya kwambiri.
Anamuuza Christopher kuti apite Ku stores kuti akatenge khasu nayenso amupase chibalo.
" Sir mpaka zafika zokatenga khasu?? inetu
ndikangofuna ndimuthandize chifukwa ndikaona Lidia
akubvutika mtima wanga umandiwawa."
Mmalo mokatenga khasu Christopher ananyamuka kumapita ndi Manuel.
Manuel sanayankhure zambiri akangoyenda ndi kufika polekana.

Tsiku lina Aisha anapita kwa Manuel kukamuuza kuti bambo ake abvomera ndipo atha kupita kukakumana nawo.
"Bambo ako kundifuna ine, mmmmm ndakaika,,, sindikufunako".
Manuel anakana kuopa kwawo kwa Aisha.
Anamukakamiza kenako anabvomera kupitako.
Oky, ndibwera mawa.
Mchimwene, wapeza mlamu,, koma ndiyetu amazikolopa komanso kwawo ndi kochita bwino, mulimba?
Manuel kufunsidwa ndi mchemwari wake.
" ndikufuna akhale mkadzi wanga msogolo, mwanji wamukonda?"
Ndamukonda komano ukufunikira kukaonekera kwawo chifukwa anzako atha kukulanda kkkkkkk
Mchemwari wake Brenda kumulangiza Manuel.
"usadandaure ndipitako mawa".

Kutacha asanapite Ku sukulu analawilira kwawo kwa Aisha , atafika anawapeza bambo a Aisha akukonzeka kuti azipita Ku ntchito.
" mnyamata ndakulandira Khala omasuka" bambo ake kumulandira mwa nsangala.
Zikomo kwambiri.
Manuel anapasidwa mpando mwa ulemu kenako Aisha anaitanidwa.
Atafika bambo ake anamuuza Aisha kuti akupanga izi chifukwa amamukonda.
Anamuuza Manuel kuti atha kuzakwatira mwana wawo koma akuyenera amalize Kaye sukulu
Manuel anabvomera ndipo anawathokonza pomumvesa.
ananyamuka kumapita Ku sukulu.

Tsiku lina Christopher anaitanidwa ndi Lidia ndipo anali okhumudwa.
Akufuna kumuuza chani?
Search Andy's stories kuti muziwerenga nkhani zambiri.

13/05/2021

WANDITAISA NTHAWI
#£√£√£√£√£√£√£√£√£√
PART 4

Choyamba pangani like page ya Andy's stories kuti nkhani zisamakuphonyeni.

Mu part 3 tinalekeza Manuel akufuna kuthamangisidwa ndi bambo ake a Aisha, tiyeni tipitilize;
Manuel : ndimudikilira mpaka azamalize.
Bambo ake : Ndikuti sindifuna,,, kapena ukufuna uchoke chothamanga!!kuyankhura
Mau awo amamveka ngati akukangana ndi Manuel.
Nthawi yonseyi Aisha anali kuseri ndi nzake Rhoda.
Atamva kuyankhura anasuzumira ndipo anamuona Manuel akunyamuka kuti azipita koma Aisha anamuimika; chifukwa cha mantha sanaime ndipo Aisha anapita pamene panali bambo ake kukawapempha; " adadi, ndikudziwa mnyamata uja anabwerera ine chifukwa anandiyankhura, mnyamata uja ndamukonda kuti nsogolo muno ndizakhale naye pa banja.
Muloleni kuti ndikhale mu mtendere wa mu mtima."
Zimene anayankhura mwana wawo Aisha sizinawasangalase ndipo anatenga mtengo ndi kumukwapula koma chodabwisa sanathawe.
Anapitiliza kumukwapura koma osathawa moti akadzi awo ndi amene anawagwira ndi kuwalanda mtengo uja.
"Bambo mupweteka mwana taonani sakuthawa ndiye akabvulala muzunzike Ku chipatala ndi inu nomwe.
Anamusiyadi ndi kukakhala pa mpando.
Aisha anapita pomwe anali bambo ake aja ndipo anati; " adadi, mwandimenya thupi lokha koma mtima wanga mwalephera kuthandiza, ngati ndamukonda inunso mukuyenera kumukonda chifukwa sakufuna kundikwatira pano koma ndikazamaliza sukulu, musaiwarenso kuti mayeso sungakhonze uli ndi maganizo ambiri mu mtima.

Zimene anayankhura Aisha zinawamvesa chisoni chifukwa Iwo amalingalira kuti sukulu sungaphatikize ndi mamuna.
Anamuuza kuti aimilire ndipo anaimiliradi, mwana wanga ndiwe wa nzeru kwambiri ndabvomera maganizo ako amene ukufuna, pa zinthu ziwiri usankhepo chimodzi, sukulu kapena banja chimene usankhe ine ndizasatira chomwecho.

Atamaliza kuyankhura anachokapo, Aisha kuti azuke amalephera chifukwa cha ululu. anayamba kulira ndipo nzake Rhoda anapita kukamuzusapo.
Anatengana kupita Ku seri kwa nyumba ndipo nzake Rhoda anamufunsa, "kodi nzanga, bambo ako angakufunire zoipa kapena zabwino?
Funso lake anali kudziwa kuti sangamufunire zoipa koma anamuuza nzake kuti akuyeneranso kudziwa Zimene mtima ukufuna .

Manuel atafika kwawo anaganiza zolowa mnyumba kukagona ngakhale unali usana, anagonadi mpaka dzuwa kulowa.
Makolo ake sanamufunse, anamupasa chakudya cha madzulo.
Kunja kutacha anaganizanso zopita Ku sukulu, ananyamukadi kumapita.
Mayi ake a Aisha anali kudabwa mwana wawo sakudzuka kuti azipita Ku sukulu.
Analowa Ku chipinda chake ndipo anamupeza atafundira mutu ndi miyendo yomwe.
Aisha !!! tadzuka nsanga uzipita Ku sukulu nthawi ikuthatu!!!!!!
Mayi ake kuyankhura mokuwa ngati akukangana naye.
Mmmm amayi ndikumva kuwawa thupi lonse ndiye sindipita.
Mayi ake atamva kuti mwana akudwala anapita kukatenga mankhwala kuzamupasa.
Masiku amapita Aisha asakupita Ku sukulu, tsiku lina anauuza Aisha kuti akambirane naye, atafika anamufunsa chimene waganiza ,banja ndi sukulu usankha chani?
" adadi,,, musaiware kuti ndinakuuzani ndikufuna ndiphunzire koma ndikazamaliza, ndizakwatiwe naye mamunayo."
Bambo ake anaganiza zopanga Zimene akufuna mwana wawo, kamuuze abwere kuti ndikambirane naye.
Bambo ake kumuuza kuti akamuuze Manuel abwere kunyumba kwawo.

Kuyambira tsiku limene Christopher anachoka osafuna kuyankhura kanthu pamene Lidia anamuuza kuti ali ndi wina kale, Lidia amasowa mtendere chifukwa sanayembekezere kuti Christopher amusiya chonchija anayamba kulingalira zokamuuza kuti akangomuyesa amanama zoti ali ndi wina.
Christopher atakumana ndi nzake Manuel Ku sukulu anayamba kukabirana zimene zawachitikira.
"~~Man,,, kwa Aisha kuja ndinachokatu chothamangisidwa.
~~Mukunama,,,,, ndi ndani? kkkkkkkkk
~~Bambo ake ngakhale mkadziyo amandimiika sindinayime kuopa chikwanje.
~~ Anakuyankha chani? kkkkkkkkkk
~~ mwana wawo akufuna aphunzire mpaka Ku college ndiye ine safuna ndimusokoneze
~~ kkkkkk anakuyankha asanalingalire bwino komabe mwina akaganizanso azakuitana.

Nanga inu man ndi Lidia munakambirana zotani, paja simunandiuze?
~~ mmmm basi zitaye, ndinangomuuza ngamo kuti ndamufira akhale wanga koma anakana amvekere; " ndili ndi wina ndiye ndi zobvuta kubvomera, ndinangonyamuka ine kumapita.
~man Chris, akulu anati miseche ilinda mwini, taona kusogoloko.
Pa nthawiyi nkuti Lidia akubwera pamene anaima Manuel ndi Christopher.
~ Chris, tabwera ndimakufuna tikambirane!!!!!!!!!
Lidia kumuitana Christopher koma mwa mantha.
Christopher anakana Kaye pomuuza kuti akuopa kumenyedwa.
Atamukakamiza anapita pamene anaima.

Mau, ako ndinali kuwalingalira monga unanenera, pano ndabvomera.
Ndiye ndingakhulupilire bwanji? poweruka tikhalire limodzi kuti ndikakhulupilire
Mmmmmm Christopher, usatero lero lomwe lino?

Christopher akuti Lidia poweruka asalire koma iye akunyinyilika,
Kodi zitha bwanji?
Search Andy's stories kuti muziwerenga nkhani.
Osaiwara makoment komanso share kwa ena.

12/05/2021

WANDITAISA NTHAWI
#£√£√£√£√£√£√£√£√£√
PART 3

"Ndikakumana naye ndimuuza zonse za kukhosi".
Umuuza ndani? Aisha anafunsa atatulukira pa malopo mosayembekezereka.
Mmmmm ujeni, wafikanso nthawi yanji komanso watenga makope, ukuphunzira kuti?
Manuel, ndakuziizimusatu komamso ukuyankha kwa mantha, anyway ndikupita Ku sukulu.
Inenso ndikupita komweko koma ndimafuna ndidusire kwanu ndikakuone ndiye pakuti takumana ndi bobo basi.

Onse ananyamukira limodzi ulendo wa Ku sukulu, paja ndiwe wa primary muzilimbikiratu kuti muzakhonze.
Aisha kuyankhura ndi Manuel, ndi momodi nanga iwe uli kalasi yanji?
Ndili form 1 , ndiyetu tionana chifukwa ine ndimadusira uku, Aisha atamuuza kuti akusiyana naye, Manuel kukamwa kunamuuma, kuti ayankhure amalephera.
" Manuel ndikuti tionana, bwanji sukuyankha? Aisha kufunsa modabwa.
Ndingakupereke ? " kundiperekera!!!!!! iwetu uli ndi mau, yankhura usamangike.

Chabwino Aisha, ndinakukonda utakhala nzanga tizichenza.
Manuel ati kumeneko kufunsira, inetu sindimachenza ndi anyamata ndiye pepa Manuel.

Kodi ndati kuchenza, ndinalakwisa ndikufuna ukhale chibwenzi changa ndizikuthandiza chimene ukusowa.
Aisha atamva kuti akumufuna chibwenzi anamuyangàna Manuel kwa chidwi kenako anafunsa; " wati chibwenzi? inetu Ndili pa sukulu ndiye zinthu ziwiri sindingakwanise ukanandiuza njira ina osati chibwenzi.
Mau a Aisha anamubalalisa, njira yanji ukunenayo, inetu sindikudziwa ukunenazo.

Mmmmm Manuel sukuziwa,,,,, unamvapo za PTM?
Ayi ndi chipani chanji?
Si chipani, iweyo upite kwathu ukawauze makolo anga kuti ukufuna ndikamaliza sukulu uzandikwatire, akandifunsa ndizakubvomera ndiye iwe uziphunzira Inenso ndikuphunzira, tikazamaliza tizakwatirane basi.
Ndiye ukandibvomera tizikumananso kumbali kumachenza?
Manuel anafunsa pofuna kudziwa, kumbali ayi koma pamaso pa makolo anga komanso sitimakhala kwa tokha kuopera kuganiza zona ngakhalenso poyenda sitingayende awiri opanda wina wa pambali.

Zimene anayankhura Aisha zinali zachilendo kwa iye komabe anabvomera kutero.
Chabwino ndakumva, ndibwera mawa ndikaweruka Ku sukulu.
Anasiyana aliyense kumapita Ku sukulu imene amaphunzira.
Manuel atafika anakumana ndi Christopher nayenso akufika kumene.
"Manuel ameneyo, anzathu ndiye mwauswa ulusi" Christopher kumuyamikira nzake.
Mmmm nzanga wa primary akuchepera, taona timabvalatu kabudura ndiye pamenepo tinganene kuti wauswa?
Komabe ukuoneka bwino, uniform ya sopano komanso nsapato chimodzimozi.
Man, ndinamukonzekera Aisha kuti akandione bho .
Christopher anadabwa za nkhani imene waiyamba Manuel.
Aisha ndiye ndani? Christopher anafunsa.
Wina wake wa form 1 ndipo wabvomera koma akuti ndikaonekere kwa makolo ake ndikawauze kuti ndikufuna ndizamukwatire tikazamaliza sukulu.
Wooow ndi zabho, ameneyo akuoneka kuti ali ndi sogolo, akufuna aphunzire.
Mau amene anayankhura Christopher anamudabwisa, iwe ukugwirizana naye, ndizingocheza naye opanda kupanga chilichonse?
Kupanga chani, zinazi osamathamangira sizimatha, muzapanga nsogolo man, oky ndiye mupita kwawo kapena ndipite ndine?
Manuel anadziwa kuti mkadzi uja anamuuza za nzeru , anabvomera kupitadi kwa Aisha.

Akuchenza nthawi yokalowa mkalasi inakwana, anaphunzira mpaka kuweruka.
Christopher anaiwara zoti anamuuza Lidia kuti akumane koma Lidia sanaiware ndipo atamuona akupita osalabadiranso za iye anamuthamangira kukamupeza.
Lidia ukupita kuti? Christopher anafunsa,
Usandiuze kuti waiwara zoti umandifuna kuti tionane!!!!!!
Ooooh sorry ndinaiwara , Manuel sogola ndikupeza kapena tionana mawa.
Manuel ananyamukadi kumapita.

"Christopher, sindichedwa mayi anga akufuna anditume Ku nsika umandifuniranji?"
Funso la Lidia analiyankha mwa chidure, ndikufuna iweyo ukhale chibwenzi changa.
Lidia anayamba kaye kunyadanyada posafuna kuzitchipisa kuyankha ngati sakufuna,"Mmmm ayi, komanso ndili naye wina ndiye kuti ndivomere pompano Mmmmm ndizobvutirapo.
Christopher atamva mmene anayankhira Lidia sanalimbane naye.
Oky basi ndapita.
Lidia anadabwa ndi mmene anayankhira Christopher chifukwa amayembekezera kuti azimuchonderera koma ayi ndithu, ananyamuka kumapita.
Usapite iwe!!!!!! nanga tathana!!
Sanayangànenso mmbuyo ndipo anayamba kumuthamangira Manuel.
Lidia anaima kwa ka nthawi posamvesa kenako ananyamuka kumapita koma ali okhumudwa kwambiri.

Tsiku losatira Manuel anapita kwawo kwa Aisha nthawi ya Ku masana, atafika anawapeza bamboo ndi mayi a Aisha akuchenza.
Anaodira ndipo anamuyankha, " bwerani pafupi takulandirani".
Atafika anamufunsa chimene wabwerera ndipo anayamba kulongosola;
Manuel: Ine ndabwerera mwana wanu Aisha, ndimafuna chitomero cha banja.
Bambo ake: Chitomero!!! Mmmmm mwana wathu ali pa sukulu tikudikira akakhonza bwino timutumize ku college.
Manuel : Musadandaure ine ndizamudikira mpaka amalize.
Bambo ake : Ndikuti ayi!! kapena ukufuna uchoke chothamanga?

Bambo a Aisha akwiya, kodi zitha bwanji?
Pangani share kuti ena awerenge nawo.
Makoment anu amandilimbikisa.

10/05/2021

WANDITAISA NTHAWI
#£√£√£√£√£√£√£√£√£√£π
PART 2

Choyamba pangani like page ya Andy's stories kuti nkhani zisamakuphonyeni.

"Man Chris, Lidia anandipasira uthenga wanu koma ndinaiwara, amati mukumane kuti akuthokozeni. kapena munayamba kuvaisana Kaye" usandifunse zambiri, tangomuitana basi.
Oky man, Lidia !!!!! iwe Lidia !!!!!! akuti ubwere!!!
Lidia atamva anayambanso kuchita manyanzi.
Anaziyangàna ngati wabvala bwino kenako anawayangàna anzake anali nawo , kenako anayamba kupita pamene anaima Manuel ndi Christopher.
Atafika anapereka moni kwa onse, kenako Lidia anayamba kuyangàna kumbali.
"Ndamva kuti umandifuna, yankhura ndikumva".
Manuel ataona kuti Lidia sakumasuka anaganiza zochokapo.
" Man Chris, paja za kusimba sayankhura pali ana, ine monga mwana ndikupaseni mpata kkkkkkkk" Manuel kuyankhura akuchokapo komanso akuseka.
: ndikuthokoza pa zonse wandichitira posawerengera nyengo imene tadusamo iwe ndi ine, ndikuti zokomo kwambiri.
: Unganditchulire chimene ndakuchitira pofika pothokoza?
: kupanda iwe nwenzi nditachitidwa chipongwe tsiku Lima komanso pondiperekera ngongole imene ikanandipangisa kuti ndiyende mbulanda pamaso pa anthu.
: Ndathokoza pokumbukira kuti ndinakuthandiza, komatu ine sindinafune kuti ndiduse ukuchitidwa chipongwe.
Mmmmmm zoona!!!!! ndiye kuti ndiwe munthu wabwino, komanso sindimayembekezera kuti ndiyankhurana nawe motere, ndimaganiza kuti unditukwana.
: ndikupitatu, ulinso ndi mau ena?
: Ndinakusungira biscuit, chonde landira usandikanire.

Christopher anamuyangàna Lidia kwa ka nthawi kenako anayangàna kumbali.
"Ndathokoza, idya chifukwa ndilibe njala" Christopher anatenga makope awiri ndi zolembera zisanu kumupasa Lidia koma nayenso anakana ponena kuti asamulipire pa zomwe zinachitika kale mu standard 4 chifukwa iye wakhululuka.
"Lidia, inetu sindinakubere cholembera chako, makolo anga amagura makope ndi zolembera zochuluka ndiye chokubera iwe amene umapeza movutikira ndi chani?
Chimene chinandiwawa ndi choti ndinatchulidwa okuba komanso kugwirisidwa chibalo.

Zimene anayankhura Christopher Lidia zinamukhunza mu mtima, " pepa ; kungoti zinali zobvuta kukhulupilira.
Ndiye utenga kapena sutenga? anafunsa Christopher, " nditenga" Lidia anagwada ndi kulandira akumwetulira.
Christopher ataona kuti walandira mwa ulemu nayenso anatemga biscuit uja.
Christopher,,,,, basitu ndapita koma ndimafuna ndikupempheko chinthu chimodzi.
Ukufuna chani?
Ndikufuna usiku wa.lero ukandilote,kkkkkkkk
Lidia ananyamuka akuseka komanso atapereka home work kwa Christopher kuti akakagona akasove.

Inetu ndinadziwa kuti man inu ndi Lidia pali chi frenzo cha kabisira , ndi chifukwa chani monga ine nzako osandiuza?
Manuel anafunsa pomudabwa nzake, "ayi man, palibe means iliyonse.
Anasiyana aliyense kumapita kwawo.

Masiku amapita, tsiku lina Lidia anakumana ndi Christopher mu nsika wa Lilongwe.
Atamuona Lidia anali osangalala naye, Maganizo omufunsira anamubwerera koma pakuti munali mu nsika analephera kulankhura.
"" Christopher, ndinakuuza kuti ukandilote, bwanji unandilota?"
Lidia kumufunsa, "ayi koma ndinalota mayi ako akundithamangisa ndi chikwanje".
Nthawi zina kumakhalako serious, mayi anga sukuwaziwa.

Ndikuwadziwa ndinakumana nawo Ku turo kkkkkkkkkk.
Christopher akuchenza ndi Lidia , Christopher anamuuza Lidia kuti mawa asalephere Ku sukulu pali zoti akamufunse.
Oky sindilephera ndibwera.

Manuel bambo ake anamutuma kogura thumba la cement, analisenza pa mutu kumabwerera kunyumba.
Atafika malo ena anaterereka ndi kugwa.
" Pepani achimwene, kungoti misewu kwathu kuno sili bwino, anapita kukamulandira thumba lija koma atafika malo ena anamubwezera ndikumuuza kuti wafika kwawo.
Ndathokoza pondilandira, ine ndi Manuel ndimakhala pasogolopo.
Zikomo, ine ndi Aisha ndimakhala nyumba iyo pamodzi ndi makolo anga.
Anasanzikana iye kumapita.

Bambo a Manuel, bwanji munamutuma mwana kogura cement ulendo wa pansi?
Mayi ake kuwafunsa amuna awo,
"Ameneyo ndi mwana wa mamuna, anzake akunyamura matumba mtawonimu sakuwaona ndiye akalephere kunyamura pamutu kkkkkkkk".
Mmmm bambo musatero, ndisanaiware, kumudzi akuti mvula yagwa ndiye ndalama ikufunika kutumizidwa nsanga kuti akagure fertilizer.
Ali mkati mokambirana Aisha anafika Ku nyumba kuja, ndimafuna Manuel ndimupasire envelope yake anagwesa pamene anagwesa thumba la cement.
Zimene anayankhura Aisha zinapangisa mai ake Manuel abwerezenso mau omwe aja.
" Mwazimveratu nokha, ziwapasani anawa katundu wa nsikhu wawo ."
Manuel anapita kukatenga envolope ija kwa Aisha.
"wandipasira ndi msikana amene amabwera mmbuyo mwathu. uja."

Ndathokoza Aisha, ndikanakonda mawa tizachenze limodzi ukuti bwanji?
Oky mawa lomwero tiona.
Aisha ananyamuka kumapita kwawo koma akulingalira mau a Manuel, "akuti mawa tichenze!!!!!!! ndinalakwisanso kukamupasa envolope yake eti?
Aisha kuziyankhulira yekha.

Manuel anagwa mchikondi mmaganizo okha ndi Aisha.
Tsiku losatira Manuel ananyamuka kupita kusuku, atafika malo ena anaganiza zoyamba wazera kwawo kwa Aisha cholinga akamuona amuitane.
Atafika malo ena Manuel anayamba kuzilankhulira yekha.

Ndikamupeza ndikamuuza mau onse akukhosi.
Ukamuuza ndani Manuel?
Uyu anali Aisha kutulukira pa malopo ndipo Manuel choti ayankhure chinamusowa.

Kodi ayankha chani?
Search Andy's stories kuti muziwerenga nkhani zambiri.

09/05/2021

WANDITAISA NTHAWI
#£√£√£√£√£√£√£√£√£√

PART. 1

Nkhani yolembedwa ndi Andrew,
Choyamba pangani like page ya Andy's stories kuti nkhani zisamakuphonyeni.

Christopher, ukupanga chani ?
"Sir ameneyu ndi nzanga ndiye ndikumuthandiza".
Mzako, walephera mkalasi ndiye ndamupasa chilango choti athilire maluwa iwe uli pano kumati " Sir ameneyu ndi nzanga" thats no sense.
Dikira ndikuuze, chilango timafuna kuti aphunzire kulimbikira kuti asamalakwe koma iwe kumati uzimuthandiza chibalo, ameneyu azakulira msogolo akazalephera mayeso.

Uyu anali mphuzitsi wa English kuyankhura mokwiya Christopher akumuthandiza Lidia chibalo Ku sukulu.
Atamaliza kuyankhura anamuuza Christopher kuti akatenge khasu Ku stores nayenso amupase ntchito kuti azigwira chifukwa zikuoneka kuti zikumusangalasa.
"kkkkkkk koma sir !!!!!! ndalakwanso chani inetu ndikamuona Lidia akugwira ntchito ndimakhala ndikumumvera chisomo, sikuti zimandisangalasa ayi".
Christopher kunenerera atamva kuti nayenso akufuna kumupasa chibalo.

Christopher ndi mnyamata amene wakulira Ku Lilongwe ndi Makolo ake.
Wakhala akuphunzira sukulu ndi Lidia kuyambira standard 4 mpaka 8.
Makolo a Christopher bambo ake ndi a polisi pamene Lidia amakhala ndi mayi ake koma amapanga business mu nsika wa Lilongwe.
Makolo ake a Lidia samasangalala akamaona mwana wawo akuchenza ndi anyamata.
Lidia ndi Christopher kuyambira standard 4 kufika standard 7 anali pa udani waukulu, samaonerana kukondwa akakumana.
Chinayambisa udani ndi kuberana kwa cholembera ali mu standard 4 .
Christopher ndi amene anatchulidwa kuti waba cholembera cha Lidia pa nthawi imene ana onse anali pa break.
Atalowa ndi pomwe anazindikira kuti cholembera chake mulibe, " Sir, cholembera changa mulibe mmakope anga, zikuonesa kuti alipo wandibera".
Aphunzitsi atamva kuti Lidia waberedwa cholembera anawauza ana onse kuti ayimilire.
Analamula leader wa mamuna kuti aseche amuna anzake pamene leader wa mkadzi asechenso akadzi anzake.
Amene anaba uja anachibisa mmakope a Christopher kuopa kugwidwa.
Mwa tsoka chinapezeka mmakope a Christopher. ngakhale amakana sizinathandize.
Ana anzake anamukuwiza kuti wakuba, anauzidwa kuti poweruka asalire.
Nthawi yoweruka anamupasa chibalo chosesa pa sukulu ponse.
Ngakhale amagwira samasangalala chifukwa sanabe ngakhale palibe anamukhulupilira.
Christopher akamuona Lidia samasangalala naye pochitisa kuti agwire chibalo komanso Lidia anali kumuda Christopher chifukwa chomubera cholembera.
Udaniwu unapitilira mpaka mu 7, tsiku lina Christopher akuchokera Ku msika anamupeza Lidia akumenyedwa ndi anthu osaziwika, sanawerengerenso kuti pali udani koma anapita pomwepo kukawamenya amene anali kumumenyawo.
Onse anathawa chifukwa cha zibakera za Christopher, mnyamata wa mphabvu.
Anthu aja atathawa Christopher sanamuyankhurenso Lidia, anangonyamuka kumapita.
Anamusiya Lidia atangoima kudabwa naye Christopher posamufunsa chimene amamumenyera.

Lidia atafika kwawo anawalongosolera mayi ake zimene zinamuchitikira, "unawaputa chani anthuwo?"
Mayi ake anamufunsa.
Palibe amayi, ndinadabwa atandigwira kuti andinyamure andilowese pa tchire ndiye ine polimbana nawo ndinamuthira mchenga mmaso winayo lenako anzake anayamba kundimenya.
Ndithokoze Christopher pofika msanga pa malopo chifukwa akanandipweteka.

Tsiku losatira Lidia anatenga biscuit kuti akamupase Christopher chifukwa chomupulumusa koma atafika Ku sukulu anadabwa nthawi ikupita Christopher sakubwera, analowa mkalasi mpaka kuweruka osamuona.
"Manuel, nzako Christopher sanabwere chabvuta ndi chani?"
Lidia kumufunsa anzake amene amachenza naye kwambiri.
"Sindikudziwa komanso usaiware kuti timachokera madera osiyana ndiye ndi kobvuta kudziwa chimene chamubvuta."
Ndayambatu kukudabwa Lidia sumayankhurana ndi Christopher ndiye lero kumati wamusowa.
Manuel kumudabwa Lidia koma iye sanayankhe ananyamuka kumapita kwawo asakusangalala.
linali tsiku la chisanu ndipo kuti lifike lolemba kumamutalikira kuzakumananso ndi Christopher.

Tsiku la mulungu akuchokera Ku Church anakumana ndi msikana wina amene anamungongola ndalama koma akamuona amamuthawa koma pa sikuli kuthawa kunakanika.
Anamuuza kuti apereke ndalama koma iye analibe.
Anzake a msikana uja anamuuza kuti asamunyengerere, akuyenera kulipira kapena amubvure zobvala.
Christopher anali kumva ngakhale anali patali.
Atafika anamumvera chisoni chifukwa amalira, "asikana inu, nzanu mwamutani" Christopher anafunsa, anatenga ndalama yanga koma sakundipasa.
Ndalama zingati?
K500 koma sakundipasa.
Ndalama yako iyi ndipo musiye azipita.
Christopher analipira ndalama ija iye kumapita.
Lidia analibe mau ataona kuti Christopher sanayankhure kanthu.
Usiku onse mmalo mowerenga notes akangoganiza za Christopher.
Kutacha Lidia anapita kusukulu kuti akakumanenso ndi Christopher.
Zinali zobvuta kuganiza chifukwa sanabwerenso.

Masiku amadusa Lidia osakumana ndi Christopher, tsiku lina Christopher atapita Ku sukulu anakumana ndi Lidia , Lidia atamuona anayamba kumwetulira koma Christopher sanali moseka ndi munthu.
"Manuel, ukadiuzireko Christopher kuti ndikufuna ndionane naye kuti ndimuthokoze.
" Wati umuthokoze!!! kodi anthu inu mukupangana zotani? anyway ndimuuza kuti mukumane poweruka si choncho, .kkkkkkkkkkkkk ukamupasetu chocolate osamusiya chonchotu kkkkkkkk.
Zinayankhura Manuel sindinamuyankhe, poweruka ndinamuona Christopher ali ndi Manuel akupita kwawo.
Atamuona Lidia anakumbukira uthenga wake.
"Man Chris , Lidia anandipasira uthenga wanu koma ndinaiwara, akuti mukumane naye akufuna akuthokozeni".
Kapenatu munayamba kuvaisana naye?
Usafuse zambiri ungomuuza abwere basi.
Ok man, Lidia!!!!!!!!!!! iwe Lidia!!! akuti ubwere!!
Lidia atamva kuti apite anayambanso kuchita manyanzi.

Kodi Lidia apitadi , zonse zili mu part 2
Makoment anu amandilimbikisa.

Andy's stories kuphunzitsa komanso kukusangalasani.

Address

Zomba

Opening Hours

Monday 09:00 - 17:00
Saturday 09:00 - 18:00

Telephone

+265994466481

Website

Alerts

Be the first to know and let us send you an email when Andy's stories posts news and promotions. Your email address will not be used for any other purpose, and you can unsubscribe at any time.

Share

Category