YONECO FM

YONECO FM YONECO FM is a page for YFM Radio Station that was established in October 2014 to educate, inform and entertain youth, women and children. 0998570456

TO ADVERTIZE on YFM Radio Call: 0882000302
[email protected]

YONECO FM is a page for Youth Net and Counselling (YONECO) Youth Radio station. Its aim is to educate, entertain and provide information on issues that affect youth, women and children in Malawi. YFM is the real voice of youth, women and children in Malawi. YFM is on 103.8 Mhz in Zomba, 101.6 Mhz in Blantyre, 97.5 Mhz in Lilongwe, 103.9 Mhz in Mzuzu, 104.6 Mhz in Thyolo and 89.1 Mhz in Chitipa. [email protected]

  Katswiri pa nkhani za ulimi a Felix Jumbe ati dziko lino silikuyenera kumadalira kugula chimanga kuchokera ku mayino a...
03/09/2025


Katswiri pa nkhani za ulimi a Felix Jumbe ati dziko lino silikuyenera kumadalira kugula chimanga kuchokera ku mayino akunja chifukwa lili ndi zinthu zonse zofunika kuti likhale lodziyimira pawokha pa nkhani ya ulimi.

Iwo ananena izi bungwe la Admarc litalengeza kuti likufuna kugula chimanga chochuluka cha matani 200,000 kuchokera kumayiko ena.

A Jumbe ati ngakhale cholinga chogula chimangachi sicholakwika popeza dziko lakhala ndi zokolola zochepa poyerekezera ndi ena, zimasonyeza kuti dziko lino likupitilira kulephera kugwiritsa ntchito mwayi wa ulimi wamthilira.

Iwo ati ngakhale boma lakhala likugawa ndalama kwa alimi ena kuti achite ulimiwu, sizikudziwika momwe ndalamazi zathandizira.

A Jumbe ati boma liyenera kupeza akatswiri odziwa bwino ulimi kuti atsogolere mapulojekiti osiyanasiyana okhudza ulimi pofuna kuti Amalawi azitha kupeza feteleza mosavuta komanso motsika mtengo.

Wolemba: Peter Davieson

  Barely a few weeks after the Ministry of Natural Resources and Climate Change launched Carbon Market Framework, the mi...
03/09/2025


Barely a few weeks after the Ministry of Natural Resources and Climate Change launched Carbon Market Framework, the ministry has signed a carbon market trade agreement with the United Arab Emirates-based company, Green Economic Partnership (GEP) to undertake a carbon emission project in the country.

In his remarks after signing in ceremony on Tuesday, the line minister, Dr Owen Chomanika, said the company will conduct its operations at Namizimu Forest Reserve in Mangochi district, a forest which has 37,000 hectares and will be able to produce 12 million tonnes of carbon.

He further said that over 21 million trees are expected to be planted by the company before starting the operations.

Meanwhile, Chief Executive Officer for GEP, Arthur Chirkinian, has disclosed that they are planning to implement the project in various forest reserves, as Malawi has a conducive environment and abundant resources for trade.

Commenting on the development, an environmental activist Mathews Malata said "it's not the face value of these agreements that matters but the substance beneath."

Carbon Trade is a sustainable environmental initiative that aims to mitigate carbon emissions through reforestation and foster environmentally friendly practices.

It generates revenue for participating countries.

By Smart Sochela (Blantyre)

  Yemwe akupikisana nawo pa mpando wa phungu wa Nyumba ya Malamulo mdera la Zomba Mtonya a Hashim Abbasi a chipani cha M...
02/09/2025


Yemwe akupikisana nawo pa mpando wa phungu wa Nyumba ya Malamulo mdera la Zomba Mtonya a Hashim Abbasi a chipani cha Malawi Congress (MCP), apereka mankhwala pa chipatala cha Chanda m’bomali.

Polankhula pamwambo opereka mankhwalawo, a Abbasi anati achita izi chifukwa cha mavuto omwe awaona pachipatala cha Chanda, ponena kuti ndi mzika ya muderali motero akumva kufunika kothandiza.

Iwo anenanso kuti, ngati adzasankhidwe pa zisankho za pa 16 September, ndi okonzeka kumanga sukulu zabwino komanso kukonza misewu ya m’derali.

Mkulu wa alangizi pa chipatalachi, a Joseph Matebule, anati ngakhale chipatala cha Chanda chatsegulidwa posachedwa, chimakumana ndi mavuto a matenda monga likodzo, zipere komanso malungo.

Iwo ati kubwera kwa mankhwala a Albendazole ndi gawo lofunika pothandiza kuthana ndi ena mwa matendawa.

Ena mwa mankhwala omwe aperekedwa ndi a multi vitamin omwe amathandiza kwambiri amayi apakati.

Chipatala cha Chanda chimathandiza anthu pafupifupi 19,000 a m’madera ozungulira ngakhale chili chaching'ono kwambiri.

Wolemba: Temwa Tembo (Zomba)

 Apolisi m’boma la Zomba adzudzula mchitidwe wa anthu otengera malamulo m’manja mwao, ponena kuti malamulo ayenera kugwi...
02/09/2025


Apolisi m’boma la Zomba adzudzula mchitidwe wa anthu otengera malamulo m’manja mwao, ponena kuti malamulo ayenera kugwira ntchito kwa aliyense mwa njira zovomerezeka.

Chenjezo ili labwera kutsatira imfa ya a Frank Masiye, azaka 47, omwe aphedwa ataganiziridwa kuti anaba foni.

Malinga ndi mneneri wa Polisi ya Zomba, a Patricia Sipiliano, a Masiye anavulazidwa ndi anthu asanatenthedwe ndi moto, zomwe zinachititsa kuti afe.

Apolisi anatengera thupi lawo ku chipatala chachikulu cha Zomba, komwe adokotala adatsimikizira kuti imfa yawo inachitika chifukwa cha mabala a moto.

A Sipiliano ati apolisi akupitiliza kafukufuku kuti apeze onse omwe anatenga mbali pa chiwembucho.

Wolemba: Peter Davieson (Zomba)

02/09/2025


Bungwe lolimbikitsa kulimbana ndi nthenda ya khansa mdziko muno, la Cancer Survivors Quest, lati dziko lino likusalirabe pa ntchito yolimbana ndi khansa yokhudza ana.

Mkulu wa bungweri a Chikhulupiliro Ng’ombe, ati nkhani zokhudza ma uthenga a nthenda ya khansa zomwe zimakambidwa kawirikawiri zimakhala zokhudza amai ndi abambo koma ana amasalidwa.

A Ng’ombe anena izi pomwe mwezi uno wa September unakhazikitsidwa kuti pa dziko lapansi mayiko azikumbukira ndikulimbikitsa mawuthenga okhudza nthenda ya khansa yomwe imakhudza ana.

Choncho iwo ati pakufunika kuti dziko lino ligwiritse ntchito mweziwu polimbikitsa mawuthenga ophunzitsa za nthendayi yomwe potengera chiwerengero cha chaka chatha mu zipatala za QECH ku Blantyre, ndi Cancer Centre ku Lilongwe, ana opyola 200 ndiwo anapezeka ndi nthendayi.

Malingana ndi bungwe la za umoyo pa dziko lonse, la WHO, ana pafupifupi 400, 000 ndiwo amapezeka ndi nthenda ya khansa chaka chirichonse ndipo 90 mwa ana 100 aliwonse pa chiwerengerochi amapezeka m’mayiko osawuka.

Mitundu ya khansa yomwe imagwira ana kawirikawiri ndi khansa ya magazi (Leukaemia), mitsempha (Lymphomas), komanso ubongo ndi msana (Central Nervous System Tumor).

Wolemba: Smart Sochela (Blantyre)

 Households in Traditional Authority Chikowi in Zomba have commended the Financial Access for Rural Markets, Smallholder...
01/09/2025


Households in Traditional Authority Chikowi in Zomba have commended the Financial Access for Rural Markets, Smallholders and Enterprises (FARMSE) program for improving access to financial services and transforming livelihoods.

Implemented by DAPP, the initiative is part of the Poverty Reduction for Vulnerable Beneficiaries and Small-Scale Enterprises Development (PROVED) project, supported by the Malawi Government, IFAD, and the private sector.

The project targets poverty reduction and economic empowerment in rural areas and has so far reached 150 Village Savings and Loan Associations (VSLAs) across Traditional Authorities Chikowi, Mlumbe, and Kumtumanje.

Speaking to YFM, Secretary for Umodzi Ching’oma VSLA, Gladys Nyirenda, said the project has empowered members economically, enabling them to start small-scale businesses and support their households.

In his remarks, FARMSE Zomba District Coordinator, Prince Lwanda, expressed satisfaction with the project's impact and revealed that efforts are underway to scale up and reach more beneficiaries.

By Alinafe Nyasulu (Zomba)

 Ngati njira yothana ndi kugulitsa komanso kusunga mafuta mosaloledwa, apolisi m’boma la Zomba amanga a Lifred Wyson, az...
01/09/2025


Ngati njira yothana ndi kugulitsa komanso kusunga mafuta mosaloledwa, apolisi m’boma la Zomba amanga a Lifred Wyson, azaka 40, chifukwa chopezeka ndi malita 300 a mafuta a mtundu wa petrol popanda chilolezo .

Mneneri wa apolisi ku Zomba, a Patricia Sipiliano, ati oganizilidwayu wapezeka ndi mafutawo m’dera la Jenala, antghu ena atawatsina khutu.

Wolemba: Peter Davieson (Zomba)

 Mpingo wa Seventh Day Adventist (SDA) m'chigawo chakummawa wakhazikitsa wayilesi ya pa intaneti yotchedwa EMC Online Ra...
01/09/2025


Mpingo wa Seventh Day Adventist (SDA) m'chigawo chakummawa wakhazikitsa wayilesi ya pa intaneti yotchedwa EMC Online Radio "Liwu la Anzeru Akummawa", ndi cholinga chofalitsa uthenga wa chiyembekezo kwa anthu ambiri.

Polankhula pa mwambo wokhazikitsa wayilesiyi, mtsogoleri wa mpingowu m’chigawo chakummawa, m'busa Dr. Sanned Lubani, ati akuyembekeza kuti kudzera mu wayilesi iyi adzafikira achinyamata ambiri, Amalawi amene ali m’dziko muno komanso omwe ali kunja, ndi uthenga wopereka chiyembekezo.

Iwo atinso, wayilesiyi izipereka maphunziro a Baibulo, komanso mapulogalamu m’zilankhulo zosiyanasiyana kuphatikizapo Chiyao, kuti ifikire anthu ambiri m’chigawochi.

Kumbali yake, mkulu owona zachuma za mpingowo, a Evison Dambula, ati m’chigawo chakummawa chiwerengero cha Akhristu ndi chochepa poyerekeza ndi madera ena, ndipo malo ena ndi ovuta kufikako kapena kukhazikitsa mipingo.

Komabe, iwo ati kudzera ku wayilesiyi, mpingowo wapeza njira yosavuta yofikira madera onse.

Wolemba Peter Davieson (Zomba)

  Anthu okhala m’dera la Namalaka m’boma la Zomba ati ali pachiwopsezo cha matenda otsegula m'mimba kutsatira kuphulika ...
31/08/2025


Anthu okhala m’dera la Namalaka m’boma la Zomba ati ali pachiwopsezo cha matenda otsegula m'mimba kutsatira kuphulika kwa suweji yomwe tsopano yatha sabata limodzi isanakonzedwe.

Polankhula ndi YFM, a Magret Sikweya anati vutoli si latsopano koma khonsolo ya mzindawu ikulephera kubweretsa yankho lokhazikika.

“M’dera muno suweji ikaphulika, zimatengeka nthawi kuti khonsoloyi izabwera kukonza. Zimenezi zimayika umoyo wathu pachiswe chifukwa madzi akusuwejiyi amayenda kudutsa ngakhale m’makomo mwa anthu,” atero a Sikweya.

Iwo anenanso kuti anakafikitsa nkhaniyi kwa atsogoleri a m’mudzi kupempha kuti apange lipoti ku khonsolo, koma akadali kuyembekezera yankho.

Wolemba: Peter Davieson

  Anthu okhala mmadera a Kamwendo ndi Sunuzu ati ali ndi nkhawa chifukwa cha kuonongeka kwa mlatho wa Mwanga womwe wagum...
31/08/2025


Anthu okhala mmadera a Kamwendo ndi Sunuzu ati ali ndi nkhawa chifukwa cha kuonongeka kwa mlatho wa Mwanga womwe wagumuka kwambiri.

Mlathowu ndiwo umalumikiza msewu wa phula wochokera ku Zomba kudutsira kwa Jali, pa boma la Phalombe mpaka ku Chitakale m'boma la Mulanje.

Ena mwa anthu omwe amagwiritsa ntchito msewuwu, awuza YFM kuti akudandaula kwambiri chifukwa cha nyengo ya mvula yomwe ikuyandikira.

“Monga momwe mukuonera, msewu ukukumbika kuyambira pansi ndipo mlatho ukuyamba kuwonongeka pang’ono pang’ono. Sitikudziwa zimene zidzachitike mvula ikayamba kugwa,” adatero mmodzi mwa iwo.

Wolemba: Temwa Tembo (Zomba)

  Bungwe la Malawi Electoral Commission (MEC) lati pa chisankho cha chaka chino lidzagwiritsa ntchito makina apadera omw...
31/08/2025


Bungwe la Malawi Electoral Commission (MEC) lati pa chisankho cha chaka chino lidzagwiritsa ntchito makina apadera omwe adzathandize kuzindikira ngati munthu wavota kale komanso ngati analembetsa ku malo omwe akufuna kuponyeramo voti.

Mneneri wa MEC, a Sangwani Mwafulirwa, ati makina amenewa adzachepetsa mavuto omwe ankachitika m’zaka zapitazi, makamaka kwa anthu amene ankayiwala kapena kutaya ziphaso zawo zovotera.

Iwo ati makina akulolanso munthu kuponya voti pogwiritsa ntchito chala, motero adzazindikira ngati ali pa m’ndandanda wa olembetsa kapena ayi.

A Mwafulirwa ati cholinga cha makinawa ndi kuthandizira kutsimikizira yemwe ali ndi ufulu wokhawo wovota, komanso kuletsa achinyengo.

Iwo anenanso kuti zambiri zomwe Amalawi anasindikiza panthawi yolembetsa mu kaundula wa voti ndizo zomwe zidzagwiritsidwe ntchito pofananitsa patsiku lomwe anthu adzaponye voti.

Wolemba: Peter Davieson

  Gulu la Friends of Chiradzulu lapereka thandizo la katundu wosiyanasiyana wa ndalama zokwana K1.2 miliyoni kwa odwala ...
30/08/2025


Gulu la Friends of Chiradzulu lapereka thandizo la katundu wosiyanasiyana wa ndalama zokwana K1.2 miliyoni kwa odwala a pa chipatala chachikulu cha Boma la Chiradzulu.

Polankhula pa mwambowu, wapampando wa gululi a Henry Alex Makondetsa anati ndi okondwa kuti atha kufikira odwala 18 ndi thandizo limeneli.

M’modzi mwa odwala omwe alandira thandizoli, a Vincent Yohane, ayamikira gululi, ponena kuti panopa zikuvuta kugula zinthu zofunika chifukwa cha mmene mitengo ya katundu ikukwerera mdziko muno.

Si koyamba gululi kupereka chithandizo ngati ichi, chifukwa mchaka cha 2019 gululi lidachitanso chimodzimodzi pa chipatalachi.

Wolemba: Temwa Tembo

Address

Youth Net & Counselling (YONECO)
Zomba
471

Telephone

+2651526199

Website

http://www.yonecofm.com/

Alerts

Be the first to know and let us send you an email when YONECO FM posts news and promotions. Your email address will not be used for any other purpose, and you can unsubscribe at any time.

Contact The Business

Send a message to YONECO FM:

Share

Category