
03/09/2025
Katswiri pa nkhani za ulimi a Felix Jumbe ati dziko lino silikuyenera kumadalira kugula chimanga kuchokera ku mayino akunja chifukwa lili ndi zinthu zonse zofunika kuti likhale lodziyimira pawokha pa nkhani ya ulimi.
Iwo ananena izi bungwe la Admarc litalengeza kuti likufuna kugula chimanga chochuluka cha matani 200,000 kuchokera kumayiko ena.
A Jumbe ati ngakhale cholinga chogula chimangachi sicholakwika popeza dziko lakhala ndi zokolola zochepa poyerekezera ndi ena, zimasonyeza kuti dziko lino likupitilira kulephera kugwiritsa ntchito mwayi wa ulimi wamthilira.
Iwo ati ngakhale boma lakhala likugawa ndalama kwa alimi ena kuti achite ulimiwu, sizikudziwika momwe ndalamazi zathandizira.
A Jumbe ati boma liyenera kupeza akatswiri odziwa bwino ulimi kuti atsogolere mapulojekiti osiyanasiyana okhudza ulimi pofuna kuti Amalawi azitha kupeza feteleza mosavuta komanso motsika mtengo.
Wolemba: Peter Davieson