YONECO FM

YONECO FM YONECO FM is a page for YFM Radio Station that was established in October 2014 to educate, inform and entertain youth, women and children. 0998570456

TO ADVERTIZE on YFM Radio Call: 0882000302
[email protected]

YONECO FM is a page for Youth Net and Counselling (YONECO) Youth Radio station. Its aim is to educate, entertain and provide information on issues that affect youth, women and children in Malawi. YFM is the real voice of youth, women and children in Malawi. YFM is on 103.8 Mhz in Zomba, 101.6 Mhz in Blantyre, 97.5 Mhz in Lilongwe, 103.9 Mhz in Mzuzu, 104.6 Mhz in Thyolo and 89.1 Mhz in Chitipa. [email protected]

  Yemwe akufuna kuzayimira ngati phungu wakunyumba yamalamulo woyima payekha mdera la Zomba Changalume a Golden Galeza a...
19/07/2025


Yemwe akufuna kuzayimira ngati phungu wakunyumba yamalamulo woyima payekha mdera la Zomba Changalume a Golden Galeza apempha achinyamata omwe analembetsa mukawundula kuti akaponye voti mwaunyinji pachisankho chikubwerachi.

Iwo ayankhula izi pa mkumano omwe anayitana achinyamata ndikuwagawira mfundo zomwe azachite akazapambana pa chisankho.

Iwo anati achinyamata akuyenera kukhala patsogolo pokavota kuti zinthu zisinthe ponena kuti chiwelengero chochuluka mdziko muno ndi cha achinyamata poyelekeza ndi amayi komanso abambo.

Mmawu ake, woyimira achinyamata kudelari a Idrissa Malenga anati achinyamata ambiri amangogwiritsidwa ntchito ndi andale koma akasankhidwa saganizira mavuto awo.

Iye anati pali ntchito zambri zomwe achinyamata angagwire zotukula dera koma zimangosowekera upangiri wa atsogoleri amasomphenya kuti ntchitozi zipite patsogolo.

Wolemba Peter Davieson

 Mkulu wa khonsolo ya mzinda wa Zomba a ArchAngel Bakolo ati kukula kwa mzindawu ndi vuto lalikulu lomwe khonsoloyi ikuk...
18/07/2025


Mkulu wa khonsolo ya mzinda wa Zomba a ArchAngel Bakolo ati kukula kwa mzindawu ndi vuto lalikulu lomwe khonsoloyi ikukumana nalo maka pa nkhani zakusintha kwa nyengo kuchepa kwa ndalama kuti zifikire zinthu zosiyanasiyana zomwe anthu amagwilitsa ntchito pa umoyo watsiku ndi tsiku.

Izi zayankhulidwa pa mkumano omwe khonsoloyi inakonza ndi cholinga chofuna kuwunikirana nkhani zosiyanasiyana zachitukuko mu mzindawu.

Iwo anati kukula kwa mzindawu kwapangitsa khonsoloyi kuwoneka yolephera kutumikira nzika zake moyenera kamba kakusowekera kwa chuma chochuluka kuti chifikire magawo onse.

A Bakolo anatinso ngakhale zovuta zili chonchi khonsoloyi yakwanitsa kuthana ndi mchitidwe ogulitsa malonda mwachisawawa, kukweza chuma chomwe khonsoloyi yakhala ikutolera kuchoka pa 700 million kufika pa 1.2 Billion zomwe zikuwonetsa kukwera kwa nkhani zachitukuko m'bomali.

Mmawu ake Khansala wa dera la Masongola a Anthony Gonani yemwenso ndi wachiwiri kwa mfumu ya mzinda wa Zomba anati kuchoka mchaka cha 2019 pomwe anasankhidwa kutumikira mipando yosiyanasiyaa akwanitsa kukweza malipiro a ogwira ntchito, kutukula nkhani za umoyo komanso kumanga nyumba zochitira malonda zamakono mu mzindawu.

Wolemba Peter Davieson

18/07/2025


Khonsola ya mzinda wa Zomba yati ntchito yotolera misonkho mu zaka zisanu zapitazi yakhala yapamwamba kwambiri poyerekeza ndi mu chaka cha 2020 pomwe khonsoloyi idali itangokhazikitsidwa chakumene.

Khonsoloyi ikumatolera ndalama pafupifupi K1.2 billion za msonkho pa chaka pomwe mu chaka cha 2020 chokha, khonsoloyi idatolera ndalama zokwana K700 million yokha basi za msonkho.

Poyankhula pa mkumano wotsiriza pomwe dziko lino likuyembekezera zisankho, mkulu wa Ku khonsolo ya mzinda wa Zomba, a Archangel Bakolo, anati mkumanowu unakonzedwa pofuna kukambirana ndikuunikilana zina mwa zomwe khonsoloyi yakwanitsa kuchita pomwe khonsoloyi ikuyembekeza kuthetsedwa pa 24 July chaka chino mwa malamulo.

Mu zaka zisanu zapitazi, khonsoloyi yakwanitsa kumanga zipinda zophunzilira ana pa sukulu ya Ndangopuma ndi Matiya, kumanga mlatho wa Njonjo - Matawale, kumanganso Nsewu wa Chinamwali - M'delemani, ndipo aphunzitsi oposera 300 akwezedwa ma udindo mumzindawu mongotchulapo zochepa zabe.

Wolemba Temwa Tembo

Bwalo la milandu la Magistrate munzinda wa Blantyre, lagamula sing'anga wa zaka 27 Layton Juma kuti akakhale kundende za...
18/07/2025

Bwalo la milandu la Magistrate munzinda wa Blantyre, lagamula sing'anga wa zaka 27 Layton Juma kuti akakhale kundende zaka 14 pa mulandu obera anthu ndalama mwachinyengo komanso zaka zisanu pa mulandu ogwililira mai wina.

Malingana ndi m'neneri wa polisi ya Ndirande Chibisa Mulimbika, pa mulandu okuba ndalama mwachinyengowu, akuti pa 26 June chaka chino mkuluyu anatenga ndalama zoposa K1 million kuchokera kwa anthu awiri kudera la Ndirande powawuza kuti awachulukisira ndalamazi kudzera m'matsenga.

Mulandu wachiwiri omwe ndiwogwililira, akuti unachitika mchaka cha 2023 pomwe mkuluyu anawuza mai wina ochokeranso ku Ndirande kuti agwiritsa ntchito mankhwala azitsamba pomupezera lamya yake ya m'manja yomwe panthawiyo inali itasowa.

Sing'angayu akuti anatenga njoka ndikuyizungulitsa mukhosi la mai yu ndipo kenaka anamugwirililira pomuwopsyeza kuti akangoyerekeza kukana ndiye kuti njokayo imuluma.

Komatu sing'angayu sanathere pomwepa ndipo anatenganso katundu wina wa m'nyumba wa mai yu kuphatikizapo zovala zomwe pamodzi zinali za ndalama zokwana K1, 500,000.

Layton Juma yemwe amagwira ntchito yake ya using'anga m'boma la Balaka, ndiwochokera m'mudzi mwa Saitikadzuwa mfumu yayikulu M'baluku m'boma la Mangochi ndipo zaka zomwe amugamula pa milandu iwiriyi asewenzera pakamodzi.

Wolemba Smart Sochela (Blantyre)

18/07/2025


Pafupifupi mabanja 17,000 omwe ndi ovutikitsitsa m’boma la Zomba, akuyembekezeka kupindula kudzera mu ndondomeko ya Mtukula Pakhomo.

Izi zadziwika pa mkumano omwe khonsolo ya boma la Zomba idachititsa m’mudzi mwa mfumu yaikulu Machilinga, m’boma la Zomba omwe cholinga chake chidali kudziwitsa anthu za momwe ndondomekoyi ikuyendera.

M'modzi mwa ogwira ntchito ku ofesi yowona za chisamaliro cha anthu ku khonsolo ya boma la Zomba, a Davie Jacob Namuthe anati mabanja 19,761 ovutikitsitsa ndi omwe adalembetsa koma pafupifupi 2,000 akanika kupindula ndi ndondomekoyi kamba kakuchedwa kulembetsa.

Ndondomeko ya Mtukula Pakhomo imayendetsedwa ndi ndalama zochokera ku boma komanso mabungwe a World Bank, European Union, boma la Germany kudzera ku bank ya KFW ndinso boma la Ireland.

Wolemba Temwa Tembo (Zomba)

 Bungwe la Youth Net and Counselling (YONECO) lati lakwanitsa kutolera ndalama zokwana pafupifupi K6 million zomwe zidab...
17/07/2025


Bungwe la Youth Net and Counselling (YONECO) lati lakwanitsa kutolera ndalama zokwana pafupifupi K6 million zomwe zidabedwa ndi mafumu ena zothandizira anthu omwe anakhudzidwa ndi namondwe komanso njala chaka chatha.

Izi zadziwika pomwe mkulu woyang’anira pulojekiti yokhudza ngozi zadzidzidzi (Malawi Drought Response Project) pamodzi ndi akulu akulu ena anayendera likulu la bungweli mu mzinda wa Zomba pofuna kuziwonera okha momwe zikuyendera ntchito za mu pulojekitiyi.

M'mawu ake mkulu wa bungwe la YONECO a MacBain Mkandawire, ati pakadali pano ndalamazi, zatoleredwa ndikuperekedwa kwa eni ake oyenelera omwe anakhudzidwa ndi ngozi zadzidzidzi m'maboma omwe pulojekitiyi ikuchitikira ndi thandizo la ndalama kuchokera ku ECHO.

A Mkandawire ati chiyambireni pulojekitiyi, bungwe lawo lalandira madandaulo oposa 400 omwe ambiri ndi okhudza anthu okhudzidwa omwe amakakamizidwa kugawana thandizo lomwe alandira.

Wolemba Temwa Tembo (Zomba)

 In a bid to improve access to primary healthcare, Bike Town Africa, in collaboration with Villages in Partnership, has ...
17/07/2025


In a bid to improve access to primary healthcare, Bike Town Africa, in collaboration with Villages in Partnership, has donated 52 bicycles to Khanda Health Centre in Zomba District.

Speaking at the handover ceremony on Thursday, Bike Town Africa President, Mike Brienza, highlighted the organization’s commitment to supporting health workers by enhancing their mobility and reducing transport costs, noting that bicycles are a fuel-free, sustainable alternative.

Villages in Partnership Country Director, Enea Nkhoma, expressed the importance of taking good care of the bicycles properly to ensure their long-term use.

Khanda Health Centre In-Charge, Rodney Msukwa, welcomed the donation, saying it will help health workers reach more patients in remote areas and play a critical role in combating diseases like cholera and malaria.

He also noted that the bicycles will support efforts to improve safe motherhood initiatives in the district.

The health centre serves a population of around 25,000 people.

By Augustine Muwotcha (Zomba)

 Bungwe lolimbikitsa chilungamo pa malonda la Competition and Fair Trading (CFTC) lakana pempho la mgwirizano wa kampani...
16/07/2025


Bungwe lolimbikitsa chilungamo pa malonda la Competition and Fair Trading (CFTC) lakana pempho la mgwirizano wa kampani ya TNM ndi bungwe loyendes masero a mpira la SULOM loti anthu ayambe kugwirisa ntchito njira yokhayo yodzera ku mpamba ya e-ticketing pofuna kugula ma tikiti olowera ku masewero a mpira mumpikisano wa ligi ya TNM.

Malingana ndi mkulu wa bungwe la CFTC, a Lloyd Vincent Nkhoma, chigamulochi chadza kutsatira pempho la magulu awiriwa lomwe linaperekedwa ku bungweri pa 18 March, chaka chino.

Muchigamulo chake bungwe la CFTC lati kugulitsa ma tikitiwa kudzera ku njira ya mpamba yokha kutha kuphinja anthu ena omwe amagwirisa ntchito njira zina monga Airtel choncho kagulisidwe ka matikitiwa kukuyenera kumachitikanso munjira yomwe imachitika padakali pano.

Bungwe la CFTC lalengeza za chigamulochi lero pa msonkhano wa atolankhani munzinda wa Blantyre komwe limalengezanso zigamulo zina zomwe lachita powunikira madandawulo omwe linalandira okhudza ntchito za malonda m'dziko muno.

Bungweri latinso lapereka zilango kwa makampani ena omwe alamulidwa kupereka chindapusa cha ndalama zokwana K4.1 million kwa makasitomala omwe anaphwanyiridwa ufulu wawo ogula katundu.

Ena mwa makampani omwe apezeka olakwa ndi Mulli Brothers Limited, Speed Courier and Logistics, Agri-Build ku Lilongwe, komanso makampani ena ogulitsa fetereza.

Wolemba Smart Sochela

16/07/2025


Bungwe la Malawi First lati ndi lokhumudwa ndi kusakazika kwa ndalama za nkhani nkhani zomwe zidayikidwa ku ntchito yomanga sukulu ya ukachenjede ya Mombera.

Poyankhula pa msonkhano wa atolankhani, mtsogoleri wa bungweli a Bon Kalindo, anati sukulu ya Mombera yasanduka chida chomwe andale ambiri amagwiritsa ntchito ponamiza a Malawi kuti adzawamangira ndi cholinga chofuna kuvoteledwa.

Pachifukwa ichi, a Kalindo kudzera ku bungwe la Malawi First, apempha bungwe la Anti Corruption Bureau (ACB), kuti lichite kafufuku ndikumanga onse omwe akukhudzidwa pa nkhaniyi.

A Kalindo apemphanso boma kuti lipereke mayankho pa chifukwa chomwe chachititsa kuti ntchitoyi isayambidwe ngakhale kuti ndalama zochuluka zinalowapo.

Iwo amemanso boma kuti litolere ndikubwenzeretsa ndalama zonse zomwe zasakazika pa ntchitoyi pasanathe masiku asanu ndi awiri (7).

Wolemba Temwa Tembo

16/07/2025


Bungwe lothana ndi ziphuphu ndi katangale la ACB, lamanga yemwe adali m'modzi mwa ogwira ntchito ku nthambi yoona za kalembedwe ntchito ka anthu ku ofesi ya za umoyo m'boma la Nsanje a Lufai Nachamba, kamba kogwiritsa ntchito udindo wawo molakwika.

Wapolisi ofalitsa nkhani m'bomali, Sub-Inspector Agnes Zalakoma watsimikiza za izi ndipo a Nachamba pakadali pano akusungidwa nchitokosi pa Polisi ya Nsanje.

M'mawu ake, a Zalakoma ati a Nachamba amangidwa dzulo ndipo akuyembekezeka kulowa kubwalo loweluzila milandu lero chakum'mawaku.

Akatu sikoyamba kuti a Nachamba apalamule mulandu ngati omwewu. pomwe muchaka cha 2021, iwowa adamangidwapo kamba kolemba ntchito anthu mosatsata Malamulo.

Wolemba Temwa Tembo

  Bungwe logawa magetsi la ESCOM lachenjeza Amalawi kuti apewe mchitidwe wachinyengo popereka ndalama iliyonse mwa nseri...
15/07/2025


Bungwe logawa magetsi la ESCOM lachenjeza Amalawi kuti apewe mchitidwe wachinyengo popereka ndalama iliyonse mwa nseri kwa ogwira ntchito ku bungweri kuti athandizidwe mwa njira ina iliyonse pa ntchito zokhudza magetsi.

Mneneri wa bungweri, a Pilirani Phiri ati mchitidwe opereka ndalama kwa anthu ogwira ntchito ku bungweri ndi cholinga chofuna kuthandizidwa mwachangu ndi mulandu waukulu ndipo ochita izi adzalandira chilango.

Mwazina a Phiri atsimikiza kuti ntchito zokonza mavuto a magetsi kapena kulumikizitsa magetsi ndi zaulere.

A Phiri ati vuto la kuchedwa kwa ogwira ntchito kubungweri kuzalumikiza magetsi limakhakapo kamba ka mavuto azachuma.

Wolemba Arshavello Mponda

 President Lazarus Chakwera’s address marking the start of the official campaign period has sparked mixed reactions from...
15/07/2025


President Lazarus Chakwera’s address marking the start of the official campaign period has sparked mixed reactions from experts.

Political analyst Chimwemwe Tsitsi has praised the President for emphasizing peace, urging political party members to respect Chakwera’s call for a fair and peaceful campaign leading up to the September 16 general election.

Another analyst, George Chaima, also commended the President’s remarks, describing the speech as powerful and reflective of a leader who cares deeply for the nation.

However, Chaima noted that the message raised questions in light of recent political violence and concerns about the conduct of Chakwera’s administration.

Chaima further acknowledged Chakwera's consistent stance against political violence, pointing out that the President has never incited unrest.

By Prosper Kanyade Balirani

Address

Zomba

Telephone

+2651526199

Website

http://www.yonecofm.com/

Alerts

Be the first to know and let us send you an email when YONECO FM posts news and promotions. Your email address will not be used for any other purpose, and you can unsubscribe at any time.

Contact The Business

Send a message to YONECO FM:

Share

Category