YONECO FM

YONECO FM YONECO FM is a page for YFM Radio Station that was established in October 2014 to educate, inform and entertain youth, women and children.

TO ADVERTIZE on YFM Radio Call: 0882000302
[email protected]

YONECO FM is a page for Youth Net and Counselling (YONECO) Youth Radio station. Its aim is to educate, entertain and provide information on issues that affect youth, women and children in Malawi. YFM is the real voice of youth, women and children in Malawi. YFM is on 103.8 Mhz in Zomba, 101.6 Mhz in Blantyre, 97.5 Mhz in Lilongwe, 103.9 Mhz in Mzuzu, 104.6 Mhz in Thyolo and 89.1 Mhz in Chitipa. [email protected]

 Katswiri pa nkhani za ulamuliro wabwino a Mavuto Bamusi, ati kusowa kwa ntchito komanso mavuto a zachuma ndi zina mwa z...
10/06/2026


Katswiri pa nkhani za ulamuliro wabwino a Mavuto Bamusi, ati kusowa kwa ntchito komanso mavuto a zachuma ndi zina mwa zifukwa zazikulu zomwe zikuchititsa anthu ambiri ku Malawi kusankha kupita kumayiko ena kukafunafuna moyo wabwino.

Poyankhula ndi YFM, a Bamusi ati anthu ambiri amapita ku mayiko monga South Africa ndi Israel pofuna kupeza ntchito ndi njira zopezera ndalama.

Komabe, iwo ati ena akafika kumeneko amakumananso ndi mavuto osiyanasiyana monga kusowa kwa chitetezo komanso nkhanza m’malo ogwirira ntchito.

Iwo atinso kuti vutoli likuwonetsa kufunika kokhazikitsa njira zolimba zothandizira achinyamata ndi nzika zina kupeza mwayi wa ntchito komanso kuchita malonda m’dziko muno osakakamizika kupita kunja.

A Bamusi apempha boma kuti liunikenso ndondomeko zake za chitukuko cha chuma kuti zithandize anthu ambiri kupeza njira zopezera ndalama, kudzidalira komanso kukhala ndi moyo wabwino m’dziko muno.

Wolemba: Yvonne Chambo

 Mtsogoleri wa mpingo wa Jesus Nation, Mneneri Shepherd Bushiri, wapempha a Malawi onse kuti atengepo gawo pothandiza nz...
10/06/2026


Mtsogoleri wa mpingo wa Jesus Nation, Mneneri Shepherd Bushiri, wapempha a Malawi onse kuti atengepo gawo pothandiza nzika za dziko lino zomwe zabwerera kuno kumudzi kuchokera ku South Africa chifukwa cha ziwawa zomwe zikuchitikira anthu ochokera m'maiko ena m’dzikolo.

Mu uthenga wawo kudzera pa tsamba la mchezo, a Bushiri apereka mawu achilimbikitso kwa anthu omwe abwerera ku Malawi kuti asataye mtima ngakhale asiya katundu ndi zinthu zina ku South Africa.

A Bushiri ati anthuwa akuyenera kukhala ndi chikhulupiliro mwa Mulungu komanso kugwira ntchito molimbika kuti akonzenso moyo wawo.

Iwo ati nawonso anakumanapo ndi zovuta atabwerera ku Malawi, koma kudzera mu thandizo la Mulungu anakwanitsa kubwezeretsa moyo wawo ndi ntchito zawo.

Pakadali pano, a Malawi osachepera 150 afika m’dziko muno kuchokera ku South Africa kudzera m’ndondomeko yomwe boma la Malawi linakhazikitsa pothandiza nzikazo kubwerera kwawo.

Wolemba: Blessings Makuta

 Chipatala chachikulu cha Zomba Mental chati m’miyezi itatu yoyambirira ya chaka cha 2026 chalandira anthu 503 omwe ali ...
10/06/2026


Chipatala chachikulu cha Zomba Mental chati m’miyezi itatu yoyambirira ya chaka cha 2026 chalandira anthu 503 omwe ali ndi vuto la misala yokhudzana ndi kugwiritsa ntchito mankhwala ozunguza bongo, makamaka chamba, komanso matenda ena monga schizophrenia.

Malinga ndi lipoti la kotala yoyamba la chaka chino, kuyambira mwezi wa January mpaka March, achinyamata azaka zapakati pa 20 ndi 45 ndiwo akutsogola pa chiwerengero cha odwala omwe akulandira chithandizo pachipatalachi.

Lipotili likusonyeza kuti mwa odwala onse 503, amuna ndi 405 omwe akuyimira 80.5 peresenti, pomwe azimayi ndi 98 omwe akuyimira 19.5 peresenti.

Chipatalachi chatinso mwa odwala onse omwe adagonekedwa m’nthawiyi, 313 anatulutsidwa atalandira chithandizo, pomwe 186 adali m’chipatala pofika kumapeto kwa mwezi wa March.

Wolemba: Peter Davieson

 Katswiri wa zachuma a Derrick Mina ati mkofunikira kuti dziko lino lipeze njira zina zopezera ndalama zakunja mmalo mon...
10/06/2026


Katswiri wa zachuma a Derrick Mina ati mkofunikira kuti dziko lino lipeze njira zina zopezera ndalama zakunja mmalo mongodalira malonda afodya okha.

Iwo ati ngakhale kuti ndi zachidziwikire kuti malonda a fodya akulowa pansi, adindo akukanika kuchitapo kanthu msanga.

A Mina ati maiko ambiri amene amalima fodya padakali pano akugwiritsa nchito zipangizo za ulimi za makono zimene alimi ambiri mdziko muno sangakwanitse chifukwa ndi zokwera mtengo kwambiri.

Iwo awonjezenso kuti kukwera mtengo kwa zipangizo za ulimi kukupangitsa alimi kuti azigwilitsa nchito zipangizo zochepa zimene zikuchititsa kuti azipititsa fodya osapatsa chikoka pa msika.

Malingana ndi bungwe la To***co Commission, pofika pa 5 mwezi uno dziko lino linali litapeza ndalama zokwana 107 million dollars mu sabata zisanu ndi ziwiri za malonda a fodya poyerekeza ndi ndalama yokwana 143 miliyoni dollars mu nyengo ngati yomweyi chaka chatha.

Wolemba: Blessings Makuta

Apolisi ku Bangwe munzinda wa Blantyre amanga mai wazaka 22, Eliza Joseph, pomuganizira kuti anasiya mwadala mwana wake ...
09/06/2026

Apolisi ku Bangwe munzinda wa Blantyre amanga mai wazaka 22, Eliza Joseph, pomuganizira kuti anasiya mwadala mwana wake wakhanda pakhonde la chipatala chachingóno cha Bangwe.

Malingana ndi m’neneri wa polisi ya Bangwe, Sam Kadyole, izi zinachitika dzulo lolemba.

Kafukufuku wa apolisi akusonyeza kuti patsikuli mai oganiziridwayu anapita pa chipatalapo nthawi ya kumadzulo ndipo anamusiya mwanayu popanda kuwonedwa ndi munthu aliyense. Mwanayu anapezedwa ndi mulonda wa pa chipatalapo yemwe amazayamba kugwira ntchito yake usiku atamva kulira kwa khandalo lomwe linali litakulungidwa mu nsalu.

Akuluakulu pa chipatalapo anatengera khandali ku chipatala cha Queen Elizabeth.

Koma usiku wa tsiku lomweri, a Joseph anawonedwa akungozungulira pa malo omwe panapezeka mwanayu zomwe zinapangitsa akuluakulu pa chipatalachi kukayikira maiyu ndipo anamugwira ndikumpereka m’manja mwa apolisi.

Pakadali pano apolisi akuyembekezeka kutengera maiyu kuchipatala cha anthu odwala nthenda ya misala kuti akayezedwe.

A Eliza Joseph ndiwochokera m’mudzi mwa Mwamadi mfumu yayikulu Machinjiri m’boma la Blantyre.

Wolemba Smart Sochela

09/06/2026

The Ministry of Finance, Economic Planning and Decentralisation has released funding for councillors' loans as well as women and youth empowerment loans under the 2026/27 national Budget.

According to a statement signed by Secretary to the Treasury, Dr. Cliff Chiunda, said the funds for councillors’ loans have been disbursed through the Local Government Finance Committee.

Dr. Chiunda said the 2026/27 Malawi National Budget, valued at K10.978 trillion, has allocated K22.9 billion towards the Youth and Women Empowerment Fund aimed at supporting entrepreneurship and economic growth.

He added that the women and youth loans will be administered through the Malawi Enterprise Development Fund (MEDF).

By Blessings Makuta

 Ma bus awiri omwe ananyamula nzika za dziko lino zokwana 150 kuchoka mdziko la South Africa, afika munzinda wa Blantyre...
09/06/2026



Ma bus awiri omwe ananyamula nzika za dziko lino zokwana 150 kuchoka mdziko la South Africa, afika munzinda wa Blantyre.

Anthuwa achoka ku South Africa kaamba ka zamtopola zomwe anthu m’dzikolo akuchitira athu a m’mayiko ena pofuna kuti achoke m’dzikolo.

Boma la Malawi ndilo lapereka ma bus-wa kuti athandizire kusamutsa anthuwa mwaulere.

Anthuwa, omwe ananyamuka ku South Africa loweruka lapitali, afikira pa bwalo la zamasewero la Kamuzu.

Padakali pano ogwira ntchito zaumoyo akuyeza anthuwa zizindikiro za nthenda ya Ebola.

Wolemba Smart Sochela.

 Anthu 78 omwe akugwira ukaidi m’ndende zosiyanasiyana m’dziko muno, akulemba nawo mayeso a standade 8 omwe ayamba lero....
08/06/2026


Anthu 78 omwe akugwira ukaidi m’ndende zosiyanasiyana m’dziko muno, akulemba nawo mayeso a standade 8 omwe ayamba lero.

Malingana ndi m’neneri wa nthambi yoyang’anira ndende m’dziko muno, a Steve Meke, mwachiwerengerochi, 68 ndi amuna ndipo 10 ndi akazi.

Mchaka cha 2025, omwe analemba nawo mayesowa analipo 58.

Mayesowa akulembedwera m’ndende za Zomba, Blantyre (Chichiri), Bvumbwe, Lilongwe (Maula), Mzuzu ndi Mzimba.

Wolemba: Smart Sochera (Blantyre)
Mchithunzi: Steve Meke

 Bungwe logwira nchito zachifundo la Shepherd Bushiri Foundation lalonjedza kuti limangira nyumba kwatswiri waluso lojam...
08/06/2026


Bungwe logwira nchito zachifundo la Shepherd Bushiri Foundation lalonjedza kuti limangira nyumba kwatswiri waluso lojambula zinthu ndi pakamwa a Chrisford Chayera.

Izi malingana ndi oyankhulila a Shepherd Bushiri a Aubrey Kasakala.

Iwo ati a Bushiri alamula ogwira ntchito ku ofesi yawo kuti afulumizitse kuyang'ana nyumba ya mkuluyu.

Wolemba: Blessings Makuta

08/06/2026


Ophunzira pafupifupi 254,000 ndi omwe ayamba kulemba mayeso a Standade 8 mmawa uno.

Izi ndi malingana ndi bungwe lolembetsa mayeso aboma la Malawi National Examinations Board (MANEB).

MANEB yati mwa ophunzila 254,000, 132,476 ndi atsikana ndipo ophunzila 122,010 ndi anyamata.

Ophunzirwa alemba mayesowa kwa masiku atatu mpaka pa 10 June 2026.

Wolemba Blessings Makuta

Address

Youth Net & Counselling (YONECO)
Zomba
471

Alerts

Be the first to know and let us send you an email when YONECO FM posts news and promotions. Your email address will not be used for any other purpose, and you can unsubscribe at any time.

Contact The Business

Send a message to YONECO FM:

Share

Category