YONECO FM

YONECO FM YONECO FM is a page for YFM Radio Station that was established in October 2014 to educate, inform and entertain youth, women and children.

TO ADVERTIZE on YFM Radio Call: 0882000302
[email protected]

YONECO FM is a page for Youth Net and Counselling (YONECO) Youth Radio station. Its aim is to educate, entertain and provide information on issues that affect youth, women and children in Malawi. YFM is the real voice of youth, women and children in Malawi. YFM is on 103.8 Mhz in Zomba, 101.6 Mhz in Blantyre, 97.5 Mhz in Lilongwe, 103.9 Mhz in Mzuzu, 104.6 Mhz in Thyolo and 89.1 Mhz in Chitipa. [email protected]

12/05/2026


Bungwe loona za ufulu wachibadwidwe la Malawi Human Rights Commission lati lero liyamba kafukufuku m'boma la Nsanje pankhani zokhuza ufulu wa anthu pamphekesera zomwe zinabuka m'bomari pankhani yokhuza kusowa kwa ziwalo zobisika.

Malinga ndi uthenga omwe bungweri latulutsa wati, mwa anthu 28 omwe akuganizilidwa kuti anatengapo nawo gawo pofalitsa nkhani zakusowa kwa malo obisika anthu asanu ndi awiri 7 ndi achichepere ndipo bungweri lati lichita chotheka powonetsetsa kuti ufulu wawo ukutetezedwa ngati ana omwe asemphana ndi lamulo.

Malinga ndimkulu wabungweri a Chikondi Chijozi achenjeza anthu kupewa kufalitsa nkhani zabodza komanso zosatsimikizika pankhani yakusowa kwa ziwalo zobisika.

Iwo ati bungweri liyetsetsa kuchita zonse zothekera kuti chilungamo chiwoneke maka kwa okhudzidwa, kwa oganizilidwa komanso kudera.

Wolemba Peter Davieson

 Unduna owona Zaumoyo ndi Ukhondo wati ndiwodzipereka kuonetsetsa kuti anthu okhala m’boma la Nsanje akupeza thandizo la...
12/05/2026


Unduna owona Zaumoyo ndi Ukhondo wati ndiwodzipereka kuonetsetsa kuti anthu okhala m’boma la Nsanje akupeza thandizo lazaumoyo labwino ngakhale bomali lili ndi zovuta zapadera zokhudza nyengo komanso zomangamanga.

Izi zayankhulidwa ndi Mlembi ku Undunawu Dr. Dan Namarika, pa ulendo wawo omwe anayendera chipatalachi kumene anaunika zovuta zomwe chipatalachi chikukumana nazo.

Iwo atsimikizira Chipatala chachikuru cha Boma la Nsanje kuti boma lithandiza popereka zipangizo zofunika zachipatala, kutumiza ogwira ntchito ya zaumoyo ophunzira bwino, komanso kukonza zomangamanga kuti thandizo lokhuza zaumoyo chipite patsogolo.

mwa zina mwa zomwe zikufunika pachipatalachi mwachangu ndi makina amakono oziziritsira mpweya kuchipatala (Cooling system) .

Boma la Nsanje ndi limodzi mwa maboma otentha kwambiri mdziko muno, ndipo nthawi zina kutenthaku kumafika madigiri 39, zomwe zimapangitsa kuti zinthu zikhale zovuta kwa odwala komanso ogwira ntchito ya zaumoyo.

Wolemba: Peter Davieson

The Institute of Internal Auditors (IIA) Malawi has advised local councils across the country to consider employing more...
11/05/2026

The Institute of Internal Auditors (IIA) Malawi has advised local councils across the country to consider employing more internal auditors to strengthen the implementation of the Constituency Development Fund (CDF), whose allocation was increased to K5 billion per constituency.

IIA Malawi Chief Executive Officer, Albert Dambula, said internal auditors play a critical role in ensuring transparency, accountability and proper management of public resources, thereby contributing to the successful implementation of CDF projects.

Dambula made the remarks as Malawi continues commemorating Global Internal Audit Awareness Month, with the campaign aimed at increasing awareness on the importance of internal auditing in both public and private institutions.

He said increased awareness about internal auditing will help institutions strengthen financial management systems and build public trust in the handling of public resources, including funds meant for development projects.

Dambula further expressed satisfaction with the growing recognition of the internal audit profession in the country, saying more institutions are beginning to appreciate the important role internal auditors play.

Meanwhile, Malawi is expected to host the 2027 African Federation of Institutes of Internal Auditors (AFIIA) Conference, expected to take place in Lilongwe.

By Smart Sochela

11/05/2026


Chiwerengero cha anthu omwe amangidwa powaganizira kuti akukhudzidwa ndi kufalitsa nkhani yabodza yokhudza kusowa kwa katundu wawo wakumalo obisika chafika pa khumi ndi anayi (14).

izi zikutsatira kumangidwanso kwa anthu ena asanu ndi anayi (9) omwe amafalitsa kuti katundu wawo waku malo obisika wasowa zomwe zinali zabodza kutsatira malipoti aku chipatala.

Wachiwiri kwa mneneli wa a polisi m'dziko muno, a Alfred Chimthere ati anthuwa ndi a Boniface Beka, a Clement Kaduya (39), a Precious Kaduya (39), a Shadrick Sande(20), a Chisomo Eliasi(18), a Jeremiah Esaya (20), a Edward Fatsani(20), a Nelson Andisen(18) ndi a Beatrice Geofry(42) ndipo onse ndi aku Nsanje.

Malingana ndi apolisi, atatengela ku chipatala anthuwa omwe akhala akuwuza anthu kuti malo awo obisika asowa apeza kuti chilichonse pamatupi awo chilibwinobwino.

Pakadali pano, apolisi akhwimitsa chitetezo m'maboma a Nsanje ndi Chikwawa kuti athane ndi anthu onse omwe akufalitsa nkhaniyi komanso kumanga aliyense okhudzidwa ndi kuphedwa kwa anthu asanu ndi awiri (7).

Wolemba Temwa Tembo

11/05/2026


Anthu pafupifupi 1.1 miliyoni akuyembekezeka kulandira katemera wa matenda a likodzo komanso njoka za m'mimba m'maboma asanu mdziko muno kuyambira pa 18 mpaka 22 May 2026.

Malinga ndi mlembi mu Unduna wa Zaumoyo, Dr. Dan Namarika, mwa chiwerengerochi, ana 872,101 a zaka zapakati pa zisanu mpaka 14 ndiwo akuyembekezeka kulandira katemerayu, pomwe akuluakulu 344,242 a zaka 15 kupitirira apo nawonso alandira.

Kampeni yopereka katemerayi ichitikira m'maboma a Blantyre, Lilongwe, Dowa, Phalombe komanso Nsanje.

Wolemba: Precious Banda

Nzika zinayi za m’dziko la Bangladeshi ziri mmanja mwa apolisi ku Limbe munzinda wa Blantyre kaamba kolowa m’dziko muno ...
10/05/2026

Nzika zinayi za m’dziko la Bangladeshi ziri mmanja mwa apolisi ku Limbe munzinda wa Blantyre kaamba kolowa m’dziko muno mosatsata lamulo.

Malingana ndi m’neneri wa polisi ya Limbe, a Aubrey Singanyama, anthuwa anamangidwa lachisanu lapitali atawapeza pa malo ena ogona alendo ku Kanjedza komwe akhalako kwa sabata ziwiri.

Kumangidwa kwa anthuwa kunachitika anthu ena akufuna kwabwino atawatsina khutu apolisi.

Anthuwa ndi a Muhammad Tayab Ullah azaka 25, Anishr Rahman, 23, Farhadul Islam, 26, ndi Rasedul Islam, 23.

Wolemba Smart Sochela

10/05/2026


Wachiwiri kwa mkulu wa apolisi mchigawo chakumwera chakumvuma, a Joyce Madzalo ati wina aliyense yemwe adzinena kuti ziwalo zake zasowa adzitengeledwa ku polisi ndipo adzipatsidwa chilango chokhwima.

A Madzalo alankhula izi pa mkumano womwe adachita ndi magulu onse okhudzidwa kwa Ngabu m'boma la Chikwawa, kutsatira kuphedwa kwa anthu atatu powaganizila kuti akukhuzidwa pa mchitidwe wosowetsa ziwalo zobisika kudzera m'matsenga.

M'modzi mwa akulu akulu apa chipatala cha Ngabu, a Selemani Nsona, ati nkhani ya kusowa kwa ziwalo ndi yabodza ndipo palibe yemwe wabwera kuchipatala kudzadandaula kuti ziwalo zake zasowa.

Ndipo mfumu yaikulu Ngabu yadandaula kuti achinyamata ndi amene akuyambitsa kufalitsa nkhani zabodza komanso kuchitira ena nkhanza.

Wolemba Temwa Tembo

Agalu pafupifupi 25,000 akuyembekezeka kubayidwa katemera wa nthenda ya chiwewe ku Blantyre. Mkulu wa bungwe la Mission ...
10/05/2026

Agalu pafupifupi 25,000 akuyembekezeka kubayidwa katemera wa nthenda ya chiwewe ku Blantyre.

Mkulu wa bungwe la Mission Rabies m’dziko muno lomwe likugwira ntchitoyi, Dr Inga Mcdermott, ati cholinga chake ndikufuna kuthana ndi nthenda ya chiwewe yomwenso ndiyowopya pa umoyo wa anthu omwe alumidwa ndi galu wachiwewe.

Poyankhula pa mwambo oyambisa ntchitoyi, Dr McDermott ati bungweri lakhazikisa malo 88 munzindawu ndipo akuyigwira mogwirizana ndi nthambi yaboma yoyang’anira za nyama.

“Chiwewe ndichowopysa kwambiri ngakhale chilinso chopeweka. Kachilombo kakangolowa muubongo, munthu, ngakhale chinyama amayamba zizindikiro za nthendayi ndipo zimasokoneza kayendedwe kabwino kathupi mpaka kudzetsa imfa,” anatero Dr. Mcdermott.

Choncho iwo apempha anthu kuti abayise agalu awo ponena kuti katemerayu ndiwawulere.

Kuwonjezera pa katemerayu, akhalanso akufula agalu ngati njira imodzi yochepesera chiwerengero cha agalu omwe amangoyendayenda kusowa chisamaliro.

Wolemba Smart Sochela

  Mtsogoleri yemwe wangosankhidwa kumene ku bungwe la MISA Malawi a Felix Washon, ati  ali okonzeka kugwira ntchito ndi ...
09/05/2026


Mtsogoleri yemwe wangosankhidwa kumene ku bungwe la MISA Malawi a Felix Washon, ati ali okonzeka kugwira ntchito ndi anzawo ena onse omwe amapikisana nawo pampando wu kuti akatumikile a tolankhani onse m'dziko muno.

Mwazina, a Washon ati mfundo zonse zomwe zinatulutsidwa ndi anzawo omwe amapikisana nawo pa mpandowu, azitenga ndikuziika pamodzi pomwe akhale akugwira ntchitoyi.

Iwo ati awonetsetsa kuti atolonkhani m'dziko muno akugwira ntchito zawo mopanda kuopsezedwa ndi magulu ena a anthu, aonetsetsanso kuti umoyo wa atolankhani uli otetezeka pomwe akugwira ntchito zawo ndinso kuti atolankhani akulandila malipiro moyenera molingana ndikusintha kwa chuma cha dziko.

A Washoni apeza mavoti 150, pamene a Innocent Mphongolo apeza mavoti 121 ndipo a Alex Banda apeza mavoti 78 pamene a Janet Mtali apeza mavoti 55.

Wolemba Temwa Tembo

Mafumu a mdera la mfumu yaikulu Malemia m'boma la Zomba awalangiza kupewa kutengera milandu yogwililira komanso yokwatiw...
09/05/2026

Mafumu a mdera la mfumu yaikulu Malemia m'boma la Zomba awalangiza kupewa kutengera milandu yogwililira komanso yokwatiwitsa ana ang'ono kumabwalo awo m'malo mokaitula kupolisi.

Izi zayankhulidwa pamwambo omwe bungwe la One for All linakonza mdera lamfumu yaikuru malemia omwe cholinga chake ndikulimbikitsa kuthetsa maukwati awana komanso kulimbikitsa ana kulimbikira maphunziro.

Malinga ndimkulu wa bungweri a James Kajawo ati, kafukufuku omwe bungweri linapanga kudelari linapeza kuti chiwelengero cha ana chokwana 72% chimasiyira sukulu panjira komanso kukwatidwa ali achichepere.

Iwo ati zina mwazifukwa zomwe anawa amalowera m'banja ndi umphawi komanso kusaonetsa chidwi kwa makolo.

M'mawu ake oyimira mkulu wazaphunziro m'boma la Zomba a Beatrice Matukuta ati ofesi yawo ikuchilimika kulimbikitsa makolo kutumiza ana kusukulu komanso kuphunzitsa anthu mdelari nkhani zamaphunziro.

M'mawu awo, a Linda Chitsulo ochokera ku polisi mchigawo chaku m'mawa anati nzokhumudwitsa kuwona mafumu ena akuweruza milandu yogwilira kubwalo lawo m'malo mokatula nkhanizi kupolisi.

Iwo anati mchitidwewu ukukoledzera mchitidwe okwatilitsa komanso kugwilira ana ponena kuti milanduyi imatha ndikupereka ndalama.

Wolemba Peter Davieson

  Ntchito yoponya voti ili mkati mmaboma onse pofuna kusankha atsogoleri atsopano a bungwe la atolankhani mdziko lino la...
09/05/2026


Ntchito yoponya voti ili mkati mmaboma onse pofuna kusankha atsogoleri atsopano a bungwe la atolankhani mdziko lino la MISA Malawi.

Mzithunzimu atolankhani akuponya voti yawo mumzinda wa Zomba.

Address

Youth Net & Counselling (YONECO)
Zomba
471

Telephone

+2651526199

Website

http://www.yonecofm.com/

Alerts

Be the first to know and let us send you an email when YONECO FM posts news and promotions. Your email address will not be used for any other purpose, and you can unsubscribe at any time.

Contact The Business

Send a message to YONECO FM:

Share

Category