10/06/2026
Katswiri pa nkhani za ulamuliro wabwino a Mavuto Bamusi, ati kusowa kwa ntchito komanso mavuto a zachuma ndi zina mwa zifukwa zazikulu zomwe zikuchititsa anthu ambiri ku Malawi kusankha kupita kumayiko ena kukafunafuna moyo wabwino.
Poyankhula ndi YFM, a Bamusi ati anthu ambiri amapita ku mayiko monga South Africa ndi Israel pofuna kupeza ntchito ndi njira zopezera ndalama.
Komabe, iwo ati ena akafika kumeneko amakumananso ndi mavuto osiyanasiyana monga kusowa kwa chitetezo komanso nkhanza m’malo ogwirira ntchito.
Iwo atinso kuti vutoli likuwonetsa kufunika kokhazikitsa njira zolimba zothandizira achinyamata ndi nzika zina kupeza mwayi wa ntchito komanso kuchita malonda m’dziko muno osakakamizika kupita kunja.
A Bamusi apempha boma kuti liunikenso ndondomeko zake za chitukuko cha chuma kuti zithandize anthu ambiri kupeza njira zopezera ndalama, kudzidalira komanso kukhala ndi moyo wabwino m’dziko muno.
Wolemba: Yvonne Chambo