12/05/2026
Bungwe loona za ufulu wachibadwidwe la Malawi Human Rights Commission lati lero liyamba kafukufuku m'boma la Nsanje pankhani zokhuza ufulu wa anthu pamphekesera zomwe zinabuka m'bomari pankhani yokhuza kusowa kwa ziwalo zobisika.
Malinga ndi uthenga omwe bungweri latulutsa wati, mwa anthu 28 omwe akuganizilidwa kuti anatengapo nawo gawo pofalitsa nkhani zakusowa kwa malo obisika anthu asanu ndi awiri 7 ndi achichepere ndipo bungweri lati lichita chotheka powonetsetsa kuti ufulu wawo ukutetezedwa ngati ana omwe asemphana ndi lamulo.
Malinga ndimkulu wabungweri a Chikondi Chijozi achenjeza anthu kupewa kufalitsa nkhani zabodza komanso zosatsimikizika pankhani yakusowa kwa ziwalo zobisika.
Iwo ati bungweri liyetsetsa kuchita zonse zothekera kuti chilungamo chiwoneke maka kwa okhudzidwa, kwa oganizilidwa komanso kudera.
Wolemba Peter Davieson