Dømingos Anthony

Dømingos Anthony Luke Cap. 11 | NIV-EN
9 “So I say to you: Ask and it will be given to you; seek and you will find; knock and the door will be opened to you"
(1)

04/06/2026
03/06/2026

Pachiyambi pamene Mulungu anafuna kulenga nsomba, anayankhula ndi nyanja. Pamene Mulungu anafuna kulenga mitengo ndi zomera zina, anayankhula ndi nthaka. Ndipo pamene Mulungu ankafuna kulenga munthu, anatembenukira kwa Iye mwini. Kenako Mulungu anati:

"Tiyeni tipange munthu m’chifanizo chathu ndi m’maonekedwe athu."

Mukachotsa nsomba m’madzi, imafa; ndipo mukazula mtengo m’nthaka, umathanso kufa. Momwemonso, munthu akalekanitsidwa ndi Mulungu, amafa mwauzimu.

Pamene tikuona kuti tili ndi moyo tere, chifukwa ndife olumikizana naye Mulungu, kotero kuti tikalekana naye Mulungu timafa muuzimu kukhala anthu obalalika ndi omvetsa chisoni. Ubale wathu ndi Mulungu chinthu chofunika kwambiri

31/05/2026

Mpingo woona uli m'malemba

31/05/2026

Akhristu FUNGO LABWINO

WE ARE NOT UNDER THE LAW-     2Tikamawerenga mavesi ambiri mchipangano chatsopano, amaonetsa kusintha zinthu zina za chi...
30/05/2026

WE ARE NOT UNDER THE LAW- 2
Tikamawerenga mavesi ambiri mchipangano chatsopano, amaonetsa kusintha zinthu zina za chilamulo poyerapoyera, tsono funso imakhala yakuti ndi chifukwa CHANI mabuku a Chipangano cha Tsopano tili nawobe?
AHEBRI 8:7 "Pakuti [pangano ] loyamba lija likadakhala lopanda chilema sakadafuna malo a lachiwirilo"

Akunena kuti pangano loyamba likadakhala langwiro sadakonzanso ina, pano inakonzedwa ina ndi chifukwa chani lopanda ungwiro ija tili nayobe?. Iyi ndi nkhani imene tikambirane lero, tiyenda ndi buku la Aroma 7:7. Koma Choyamba dziwani kuti Chipangano cha kale sichidzachotsedwa m'baibulo, koma chidzagwiritsidwa ntchito moyenera, chifukwa chili ndi ntchito yake yapaderadera.

AROMA 7:6 "Koma tsopano tinamasulidwa kuchilamulo, popeza tinafa kwa ichi chimene tinagwidwa nacho kale; chotero kuti titumikire mu mzimu watsopano, si m'chilembo chakale ai".

Iyi ndi mfundo yoyamba yoti tiidziwe tisanapitirize yakuti tinamasulidwa ku chilamulo.

AROMA 7:7 "Pamenepo tidzatani? Kodi chilamulo chili uchimo? Msatero ai. Koma ine sindikadazindikira uchimo, koma mwa lamulo ndimo; pakuti sindikadazindikira chilakolako sichikadati chilamulo, Usasirire"

Kodi chifukwa chakuti tinamasulidwa ku chilamulo ndiye kuti chilamulo ndi uchimo? Si choncho ayi. Chilamulo chili galasi kapena kalirole, ukayang'ana pa galasi, umatha kuona pamene sipali bwino ndi thupi lako, umatha kuona ngati ndiwe wakuda nkhope kapena koyera, chilamulo chimationetsa kuperewera kwathu, anthu ambiri ukawafunsa kuti, kuti munthu Apulumuke akuyenera kutani?, yankho yophweka amayankha kuti "Akuyenera kusunga malamulo khumi". Koma yankho si imeneyi chifukwa palibe amene angakwanitse kusunga malamulo khumi, pakuti ngakhale Sabata sikuti eni ake a Sabatawo ankasunga chonchi ayi, inde, zimene zikuonetsa kusiyako kapena kulephera pa kasungidwe kake. mwa chitsanzo pa malamulo khumi pali lamulo yakuti "Usaphe", kukufunsani inu kuti mumapha? mukhoza kunena kuti ayi, koma Mateu 5:21-22 amanena kuti aliyense wokwiira mnzake ali wakupha, komanso mu 1 Yohane 3:15 amanena kuti: "Yense wakudana ndi mbale wake ali wakupha munthu; ndipo mudziwa kuti wakupha munthu aliyense alibe moyo wosatha wakukhala mwa iye". Ndi ndani amene sakwiya pano? tonse timakwiya ndipo talephera pa lamulo lakuti "usaphe".... lamulo lina lakuti "Usachite Chigololo", Mateu 5:28 akuti: "yense wakuyang'ana mkazi kumkhumba, pamenepo watha kuchita naye chigololo mumtima mwake". aaaaa Talepheranso pa lamulo ili. Tsono ngati ku chilamulo ndikupezeka olephera ndikapulumuka bwanji?.

Vuto la ife anthu kusamvetsetsa, imvani kunena kuti Yesu Khristu kapena imfa ya Yesu Khristu inalowa m'malo mwa chilamulo, chifukwa malo amene chilamulo sichinakwanitsa kupanga chifukwa cha kupanda ungwiro kwake, mtanda wa Yesu unakwanitsa. Inde Baibulo ikutero Aroma 8:3 akuti "Pakuti chimene chilamulo sichinathe kuchita, popeza chinafooka mwa thupi, Mulungu anatumiza Mwana wake wa Iye yekha m'chifanizo cha thupi la uchimo, ndi chifukwa cha uchimo, natsutsa uchimo m'thupi". Tsono timvere chilamulo kapena timvere mwana wa Mulunguyo?

AGALATIYA 2:21 "Sindichiyesa chopanda pake chisomo cha Mulungu; pakuti ngati chilungamo chili mwa lamulo, Khristu adafa chabe"

Ngati ndi zotheka munthu kupeza moyo wosatha chifukwa chomvera malamulo kapena chilamulo cha Asirael chija, ndiye kuti Yesu Khristu anafa pachabe, koma sizili choncho ayi, lero ife tili pansi pa Chisomo osati Chilamulo, ndiyeno ndilankhule ndi inu okakamira ku chilamulo kunena kuti "Mulibe kanthu ndi Khristu, inu amene muyesedwa olungama ndi chilamulo; mudagwa posiyana nacho chisomo"_AGALATIYA 5:4
Chifukwa mukudziika nokha pansi pa chilamulo chimene winawake adachifera kale kuti akumasuleni, tsono mudagwa posiyana nacho Chisomo, komanso dziwani kuti: Aliyense amene akufuna kutumikira Mulungu monga mwa chilamulo, ali wamangawa kuchita chilamulo chonse". AGALATIYA 5:3. Ndipo akhala otembereredwa akasiyako zina (Agalatiya 3:10).
So pamene wagwira galasi ndi kudziona kuti ndiwe wakuda umakasamba madzi, tamverani, ndikunena kuti pamene mwagwira galasi ndi kuyamba kumadziona pagalasipo, ndipo mukaona kuti nkhope yanu ndi yakuda mumatenga madzi ndi kusamba kuchotsa kudako. Kodi ukaona Kuti ndiwe wakuda mumasamba galasi yomweyo ngati? ayi, galasi ntchito yake ndi kukuonetsa m'mene ulili, ndipo ukatero utenge Chinthu c
hina, madzi ndipo usambe, inde chilamulo ndi galasi ndipo mwazi wa Yesu Khristu ali madzi amene amatisambitsa ife kutichotsera uchimo. Kodi ndikadadziwa bwanji ine kuti Kusirira ndi uchimo, chilamulo chikadapanda kunena kuti usasirire?, nanga ndikadaona bwanji kuti ndine wakuda popanda galasi? Nanga ndikadakhala bwanji oyera popanda mwazi wa Yesu kunditsuka?. Atamandike Yesu Khristu wotisambitsa ku machimo onse.

Koma pali ka chinsinsi kena, anthu ena maso awo anaphimbidwa ndipo izi sadzamva ayi, inde, 2 AKORINTO 3:14-16 "koma mitima yao inaumitsidwa; pakuti kufikira lero lomwe lino, pa kuwerenga kwa pangano lakale chophimba chomwechi chikhalabe chosavundukuka, chimene chilikuchotsedwa mwa Khristu. Koma kufikira lero, pamene awerengedwa Mose, chophimba chigona pamtima pao. Koma pamene akatembenukira kwa Mulungu, chophimbacho chichotsedwa". Nkhani ya chilamulo sungamvetse ngati ukuyendabe mu standard ya chilamulo.

AGALATIYA 5:14 "Pakuti mau amodzi akwaniritsa chilamulo chonse ndiwo; Uzikonda mnzako monga udzikonda iwe mwini"

KODI NDIYE KUTI TISAMAWERENGE CHIPANGANO CHA KALE? 🤔. TIKUMANENSO MU GAWO INA YA NKHANIYI.

WE ARE NOT UNDER THE LAW-
OLEMBA: Domingos Anthony
🇲🇿 | CHURCH OF CHRIST

WE ARE NOT UNDER LAW - SITILI PANSI PA CHILAMULOMonga m'mene mumamvetsetsera kuti kupereka Nsembe za nyama kunatha chifu...
29/05/2026

WE ARE NOT UNDER LAW - SITILI PANSI PA CHILAMULO
Monga m'mene mumamvetsetsera kuti kupereka Nsembe za nyama kunatha chifukwa Yesu Khristu anatifera; ndikanakonda mutaimvetsetsanso iyi mosavuta.

Ndimanena mobwereza kunena kuti, chimodzi mwa zifukwa zimene anafera Paulo mtumwi, chinali chifukwa cha kulalikira Yesu yekha ndi kuwauza anthu kuti anamasulidwa ku chilamulo, ambiri amene ankamulondalonda anali Ayuda anzake osunga chilamulo mkumakana Yesu Khristu. Tikamanena za chilamulo tikunena za malamulo opezeka m'mabuku 5 oyambirira amene ndi chigawo choyamba cha Baibulo, m'menemo munali Malamulo okhudza: Kapembedzedwe, Kupereka nsembe za nyama, Paskha kapena maphwando a chipembedzo, zakudya zoletsedwa ndi zosaletsedwa, Sabata, mdulidwe... Ndi zina zambiri. Mulungu anapereka malamulo awa kwa ana a Israel kuti aziyenda nawo ndi kukhala m'menemo. Mvetsetsani kuti tikanena chilamulo sitikunena za malamulo khumi okha ayi, tikunena standard yonse imene Asirael ankayenda nayo ngati anthu a Mulungu.

Tisanapitirize dziwani kuti Mulungu ndi mwini mphamvu, ndi mwini ulamuliro, sauzidwa chochita ndi mwana wa munthu pansi pano, akapereka lamulo anthu amafunika amvere, ndipo akasintha lamulolo anthu amafunika amverenso chifukwa iyeyo ndi mwini ulamuliro wonse. Ndi chifukwa chake lero sitikupereka nsembe za nyama chifukwa mwini wake monga mwini ulamuliro anasintha.

AGALATIYA 3:23 "Koma chisanadze chikhulupiriro tinasungidwa pomvera lamulo otsekedwa kufikira chikhulupiriro chimene chikavumbulutsidwa bwinobwino".- Asanabwere Yesu Khristu kudzatifera tinali pansi pomvera chilamulo cha Mose, kufikira nthawi imene Yesu Khristu anabwera, ndipo chilamulo chinali mthunzi chabe wa kubwera kwa Yesu Khristu, ndipo Yesu Kristu atabwera anakwanilitsa chilamulo mwa kuchita zonse zimene chilamulo chinanena za iye. "Momwemo chilamulo chidakhala namkungwi wathu wakutifikitsa kwa Khristu, kuti tikayesedwe olungama ndi chikhulupiriro" AGALATIYA 3:24
- Chilamulo chinali ngati Namkungwi wotitsogolera kwa Yesu Kristu, wotipereka kwa Yesu Khristu kuti tikayesedwe olungama mwa chikhulupiliro. "Koma popeza chadza chikhulupiriro, sitikhalanso omvera namkungwi". Pakuti Yesu Khristu anabwera, sitikhalanso pansi pa chilamulo. AGALATIYA 3:25

AGALATIYA 4:4-5 "koma pokwaniridwa nthawi, Mulungu anatuma Mwana wake, wobadwa ndi mkazi, wobadwa wakumvera lamulo,
kuti akaombole iwo akumvera lamulo, kuti ife tikalandire umwana". Yesu Khristu anali myuda monga mwa thupi ndipo analinso omvera chilamulo, Koma Apa akunena kuti cholinga chake chinali kudzaombola anthu omvera chilamulo kuti akabadwenso nakalandire umwana atakhala pansi pa Chisomo osati pa chilamulo.

AROMA 7:4.6 "Chotero, abale anga, inunso munayesedwa akufa ku chilamulo ndi thupi la Khristu; kuti mukakhale ake a wina, ndiye amene anaukitsidwa kwa akufa, kuti ife timbalire Mulungu zipatso. Koma tsopano tinamasulidwa kuchilamulo, popeza tinafa kwa ichi chimene tinagwidwa nacho kale; chotero kuti titumikire mu mzimu watsopano, si m'chilembo chakale ai".

Ife sitili pansi pa chilamulo chimene Asirael ankayenda nacho ayi, ife tili pansi pa Chisomo chobwera kudzera mwa Yesu Khristu, Chifukwa cha kusadziwa anthu akumtumikira Mulungu pogwiritsa ntchito malamulo omwewo a kuletsedwa Kwa Kupereka nsembe za nyama, chifukwa cha kusadziwa anthu akumtumikira Mulungu m'chilembo cha kale osati mwa Mzimu,

AGALATIYA 5:1 "Khristu anatisandutsa mfulu, kuti tikhale mfulu; chifukwa chake chilimikani, musakodwenso ndi goli la ukapolo".

Yesu Khristu anatipanga ife amene tinakhulupirira dzina lake kukhala mfulu, ndife omasuliridwa ku chilamulo, tsono alipo anthu amene amakukokerani ku zomwezo za kale, ku zomwezo zimene Mulungu anatimasula kuti muzizichitirabe ukapolo, zimenezo ndi zanu, chifukwa Yesu Khristu anatimasula kale ku zomwezo. ndipo Wolemba buku la Chichewa la (Buku lopatulika ndilo Mau a Mulungu) mu Chapter 3 cha Agalatiya muli mau otsogolera akuti "Cilamulo sicikhoza kupulumutsa; cititsogoiera kutifikitsa kwa Kristu", komanso mu Chapter 4 muli mau otsogolera akuti "Uthenga Wabwino utimasula ku cilamulo". Kwa munthu wosankhidwa izi akhoza kumvetsa ndithu, Ndipo ndinene kuti kukhala pansi pa chilamulo masiku ano kuli ngati kumachita malamulo amene Nowa anapatsidwa oti amange chingalawa, izi ndi chifukwa cha kusadziwa nthawi za Baibulo, sadziwa kuti chikhristu chayambira pati m'baibulo, nanga chilamulo ndi chiti! sadziwa kuti timutumikire Mulungu pogwiritsa ntchito chiyani, Tangoganizani inu muli mchikristu mubwereranso bwanji mkumamvera malamulo a Nowa, nanga zikusiyana bwanji ndi malamulo a Mose?
MUTU WOTSATIRA: "NGATI SITILI PANSI PA CHILAMULO KOMA PA CHISOMO; NDI CHIFUKWA CHANI MABUKU A CHILAMULOWO ANAWAPHATIKIZA M'BAIBULO?".

Kodi chilamulo ndi chofunika?....... Tikumane mu gawo inayo.
Olemba: Domingos Anthony | CHURCH OF CHRIST

29/05/2026

TIKUKHALA NTHAWI YA MAKONO KOMA TISAKHALE CHIKHRISTU MWA MAKONO.

Inde, tikukhala mu nthawi imene zinthu ndi zosiyana kwambiri ndi kalekale, ndi zosiyana kwambiri ndi nthawi imene Ambuye Yesu anali pansi pano, ndi zosiyana kwambiri ndi nthawi imene makolo athu anali aang'ono. Tili mu nthawi ya Technology, tili munthawi ya zotanganitsa zambiri, ndipo tili mu nthawi ya makono. Komano ngakhale zili choncho, tili munthawi imene Chikhristu ndi chonyozeka kwambiri, nthawi imene Kupemphera mukuoneka ngati kutaya nthawi, koma ife amene tikudziwa chilungamo tikhale maso. tisakhale chikhristu chamakono.
Imagine pa zimene mumaonera pa social Media, Kodi mukhoza kulimba mtima kumpanga invite Yesu Khristu kuti adzaone nanu? Kodi ataona akhoza kusangalala nazo?. Kodi mavideo anu mu foni yanu Mulungu akamaona amasangalala? Nyimbo zimene mumamvera, atati Yesu Khristu akufuna kumvera nanu Kodi akhoza kusangalala nazo??

Tili mu nthawi ya makono koma tisakhale chikhristu chamakono lHOSEYA 4:6 Anthu anga aonongeka chifukwa cha kusadziwa"....

27/05/2026

2 AKORINTO 4:16 Chifukwa chake sitifooka; koma ungakhale umunthu wathu wakunja uvunda, wa m'kati mwathu ukonzedwa kwatsopano tsiku ndi tsiku.

27/05/2026

"Monga m'mene Mulungu anachitira Asirael, powamenyera nkhondo pamaso pa adani awo achite chimodzimodzi ndi ife "

THE BOOK OF ENOCH - ENOKIMunamvapo inu za buku la Enoki, limene ndi buku imene siitenga gawo m'mabuku a Baibulo, funso m...
26/05/2026

THE BOOK OF ENOCH - ENOKI
Munamvapo inu za buku la Enoki, limene ndi buku imene siitenga gawo m'mabuku a Baibulo, funso mkumati ndi chifukwa chani? Tsono ndi chifukwa chani buku la Enoki lili kunja kwa Baibulo?
Buku la Enoki ndi imodzi mwa mabuku akalekale kwambiri, ndi buku la chinsinsi kwambiri limene lili ndi maulosi ndi mabvumbulutso a kumwamba, kuphatikiza ku nkhani ya Angelo amphamvu komanso ma alliens, ndi zinthu zina zoopsa, akuti linabisidwa chifukwa limaulula zambiri zokhudza Mulungu, koma Kodi ndi Zoona kuti Mulungu analola kuti bukuli libisidwe ndi cholinga choti tingadziwe zinsinsi za kumwamba?

WHO IS ENOCH? - ENOKI NDI NDANI?

Tisanafotokoze za Buku la Enoki, tiyeni tione za Enoki, kuti anali ndani??.. Tiwerengere limodzi buku la Genesis 5:21-24
"Ndipo Enoki anakhala ndi moyo zaka makumi asanu ndi limodzi kudza zisanu, nabala Metusela: ndipo Enoki anayendabe ndi Mulungu, atabala Metusela, zaka mazana atatu, nabala ana aamuna ndi aakazi; masiku ake onse a Enoki anali mazana atatu kudza makumi asanu ndi limodzi ndi zisanu; ndipo Enoki anayendabe ndi Mulungu; ndipo panalibe iye; pakuti Mulungu anamtenga"

Enoki anali wa m'badwo wa number 7 kuchokera Kwa adamu, sanali munthu wamba ayi, Baibulo imatsikimiza kuti Enoki anayenda ndi Mulungu mpaka Mulungu anamutenga wa moyo, anali paubale wabwino ndi Mulungu, aneneri ena a Chipangano cha kale ananena kuti Enoki anali munthu wodabwitsa kwambiri ndipo Mulungu adamulenga kuti apange ntchito yapaderadera ya Mulungu, chifukwa cha chimenechi anthu ena amakhulupilira kuti Enoki anasiya buku la mabvumbulutso, la zinsinsi za Mulungu ndi Angelo, pokhala Kuti anali munthu wa special pamaso pa Mulungu. Mwina chifukwa cha kuopsa kwa chikhulupiliro chake mwina Mulungu sanalole kuti buku la Enoki liikedwe m'baibulo.

Koma Kodi buku la Enoki limati chiyani? Chimodzi mwa zinthu zopatsa chidwi ndi chakuti, monga mwa buku la Enoki, Chinthu chimene chinachitika chigumula chisanachitike, bukulo limanena kuti Angelo monga 200 anatsika pansi pano mkudzakwatira akazi okongola kwambiri, ndipo ndi mwa mtundu umeneu pamene kunabadwa ma Nephillis, zianthu zikuluzikulu, half human being half angel, zinayamba kuchulukana mwa changu kwambiri, sinayamba kumadya zouluka ndi za nyanja, kenako zinayamba kumadya ngakhale anthu, dziko linali litavunda, kufikira nthawi ya kumangidwa kwa chombo cha Nowa.
GENESIS 6:1-4 "Ndipo panali pamene anthu anayamba kuchuluka padziko, ndi ana akazi anawabadwira iwo, kuti ana amuna a Mulungu anayang'ana ana akazi a anthu, kuti iwo anali okongola; ndipo anadzitengera okha akazi onse amene anawasankha. Pa dziko lapansi panali anthu akulukulu masiku omwewo ndiponso pambuyo pake, ana amuna a Mulungu atalowa kwa ana akazi a anthu, ndipo anabalira iwo ana, amenewo ndiwo anthu amphamvu akalekale, anthu omveka".

Buku la Enoki limapitiriza kunena kuti
Angelowo anaphunzitsa akazi awo ndi Anthu ena za arts za ufiti, lupanga, zizindikiro, kupembedza nyenyezi, zida za nkhondo, komanso kubzala mitengo oti mkukhala mankhwala ochilitsa, monga mwa bukulo, chifukwa cha zimenezi chikhulupiliro cha anthu okhulupirira Mulungu chinayamba kuchepa ndipo zoipa zinkachitika tsiku lililonse. Buku la Enoki lamanena kuti Mulungu anatumiza Angelo ena amene anachita nkhondo ndi Angelo opandukirawa, ndipo anawamanga mkuwaponya kumalo a mdima kudikira chiweruzo, ndipo zitatero Mulungu anatumiza chigumula napulumutsa Nowa ndi banja lake". Chifukwa cha zimenezi anthu amakhulupilira kuti buku la Enoki ndi loona, monga mwa Genesis 6, ndipo anthu amenewa amanena kuti Mulungu sanalole kuti buku la Enoki lionekere kuti lingaulule zinsinsi zobisika zokhudza ma alliens amene timamva kuti amakhala mmagalax ena, mavesi ena a bululo amanena kuti Enoki ankapita kumwamba kukatenga ma information kwa Mulungu, za kulengedwa Kwa dziko, kubwera kwa Yesu, ndi mathero a dziko lapansi. Kalekale Akristu ophatikiza chikhristu ndi chikhalidwe, anaitenga bukulo ngati louziridwa ndi Mulungu koma kuyambira mu “century ya 9 AD" buku limeneli linasowa ndipo linapezekanso mu 1773 Mumpingo wa ku Ethiopia ndipo linatengedwera ku Europe kuti akaimasulire ndipo anthu anayambanso kuiwerenga.

Koma Kodi zimenezi ndi zoona? Kodi Mulungu angabisedi buku la munthu amene anamukonda mpaka kumutenga wa moyo kupita kumwamba? Chabwino ngati si louziridwa ndi Mulungu ndi chifukwa chani Yuda akunena za Enock.
YUDA 1:14:15 "Ndipo kwa iwo, Enoki, wachisanu ndi chiwiri kuyambira kwa Adamu, ananenera kuti, Taona, wadza Ambuye ndi oyera ake zikwi makumi, kudzachitira onse chiweruziro, ndi kutsutsa osapembedza onse, pa ntchito zao zonse zosapembedza, ndi pa zolimba zimene ochimwa osapembedza adalankhula pa Iye".

Ambiri amakhulupirira kuti Yuda sanatchule za buku la Enoki, Iye akungokumbukira zimene Enoki adanena, mfunso mkumati ngati mauwo sanali mbuku lililonse, Yuda anawadziwa bwanji kuti analembedwa patadutsa zaka mazana?. Chabwino, ngati bukulo linauziridwa ndi Mulungu, mkutheka analandira mauwo mwa bvumbulutso, Yuda sanene kuti akugwiritsa ntchito buku la Enoki, anangonena kuti Enoki analosera, Ndiye tikuona kuti Akristu atatsala makamaka amene anali otsatira chiphunzitso cha Yesu Khristu anali otsogoleredwa ndi “Canonical book” kapena mabukhu ouziridwa ndi Mulungu chimene chinawazindikiritsa Kuti adziwe ngati mabukuwo ndi ouziridwa ndi Mulungu anali mzimu woyera.

Buku la Enoki silinauziridwa ndi Mulungu, silikudziwika kuti linalembedwa liti, zikuonetsa kuti ndi winawake Amene analemba mu dzina la Enock, bukuli silitenga gawo m'baibulo, muli mau ena amene amatsutsana ndi mawu a Mulungu, Sikuti Amene analemba ndi Enoki wa m'baibulo uja ayi, munthuyu ankadziwa za moyo wa Enoki. Palibe umboni wakuti Enoki anasiya buku limene linapulumuka ku chigumula, kuti ifike masiku athu ano.

Kodi mukudziwa Kuti si buku la Enoki yokha imene inakaikiridwa kuti si youziridwa ndi Mulungu? mabukuwa timawatcha kuti "Mabuku a apokirifa", Tamverani,

Mabuku a Apokirifa (Apocrypha) ndi chiyani?

Mabuku a apokirifa ndi mabuku akale okhudzana ndi mbiri ya Ayuda ndi Akhristu, koma sali m’Baibulo la matchalitchi ena, ngakhale ena amawavomereza.
Mawu akuti “apokirifa” amatanthauza “obisika” kapena “osavomerezedwa mwalamulo”.

Mabuku a Apokirifa a Chipangano Chakale
Mabuku odziwika kwambiri ndi awa:
-Tobiti
-Yuditi
-Nzeru za Solomo
-Siraki (Ekleziyastiki)
-Baruki
-1 Makabeo
-2 Makabeo
-Zowonjezera za buku la Esteri
-Zowonjezera za Danieli (Susana, Bel ndi Chinjoka, Pemphero la Azariya)

Mabuku ena a apokirifa
Palinso mabuku ena akale omwe sanaphatikizidwe m’Baibulo ambiri:
-Buku la Enoki
-Buku la Jubileyi
-Uthenga wa Tomasi
-Uthenga wa Petro
-M’busa wa Heremu

Kusiyana kwa Baibulo pakati pa matchalitchi:

✝️ Katolika
Amavomereza mabuku a apokirifa ambiri
Amawatcha deuterocanonical books.

✝️ Chiprotestanti
Sagwiritsa ntchito mabuku a apokirifa m’Baibulo
Amangovomereza mabuku 66

✝️ Orthodox (Ethiopia)
Ali ndi Baibulo lalikulu kwambiri
Limaphatikizapo ngakhale Buku la Enoki.

- 📊 Baibulo mwachidule
📘 Baibulo la Katolika
Mabuku 73

📘 Baibulo la Chiprotestanti
Mabuku 66

📘 Baibulo la Orthodox Ethiopia
Mabuku oposa 80
2 TIMOTEO 3:16 "Lemba lililonse (lomwe lili mu Baibulo) adaliuzira Mulungu, ndipo lipindulitsa pa chiphunzitso, chitsutsano, chikonzero, chilangizo cha m'chilungamo".

Ambuye akudalitseni nonse
- Domingos Anthony

Endereço

Tete

Website

Notificações

Seja o primeiro a receber as novidades e deixe-nos enviar-lhe um email quando Dømingos Anthony publica notícias e promoções. O seu endereço de email não será utilizado para qualquer outro propósito, e pode cancelar a subscrição a qualquer momento.

Entre Em Contato Com O Negócio

Envie uma mensagem para Dømingos Anthony:

Compartilhar