28/09/2025
𝗖𝗛𝗜𝗙𝗨𝗞𝗪𝗔 𝗖𝗛𝗜𝗠𝗘𝗡𝗘 𝗠𝗨𝗟𝗨𝗡𝗚𝗨 𝗦𝗔𝗬𝗔𝗡𝗞𝗛𝗔 𝗣𝗘𝗠𝗣𝗛𝗘𝗥𝗢 𝗟𝗔 𝗠𝗨𝗡𝗧𝗛𝗨
Mwina nthawi inayake munadzifunsapo kuti: "Kodi ndi chifukwa chani Mulungu sanayankhe pemphero langa?"
Ndiye ndabwera kudzakuuzani chifukwa chimene Mulungu sayankha pemphero lanu
Nthawi yakumbukuyoyi muthawi ya Mneneri Yeremiya, ana a Israel makamaka amfuko la Yuda, anakumana ndi masautso oopsa, anakumana ndi njala, anakumana ndi nkhondo ndi zina zambiri, ndiyeno mtundu uwu unali kufuulira kwa Mulungu kuti awathandize, koma Mulungu sanawamvere.
Yeremiya Mneneri ankafuna kuwapempherera anthuwo kuti masautso awadutse, koma Mulungu analetsa.
Tiwerenge
"Kenaka Yehova anandiwuza kuti, “Usawapempherere anthu awa kuti zinthu ziwayendere bwino. Ngakhale asale zakudya, Ine sindidzamva kulira kwawo; ngakhale apereke nsembe zopsereza ndi chopereka cha chakudya, sindidzazilandira. Mʼmalo mwake, ndidzawapha ndi lupanga, njala ndi mliri.”
Yeremiya 14:11-12
Abale, Mulungu anati "Ngakhale 'asale kudya', ine sindidzamva pemphero lawo, ndipo ngakhale apereke msembe ine sindidzalandira msembe zawo.
Chonde werengani bwinobwino Ndinso modekha,
apa tikuona kuti Mulungu anakana kuti Yeremiya apempherere anthu aja, ndipo werenganinso vs iyi: "Choncho iwe Yeremiya usawapempherere anthu awa ngakhale kuwapepesera kapenanso kuwapembedzera; usandidandaulire, chifukwa Ine sindidzakumvera.
Yeremiya 7:16
Mulungu anamuuzitsitsa Yeremiya kuti: "Usawapemphere awa, ndipo ngakhale upemphere 'Ine sindidzakumvera'😭
Koma ndi chifukwa chani Mulungu anakanitsitsa chotere kuthandiza anthu ake omwe?
Tiwerengenso ves iyi: "Kenaka Yehova anandiwuza kuti, “Ngakhale Mose ndi Samueli akanayima pamaso panga kupempherera anthu awa, Ine sindikanawachitira chisoni. Achotseni ndipo ndisawaonenso! Aleke apite! ”
Yeremiya 15:1
Mulungu kuchita kunena kuti: "Ngakhale Mose ndi Samuel atabwera kudzapemphera anthu awa ine singamvere".
Abale mukhoza kumapemphererana, koma Mulungu atakana kumvera pemphero lanu inu musanapemphere.
koma tiyeni tiyendere limodzi, tidziwe chifukwa chimene Mulungu amalankhulira mau oopsa ngati awa.
Tiwerenge
"Maso anga akuona makhalidwe awo onse; sanabisike pamaso panga. Palibe tchimo limene sindikulidziwa.
Yeremiya 16:17
Yaa, apa tatha kuona chimene chinkapangitsa kuti Mulungu akane kumvera kufuula kwa aisrael.
Mulungu sanamvere chifukwa cha "Chimo", anali anthu amwano pamaso pa Mulungu, amene ankapanga zonyansa zambiri, Ndi chifukwa chake anakwiitsa Mulungu ndipo Mulungu sanafuna kuwamveranso.
Abale ndi alongo ndi maulendo angati amene mwapemphera koma simunayankhidwe?
Ndi maulendo angati amene mwasala kudya kuti chinachake chiyende bwino koma sichinayende?
Ok, Mu zonsezi munayamba mwadzifufuzapo? Munayamba mwadziona mkati mwanumo?.
Ine, ndikhoza kukupemphererani, koma Mulungu sangamvere ngati inu eni bvuto muli ndi chimo mkati mwanu, Mulungu sangayankhe chifukwa inu muli ndi "Chimo",
Dziwani kuti 'Mulungu sangapereke zosowa za moyo wanu ngati inu simunadzipereke kwa Iye".
Chimo limatilekanitsa ndi Mulungu, ndipo timakhala kutalitali ndi Mulungu, ndipo tikampemphera timaona ngati makutu a Mulungu atsekeka, koma baibulo limati: "Ayi, sikuti makutu a Mulungu atsekeka, Koma machimo anu akusiyanitsani ndi Mulungu wanu".
Musanapempherere muzidzifufuza kaye, Mukhoza kusala kudya, mukhoza kulimbikira kaya kupemphera, kaya kulimbikira kupereka chopereka, koma ngati mkati mwanumo muli ndi chimo, Mulungu samvera pemphero lanu, Mukhale mukudziwa chimenechi.
Yang'anirani mayendedwe anu, yang'anirai mabvalidwe anu, Kodi mumabvala ngati wokhulupirira?, Musasandutse kachisi wa Mulungu kukhala wa Ziwandaaaa, Pakuti mnyumba ya Mulungu ndi yoyera ndipo ndi inu mukuwerenganu.
Ndiye ngati muli nacho cholakwa chimene mukuchidziwa "Lapani" Mupemphereredwe kuti Mulungu akhululukire chimo lanu.
.
If you want WhatsApp Group take this namber and call me on WhatsApp.......+258 860867086.
MUKHALE NDI TSIKU LABWINO NONSE
My Writer Anthony