Dømingos Anthony

Dømingos Anthony Informações para nos contactar, mapa e direções, formulário para nos contactar, horário de funcionamento, serviços, classificações, fotos, vídeos e anúncios de Dømingos Anthony, Produtor de vídeo, Tete.
(1)

22/10/2025

Mukhale odzichepetsa kwathunthu ndi ofatsa; mukhale oleza mtima, ololerana wina ndi mnzake mwachikondi.
Aefeso 4:2

22/10/2025

"Momwemonso akazi akhale olemekezeka, osadierekeza, odzisunga, okhulupirika m'zonse"
1 TIMOTEO 3:11

13/10/2025

🙏
Church of Christ - Central Region Youth Ministry

08/10/2025

‎ “Nzeru Yochokera Kumwamba”

‎📖 Mawu a tsiku: Yakobo 3:17

‎> “Koma nzeru yochokera kumwamba iyamba kukhala yoyera, nikhalanso yamtendere, yaulere, yomvera bwino, yodzala chifundo ndi zipatso zabwino, yopanda tsankho, yosadzikometsera pamaso.”

‎1. Tanthauzo la “Nzeru Yochokera Kumwamba”

‎Nzeru yochokera kumwamba ndi nzeru imene imachokera kwa Mulungu, osati ku luntha la anthu.
‎Munthu wokhala ndi nzeru imeneyi amadziwika ndi chikhalidwe chake — amakhala wamtendere, wachifundo, wosakonda mikangano, komanso wokonda anthu onse.
‎Nzeru imeneyi imapangitsa munthu kukhala wachikondi, womasuka, komanso wopanda kudzikuza.

‎ 2. Zizindikiro za Nzeru Yochokera Kumwamba

‎1. Yoyera – imachokera ku mtima wosakonda tchimo.


‎2. Yamtendere – imafuna mtendere osati mikangano.

‎3. Yaulere (yofatsa) – imasonyeza chikondi ndi kuleza mtima.

‎4. Yomvera bwino – imavomereza choonadi ndi malangizo.

‎5. Yodzala chifundo ndi zipatso zabwino – imachita zabwino ndi kuthandiza ena.

‎6. Yopanda tsankho – imachitira aliyense mofanana.

‎7. Yosadzikometsera pamaso – si yofuna kutchuka kapena ulemu wa anthu.

‎3. Zimene Nzeru Ya Kumwamba Imachita Mu Moyo Wathu
‎Imasintha momwe timaganizira ndi kulankhulira.
‎Imabweretsa mtendere m’banja, m’gulu, komanso m’mpingo.
‎Imatithandiza kuchita zinthu ndi mtima woyera, osati chifukwa cha phindu.
‎Imatipangitsa kukhala owoneka ngati ana a Mulungu m’dziko lodzaza ndi chisokonezo.

‎4. Kuganizira kwa Moyo

‎> Kodi zomwe ndikuchita masiku ano zimasonyeza nzeru ya kumwamba kapena ya dziko?
‎Kodi mawu anga ndi zochita zanga zimabweretsa mtendere kapena chisokonezo?
‎Kodi ndikuchitira aliyense mofanana, ngakhale amene sali ngati ine?

‎5. Pemphero

‎> Ambuye Mulungu,
‎Ndipatseni nzeru yochokera kwa Inu —
‎nzeru yoyera, yamtendere, yodzala chifundo.
‎Ndithandizeni kukhala munthu wosakhumba kutchuka,
‎koma wokonda mtendere ndi chikondi.
‎Ndithandizeni kukhala chitsanzo cha nzeru ya kumwamba
‎kwa ena m’moyo wanga wa tsiku ndi tsiku.

‎Mu

07/10/2025

Kodi moyo ndi chani?

05/10/2025

Kale kale, panali mwamuna wosauka dzina lake Samuel. Tsiku lina madzulo, anapita kumanda komwe mwana wake wamkazi anamwalira. Anakhala pansi pafupi ndi manda, akuyang’ana duwa limene anayika pa tsiku la maliro — tsopano linali loyamba kutuluka.

Samuel anayang’ana kumwamba, mtima wake wodzaza ndi chisoni, ndipo ananena mwakachetechete:
— Ambuye, chifukwa chiyani mwamutenga msanga chonchi?

Pamene misozi inali ikuyenda m’maso mwake, anakumbukira mmene mwana wake ankaseka komanso mmene ankakonda kupemphera. Nthawi yomweyo anazindikira kuti ngakhale thupi la mwana lili pansi pano, mzimu wake uli ndi Mulungu.

Ananyamuka, anafutukula maso ake, nati:
— Zikomo, Ambuye. Ndikupitiriza kukhala ndi chiyembekezo.

Nthawi yomweyo, dzuwa linatuluka kuchokera mu mitambo. 🌅

Vesi:

> “Kulira kungakhale usiku wonse, koma chimwemwe chimabwera m'mawa.”
— Salimo 30:5

03/10/2025

"UBWINO WOKWATIRA MKAZI WOKONDA PEMPHERO"

1. Asanapange chilichonse amamuuza Mulungu kuti amutsogoleri a mutetezere ndi kumpatsa zisomo
2. Ngakhale iwe usakudziwa amakuyikiza m'mapemphero kuti Mulungu akutetezere akutsogoleri ndi wokupatsa zisomo
3. Umakhala ngati wakwatira mwana wa mfumu muzambiri kumakonderedwa
4. Mukamuthwera mtima ndikumukhumudwitsa sathamangira kukweza kuti muyambe phokoso amapinda mahondo ake pansi mwamseli iwo sakudziwa Mulungu ndi kumpempha Mulungu zoyenela kuchita ndi mmene angachitile kuti mulumikizananso
5. Mukakumana ndi mavuto amakulimbikitsa komanso kuukumbutsa kuti Mulungu ndiye thandizo ndipo nthawira panu
6. Mulungu amamupatsa nzeru zochuluka upangiri wabwino wosamalira nyumba yanu yonse
7. Amakhalabe okongola nthawi zonse chifukwa amayenda ndi Mzimu woyera omwe umawala pa iye.
8. Mkazi wa pemphero Ndi golide chuma chenicheni chopezekeratu chomwe anthu ambiri amakhala akuchisaka koma samachipeza mophweka.
9. Madalitso amene Mulungu amamukhutulira amakhala a nonse ndipo odalitsidwa ndi Mulungu satembereredwa. .
Akazinu.. m'mapemphera? Dziwani kuti banja labwino limakoma ngati nonse mumaopa Mulungu. Chisankho chanu cha lero chikhoza kukhala minga yanu pa mawa ngati simungapange Check za ubale wa nzanuyo ndi Mulungu.
TRUTHS SET'S FREE

28/09/2025

𝗖𝗛𝗜𝗙𝗨𝗞𝗪𝗔 𝗖𝗛𝗜𝗠𝗘𝗡𝗘 𝗠𝗨𝗟𝗨𝗡𝗚𝗨 𝗦𝗔𝗬𝗔𝗡𝗞𝗛𝗔 𝗣𝗘𝗠𝗣𝗛𝗘𝗥𝗢 𝗟𝗔 𝗠𝗨𝗡𝗧𝗛𝗨
Mwina nthawi inayake munadzifunsapo kuti: "Kodi ndi chifukwa chani Mulungu sanayankhe pemphero langa?"
Ndiye ndabwera kudzakuuzani chifukwa chimene Mulungu sayankha pemphero lanu
Nthawi yakumbukuyoyi muthawi ya Mneneri Yeremiya, ana a Israel makamaka amfuko la Yuda, anakumana ndi masautso oopsa, anakumana ndi njala, anakumana ndi nkhondo ndi zina zambiri, ndiyeno mtundu uwu unali kufuulira kwa Mulungu kuti awathandize, koma Mulungu sanawamvere.
Yeremiya Mneneri ankafuna kuwapempherera anthuwo kuti masautso awadutse, koma Mulungu analetsa.
Tiwerenge
"Kenaka Yehova anandiwuza kuti, “Usawapempherere anthu awa kuti zinthu ziwayendere bwino. Ngakhale asale zakudya, Ine sindidzamva kulira kwawo; ngakhale apereke nsembe zopsereza ndi chopereka cha chakudya, sindidzazilandira. Mʼmalo mwake, ndidzawapha ndi lupanga, njala ndi mliri.”
Yeremiya 14:11-12
Abale, Mulungu anati "Ngakhale 'asale kudya', ine sindidzamva pemphero lawo, ndipo ngakhale apereke msembe ine sindidzalandira msembe zawo.
Chonde werengani bwinobwino Ndinso modekha,
apa tikuona kuti Mulungu anakana kuti Yeremiya apempherere anthu aja, ndipo werenganinso vs iyi: "Choncho iwe Yeremiya usawapempherere anthu awa ngakhale kuwapepesera kapenanso kuwapembedzera; usandidandaulire, chifukwa Ine sindidzakumvera.
Yeremiya 7:16
Mulungu anamuuzitsitsa Yeremiya kuti: "Usawapemphere awa, ndipo ngakhale upemphere 'Ine sindidzakumvera'😭
Koma ndi chifukwa chani Mulungu anakanitsitsa chotere kuthandiza anthu ake omwe?
Tiwerengenso ves iyi: "Kenaka Yehova anandiwuza kuti, “Ngakhale Mose ndi Samueli akanayima pamaso panga kupempherera anthu awa, Ine sindikanawachitira chisoni. Achotseni ndipo ndisawaonenso! Aleke apite! ”
Yeremiya 15:1
Mulungu kuchita kunena kuti: "Ngakhale Mose ndi Samuel atabwera kudzapemphera anthu awa ine singamvere".
Abale mukhoza kumapemphererana, koma Mulungu atakana kumvera pemphero lanu inu musanapemphere.
koma tiyeni tiyendere limodzi, tidziwe chifukwa chimene Mulungu amalankhulira mau oopsa ngati awa.
Tiwerenge
"Maso anga akuona makhalidwe awo onse; sanabisike pamaso panga. Palibe tchimo limene sindikulidziwa.
Yeremiya 16:17
Yaa, apa tatha kuona chimene chinkapangitsa kuti Mulungu akane kumvera kufuula kwa aisrael.
Mulungu sanamvere chifukwa cha "Chimo", anali anthu amwano pamaso pa Mulungu, amene ankapanga zonyansa zambiri, Ndi chifukwa chake anakwiitsa Mulungu ndipo Mulungu sanafuna kuwamveranso.
Abale ndi alongo ndi maulendo angati amene mwapemphera koma simunayankhidwe?
Ndi maulendo angati amene mwasala kudya kuti chinachake chiyende bwino koma sichinayende?
Ok, Mu zonsezi munayamba mwadzifufuzapo? Munayamba mwadziona mkati mwanumo?.
Ine, ndikhoza kukupemphererani, koma Mulungu sangamvere ngati inu eni bvuto muli ndi chimo mkati mwanu, Mulungu sangayankhe chifukwa inu muli ndi "Chimo",
Dziwani kuti 'Mulungu sangapereke zosowa za moyo wanu ngati inu simunadzipereke kwa Iye".
Chimo limatilekanitsa ndi Mulungu, ndipo timakhala kutalitali ndi Mulungu, ndipo tikampemphera timaona ngati makutu a Mulungu atsekeka, koma baibulo limati: "Ayi, sikuti makutu a Mulungu atsekeka, Koma machimo anu akusiyanitsani ndi Mulungu wanu".
Musanapempherere muzidzifufuza kaye, Mukhoza kusala kudya, mukhoza kulimbikira kaya kupemphera, kaya kulimbikira kupereka chopereka, koma ngati mkati mwanumo muli ndi chimo, Mulungu samvera pemphero lanu, Mukhale mukudziwa chimenechi.
Yang'anirani mayendedwe anu, yang'anirai mabvalidwe anu, Kodi mumabvala ngati wokhulupirira?, Musasandutse kachisi wa Mulungu kukhala wa Ziwandaaaa, Pakuti mnyumba ya Mulungu ndi yoyera ndipo ndi inu mukuwerenganu.
Ndiye ngati muli nacho cholakwa chimene mukuchidziwa "Lapani" Mupemphereredwe kuti Mulungu akhululukire chimo lanu.
.
If you want WhatsApp Group take this namber and call me on WhatsApp.......+258 860867086.

MUKHALE NDI TSIKU LABWINO NONSE
My Writer Anthony

Endereço

Tete

Website

Notificações

Seja o primeiro a receber as novidades e deixe-nos enviar-lhe um email quando Dømingos Anthony publica notícias e promoções. O seu endereço de email não será utilizado para qualquer outro propósito, e pode cancelar a subscrição a qualquer momento.

Entre Em Contato Com O Negócio

Envie uma mensagem para Dømingos Anthony:

Compartilhar