26/05/2026
THE BOOK OF ENOCH - ENOKI
Munamvapo inu za buku la Enoki, limene ndi buku imene siitenga gawo m'mabuku a Baibulo, funso mkumati ndi chifukwa chani? Tsono ndi chifukwa chani buku la Enoki lili kunja kwa Baibulo?
Buku la Enoki ndi imodzi mwa mabuku akalekale kwambiri, ndi buku la chinsinsi kwambiri limene lili ndi maulosi ndi mabvumbulutso a kumwamba, kuphatikiza ku nkhani ya Angelo amphamvu komanso ma alliens, ndi zinthu zina zoopsa, akuti linabisidwa chifukwa limaulula zambiri zokhudza Mulungu, koma Kodi ndi Zoona kuti Mulungu analola kuti bukuli libisidwe ndi cholinga choti tingadziwe zinsinsi za kumwamba?
WHO IS ENOCH? - ENOKI NDI NDANI?
Tisanafotokoze za Buku la Enoki, tiyeni tione za Enoki, kuti anali ndani??.. Tiwerengere limodzi buku la Genesis 5:21-24
"Ndipo Enoki anakhala ndi moyo zaka makumi asanu ndi limodzi kudza zisanu, nabala Metusela: ndipo Enoki anayendabe ndi Mulungu, atabala Metusela, zaka mazana atatu, nabala ana aamuna ndi aakazi; masiku ake onse a Enoki anali mazana atatu kudza makumi asanu ndi limodzi ndi zisanu; ndipo Enoki anayendabe ndi Mulungu; ndipo panalibe iye; pakuti Mulungu anamtenga"
Enoki anali wa m'badwo wa number 7 kuchokera Kwa adamu, sanali munthu wamba ayi, Baibulo imatsikimiza kuti Enoki anayenda ndi Mulungu mpaka Mulungu anamutenga wa moyo, anali paubale wabwino ndi Mulungu, aneneri ena a Chipangano cha kale ananena kuti Enoki anali munthu wodabwitsa kwambiri ndipo Mulungu adamulenga kuti apange ntchito yapaderadera ya Mulungu, chifukwa cha chimenechi anthu ena amakhulupilira kuti Enoki anasiya buku la mabvumbulutso, la zinsinsi za Mulungu ndi Angelo, pokhala Kuti anali munthu wa special pamaso pa Mulungu. Mwina chifukwa cha kuopsa kwa chikhulupiliro chake mwina Mulungu sanalole kuti buku la Enoki liikedwe m'baibulo.
Koma Kodi buku la Enoki limati chiyani? Chimodzi mwa zinthu zopatsa chidwi ndi chakuti, monga mwa buku la Enoki, Chinthu chimene chinachitika chigumula chisanachitike, bukulo limanena kuti Angelo monga 200 anatsika pansi pano mkudzakwatira akazi okongola kwambiri, ndipo ndi mwa mtundu umeneu pamene kunabadwa ma Nephillis, zianthu zikuluzikulu, half human being half angel, zinayamba kuchulukana mwa changu kwambiri, sinayamba kumadya zouluka ndi za nyanja, kenako zinayamba kumadya ngakhale anthu, dziko linali litavunda, kufikira nthawi ya kumangidwa kwa chombo cha Nowa.
GENESIS 6:1-4 "Ndipo panali pamene anthu anayamba kuchuluka padziko, ndi ana akazi anawabadwira iwo, kuti ana amuna a Mulungu anayang'ana ana akazi a anthu, kuti iwo anali okongola; ndipo anadzitengera okha akazi onse amene anawasankha. Pa dziko lapansi panali anthu akulukulu masiku omwewo ndiponso pambuyo pake, ana amuna a Mulungu atalowa kwa ana akazi a anthu, ndipo anabalira iwo ana, amenewo ndiwo anthu amphamvu akalekale, anthu omveka".
Buku la Enoki limapitiriza kunena kuti
Angelowo anaphunzitsa akazi awo ndi Anthu ena za arts za ufiti, lupanga, zizindikiro, kupembedza nyenyezi, zida za nkhondo, komanso kubzala mitengo oti mkukhala mankhwala ochilitsa, monga mwa bukulo, chifukwa cha zimenezi chikhulupiliro cha anthu okhulupirira Mulungu chinayamba kuchepa ndipo zoipa zinkachitika tsiku lililonse. Buku la Enoki lamanena kuti Mulungu anatumiza Angelo ena amene anachita nkhondo ndi Angelo opandukirawa, ndipo anawamanga mkuwaponya kumalo a mdima kudikira chiweruzo, ndipo zitatero Mulungu anatumiza chigumula napulumutsa Nowa ndi banja lake". Chifukwa cha zimenezi anthu amakhulupilira kuti buku la Enoki ndi loona, monga mwa Genesis 6, ndipo anthu amenewa amanena kuti Mulungu sanalole kuti buku la Enoki lionekere kuti lingaulule zinsinsi zobisika zokhudza ma alliens amene timamva kuti amakhala mmagalax ena, mavesi ena a bululo amanena kuti Enoki ankapita kumwamba kukatenga ma information kwa Mulungu, za kulengedwa Kwa dziko, kubwera kwa Yesu, ndi mathero a dziko lapansi. Kalekale Akristu ophatikiza chikhristu ndi chikhalidwe, anaitenga bukulo ngati louziridwa ndi Mulungu koma kuyambira mu “century ya 9 AD" buku limeneli linasowa ndipo linapezekanso mu 1773 Mumpingo wa ku Ethiopia ndipo linatengedwera ku Europe kuti akaimasulire ndipo anthu anayambanso kuiwerenga.
Koma Kodi zimenezi ndi zoona? Kodi Mulungu angabisedi buku la munthu amene anamukonda mpaka kumutenga wa moyo kupita kumwamba? Chabwino ngati si louziridwa ndi Mulungu ndi chifukwa chani Yuda akunena za Enock.
YUDA 1:14:15 "Ndipo kwa iwo, Enoki, wachisanu ndi chiwiri kuyambira kwa Adamu, ananenera kuti, Taona, wadza Ambuye ndi oyera ake zikwi makumi, kudzachitira onse chiweruziro, ndi kutsutsa osapembedza onse, pa ntchito zao zonse zosapembedza, ndi pa zolimba zimene ochimwa osapembedza adalankhula pa Iye".
Ambiri amakhulupirira kuti Yuda sanatchule za buku la Enoki, Iye akungokumbukira zimene Enoki adanena, mfunso mkumati ngati mauwo sanali mbuku lililonse, Yuda anawadziwa bwanji kuti analembedwa patadutsa zaka mazana?. Chabwino, ngati bukulo linauziridwa ndi Mulungu, mkutheka analandira mauwo mwa bvumbulutso, Yuda sanene kuti akugwiritsa ntchito buku la Enoki, anangonena kuti Enoki analosera, Ndiye tikuona kuti Akristu atatsala makamaka amene anali otsatira chiphunzitso cha Yesu Khristu anali otsogoleredwa ndi “Canonical book” kapena mabukhu ouziridwa ndi Mulungu chimene chinawazindikiritsa Kuti adziwe ngati mabukuwo ndi ouziridwa ndi Mulungu anali mzimu woyera.
Buku la Enoki silinauziridwa ndi Mulungu, silikudziwika kuti linalembedwa liti, zikuonetsa kuti ndi winawake Amene analemba mu dzina la Enock, bukuli silitenga gawo m'baibulo, muli mau ena amene amatsutsana ndi mawu a Mulungu, Sikuti Amene analemba ndi Enoki wa m'baibulo uja ayi, munthuyu ankadziwa za moyo wa Enoki. Palibe umboni wakuti Enoki anasiya buku limene linapulumuka ku chigumula, kuti ifike masiku athu ano.
Kodi mukudziwa Kuti si buku la Enoki yokha imene inakaikiridwa kuti si youziridwa ndi Mulungu? mabukuwa timawatcha kuti "Mabuku a apokirifa", Tamverani,
Mabuku a Apokirifa (Apocrypha) ndi chiyani?
Mabuku a apokirifa ndi mabuku akale okhudzana ndi mbiri ya Ayuda ndi Akhristu, koma sali m’Baibulo la matchalitchi ena, ngakhale ena amawavomereza.
Mawu akuti “apokirifa” amatanthauza “obisika” kapena “osavomerezedwa mwalamulo”.
Mabuku a Apokirifa a Chipangano Chakale
Mabuku odziwika kwambiri ndi awa:
-Tobiti
-Yuditi
-Nzeru za Solomo
-Siraki (Ekleziyastiki)
-Baruki
-1 Makabeo
-2 Makabeo
-Zowonjezera za buku la Esteri
-Zowonjezera za Danieli (Susana, Bel ndi Chinjoka, Pemphero la Azariya)
Mabuku ena a apokirifa
Palinso mabuku ena akale omwe sanaphatikizidwe m’Baibulo ambiri:
-Buku la Enoki
-Buku la Jubileyi
-Uthenga wa Tomasi
-Uthenga wa Petro
-M’busa wa Heremu
Kusiyana kwa Baibulo pakati pa matchalitchi:
✝️ Katolika
Amavomereza mabuku a apokirifa ambiri
Amawatcha deuterocanonical books.
✝️ Chiprotestanti
Sagwiritsa ntchito mabuku a apokirifa m’Baibulo
Amangovomereza mabuku 66
✝️ Orthodox (Ethiopia)
Ali ndi Baibulo lalikulu kwambiri
Limaphatikizapo ngakhale Buku la Enoki.
- 📊 Baibulo mwachidule
📘 Baibulo la Katolika
Mabuku 73
📘 Baibulo la Chiprotestanti
Mabuku 66
📘 Baibulo la Orthodox Ethiopia
Mabuku oposa 80
2 TIMOTEO 3:16 "Lemba lililonse (lomwe lili mu Baibulo) adaliuzira Mulungu, ndipo lipindulitsa pa chiphunzitso, chitsutsano, chikonzero, chilangizo cha m'chilungamo".
Ambuye akudalitseni nonse
- Domingos Anthony