Madolo Multimedia

Madolo Multimedia Arts & Entertainment | Sports | Gossips | Politics | Developments | PR & Marketing | Research | Media Consultancy
(4)

Katswiri woimba wa chamba cha afro kell Kay watulutsa kanema wa nyimbo yake ya Ndalila kutsatira pempho kuchokera kwa om...
11/09/2026

Katswiri woimba wa chamba cha afro kell Kay watulutsa kanema wa nyimbo yake ya Ndalila kutsatira pempho kuchokera kwa omutsatila ake pa Masamba a Mchezo.

Izi zadza woimbayu atatulutsa nyimboyi koma yomvera ndipo omutsatilawa anakakamiza katswiriyu kuti atulutse kanema wa nyimboyi ndipo izi zachitika.

Malinga ndi Kall Kay panali chikonzero kuti nyimboyi itulutsidwe
pakangodutsa sabata imodzi ndipo zonse zinali kale mchimake

Pakadali pano kanema wa ndalira akuthamanga kwambiri pa Masamba a intaneti monga you tube komanso anthu ambiri akukamba zabwino za nyimboyi.

Katswiri Osewera pakati ku timu ya dziko lino ya the scorchers yemwe amatumikira timu ya ZISD Football club ya dziko la ...
11/09/2026

Katswiri Osewera pakati ku timu ya dziko lino ya the scorchers yemwe amatumikira timu ya ZISD Football club ya dziko la Zambia Tendai Sane wabwerera ku timu yake kutsatira kutha kwa mpikitsano wa maiko amuno mu africa ( WAFCON)

Tendai Sane wanyamuka lero pomwe ligi yaku zambia ya Zambia Women Premier Soccer ligi ikhale ikuyamba posachedwa

Sane wakhala katswiri odalilika ku timuyi pomwe wayithandiza kuti isatuluke mu ligi yaku zambia Season yatha

Pomwe ikukonzekera kukumana ndi Mighty Wanderers Lamlungu mu mpikisano wa CAF Champions League, Simba SC yapereka mphats...
11/09/2026

Pomwe ikukonzekera kukumana ndi Mighty Wanderers Lamlungu mu mpikisano wa CAF Champions League, Simba SC yapereka mphatso kwa ana amasiye ku Mwandaliwa Orphanage Center ku Mbweni, Dar es Salaam.

Timuyi yati, yapanga Izi pofuna kuti mulungu awadalitse kuti azaphwanye Manoma lamlungu.

MUTHARIKA WAPEMPHA MGWIRIZANO PAKATI PA BOMA NDI OCHITA MALONDAPulezidenti wa dziko lino, Pulofesa Arthur Peter Mutharik...
11/09/2026

MUTHARIKA WAPEMPHA MGWIRIZANO PAKATI PA BOMA NDI OCHITA MALONDA

Pulezidenti wa dziko lino, Pulofesa Arthur Peter Mutharika, wapempha kuti boma lipitirize kugwirizana ndi mabungwe azamalonda pofuna kupititsa patsogolo chitukuko cha dziko lino.

Mutharika wanena izi lero ku Kamuzu Palace mu mzinda wa Lilongwe atakumana ndi nthumwi za bungwe la Malawi Confederation of Chambers of Commerce and Industry (MCCCI).

Pamsonkhanowu, Mutharika wati boma ndi mabungwe azamalonda akuyenera kugwirizana pothana ndi mavuto azachuma komanso kutukula ntchito za zachuma mdziko muno.

Mkulukutamoyo watinso kukumana kwake ndi MCCCI kunali kofunika chifukwa mbali zonse zakambirana za ndalama zakunja, ndalama zolowa m’dziko, malonda komanso chitukuko cha dziko.

11/09/2026

M'phunzitsi ogwilizira wa timu ya Mighty Wanderers MacDonald Nginde Mtetemera wati, ali ndi chikhulupiliro kuti apambana masewero omwe akusewera ndi timu ya Simba lamulungu pa 13 September.

Nginde wati, timuyi yakonza zofooka zomwe anaziona mumasewero omwe anasewera pa Bingu National Stadium ndipo anyamata awonetsa njala yofuna kupweteka timu ya Simba.

đź“·TIMES 360 MW

Katswiri osewera kutsogolo yemwe mgwilizano wake watha ndi timu ya Zanaco FC yaku Zambia Robert Saizi, sopano walowa mu ...
11/09/2026

Katswiri osewera kutsogolo yemwe mgwilizano wake watha ndi timu ya Zanaco FC yaku Zambia Robert Saizi, sopano walowa mu mgwilizano ndi timu ya Silver Strikers.

Saizi wasaina kuti atumikira timuyi mpakana kumapeto kwa chaka cha mpira (football season) cha 2026-2027 ndipo pali mwayi oti atha kuzaonjezera.

Saizi asanapite ku Zambia, anasewerapo mu timu ya Bangwe All Stars nthawi yomwe inali mu TNM Super League.

11/09/2026

Inos Chatama yemwe ndi mphunzitsi wa timu ya dziko lino koma osewera ake kukhala osaposera zaka makumi awiri kuyakhulapo pomwe timuyi ikukozekera mpikitsano wa Cosafa cup

Ada Bwana Micium Mhone kuzitolera mphamvu pamene akudikira Mighty Wanderers kuti ibweleko ku Tanzania, ndipo azaswane pa...
11/09/2026

Ada Bwana Micium Mhone kuzitolera mphamvu pamene akudikira Mighty Wanderers kuti ibweleko ku Tanzania, ndipo azaswane pa 19 September pa Nankhaka Stadium.

Tanzania U20 Women Bow Out of World Cup Without a PointTanzania’s U20 women’s football side has bowed out of the FIFA U2...
11/09/2026

Tanzania U20 Women Bow Out of World Cup Without a Point

Tanzania’s U20 women’s football side has bowed out of the FIFA U20 Women’s World Cup in Poland after suffering defeat in all three group matches.

The team conceded a total of 13 goals during the tournament. Despite the results, Tanzania’s qualification marked an important milestone, as they were one of four African nations to reach the finals in Poland

 : Bungwe la Malawi Law Society lati nalo silikuyimva ndipo lalowa nawo mu gulu lowunikila chiletso chomwe a Austin Mkok...
11/09/2026

: Bungwe la Malawi Law Society lati nalo silikuyimva ndipo lalowa nawo mu gulu lowunikila chiletso chomwe a Austin Mkoka anakatenga ku bwalo la milandu choletsa sipikala wa nyumba ya malamulo a Sameer Suleman kukhazikitsa makomiti oti afufuze za katangale muma kampane a boma.

Purezidenti wa MLS, Davis Njobvu, wati bungweli lasankha kulowa nawo pa mlanduwu chifukwa ukukhudza malamulo a m’dziko, kuphatikizapo mfundo ya kugawikana kwa mphamvu pakati pa nthambi za boma

Njobvu wati, pakanali pano akumalizitsa zikalata zofunikira, zomwe adzapereke ku khoti zofotokoza chifukwa chomwe bungweli likufunila kutenga nawo mbali pa nkhaniyi.

Address

Nol
Lilongwe

Alerts

Be the first to know and let us send you an email when Madolo Multimedia posts news and promotions. Your email address will not be used for any other purpose, and you can unsubscribe at any time.

Shortcuts

Share