Chitsime Communication Media

Chitsime Communication Media NEWS THAT IS ACCURATE FAIR & IMPATIAL.

 #π‚π‚πŒππ„π–π’Asilikali ku Madagascar alengeza kuti alanda boma ndipo achotsa pa udindo mtsogoleri wake, Andry Rajoelina.Ndip...
15/10/2025

#π‚π‚πŒππ„π–π’

Asilikali ku Madagascar alengeza kuti alanda boma ndipo achotsa pa udindo mtsogoleri wake, Andry Rajoelina.

Ndipo asilikaliwa aimitsanso malamulo a dzikolo ndipo nthambi zonse za boma azithetsanso pamene akhazikitsa ulamulilo ongogwilizila wa a silikali.

Kotero mtsogoleri wa asilikaliwa ndi Col. Michael Randrianirina ndipo ndiyemwenso ali mtsogoleri watsopano wa dzikolo.

Malingana ndi wayilesi ya BBC, masiku apitawa a phungu a nyumba ya malamulo ya dzikolo anachotsa pa udindo mtsogoleri wa dzikolo.

Pakadali pano komwe wathawira Rajoelina sikukudziwika koma malipoti ena akuti anatuluka m'dzikolo pa ndege ya asilikali a dziko la France.

ChitsimChitsime Communication Mediae Lottie Felix Banda/2025

 Mwaswera bwanji chidzulo Chino konse komwe muliMUKUKUDZIWA INU KUTI MUDZAFA. Anthu akumudzi kwanu adzakhala pansi kukam...
15/10/2025



Mwaswera bwanji chidzulo Chino konse komwe muli

MUKUKUDZIWA INU KUTI MUDZAFA.

Anthu akumudzi kwanu adzakhala pansi kukambilana za mwambo wa maliro mene uyendere, Azimayi amudzi adzayamba kutunga madzi, Ena adzayamba kutsuka mbare pamwambowo
Azimayi adzasokha ufa ngakhale alibe oti adye madzulo.

Anyamata amudzi omwe timati achamba onukha thukuta aja adzakumba Manda oti thupi lako iweyo ligonemo

Mudzi onse udzaoneka wachisoni Ndipo anthu m'mudzi Mwanu adzalira kwambili chosecho sadadyeko ngakhale K50 Yako.

Anzako adza umati akutauni adzafika pamaliropo atanyamula mafoni awo amakono ndipo adzayamba kutumbwa kuti network ikuvuta kuno, ena adzayamba kuseka mene zakudya zaphikidwira pamaliro Ako, ena adzakana ngakhale kumwa madzi akwanu.

Adzamuuza oyendetsa mwabo kuti akonzeko misewu yanuyi ndiyokumbika tikufunaso tiyende in good time chizungu chake, Adzajambulitsa panthumbila Yako mkuika ma status maliro Ako.

Adzanyamuka mwambo usadathe kuti amvekere amakhala kutali nthawi, Alinkati maulendo adzaima pamowa kumwako uwiri utatu uku akucheza tamuika basi ameneuja Awuse muntendere.

Anthu akumudzi kwanu adzaonekabe achisoni kwasabata yose ndipo mudzi onse udzakhamukila kwanu kudzangwila ntchito zapakhomo pasiwa yako
Ndipo azibambo pabawo padza sadzaoneka kwasabata yose kuli kupereka ulemu mmudzi kamba ka iweyo.
Chosecho sadadyeko ngakhale K50 Yako.

Abare ndi alongo tikamakhala tizidziwa kuti anthu akumudzi amakhala ndi chikondi

Tiyen tiziwakumbukila ngati kuthekera kulipo kaya kuposera apo mkumawalipilirako school fizi kaya ndithandizo lanji lomwe tingafikilero.

Ambuye atikumbutse komwe tachoka

( Amen)

Pitilizani kutsatira
Chitsime Communication Media

Lottie Felix Banda 15/10/2025

Pomwe anthu  lero akukumbukira tsiku la anakubala, George Jobe mkulu wa bungwe la Malawi Health Equity Network (MHEN) la...
15/10/2025

Pomwe anthu lero akukumbukira tsiku la anakubala, George Jobe mkulu wa bungwe la Malawi Health Equity Network (MHEN) lakumbutsa anthu kuti asaiwale kufunika kosamba mmanja.

Lerobmonga tsiku lokumbukira ukhondo posamba mmanja likukumbukiridwa pa mutu woti" " Dolo amasamba mmanja ndi sopo"

Jobe wati ndi udindo watonse kulimbikitsa kusamba mmanja pafupipafupi kuti tithe kupewa matenda osiyanasiyana.

Iwo ati posachedwapa tikhala tikulandira mvula choncho aliyense akuyenera kutenga udindo opewa matenda monga Kolera,Mpox komanso Mphere omwe amayamba ndikusowa Kwa ukhondo.

Ellias Musere

15/10/2025

HAPPY MOTHER'S DAY TO ALL MOTHERS

MY ALMIGHTY GOD BLESS OUR MOTHERS

Shout out to my newest followers! Excited to have you onboard! Paul Difikoti Munthali, Peter Watsopano Wyson, Sympathy M...
15/10/2025

Shout out to my newest followers! Excited to have you onboard! Paul Difikoti Munthali, Peter Watsopano Wyson, Sympathy Mathandizo Chikwanda, Yohane J Khongo, Peter Chilambe, Maxwell Mthunzi, Stanley Kasawala, Rhones Kalirani, Peter Nambazo, Peter Namitowa, Noah Emmanuel, Alfred M R Banda, Kadyanji Redson, Jamesi Chitseko, CΓͺΓ«kΓ£y GΓΈΓ΅dΓΈΓ±Γ©, Veronica Bo Nga, Adonis Siyado, Soza Chiongah Francis, Wellus Nkosi, Chawanangwah Theu, Patrick Phiri Misheck, Jozzy Hamuzza, Enock Enockie, Idrisa Yousuf, Tryvin Banda, Vincent Makhwatha, James Clement Chisoni, Innocent Mulanje, Henry Fatsani, Ganizani Helema, Bennet Chitambaya, Rabson Gowah, Babula Arab, Innocent Mwenye, Obviou Mngombe, Matiya Issa, Adams Ponderani, Mustafa Wayison, Lucius Chigamba, Lawrence Chiphiko, Samuel F Banda, Paul Mw, Annie Missi, Ine Pano Mw, Hasheem Salar, Rodey Maganga, Foster Donda Mbewe, Atibah Adamu Kazembe, Geoffrey Laston, Ernest Ngoma
Timakunyadirani nonse

14/10/2025



BOMA LAYIMITSA KAYE KULEMBA ANTHU NTCHITO KOMASO KUKWEZA MAUDINDO

Boma lati layimitsa kaye ndondomeko zonse zolembera ntchito anthu komanso kukweza maudindo ogwira ntchito ake zomwe zimachitika pansi pa nthambi yowona za makhonsolo pofuna kuchepetsa ndalama zomwe limagwilitsa ntchito M'dziko muno.

Ndipo kalata yake mlembi wamkulu wa boma Dr.Justin Said wati pakadali pano apeza kuti ndalama zomwe boma limagwilitsa ntchito polipira ogwira ntchitowa zikukwera kwambiri pomwe chuma cha dziko lino sichikuyenda bwino.

Masiku apitawa boma linalengezanso kuti laimitsa ndondomeko zolembera ntchito anthu komanso kugura katundu ku nthambi zake zonse zomwe boma lapitali linayamba.

Chitsime Communication Media

Lottie Felix Banda 14 /10 /2025

Send a message to learn more

 As Parliament of Malawi intensifies preparations for the Orientation and Swearing-In of Members of Parliament-elect, NB...
14/10/2025



As Parliament of Malawi intensifies preparations for the Orientation and Swearing-In of Members of Parliament-elect, NBS Bank has extended its support with a donation of K10 million towards the event.

Speaking during the handover ceremony on Tuesday at Parliament Building in Lilongwe, NBS Bank National Sales Manager Aida Chilumpha said the donation reflects the bank’s commitment to strengthening its long-standing partnership with the National Assembly.

β€œNBS Bank has had a memorandum of understanding with the National Assembly since 2022. When Parliament approached us to support the orientation of new Members of Parliament, we thought it wise to step in and continue this relationship. For us, the National Assembly is like home β€” we are supporting a family,” said Chilumpha.

Deputy Clerk of Parliament responsible for Procedural Services, Joseph Manzi, described the response from various partners as overwhelming and commended NBS Bank for its timely contribution.

"Parliament is very thankful to NBS Bank for this intervention. The bank has demonstrated that it is indeed a friend in need, coming to our aid at a crucial time,” said Manzi.

He explained that the orientation programme requires substantial resources, including venue costs at the Bingu International Convention Centre (BICC) in Lilongwe. He noted that contributions like NBS Bank’s are essential in ensuring the smooth running of the event.

NBS Bank joins a growing list of partners supporting the orientation programme. Other notable contributions include:

UNDP – $140,000 plus cocktail

Chinese Embassy – $20,000 plus cocktail

Old Mutual Limited – K30 million plus cocktail

EU in collaboration with Save the Children and Centre for Civil Society Strengthening – K30 million

FDH Bank – K25 million plus cocktail

National Bank of Malawi – K20 million

Nico Holdings – K20 million

CDH Bank – K10 million plus cocktail

MASM – K10 million

ESCOM – K10 million

Standard Bank – K5 million plus cocktail

AFIDEP – K3.9 million

The Members of Parliament-elect are expected to arrive in Lilongwe on Friday, 17th October, 2025 ahead of registration on Saturday and Sunday and the official opening of the orientation programme on Monday, 20th October, 2025 at BICC.

Chitsime Communication Media

Lottie Felix Banda 14/10/2025

 ABAMBO AWIRI ALI MCHITOKOSI KU THYOLO ATABA NJINGA YA MOTOAJoseph Nanjiri zaja 24 ndi a Blessings Minthenga azaka 23 al...
14/10/2025



ABAMBO AWIRI ALI MCHITOKOSI
KU THYOLO ATABA NJINGA YA MOTO

AJoseph Nanjiri zaja 24 ndi a Blessings Minthenga azaka 23 ali m'chitokosi cha polisi ya Masambanjati ku Thyolo powaganizira kuti anaba njinga ya moto ndikumuvulaza mwini njingayo.

Ndipo wofalitsa nkhani za polisi ya Masambanjati a Amosi Banda ati pa 12 October a Blessings James omwe ndi ochita malonda yo kabaza, anapemphedwa ndi oganiziridwawa kuti awanyamule pa njingayo kuchokera ku Bangwe mu nzinda wa Blantyre kupita nawo ku Thekerani M'boma la Thyolo kwa mkulu wina ochita mankhwala azitsamba.

Komaso aBanda ati, atafika ku Thekerani anthuwo anawoloka kupita ku Mozambique, ndipo pobwerera oganiziridwawo anachitira chipongwe oyendetsa njingayo, kumusiya atakomoka.

"Ndipo atatsitsimuka, anapeza kuti phone yake ya mtundu wa Itel A60, ya k70 000, komanso njinga ya moto ya King Boss yofiira amubera." Anatero a Banda polankhulana CCM Online

Kotero anapita pa mudzi pena pomwe anthu achifundo adamutengera ku chipatala cha Thekerani Mission kenako anakadandaula ku polisi ya Masambanjati ndipo kutsatira kafukufuku wa apolisi, akwanitsa kupeza njingayo ndi kumanga mbamvazo.

A Nanjiri amachokera m'mudzi wa Mtunduwatha, T/A Nsabwe ku Thyolo ndipo Minthenga amachokera m'mudzi wa Matewere T/A Mabuka m'boma la Mulanje.

Chitsime Communication Media

Lottie Felix Banda 14/10/2025

ZamaseweroTimes Sports journalist  Mabvuto Kambuwe is the winner of  the 2024 Castel Challenge Cup award for the Best pr...
14/10/2025

Zamasewero

Times Sports journalist Mabvuto Kambuwe is the winner of the 2024 Castel Challenge Cup award for the Best print Journalist.

This is according to a joint statement issued today by the Football Journalists Association of Malawi and Castel Malawi.

According to Kambuwe it is always happy and motivating when people recognize someone's work.

Other awardees include Praise Majawa of MBC as Best Online Journalist,
Tadala Manda Of Mibawa Television as best in television and Nation Publication's Limited Bobby Kabango as the Best Photo Journalist.

Wongani Sichinga, Raymond Siyaya and Isaac Grant are winners in North, South and central community radio reporters.

Chitsime Communication Media

Lottie Felix Banda 14/10/2025

 MADALITSO TSANZO ALI MMANJA MWA APOLOISI Madalitso Tsanzo wa m'mudzi mwa Missi kwa Mfumu yaikulu Chakhaza Ku mponela Ku...
14/10/2025



MADALITSO TSANZO ALI MMANJA MWA APOLOISI
Madalitso Tsanzo wa m'mudzi mwa Missi kwa Mfumu yaikulu Chakhaza Ku mponela Ku dowa Ali mmanja mwa apolisi kaamba kopezeka ndi mankhwala akuchipatala popanda makalata.

Mneneli wa polisi ya Mponela Sergent Macpartson Msadala wati bamboyu amugwila pa Trading ya Mponela ku m'mawa wa lero. mkuluyi anali ndi mankhwalawa m'chikwama chake chomwe anabelekera panthawiyo.

Malingana ndi Msadala apolisi atamva izi anatsatila mkuluyi ndipo atayang'ana mchikwamachi anapezeka ndi mankhwalawa koma atamufusa zamapepala anakanika kulongosola zomwe zinachititsa kuti amangidwe.

Iye wati apolisi wa anapeza mankhwala monga Azitromicina okwana ma pilitsi 27, mabokosi 1000 a Salbutamola, timabotolo 60 ta Medogen Suspension obaya komaso Declofenac okwana 400.

Ndipo atapitso Ku nyumba kwake mkuluyi apolisiwa anapezaso ma capsules okwana 1000 a Amoxicillin komaso Metrodonazole a mapilitsi okwana 1000.

Chitsime Communication Media

Lottie Felix Banda 14/10/2025

 #π‚π‚πŒππ„π–π’TIKUFUNA TITUKULE ACHINYAMATA KU MCHINJI.Wofesi yowona za achinyamata M'boma Mchinji yati ikulingalila zolimbik...
14/10/2025

#π‚π‚πŒππ„π–π’

TIKUFUNA TITUKULE ACHINYAMATA KU MCHINJI.

Wofesi yowona za achinyamata M'boma Mchinji yati ikulingalila zolimbikitsa achinyamata 30 pa 100 kukhala makomiti owona zachitukuko ndi kuti achinyamata adzipeza thandizo lachitukuko mosavuta M'bomali

Ian Sukali wati maofesi aboma ndi mabugwe omwe siaboma akuyenera kuyika patsogolo achinyamata kutenga nawo gawo pantchito zachitukuko ndi kupereka ziganizo.

Ndipo ati ofesiyi padakali pano ikusula achinyamata kukhala ndi upangiri wa m`mene angasithire zithu m`madera awo.

Izi zikudza kutsatira kudandaula kwa achinyamata m`bomali omwe akuti ambiri mwa iwo akusowa ntchito, zitukuko zambiri samatenga nawo gawo komanso samawasakha maudindo.

ChitsimChitsime Communication Mediae Lottie Felix Banda2025

 #π‚π‚πŒ??π„π–π’πŒπ€π•π„ππƒπ€ π€πŒπ”π™πˆππƒπ€ π–π€π‹πˆπ‹πŽππ†π–π„ π€πŠπ”π…π”ππ€ πŠπ”ππ„ππ„π’π€  πŠπ–π€ π‚π‡π€πŠπ–π„π‘π€Opanga malonda mu mzinda wa Lilongwe motsogozedwa nd...
14/10/2025

#π‚π‚πŒ??𝐄𝐖𝐒

πŒπ€π•π„ππƒπ€ π€πŒπ”π™πˆππƒπ€ π–π€π‹πˆπ‹πŽππ†π–π„ π€πŠπ”π…π”ππ€ πŠπ”ππ„ππ„π’π€ πŠπ–π€ π‚π‡π€πŠπ–π„π‘π€

Opanga malonda mu mzinda wa Lilongwe motsogozedwa ndi atsogoleri amsika ati apanga chiganizo choti akakumana ndi mtsogoleri wa kale wa dziko lino Lazarus Chakwera.

Cholinga cha mkumano ndikupepesa kuti amawona ngati akasintha mtsogoleri wa dziko malonda aziyenda kuponsa mmene amayendela kale.

Francis phiri omwe ndi mtsogoleri wa omwe amameta wati Chichokeleni achakwera ntchito zawo zalowa pansi.John yakobe omwe amatsogoleri omwe amagwira ntchito yowotchelera ati adakadziwa sadakapeleka voti ku chipani cha Dpp.

Atsogoleri a m'sika wa Lilongwe ati chisinthileni boma zinthu zakwera mtengo kwambiri monga bello lazovala lomwe amawoda 600,000 pana lafika 900,000 zomwe zapangitsa ambiri kukhala pansi.

Chitsime Communication Media

Lottie Felix Banda 14 /10 /2025

Address

Plane Street
Johannesburg

Telephone

+27710989717

Website

Alerts

Be the first to know and let us send you an email when Chitsime Communication Media posts news and promotions. Your email address will not be used for any other purpose, and you can unsubscribe at any time.

Contact The Business

Send a message to Chitsime Communication Media:

Share