Chitsime Communication Media

Chitsime Communication Media NEWS THAT IS ACCURATE FAIR & IMPATIAL.

20/08/2025



Mtsogoleri Wadziko lino Dr Lazarus Chakwera ali ku Phiri la Njuzi komwe alandiridwa ndi anthu ochuluka.

Ndipo anthu akumeneko ayamikira mtsogoleri Wadziko lino Dr Chakwera polimbikitsa mtima osasankhana mitundu komanso chikhalidwe chawo chabwino chosakondera pogwira ntchito za chitukuko.

Ndipo anthu akumeneko atsimikizira Chakwera kuti akaponya voti. Chifukwa Anthu 40,000 ndi omwe adalembetsa voti kudera la Phiri la Njuzi.

Chitsime Communication Media

Lottie Felix Banda

 . Timu ya Ekhaya FC yalengeza kuti  osewera atatu, otchinga pagolo Joshua Waka komanso osewera pakati Moses Banda ndi B...
20/08/2025

.

Timu ya Ekhaya FC yalengeza kuti osewera atatu, otchinga pagolo Joshua Waka komanso osewera pakati Moses Banda ndi Blessings Malinda ndi osewera a timuyi tsopano.

Waka amugula kuchokera ku timu ya Blue Eagles pa mtengo wa 10 million kwacha pomwe Banda ndi Malinda awagula ku timu ya Civo koma ndalama zomwe apereka sanaziulure.

Polankhura Waka wati ndi okondwa kukhala mbali imodzi ya timu ya Ekhaya.

" Panali ma timu ena akulu omwe amandifunanso koma ku Ekhaya ndi komwe mtima wanga wasankha ndipo ondikonda ayembekezere ntchito zanga zabwino ," watelo Joshua.

Naye mphunzitsi wa timuyi Enos Chatama wati osewerawa abweretsa mpikisano wabwino ku timuyi ndipo akuyembekezera ntchito zawo kulimbitsa timu ya Ekhaya.

Masewero oyamba a mphangala zitatuzi akhala lamulungu pa bwalo la Kamuzu ndi timu ya Mzuzu City Hammers.

Olemba:Innocent Chipumba Phiri-The Bench Top Goal Scorer (Zampira Sakwiya)..

 MKANDA KOMASO MWAMI TOTAL FILING MALAMULO ASINTHA.Mkanda- Total filing station komaso Mwami- Total filing station Takon...
20/08/2025


MKANDA KOMASO MWAMI TOTAL FILING MALAMULO ASINTHA.

Mkanda- Total filing station komaso Mwami- Total filing station Takondwa ku Mchinji ndi ena mwa malo ogulitsa mafuta omwe bungwe la Malawi Energy Regulatory Authority (MERA) lalamula kuti azigwira ntchito kuyambira nthawi ya 6 koloko m'mawa kulekeza 6 koloko madzulo.

Malingana ndi chikalata chomwe atulutsa a MERA, lamuloli likubwera chifukwa cha kuchepa kwa mafuta komwe kwachulukila chifukwa cha kugulitsa mosaloledwa, kusunga mafuta mwachinyengo komanso kugulitsa pamsika wosavomerezeka.

MERA ikuchenjeza kuti malo ogulitsa mafuta osatsatira lamuloli adzalandila chilango.

Chitsime Communication Media

Lottie Felix Banda

 . Osewera kutsogolo, Luke Chima, wayamba kuchita zokonzekera ndi timu ya Premier Bet Dedza Dynamos.Chima yemwe season y...
20/08/2025

.

Osewera kutsogolo, Luke Chima, wayamba kuchita zokonzekera ndi timu ya Premier Bet Dedza Dynamos.

Chima yemwe season yatha anali ku Moyale Barracks FC akuchita zokonzekera ndi timuyi pofuna kuthetsa vuto losowa zigoli lomwe Dynamos inali nawo gawo loyambilira la TNM Super league.

Ku timuyi kwafikanso osewera 8 omwe amatumukira kumatimu osewera maligi ang'ono-ang'ono omwe mwa asanu ndiosewera kutsogolo.

Timuyi ikhala ikulengeza posachedwa za mgwirizano omwe agwirizane ndi osewerawa.

Olemba:Innocent Chipumba Phiri-The Bench Top Goal Scorer (Zampira Sakwiya)..

 . Pali chiyembekezo kuti ntchito yotsilizitsa kumanga bwalo lamakono la Griffin Sayenda Sports Complex itha kuyambirans...
20/08/2025

.

Pali chiyembekezo kuti ntchito yotsilizitsa kumanga bwalo lamakono la Griffin Sayenda Sports Complex itha kuyambiranso kutsatira zokambirani ndi company zomangamanga.

Ntchito yotsilizitsa malowa, inaima m'chaka cha 2022, pomwe dziko lino limachititsa mpikisano wa Africa Union Sports Council (AUSC) Region 5 munzinda wa Lilongwe.

Mneneri ofalitsa nkhani ku unduna wa zamasewero a Macmillan Mwale, auza Ccm kuti ntchito yotsilizitsa maliwa itha kuyamba nthawi iliyonse kutsatira kukambirana ndi company zomangamanga kuti zigwire ntchitoyi.

Iwo ati pakadali pano, ntchitoyi itha kutenga miyezi iwiri kuti itsirizike ndipo mwazina ntchitoyi ikayambika akhala akuika madzi, magetsi komanso zipata zamakono zomwe zizigwiritsidwa pa malowa.

Kupatula masewero a mpira wamanja, malo a Griffin Sayenda amagwiseweredweranso masewero ena monga, volleyball, basketball.

Ngakhale ntchitoyi ikuyembekezeka kuyambanso posachedwapa dziko la Malawi, likuyembekezeka kuchititsa mpikisano wamaiko amu Africa kumapeto a chaka chino.

Dziko la Malawi linachititsa mpikisanowu kotsiriza m'chaka cha 2013, pa Blantyre Sports Arena lomwe kale limkatchedwa Blantyre Youth Center.

Olemba:Innocent Chipumba Phiri-The Bench Top Goal Scorer (Zampira Sakwiya).

  Timu ya Mighty Wanderers yadyelera maso osewera wawo wakale wa kutsogolo, Muhammad Sulumba, ndicholinga choti abwelere...
20/08/2025



Timu ya Mighty Wanderers yadyelera maso osewera wawo wakale wa kutsogolo, Muhammad Sulumba, ndicholinga choti abwelerenso ku timuyi.

Izi ndimalinga ndizomwe nyuzipepala ya Times yalemba lero.

Lingaliro lofuna kusaina Sulumba labwera pofuna kulimbitsa kutsogolo kwa timuyi potengera kuti akhala akusewera mu CAF Confederation Cup.

NKHAN ZAKUNJA
LALIGA CUP.

Real Madrid Vs Osasuna
81'
Real Madrid 1-0 Osasuna
Mbappe 51 (scored).

By Innosent Chipumba Phiri-The Bench Top Goal Scorer (Zampira Sakwiya)

MORNING DEVOTION. Lekani kudziyankhulira mawu oyipa( odzitemberera ndikudziweruza)-Ambiri mwa ife timadzinenera kuti sit...
20/08/2025

MORNING DEVOTION.

Lekani kudziyankhulira mawu oyipa( odzitemberera ndikudziweruza)
-Ambiri mwa ife timadzinenera kuti sitingatukuke, sitingalemere, sitingapeze banja,aitingafike patali ndi maphunziro, sitingabereke etc.

-Ngakhale nyengo zitalimba motani phunzirani kudziyankhulira mawu abwino komanso odzidalitsa osati kudzitemberera.
-Dziwani kuti mawu amapha komanso Kupereka moyo ku zinthu zathu
-Mawu ndiye gwero la chipambano kapena kugonjetsedwa mmoyo uno.
-Mu dziko la uzimu, Angelo komanso Mzimu wa Mulungu amakalenga ndikugwira ntchito pa mawu omwe tawayankhula molingana ndi Bible
-Mu dziko lauzimu momwemo(kumidima), ziwanda komanso Satana, amagwiritsa ntchito ndikukwaniritsa mawu onse opanda pake omwe tadziyankhulira
-Kuwonjezera apa, osalola munthu kukuyankhulirani mawu opanda pake ( okutembererani/ kukunyozani kapenanso kukuyang'anirani pansi.
____________________________
MATEYU 12:36
"Ndikukuuzani kuti liwu lirilonse lopanda pake lomwe timayankhula, tidzaweruzidwa nalo pa tsiku la chiweruzo"

MIYAMBO 18:20-21
Mimba ya munthu, imakhuta ndi zipatso zochokera pakamwa pake. Lirime liri ndi mphamvu yopereka moyo kapena imfa ndipo olikonda adzadya zipatso zake"

Lero Munali Ndine INNOCENT CHIPUMBA PHIRI.

19/08/2025

Ccm
NewUpdate.

Lipoti la Smart DNA mdziko la Nigeria lawonetsa kuti zotsatira zabanja limodzi mwa mabanja anayi aliwonse omwe amayezetsa kuti apeze umwini wa ana obadwa, zimakhala zosemphana pakati pa makolo ndi ana.

Izi zikutanthauza kuti makolo ambiri m’dzikolo akulera ana oti siawo kaamba kakusakhulupirika m'banja ndi okondedwa awo.

Malinga ndi DW, Smart DNA Nigeria yapeza kuti abambo 25 pa 100 alionse pa omwe anayezedwa si eni ana obadwa mmabanja mwawo.

Kafukufukuyu watinso ana ambiri omwe amasemphana ndi zotsatira za DNA ndi atate awo anali ana amuna oyamba kubadwa m'banja.

Olemba: Innocent Chipumba Phiri-Kasungu.

   Potsatira chiletso chomwe akulu-akulu oyang'anira bwalo la Chitipa apereka choti FCB Nyasa Big Bullets isachite zokon...
19/08/2025



Potsatira chiletso chomwe akulu-akulu oyang'anira bwalo la Chitipa apereka choti FCB Nyasa Big Bullets isachite zokonzekera masewero a TNM Super league omwe akhale akukumana ndi Chitipa United loweruka likudzali, Mapale anakaongola miyendo pa bwalo lina lowandikana ndi bwalo la Ndege m'bomali.

Iyi ndi njira yokhayo yoti osewera athe kukonzekera masewerowa kamba ka chiletso chomwe oyang'anira bwalo la Chitipa anapereka.

Bullets inapita ku chigawo cha kumpoto sabata yatha komwe kumathero a sabata yathayi anagonjetsa Chilumba Barracks 5-0 pa bwalo lomweli mumpikitsano wa FDH Bank Cup.

Olemba :Innocent Chipumba Phiri-The Bench Top Goal Scorer (Zampira Sakwiya)...

Chisankho cha  khansala ku dera la Luwinga ku m'mawa kwa mzinda wa  Mzuzu chaimitsidwa mpaka mtsogolo munoBungwe la MEC ...
19/08/2025

Chisankho cha khansala ku dera la Luwinga ku m'mawa kwa mzinda wa Mzuzu chaimitsidwa mpaka mtsogolo muno

Bungwe la MEC ndiwo laimisa chisankhochi kusatila imfa ya mmodzi mwa opikisana nawo yemwe amaimila chipani cha UDF.

Ndipo chipani cha UDF chati ndichokhumudwa chifukwa Cha imfayi

Ellias Musere

Mkazi wamtsogoleri wakale wa dziko lino yemwenso ndi mtsogoleli wachipani cha DPP a Gertrude Mutharika, wapempha Anthu k...
19/08/2025

Mkazi wamtsogoleri wakale wa dziko lino yemwenso ndi mtsogoleli wachipani cha DPP a Gertrude Mutharika, wapempha Anthu kuzavotera yemwe Ali ndikuthekela kotukula miyoyo ya amalawi.

Iye wati Anthu asate mfundo zomwe zingapindulile dziko lino ,,osati mabodza a

Iwo ayankhula izi ku Mangochi pa mtsonkhano omwe ,a Overton Imedi,anachotitsa

Elias Musere

Chipani cha UTM chati sichikupqngq mgwririzano ndi Chipani chilichonse.Mtsogoleli wachipanichi  Dalitso Kabambe wati pak...
19/08/2025

Chipani cha UTM chati sichikupqngq mgwririzano ndi Chipani chilichonse.

Mtsogoleli wachipanichi Dalitso Kabambe wati pakadali pano nthawi yatha ndipo sipakufunikqnso kupanga mgwririzano.

Iwo apempha Anthu otsatila chipanichi kuti akawavotere pa chisankho chikubwelachi chifukwa akapikisana nawo ngati mtsogoleli.

Ellias Musere

Communication Media #

Address

Plane Street
Johannesburg

Telephone

+27710989717

Website

Alerts

Be the first to know and let us send you an email when Chitsime Communication Media posts news and promotions. Your email address will not be used for any other purpose, and you can unsubscribe at any time.

Contact The Business

Send a message to Chitsime Communication Media:

Share