20/08/2025
.
Pali chiyembekezo kuti ntchito yotsilizitsa kumanga bwalo lamakono la Griffin Sayenda Sports Complex itha kuyambiranso kutsatira zokambirani ndi company zomangamanga.
Ntchito yotsilizitsa malowa, inaima m'chaka cha 2022, pomwe dziko lino limachititsa mpikisano wa Africa Union Sports Council (AUSC) Region 5 munzinda wa Lilongwe.
Mneneri ofalitsa nkhani ku unduna wa zamasewero a Macmillan Mwale, auza Ccm kuti ntchito yotsilizitsa maliwa itha kuyamba nthawi iliyonse kutsatira kukambirana ndi company zomangamanga kuti zigwire ntchitoyi.
Iwo ati pakadali pano, ntchitoyi itha kutenga miyezi iwiri kuti itsirizike ndipo mwazina ntchitoyi ikayambika akhala akuika madzi, magetsi komanso zipata zamakono zomwe zizigwiritsidwa pa malowa.
Kupatula masewero a mpira wamanja, malo a Griffin Sayenda amagwiseweredweranso masewero ena monga, volleyball, basketball.
Ngakhale ntchitoyi ikuyembekezeka kuyambanso posachedwapa dziko la Malawi, likuyembekezeka kuchititsa mpikisano wamaiko amu Africa kumapeto a chaka chino.
Dziko la Malawi linachititsa mpikisanowu kotsiriza m'chaka cha 2013, pa Blantyre Sports Arena lomwe kale limkatchedwa Blantyre Youth Center.
Olemba:Innocent Chipumba Phiri-The Bench Top Goal Scorer (Zampira Sakwiya).