Chitsime Communication Media

Chitsime Communication Media NEWS THAT IS ACCURATE FAIR & IMPATIAL.

 .Unduna wa zachuma waitana ena mwa makhansala mdziko muno kuti akaperekepo maganizo awo pa ndondomeko ya chuma cha boma...
11/01/2026

.

Unduna wa zachuma waitana ena mwa makhansala mdziko muno kuti akaperekepo maganizo awo pa ndondomeko ya chuma cha boma cha 2026-2027.

Mmodzi mwa makhansala omwe CCMnews yapeza, ndi a Maloto Chimkombero yemwe ndi khansala wa Kalira Masamba ward m'boma la Ntchisi.

Unduna wa zachuma motsogozedwa ndi nduna ya undunawu, Hon Joseph Mwanamveka akuyenda mzigawo za dziko lino komwe akumakumana ndi akatswiri komanso adindo ochepa chabe kuti apereke maganizo awo pa zomwe akufuna kuti zikhale mu ndodomeko ya chuma cha boma yomwe iyambe kugwila ntchito pa 1 April chaka chino.

Khansala waku Ntchisiyu, yemwenso ndi wapampando wa khonsolo ya Ntchisi, waikidwa mu gulu lomwe likapereke maganizo ake mu mzinda wa Mzuzu mawa lino pa 12 January 2026.

Mwa zina, a Chimkombero ati akapempha undunawu kuti ukweze malipiro amakhansala, kuika ndondomeko yoti makhansala azigula nawo galimoto zopanda msonkho monga momwe amachitira ma MP, komanso kuti ma DC azigulilidwa galimoto yawoyawo akamagwira ntchito.

Pa nkhani yokhudza ndalama zachitukuko za kudera la phungu (CDF), Chimkombero wati akapempha undunawu kuti ukhazikitse ndondomeko zokhwima komanso zopereka mphamvu ku anthu akumudzi kuti azitha kupanga nawo ziganizo ndikulondoloza momwe CDF iziyendera.

Malingana ndi khansala yu, izi zithandiza kuchepetsa chinyengo chomwe chimakhalapo pa ndalama za chitukuko mmadera zomwe pamapeto pake zimaphinja anthu osauka maka achinyamata, amai ndi ana.

Khansala Chimkombero, yemwenso ndi wachiwiri kwa Prezident wa Malawi Local Government Association (MALGA), ndi mmodzi mwa andale achinyamata amene boma likumawafuna pafupipafupi pa zinthu zokhudza dziko lino.

Ndipo mmau ake, Chimkombero wapempha achinyamata kuti asamaope kutenga nawo gawo pa utsogoleri wa ndale m'dziko muno.

Khansala Chimkombero ndi mmodzi mwa makhansala asanu( 5) omwe akakhale nawo ku zokambiranazi.

Wolemba: Tchovaldinho Linyama-Ntchisi (11-01-2026).

 .Gulu la amayi omvera wayilesi ya Mzati la Mchezo wa Amayi m'boma la Mulanje lapeleka thandizo la katundu osiyanasiyana...
11/01/2026

.

Gulu la amayi omvera wayilesi ya Mzati la Mchezo wa Amayi m'boma la Mulanje lapeleka thandizo la katundu osiyanasiyana kwa Anthu achikulire asanu a m'mudzi mwa Njojo, mfumu yayikulu Mabuka m'boma la Mulanje Alandira Katundu osiyanasiyana kuchokera kwa Gulu la Amayi Omvera Wailesi Ya Mzati la Mchezo.

Thandizoli ndi monga Sopo, mchere, machesi, ufa, nsalu ndi mafuta ophikira.

A Catherine Khonjeni omwe ndi Mkhala pampando wa gulu limeneli ati apelekeka thandizoli potengera mavuto omwe anthuwa amakumana nawo pa umoyo wawo wa tsiku ndi tsiku ndipo ati ndi khumbo lawo kufikira anthu ochuluka ndi thandizoli.

M'mau ake, mfumu Njojo yayamikira gululi kaamba ka thandizoli ponena kuti liwathandiza anthuwa popeza moyo wawo umakhala ovuta kaamba kosowa chisamaliro.

Wolemba: Tchovaldinho Linyama (11-01-2026).

Dzuro loweruka pa 10, January,2026 M'busa Alexander Kambiri yemwe adatumikirapo pa mpingo wa Mthawira m'boma la Ntchisi ...
11/01/2026

Dzuro loweruka pa 10, January,2026 M'busa Alexander Kambiri yemwe adatumikirapo pa mpingo wa Mthawira m'boma la Ntchisi wasankhidwa kukhala wachiwiri kwa mlangizi wa mtsogoleri wa dziko lino a professor Aurth Peter Mutharika pa nkhani za chipembedzo.

Malinga ndi kalata yomwe yasainidwa ndi mlembi wamkulu wa boma Dr Justin Saidi, Reverend Kambiri ayamba kale kugwira ntchito yawo pa udindowu.

Wolemba: Tchovaldinho Linyama (11-01-2026).

10/01/2026

.

A zaki Finta a zaka makumi atatu ndi ziwiri (32) omwe amaganizira kuti aba ng'ombe mdziko la Mozambique, afa m'boma la Nsanje ng'ona itawamudya ndikungotsala mutu wokha pamene amafuna kuwoloka mtsinje wa Ruo pothawa anthu olusa omwe amafuna kuwagwira.

Ofalitsa nkhani za a polisi m'boma la Nsanje a Agnes Zalakoma ati bamboyo, yemwe wakhala akudziwika ndi umbava wa ng'ombe, anawolosa ng'ombe pa doko la Makhanga limodzi ndi anzawo ena awiri pamene anthu anawazindikira kuti anali ataziba ku Mozambique.

A Zalakoma ati kenako a Finta pamodzi ndi anzawo anayamba kuthawa ndipo iwo anaganiza zoti awoloke mtsinje wa Ruo kuti abwelenso mbali yaku Mozambique mpamene amakumana ndi tsokalo.

A Zaki Finta amachokera pamudzi wa Nyang'a kwa TA Mbenje m'boma lomweli.

Wolemba: Tchovaldinho Linyama-Ntchisi (10-01-2026).

NDITUMIZA TIMUYI KUNJA KWADZIKO LINO _ MpinganjiraMtsogoleri wa timu ya Mighty Wanderers, Thomson Mpinganjira, ati atumi...
10/01/2026

NDITUMIZA TIMUYI KUNJA KWADZIKO LINO _ Mpinganjira

Mtsogoleri wa timu ya Mighty Wanderers, Thomson Mpinganjira, ati atumiza timuyi kunja kwa dziko lino kukakonzekera Mipikisano ya chaka chino isanayambe.

Mtsogoleri yu wati pochita izi ikhala mbali imodzi yokonzekeretsa timuyi kusewera mpikisano wa CAF Champions League.

Chaka chatha, Wanderers inalowa mpikisano wa CAF Confederations Cup komwe inagonja mu ndime yoyamba ndi Jwaneng Galaxy ya m'dziko la Botswana.


( Benjamin Francisco )

 Bambo wina ku ku Mchinji ali mmanja mwa apolisi kamba konamiza anthu kuti ndi msilikali wa MDF.Ofalisa nkhani za apolis...
09/01/2026



Bambo wina ku ku Mchinji ali mmanja mwa apolisi kamba konamiza anthu kuti ndi msilikali wa MDF.

Ofalisa nkhani za apolisi bomali Limbani Mpinganjira wati mkuluyu ndi Michael Tambala,wazaka 42.

Mpinganjira wati mkuluyu wakhala akuzungulira pa chipatala cha bomali ponepa kuti watumidwa kuzaoma za mmene katundu amalowera komanso kutuluka pa chipatalachi.

Koma atafusidwa kuti awonetse chiphatso chogwirira ntchito yake ,anakanika kuwonetsa,zomwe zinapangitsa kuti apolisi amunjate.

Michael Tambala amachokera m'mudzi wa Tambala, mfumu yaikulu Kwataine m'boma la Ntcheu.


 .Oweruza ku bwalo la milandu la  Apilo Dorothy Nyakaunda wakana pempho la mlembi wa chipani cha MCP Richard Chimwendo B...
09/01/2026

.

Oweruza ku bwalo la milandu la Apilo Dorothy Nyakaunda wakana pempho la mlembi wa chipani cha MCP Richard Chimwendo Banda loiimitsa apolisi kumusungabe podikila mulandu wake.

Bwaloli lagwilizana ndi oimila boma pa mulanduwu Dzikondianthu Malunda kuti pempholi lapita mu bwalo lolakwika.

A Richard Chimwendo Banda apitilirabe kusungidwa ndi apolisi kudikilira chigamulo cha bwalo la milandu lalikulu pa pempho lake la belo.

Wolemba:Tchovaldinho Linyama

  NKHANI YA CHISONI . A Madalits Kazombo yemwe adali wachiwiri kwa sipikala wa nyumba ya malamulo komanso phungu wadera ...
08/01/2026


NKHANI YA CHISONI .

A Madalits Kazombo yemwe adali wachiwiri kwa sipikala wa nyumba ya malamulo komanso phungu wadera la kummawa kwa boma la Kasungu mu ulamuliro wa MCP a wamwalira.

Nduna yakale ya zaumoyo yemwenso ndi akubanja kwa a Kazombo, Khumbize Kandodo Chiponda watsimikiza za nkhaniyi ndipo wati anangogwa, koma atathamangira nawo kuchipatala ndikomwe azaumoyo atsimikiza za imfayi.

Kazombo womwe anali mu chipani cha Malawi Congress (MCP), anakhala MP wadera la kummawa kwa boma la Kasungu kuyambira m'chaka cha 2014, kenako anadzapambananso m'chaka 2019, ndi kugonja mu chaka cha 2025.

By Innosent Chipumba Phiri-Kasungu

 Bungwe la Football Association of Malawi ( FAM ) lachejeza Matimu komatso laika malire kuma timu onse kuti achotse osew...
08/01/2026



Bungwe la Football Association of Malawi ( FAM ) lachejeza Matimu komatso laika malire kuma timu onse kuti achotse osewera omwe sakuwafuna kufikila pa 28 February.

Fam yachita izi chifukwa Cha khalidwe lamatimu ena omwe amachosa osewera awo nthawi yoyamba season ina itawandikila.

Izi zimapangitsa kuti osewera ena kukhale kovuta kupeza matimu oti asewelele.


( Benjamin Francisco )

MAANJA ENA AKUSOWA MTENGO OGWILA.Boma la Mchinji Maanja oposa 60 ali kakasi kusatila mvula ya mkuntho yomwe yagwetsa nyu...
08/01/2026

MAANJA ENA AKUSOWA MTENGO OGWILA.

Boma la Mchinji Maanja oposa 60 ali kakasi kusatila mvula ya mkuntho yomwe yagwetsa nyumba zawo mmudzi wa Ndawambe.

A Lenos Mandowa omwe ndi modzi mwa anthu okhudzidwa ati mvulayi inagwa kwa maola pafupi fupi asanu.

Pakanali pano yemwe akugwilizira udindo wa mkulu waofesi yoona zangozi zogwa mwazizi m'bomali Chisomo Kuchepa wati atumiza alangizi aofesiyi kuderali.


( Benjamin Francisco )

 Mtsogoleri wadziko lino Pro.Peter Muthalika ,mawa akhala nawo pa mwambo olumbiritsa anthu omwe asankhidwa mmaudindo osi...
08/01/2026



Mtsogoleri wadziko lino Pro.Peter Muthalika ,mawa akhala nawo pa mwambo olumbiritsa anthu omwe asankhidwa mmaudindo osiyanasiyana mdziko muno.

Mlembi wakulu waboma a Justin Saidi asimikiza izi kuzera mu kalata yomwe atulusa lero,

Mwambowu ukachitikira ku nyumba yaboma ya Kamuzu munzinda wa Lilongwe.


Address

Plane Street
Johannesburg

Telephone

+27710989717

Website

Alerts

Be the first to know and let us send you an email when Chitsime Communication Media posts news and promotions. Your email address will not be used for any other purpose, and you can unsubscribe at any time.

Contact The Business

Send a message to Chitsime Communication Media:

Share